< 2 Samueli 20 >
1 Ndipo munthu wina wokonda kuyambitsa chisokonezo, dzina lake Seba, mwana wa Bikiri wa fuko la Benjamini, anali komweko. Iye analiza lipenga ndipo anafuwula kuti, “Ife tilibe chathu mu mfumu wa Davide, tilibe gawo mwa mwana wa Yese! Inu Aisraeli aliyense apite ku nyumba kwake!”
Og der var tilfældigvis en Belials Mand, hvis Navn var Seba, Bikris Søn, en Mand af Benjamin, og han blæste i Trompeten og sagde: Vi have ingen Del i David, ej heller have vi Arv i Isais Søn; hver til sit Telt, o Israel!
2 Kotero Aisraeli onse anamuthawa Davide ndipo anatsatira Seba mwana wa Bikiri. Koma anthu a ku Yuda anakhala ndi mfumu yawo njira yonse kuchokera ku Yorodani mpaka ku Yerusalemu.
Da drog hver Mand i Israel op fra David efter Seba, Bikris Søn; men Judas Mænd fulgte med deres Konge fra Jordanen og indtil Jerusalem.
3 Davide atabwerera ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu, iye anatenga azikazi khumi aja amene anawasiya kuti aziyangʼanira nyumba yaufumu, ndipo anawayika mʼnyumba imene anayikapo mlonda. Iye ankawadyetsa koma sanagone nawonso. Anasungidwa kwa okha mpaka tsiku la kufa kwawo ndipo anakhala ngati akazi amasiye.
Og David kom til sit Hus til Jerusalem, og Kongen tog de ti Kvinder, de Medhustruer, som han lod blive til at bevare Huset, og satte dem hen i et Hus i Forvaring og forsørgede dem, og han gik ikke ind til dem; og de vare indelukkede indtil deres Dødsdag, levende i Enkestand.
4 Kenaka mfumu inati kwa Amasa, “Itanitsa ankhondo a Yuda kuti abwere kwa ine pasanathe masiku atatu, ndipo iwe udzakhale nawo.”
Og Kongen sagde til Amasa: Kald mig Mændene af Juda sammen til den tredje Dag, og vær saa her igen!
5 Motero Amasa anakayitana Ayuda, koma anachedwa, napitirira pa nthawi imene mfumu inamuyikira.
Og Amasa gik bort for at kalde Judas Mænd sammen; men han tøvede over den bestemte Tid, som var ham bestemt.
6 Davide anati kwa Abisai, “Tsono Seba mwana wa Bikiri adzatipweteka kuposa momwe Abisalomu anatichitira. Tenga asilikali a mbuye wako ndipo umuthamangitse, mwina adzapeza mizinda yotetezedwa ndi kutithawa ife.”
Da sagde David til Abisaj: Nu vil Seba, Bikris Søn, gøre os mere ondt end Absalom; tag du din Herres Tjener og forfølg ham, at han ikke rinder faste Stæder for sig og undkommer fra vore Øjne.
7 Kotero anthu a Yowabu, Akereti ndi Apeleti ndiponso asilikali onse amphamvu anapita motsogozedwa ndi Abisai. Iwo anayenda kuchokera ku Yerusalemu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Da droge Joabs Mænd ud efter ham, og de Krethi og de Plethi og alle de vældige, og de droge ud af Jerusalem til at forfølge Seba, Bikris Søn.
8 Ali pa mwala waukulu wa ku Gibiyoni, Amasa anabwera kudzakumana nawo. Yowabu anali atavala chovala chausilikali ndipo pamwamba pa malayawo, mʼchiwuno mwake anavala lamba womangirirapo lupanga lili moyikamo mwakemo. Akuyenda linasololoka kuchoka moyikamo mwake.
Der de vare ved den store Sten, som er ved Gibeon, da kom Amasa frem for dem; og Joab var iført sin Vaabenkjortel som sin Klædning, og derover havde han Bæltet med et Sværd, som hang ved hans Lænder i sin Balg, og der han gik frem, da faldt dette ud.
9 Yowabu anati kwa Amasa, “Kodi uli bwanji mʼbale wanga?” Kenaka Yowabu anamugwira ndevu Amasa uja ndi dzanja lake lamanja ndi kupsompsona.
Og Joab sagde til Amasa: Gaar det dig vel, min Broder? og Joab greb Amasa ved Skægget med den højre Haand for at kysse ham.
10 Amasa sanayangʼanitsitse lupanga limene linali mʼdzanja la Yowabu, ndipo Yowabu anamubaya nalo mʼmimba ndipo matumbo ake anatuluka ndi kugwera pansi. Popanda kubayanso kachiwiri, Amasa anafa. Ndipo Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anathamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Og Amasa tog sig ikke i Vare for Sværdet, som var i Joabs Haand, saa denne stak ham dermed i Underlivet og udøste hans Indvolde paa Jorden; og han stak ham ikke anden Gang, thi han var død; men Joab og hans Broder Abisaj forfulgte Seba, Bikris Søn.
11 Mmodzi mwa ankhondo a Yowabu anakayimirira pafupi ndi mtembo wa Amasa ndipo anati, “Aliyense amene amakonda Yowabu ndi aliyense amene ali wa Davide, atsatire Yowabu!”
Og der blev en Mand af Joabs unge Karle staaende hos ham og sagde: Hvo er der, som har Lyst til Joab, og hvo er der, som er for David, han følge efter Joab!
12 Amasa anagona pakati pa msewu atasamba magazi ake, ndipo munthuyo anaona kuti asilikali onse amayima pamenepo. Atazindikira kuti aliyense amene ankafika pamene panali Amasa amayima, iye anamuchotsa mu msewu ndi kumukokera mʼmunda ndipo anamuphimba ndi nsalu.
Og Amasa laa væltet i Blodet midt paa Landevejen; der Manden saa, at alt Folket blev staaende, da bragte han Amasa fra Landevejen over paa Ageren og kastede Klæder over ham, efterdi han saa, at hvo som kom til ham, blev staaende.
13 Amasa atachotsedwa pa msewu anthu onse anapita ndi Yowabu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Der han var bragt bort fra Landevejen, da gik hver Mand frem efter Joab til at forfølge Seba, Bikris Søn.
14 Seba anadutsa mafuko onse a Israeli mpaka ku Abeli ndi Beti-Maaka ndiponso chigawo chonse cha Abeli, amene anasonkhana pamodzi ndi kumutsata iye.
Og han drog igennem alle Israels Stammer indtil Abel, nemlig Beth-Maaka og hele Berim; og de samledes og kom ogsaa efter ham.
15 Ankhondo onse pamodzi ndi Yowabu anafika ndi kumuzungulira Seba mu Abeli-Beti-Maaka. Iwo anapanga mzere wa nkhondo mpaka ku mzinda, ndipo unayangʼanana ndi malo otetezera a kunja. Pamene amalimbana ndi khoma kuti aligwetse,
Og de kom og indesluttede ham i Abel-Beth-Maaka og kastede en Vold op imod Staden, og den stod op til Muren; og alt Folket, som var med Joab, søgte at ødelægge og at nedrive Muren.
16 mayi wina wanzeru anafuwula kuchokera mu mzindawo, “Tamverani! Tamverani! Muwuzeni Yowabu abwere pano kuti ndiyankhule naye.”
Da raabte en forstandig Kvinde af Staden: Hører, hører! siger dog til Joab: Kom nær herhid, og jeg vil tale til dig.
17 Yowabu anayandikira kumene kunali mayiyo, ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndinu Yowabu?” Iye anayankha kuti, “Ndine.” Mayiyo anati, “Tamverani zimene mtumiki wanu akuti anene.” Yowabu anayankha kuti, “Ndikumvetsera.”
Og der han kom nær til hende, da sagde Kvinden: Er du Joab? og han sagde: Ja; og hun sagde til ham: Hør din Tjenerindes Tale; og han sagde: Jeg hører.
18 Iye anapitiriza kunena kuti, “Kalekale ankanena kuti, ‘Kapeze yankho lako ku Abeli,’ ndipo nkhani imathera pamenepo.
Og hun sagde: Fordum plejede man saaledes at tale, sigende: Man skal spørge sig for i Abel, og saaledes fuldbyrdede man det.
19 Ife ndife anthu a mtendere ndi okhulupirika mu Israeli. Inu mukufuna kuwononga mzinda umene ndi mayi mu Israeli. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kufafaniza cholowa cha Yehova?”
Jeg er en af de fredsommelige, de trofaste i Israel; du søger efter at dræbe en Stad og en Moder i Israel, hvorfor vil du opsluge Herrens Arv?
20 Yowabu anayankha kuti, “Ayi ndisatero. Ine sindikufuna kuwufafaniza kapena kuwuwononga.
Og Joab svarede og sagde: Det være langt fra, det være langt fra mig, at jeg skulde opsluge, at jeg skulde ødelægge!
21 Nkhani simeneyo ayi. Koma munthu wina wa ku dziko lamapiri la Efereimu, dzina lake Seba mwana wa Bikiri, wawukira mfumu Davide. Muperekeni munthuyo ndipo ine ndidzachoka pa mzinda uno.” Mayiyo anati kwa Yowabu, “Mutu wake tikuponyerani pa khoma pano.”
Sagen forholder sig ikke saaledes; men en Mand af Efraims Bjerg, hvis Navn er Seba, Bikris Søn, har opløftet sin Haand imod Kongen, imod David, giver mig ham alene, saa vil jeg drage fra Staden; og Kvinden sagde til Joab: Se, hans Hoved skal kastes til dig over Muren.
22 Ndipo mayiyo anapita kwa anthu onse ndi malangizo ake anzeru, ndipo anadula mutu wa Seba mwana wa Bikiri ndipo anawuponya kwa Yowabu. Kotero iye analiza lipenga ndipo anthu ake anachoka pa mzindawo, aliyense nʼkubwerera kwawo. Ndipo Yowabu anabwerera kwa mfumu ku Yerusalemu.
Og Kvinden kom til alt Folket med sin Visdom, og de afhuggede Sebas, Bikris Søns, Hoved, og kastede det ud til Joab; da blæste han i Trompeten, og de adspredtes fra Staden, hver til sine Telte; og Joab kom tilbage til Jerusalem, til Kongen.
23 Yowabu ndiye amalamulira gulu lonse la ankhondo. Benaya mwana wa Yehoyada amalamulira Akereti ndi Apeleti.
Og Joab var over al Israels Hær, og Benaja, Jojadas Søn, var over Krethi og over Plethi;
24 Adoramu amayangʼanira anthu ogwira ntchito ya thangata, Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika,
og Adoram var Rentemester, og Josafat, Ahiluds Søn, var Historieskriver;
25 Seva anali mlembi wa mfumu. Zadoki ndi Abiatara anali ansembe
og Seja var Skriver, og Zadok og Abjathar vare Præster;
26 ndipo Ira wa ku Yairi anali wansembe wa Davide.
dertilmed var Jairiteren, Ira, ypperste Raad for David.