< 2 Samueli 2 >

1 Patapita nthawi, Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite ku umodzi mwa mizinda ya Yuda?” Yehova anayankha kuti, “Pita.” Davide anafunsanso kuti, “Kodi ndipite kuti?” Yehova anayankha kuti, “Ku Hebroni.”
Sabara gah ılğevç'uyle qiyğa, Davudee Rəbbike qiyghanan: – Zı Yahudayne nenemecar şahareeqa hak'nene? Rəbbee eyhen: – Hak'ne. Davudee qiyghanan: – Nyaqane hak'ne? Rəbbee eyhen: – Xevroneeqa.
2 Choncho Davide anapita kumeneko ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wamasiye uja wa Nabala wa ku Karimeli.
Davudur maqa cune q'öyursana xhunaşşeyka hayk'anna: İzre'elyğançena Axinoamır, Karmelyğançena Navalna sip'ıriy Avigailer.
3 Davide anatenganso anthu amene anali nawo aliyense ndi banja lake, ndipo anakakhala ku midzi ya ku Hebroni.
Davudee cukan insanarıb cone xizanbışika Xevronqa qabı, mançine hiqiy-allane şaharbışee manbışis aaxvasın cigabı hele.
4 Kenaka amuna a ku Yuda anabwera ku Hebroni ndipo kumeneko anadzoza Davide kukhala mfumu ya fuko la Yuda. Davide atawuzidwa kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi ndi amene anayika mʼmanda Sauli,
Yahudayeençen insanar abı, Davudulqa q'ış qadğu, maa'ar mang'uke Yahudayne nasılına paççah ha'a. Maa'ad Davuduk'le uvhumee, Şaul Gileadeene Yaveşne milletın k'eyxhıva,
5 iye anatuma amithenga kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti akayankhule nawo kuti, “Yehova akudalitseni poonetsa kukoma mtima kwanu kwa Sauli mbuye wanu pomuyika mʼmanda.
Davudee maqa cun insanar g'uxoole. Mang'vee cune insanaaşik'le eyhen: – Maane milletılqa in yizın cuvab hixhar he'e: «Rəbbee şos xayir-düə hevlecen, vuşda xərna eyxhene Şaulus, şu yugvalla hav'u, mana k'eyxhıva.
6 Tsopano Yehova akuonetseni kukoma mtima ndi kukhulupirika kwake ndipo inenso ndidzakukomerani mtima chifukwa munachita zimenezi.
Hasre mane vuşde işil-alla Rəbbee Cuna badal dyooxhena yugvalla şos haagvecen. Zınad mane vuşde işil-alla şos yugun ha'as.
7 Tsopano khalani amphamvu ndi olimba mtima, pakuti Sauli mbuye wanu wafa, ndipo fuko la Yuda landidzoza kukhala mfumu yawo.”
Vuşda xərna eyxhena Şaul qik'uva şu həşde xıleppı avqa qıma'a, it'umba ulyoozre. Yahudayne nasılen, cosda paççah zake hı'ı».
8 Pa nthawi imeneyi Abineri mwana wa Neri, wolamulira ankhondo a Sauli, anatenga Isi-Boseti mwana wa Sauli ndi kubwera naye ku Mahanaimu.
Şaulne g'oşunbışde q'oma ulyorzuling'vee Nerne duxee Avneree, Şaulna dix İşboşet cukasana Maxanayimeeqa qıkkı ıxha.
9 Iye anamuyika kuti akhale mfumu yoyangʼanira Giliyadi, Asuri ndi Yezireeli, pamodzi ndi Efereimu, Benjamini ndi Israeli yense.
Maa'ar Avneree mana Gileadne, Aşuriyne, İzre'elyne, Efrayimne, Benyaminne cigabışee vooxhene insanaaşde – gırgıne İzrailyna paççah ha'a.
10 Isi-Boseti mwana wa Sauli anali wa zaka makumi anayi pamene anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira zaka ziwiri. Koma fuko la Yuda linatsatira Davide.
Şaulne duxayqa, İşboşetıqa, İzrailyna paççah ıxhayng'a yoq'ts'al senniy vod. Mang'una paççahiyvalla q'ölle senna ts'ıts'avxha. Yahudayne nasılınmee, Davudun sura aqqı ıxha.
11 Davide anakhala mfumu ku Hebroni akulamulira fuko la Yuda, kwa zaka zisanu ndi chimodzi ndi miyezi isanu ndi umodzi.
Davudee Xevronee, Yahudayne nasıles paççahiyvalla yighılle sennayiy yixhıble vazna hav'u.
12 Abineri mwana wa Neri, pamodzi ndi ankhondo a Isi-Boseti mwana wa Sauli, anachoka ku Mahanaimu ndi kupita ku Gibiyoni.
Yiğbışde sa yiğıl Nerna dix Avner, Şaulne duxayne İşboşetne insanaaşika Maxanayimğançe Giveoneeqa hayk'an.
13 Yowabu mwana wa Zeruya pamodzi ndi ankhondo a Davide anapita ndi kukakumana nawo ku dziwe la ku Gibiyoni. Gulu lina linakhala mbali ina ya dziwelo pamene gulu lina linakhala mbali inayo.
Tseruya donane zəiyfayna dix Yoavmee, Davudne insanaaşika Giveonusneene xhyan sadıyne cigaysqa, manbışde ögilqa qığeç'e. Yoav cune insanaaşika xhyan sadıyne cigayne sa aq'val, Avnerır cune insanaaşika – manisa aq'val giy'ar.
14 Kenaka Abineri anati kwa Yowabu, “Tiye tibweretse ena mwa anyamata athu kuti amenyane patsogolo pathupa.” Yowabu anayankha, “Chabwino, amenyane.”
Avneree Yoavık'le eyhen: – Havaasre mek'vunbı suğootsu, yişde ögil saç'ivkvecen. Yoaveeyid eyhen: – Havaasre saç'ivkvecen.
15 Kotero anayimirira ndipo anawawerenga: anyamata khumi ndi awiri a fuko la Benjamini ndi Isi-Boseti mwana wa Sauli ndiponso anyamata khumi ndi awiri a Davide.
Şaulne duxayne İşboşetne sural sıç'ookvan Benyaminaaşin mek'vunbı qəpqı'mee, yits'ıq'vayre insan eyxhe. Davudne suraler yits'ıq'vayre eyxhe.
16 Tsono aliyense anagwira mutu wa mnzake namubaya mnzakeyo mʼnthiti ndi mpeni ndipo onse anagwera pansi limodzi. Kotero malo amenewo ku Gibiyoni amatchedwa Helikati Hazurimu.
Manbışe sana-sananbı vuk'ulbışike avqu, g'ılıncbı hiyxə. Manbışin gırgınbı habat'anbı. Mançil-allad Giveoneene mane cigayk'le Xelqat-Hatsurimva (G'ılıncbışin çol) eyhe.
17 Tsiku limeneli nkhondo yake inali yoopsa kwambiri, ndipo Abineri ndi ankhondo a Israeli anagonjetsedwa ndi ankhondo a Davide.
Mane yiğıl ma'ad geed it'umın saç'ikkvuy ıxha. Avneriy İzrailybı, Davudne insanaaşis maa'ab avub avxu.
18 Ana atatu aamuna a Zeruya, Yowabu, Abisai ndi Asaheli anali komweko. Koma Asaheli anali waliwiro ngati insa.
Tseruya donane zəiyfayna xhebırsana dix: Yoav, Avişay, Asahelib maa'ab vooxhe. Asahel, çolana ceyran xhinne, g'elike ek'ra ıxha.
19 Iye anathamangitsa Abineri ndipo sanakhotere kumanja kapena kumanzere pamene amamutsatira.
Mana neng'uqacar ilydyakkı, Avnerıqa qihna girxhu. Mang'uqar qihna g'adayhvanmee,
20 Abineri anayangʼana mʼmbuyo ndipo anafunsa, “Kodi ndiwe Asaheli?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
Avner yı'q'əlqa ilyakkı, eyhen: – Asahel, ğune vor? Mang'vee eyhen: – Ho'o, zı vorna.
21 Ndipo Abineri anati kwa iye, “Khotera kumanja kapena kumanzere: tsatira mmodzi mwa anyamatawa ndipo umulande zida zake.” Koma Asaheli sanasiye kumuthamangitsa.
Avneree mang'uk'le eyhen: – Yiğne sağıqa, soluqa sa ilekke. Mane mek'vunbışda sa aqqı, manbışin silahbı g'ayşe. Asaheleemee Avnerıke xıl ts'ıts'a'a vuxha deş.
22 Abineri anamuchenjezanso Asaheli, “Siya kuthamangitsa ine! Kodi ndikukanthe chifukwa chiyani? Kodi ndikaonana naye bwanji mʼbale wako Yowabu?”
Avneree, Asahelik'le meed eyhen: – Zaqar qihna gimexha, zake xıl ts'ıts'ee'e! Nişil-allane zı ğu gik'as? Qiyğa zı yiğne çoçune Yoavne aq'veeqa nəxürna ilyakkas?
23 Koma iye anakana kuleka kumuthamangitsa. Choncho Abineri anabaya Asaheli mʼmimba ndi msonga ya mkondo wake ndipo mkondowo unatulukira mbali ina. Iye anagwa ndi kufera pamalo pomwepo. Ndipo munthu aliyense amayima akafika pamalo pamene anagwera ndi kufa.
Asahelee meeb mang'uke xıl ts'ıts'aa'a deş. Manke Avneree cun nize alyat'u, cık'rıhiyna mang'une vuxhnele k'ena məxüd ı'xiyxə, cık'rı mang'une yı'q'ək ciga hı'ı qığeç'e. Asahel qukkyorkul cigeecar qek'ana. Mançile qiyğa Asahel qik'uyne cigaysse ı'lğən gırgınbı, maa'ab ulydyobzur ılğeebaç'e vuxha deş.
24 Koma Yowabu ndi Abisai anathamangitsa Abineri, ndipo dzuwa likulowa, anafika ku phiri la Ama, pafupi ndi Giya pa njira yopita ku chipululu cha ku Gibiyoni.
Yoaviy Avişay Avnerıqa qihna g'adaaxhvan. Verığ k'yooçemee, manbı qabı hiviyxharanbı Giveonne sahrayne yəqqı'lyne Giahne ögilyne Ammava eyhene tepalqa.
25 Pamenepo anthu a fuko la Benjamini anasonkhana kudzathandiza Abineri. Iwo anapanga gulu ndipo anayima pamwamba pa phiri.
Benyaminaaşinbı Avnerne hiqiy-alla savayle. Qiyğab apk'ın, sa tepayne q'omaqa ılqeepç'ı, maayib ulyoozaranbı.
26 Abineri anayitana Yowabu, “Kodi tipitirize kumenyana mpaka kalekale? Kodi sukuzindikira kuti mathero ake kudzakhala kuwawidwa mitima? Kodi udzawaletsa liti ankhondo ako kuthamangitsa abale awo?”
Avneree ts'irıka Yoavık'le eyhen: – Şi mısılqameene g'ılıncıke hapt'as? Nya'a, vak'le ats'a dişdiy, nekke qiyğa yugdacad ixhes deş? Ğu yiğne insanaaşik'le mısane eyhes, cone çocaaşiqab qihna gimabak'va?
27 Yowabu anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, ukanapanda kuyankhula, ankhondo anga akanapitiriza kuthamangitsa abale awo mpaka mmawa.”
Yoavee eyhen: – Vorne Allahılqa k'ın ixhen, ğu manva ittevhuynxhiy, yizın insanar cone çocaaşiqa qihna miç'eebilqamee gyapk'asınbıniy.
28 Chomwecho Yowabu analiza lipenga, ndipo ankhondo onse anayima. Iwo analeka kuthamangitsa Aisraeli kapena kumenyana nawo.
Qiyğa Yoavee şeypur əlüvxümee, manbışin gırgınbı ulyoozaranbı. İzrailybışiqa qihna gyapk'iy ç'əvə'an, manbışika sayib sıç'ookka deş.
29 Usiku wonsewo Abineri ndi ankhondo ake anayenda kudutsa Araba. Iwo anawoloka Yorodani, napitirira mpaka kudutsa dera lonse la Bitironi ndipo anafika ku Mahanaimu.
Avneriy cun insanar xəmvolle Arava eyhene q'adaalile k'ena avayk'an. Manbı İordanne damayle ılğeepç'ı, Bitronule k'ena qabı, Maxanayimeeqa hiviyxhar.
30 Choncho Yowabu anabwerera kuchokera kothamangitsa Abineri ndipo anasonkhanitsa ankhondo ake onse. Kupatula Asaheli, panali ankhondo khumi ndi anayi a Davide amene anasowa.
Yoavee, Avnerıqa qihna girxhuy ç'əv hı'ı sark'ılymee, cuna g'oşun sa'a. Asahelıle ğayrı Davudne insanaaşike yits'ıyüç'ər insan hiyxhar deşiy.
31 Koma ankhondo a Davide anapha ankhondo a fuko la Benjamini 360 amene anali ndi Abineri.
Davudne insanaaşemee, Benyaminaaşina, Avnerne insanaaşina, xhebıd vəşşe yixhts'al insan gek'a.
32 Iwo anatenga Asaheli ndi kukamuyika mʼmanda a abambo ake ku Betelehemu. Ndipo Yowabu ndi ankhondo ake anayenda usiku wonse ndi kufika ku Hebroni kukucha.
Asahel Bet-Lexemqa qıkkı, cune dekkına nyaq'vanane mağaree k'eyxha. Yoaveeyiy cune insanaaşe xəmvolle yəq avayk'an, miç'eebiys manbı qabı Xevronqa hiviyxhar.

< 2 Samueli 2 >