< 2 Samueli 21 >

1 Pa nthawi ya ulamuliro wa Davide kunali njala kwa zaka zitatu zotsatana. Kotero Davide anapemphera kwa Yehova. Yehova anati, “Izi zachitika chifukwa chakuti Sauli ndi banja lake akanali ndi mlandu wakupha Agibiyoni.”
And it was a famine in [the] days of David three years year after year and he sought David [the] face of Yahweh. And he said Yahweh because of Saul and because of [the] house of blood on that he put to death the Gibeonites.
2 Mfumu inayitanitsa Agibiyoni ndipo inayankhula nawo. (Tsono Agibiyoni sanali Aisraeli, koma otsala mwa Aamori. Aisraeli analumbira kuwasiya ndi moyo, koma Sauli chifukwa cha chikondi cha pa Israeli ndi Yuda, anafuna kuwawonongeratu).
And he summoned the king the Gibeonites and he said to them and the Gibeonites not [were] from [the] people of Israel they that except from [the] remnant of the Amorite[s] and [the] people of Israel they had sworn an oath to them and he had sought Saul to strike down them because was zealous he for [the] people of Israel and Judah.
3 Davide anafunsa Agibiyoni kuti, “Kodi ine ndikuchitireni chiyani? Ndipepese bwanji kuti inu mudalitse cholowa cha Yehova?”
And he said David to the Gibeonites what? will I do for you and how? will I make amends and bless [the] inheritance of Yahweh.
4 Agibiyoni anamuyankha kuti, “Ife tilibe ufulu woti nʼkulamula Sauli ndi banja lake kuti atipatse siliva kapena golide, tilibenso ufulu woti nʼkupha wina aliyense mu Israeli.” Davide anafunsa, “Mukufuna ine ndikuchitireni chiyani?”
And they said to him the Gibeonites not (to us *Q(K)*) silver and gold with Saul and with house his and not to us a man to put to death in Israel and he said what? [are] you saying I will do for you.
5 Iwo anayankha mfumu kuti, “Tsono za munthu amene anatiwononga ndi kukonza chiwembu choti titheretu ndi kukhala wopanda malo mu Israeli,
And they said to the king the man who he made an end of us and who he planned to us we were destroyed from standing in all [the] territory of Israel.
6 mutipatse adzukulu ake aamuna asanu ndi awiri kuti tiwaphe ndi kuwapereka pamaso pa Yehova ku Gibeya wa Sauli, wosankhidwa wa Yehova.” Choncho mfumu inati, “Ine ndidzakupatsani.”
(Let it be given *Q(K)*) to us seven men from descendants his and we will impale them to Yahweh at Gibeah of Saul [the] chosen one of Yahweh. And he said the king I I will give [them].
7 Koma mfumu inasunga Mefiboseti mwana wa Yonatani, mwana wa Sauli, chifukwa cha kulumbira kumene mfumu Davide ndi Yonatani mwana wa Sauli anachita pamaso pa Yehova.
And he had compassion the king on Mephi-bosheth [the] son of Jonathan [the] son of Saul on [the] oath of Yahweh which [was] between them between David and between Jonathan [the] son of Saul.
8 Ndipo mfumu inatenga Arimoni ndi Mefiboseti, ana aamuna awiri a Rizipa, mwana wamkazi wa Ayiwa, amene anaberekera Sauli pamodzi ndi ana asanu a Merabi mwana wamkazi wa Sauli, amene anabereka Adirieli mwana wa Barizilai Mmeholati.
And he took the king [the] two [the] sons of Rizpah [the] daughter of Aiah whom she had borne to Saul Armoni and Mephibosheth and [the] five [the] sons of Michal [the] daughter of Saul whom she had borne to Adriel [the] son of Barzillai the Meholathite.
9 Iye anawapereka kwa anthu a ku Gibiyoni, amene anawapha nawayika pa phiri la Yehova. Onse asanu ndi awiri anafera limodzi. Iwo anaphedwa masiku oyamba kukolola barele.
And he gave them in [the] hand of the Gibeonites and they impaled them on the mountain before Yahweh and they fell ([the] seven of them *Q(K)*) together (and they *Q(k)*) they were put to death in [the] days of harvest in the first (at [the] beginning of *Q(K)*) [the] harvest of barley.
10 Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa anatenga chiguduli ndi kudziyalira pa mwala (pamene panali mitemboyo). Kuyambira nthawi yoyamba kukolola mpaka pamene mvula inayambanso kugwa, iye sanalole kuti mbalame zikhudze mitemboyo masana kapena nyama zakuthengo usiku.
And she took Rizpah [the] daughter of Aiah sackcloth and she spread out it for herself to the rock from [the] beginning of harvest until it was poured out water on them from the heavens and not she permitted [the] bird[s] of the heavens to rest on them by day and [the] animal[s] of the field night.
11 Davide atawuzidwa zimene Rizipa mwana wamkazi wa Ayiwa, mzikazi wa Sauli anachita,
And it was told to David [that] which she had done Rizpah [the] daughter of Aiah [the] concubine of Saul.
12 anapita kukatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi (iwo anawatenga mwamseri kuchoka pabwalo la ku Beti-Sani, kumene Afilisti anawapachika atapha Sauli ku Gilibowa).
And he went David and he took [the] bones of Saul and [the] bones of Jonathan son his from with [the] citizens of Jabesh Gilead who they had stolen them from [the] open square of Beth Shan where (they had hung up them there [the] Philistines *Q(K)*) on [the] day struck down [the] Philistines Saul on Gilboa.
13 Davide anakatenga mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani kumeneko ndiponso mafupa otayidwa a amene anaphedwa nawasonkhanitsa pamodzi.
And he brought up from there [the] bones of Saul and [the] bones of Jonathan son his and they gathered [the] bones of the impaled [men].
14 Iwo anayika mafupa a Sauli ndi mwana wake Yonatani mʼmanda a Kisi abambo ake a Sauli ku Zera mʼdziko la Benjamini, ndipo anachita zonse zimene mfumu inalamula. Atachita zimenezi, Mulungu anayankha pemphero lopempherera dzikolo.
And they buried [the] bones of Saul and Jonathan son his in [the] land of Benjamin at Zela in [the] tomb of Kish father his and they did all that he commanded the king and he was entreated God for the land after thus.
15 Nthawi inanso panali nkhondo pakati pa Afilisti ndi Aisraeli, Davide anapita ndi ankhondo ake kukamenyana ndi Afilisti ndipo iye anatopa kwambiri.
And it belonged again war to the Philistines with Israel and he went down David and servants his with him and they fought with [the] Philistines and he was weary David.
16 Ndipo Isibi-Benobi, mmodzi mwa zidzukulu za Rafa, amene mkondo wake unkalemera makilogalamu atatu ndi theka ndipo analinso ndi lupanga latsopano, anati adzapha Davide.
(And Ishbi-*Q(K)*) Benob who - [was] among those born of the Raphah and [the] weight of spear his [was] three hundred [the] weight of bronze and he [was] girded a new [weapon] and he said to strike down David.
17 Koma Abisai mwana wa Zeruya anabwera kudzapulumutsa Davide. Iye anamukantha Mfilisitiyo ndi kumupha. Pamenepo asilikali a Davide analumbira kwa iye kuti, “Inu simudzapita nafenso ku nkhondo, kuti nyale ya Israeli isadzazimitsidwe.”
And he helped him Abishai [the] son of Zeruiah and he struck the Philistine and he killed him then they swore [the] men of David to him saying not you will go out again with us for battle and not you will extinguish [the] lamp of Israel.
18 Patapita nthawi, panali nkhondo ina ndi Afilisti ku Gobu. Pa nthawi imeneyo Sibekai Mhusati anapha Safu, mmodzi mwa zidzukulu za Arefai.
And it was after thus and it was again war at Gob with [the] Philistines then he struck down Sibbecai the Hushathite Saph who [was] among those born of the Raphah.
19 Pa nkhondo inanso ndi Afilisti ku Gobu, Elihanani mwana wa Yaare-Oregimu wa ku Betelehemu anapha Goliati Mgiti, amene anali ndi mkondo ngati ndodo yowombera nsalu.
And it was again war at Gob with [the] Philistines and he struck down Elhanan [the] son of Jaare-Oregim [the] Beth-lehemite Goliath the Gittite and [the] wood of spear his [was] like a beam of weavers.
20 Pa nkhondo inanso imene inachitika ku Gati panali munthu wina wamtali kwambiri wa zala zisanu ndi chimodzi mʼmanja ndi mʼmapazi ndipo zonse pamodzi zinalipo 24. Iyenso anali chidzukulu cha Rafa.
And it was again war at Gath and he was - a man of (stature *Q(K)*) and [the] fingers of hands his and [the] toes of feet his [were] six and six [was] twenty and four [the] number and also he he was born to the Raphah.
21 Pamene iye ankanyoza Aisraeli, Yonatani mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anamupha.
And he taunted Israel and he struck down him Jonathan [the] son of (Shimeah *Q(K)*) [the] brother of David.
22 Anthu anayi amenewa anali zidzukulu za Rafa ku Gati, ndipo onse anaphedwa ndi Davide ndi ankhondo ake.
Four these they were born to the Raphah in Gath and they fell by [the] hand of David and by [the] hand of servants his.

< 2 Samueli 21 >