< 2 Samueli 2 >

1 Patapita nthawi, Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite ku umodzi mwa mizinda ya Yuda?” Yehova anayankha kuti, “Pita.” Davide anafunsanso kuti, “Kodi ndipite kuti?” Yehova anayankha kuti, “Ku Hebroni.”
Et après ces événements, David interrogea l'Éternel en ces termes: Dois-je gagner l'une des villes de Juda? Et l'Éternel lui dit:
2 Choncho Davide anapita kumeneko ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wamasiye uja wa Nabala wa ku Karimeli.
Oui. Et David dit: Laquelle? Et Il répondit: Hébron. Et David s'y transporta avec ses deux femmes, Ahinoam de Jizréel, et Abigaïl, femme de Nabal, le Carmélite.
3 Davide anatenganso anthu amene anali nawo aliyense ndi banja lake, ndipo anakakhala ku midzi ya ku Hebroni.
Il y emmena de même avec lui les hommes qui l'accompagnaient, chacun d'eux avec sa maison, et ils demeurèrent dans les villes attenantes à Hébron.
4 Kenaka amuna a ku Yuda anabwera ku Hebroni ndipo kumeneko anadzoza Davide kukhala mfumu ya fuko la Yuda. Davide atawuzidwa kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi ndi amene anayika mʼmanda Sauli,
Alors arrivèrent des hommes de Juda, et là ils oignirent David comme roi de la maison de Juda.
5 iye anatuma amithenga kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti akayankhule nawo kuti, “Yehova akudalitseni poonetsa kukoma mtima kwanu kwa Sauli mbuye wanu pomuyika mʼmanda.
Et l'on apporta cet avis à David: Ce sont les hommes de Jabès en Galaad, qui ont donné la sépulture à Saül. Aussitôt David dépêcha des envoyés aux hommes de Jabès en Galaad avec ce message: Soyez les bénis de l'Éternel pour votre acte de piété envers votre Seigneur, envers Saül à qui vous avez donné la sépulture.
6 Tsopano Yehova akuonetseni kukoma mtima ndi kukhulupirika kwake ndipo inenso ndidzakukomerani mtima chifukwa munachita zimenezi.
Qu'en retour l'Éternel vous témoigne Son amour et Sa fidélité! de mon côté je vous donne ce témoignage de bonté, en suite de ce que vous avez fait.
7 Tsopano khalani amphamvu ndi olimba mtima, pakuti Sauli mbuye wanu wafa, ndipo fuko la Yuda landidzoza kukhala mfumu yawo.”
Maintenant ayez toujours la main ferme, et soyez des braves! car si votre Seigneur Saül est mort, moi, j'ai été oint par la maison de Juda pour être son Roi.
8 Pa nthawi imeneyi Abineri mwana wa Neri, wolamulira ankhondo a Sauli, anatenga Isi-Boseti mwana wa Sauli ndi kubwera naye ku Mahanaimu.
Cependant Abner, fils de Ner, général d'armée de Saül, prit Isboseth, fils de Saül, et le fit passer à Mahanaïm
9 Iye anamuyika kuti akhale mfumu yoyangʼanira Giliyadi, Asuri ndi Yezireeli, pamodzi ndi Efereimu, Benjamini ndi Israeli yense.
et l'établit roi de Galaad, et des Assurites et de Jizréel, et d'Ephraïm et de Benjamin, ainsi de tout Israël.
10 Isi-Boseti mwana wa Sauli anali wa zaka makumi anayi pamene anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira zaka ziwiri. Koma fuko la Yuda linatsatira Davide.
Isboseth, fils de Saül, avait quarante ans, lorsqu'il devint roi d'Israël, et il régna deux ans; la maison de Juda seule s'attachait à David.
11 Davide anakhala mfumu ku Hebroni akulamulira fuko la Yuda, kwa zaka zisanu ndi chimodzi ndi miyezi isanu ndi umodzi.
Et la durée du temps que David passa à Hébron, comme roi de la maison de Juda, fut de sept ans et six mois.
12 Abineri mwana wa Neri, pamodzi ndi ankhondo a Isi-Boseti mwana wa Sauli, anachoka ku Mahanaimu ndi kupita ku Gibiyoni.
Et Abner, fils de Ner, avec les serviteurs d'Isboseth, fils de Saül, sortit de Mahanaïm pour marcher sur Gabaon.
13 Yowabu mwana wa Zeruya pamodzi ndi ankhondo a Davide anapita ndi kukakumana nawo ku dziwe la ku Gibiyoni. Gulu lina linakhala mbali ina ya dziwelo pamene gulu lina linakhala mbali inayo.
Et Joab, fils de Tseruïa, et les serviteurs de David se mirent en campagne, et ils se rencontrèrent de part et d'autre à l'étang de Gabaon, et ils prirent position ceux-ci d'un côté de l'étang, ceux-là de l'autre.
14 Kenaka Abineri anati kwa Yowabu, “Tiye tibweretse ena mwa anyamata athu kuti amenyane patsogolo pathupa.” Yowabu anayankha, “Chabwino, amenyane.”
Alors Abner dit à Joab: Prenons pour champions des jeunes gens soldats, et qu'ils s'escarmouchent devant nous! Et Joab dit: Prenons ces champions.
15 Kotero anayimirira ndipo anawawerenga: anyamata khumi ndi awiri a fuko la Benjamini ndi Isi-Boseti mwana wa Sauli ndiponso anyamata khumi ndi awiri a Davide.
Et ils se mirent sur pied et ils s'avancèrent au nombre de douze pour Benjamin et Isboseth, fils de Saül, et douze des serviteurs de David.
16 Tsono aliyense anagwira mutu wa mnzake namubaya mnzakeyo mʼnthiti ndi mpeni ndipo onse anagwera pansi limodzi. Kotero malo amenewo ku Gibiyoni amatchedwa Helikati Hazurimu.
Et chacun d'eux saisit la tête de son adversaire, et chacun d'eux enfonça son épée dans le flanc de son adversaire, et ils tombèrent tous à la fois. Et l'on donna à cet emplacement le nom de Helkath-Hatsourim (champ des lames): il est près de Gabaon.
17 Tsiku limeneli nkhondo yake inali yoopsa kwambiri, ndipo Abineri ndi ankhondo a Israeli anagonjetsedwa ndi ankhondo a Davide.
En cette journée le combat fut très rude et Abner et les hommes d'Israël furent défaits par les serviteurs de David.
18 Ana atatu aamuna a Zeruya, Yowabu, Abisai ndi Asaheli anali komweko. Koma Asaheli anali waliwiro ngati insa.
Et il y avait là trois fils de Tseruïa: Joab et Abisaï et Hasahel. Et Hasahel avait dans ses pieds l'agilité d'une gazelle qui court dans les champs.
19 Iye anathamangitsa Abineri ndipo sanakhotere kumanja kapena kumanzere pamene amamutsatira.
Et Hasahel poursuivait Abner sans s'écarter ni à droite ni à gauche des traces d'Abner.
20 Abineri anayangʼana mʼmbuyo ndipo anafunsa, “Kodi ndiwe Asaheli?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
Et Abner se tournant en arrière dit: Est-ce toi qui es Hasahel? Et il répondit: C'est moi-même.
21 Ndipo Abineri anati kwa iye, “Khotera kumanja kapena kumanzere: tsatira mmodzi mwa anyamatawa ndipo umulande zida zake.” Koma Asaheli sanasiye kumuthamangitsa.
Et Abner lui dit: Tire-toi de côté à ta droite ou à ta gauche, et attaque-toi à l'un de ces jeunes hommes, et t'empare de son armure. Mais Hasahel ne voulut pas se désister de sa poursuite.
22 Abineri anamuchenjezanso Asaheli, “Siya kuthamangitsa ine! Kodi ndikukanthe chifukwa chiyani? Kodi ndikaonana naye bwanji mʼbale wako Yowabu?”
Et Abner répéta à Hasahel: Renonce à me poursuivre! pourquoi devrais-je t'étendre sur le carreau? Comment alors pourrais-je me présenter à ton frère Joab?
23 Koma iye anakana kuleka kumuthamangitsa. Choncho Abineri anabaya Asaheli mʼmimba ndi msonga ya mkondo wake ndipo mkondowo unatulukira mbali ina. Iye anagwa ndi kufera pamalo pomwepo. Ndipo munthu aliyense amayima akafika pamalo pamene anagwera ndi kufa.
Mais il refusa de céder. Alors Abner lui porta au ventre un coup du talon de sa lance qui ressortit par derrière, et Hasahel tomba et mourut sur la place. Et tous ceux qui arrivaient à l'endroit où Hasahel était tombé et mort, s'arrêtaient.
24 Koma Yowabu ndi Abisai anathamangitsa Abineri, ndipo dzuwa likulowa, anafika ku phiri la Ama, pafupi ndi Giya pa njira yopita ku chipululu cha ku Gibiyoni.
Et Joab et Abisaï poursuivirent Abner, et au coucher du soleil ils atteignirent le monticule d'Amma, situé devant Giah sur la route du désert de Gabaon.
25 Pamenepo anthu a fuko la Benjamini anasonkhana kudzathandiza Abineri. Iwo anapanga gulu ndipo anayima pamwamba pa phiri.
Et les Benjaminites vinrent se grouper à la suite d'Abner et se formèrent en légion et prirent position au sommet d'un coteau.
26 Abineri anayitana Yowabu, “Kodi tipitirize kumenyana mpaka kalekale? Kodi sukuzindikira kuti mathero ake kudzakhala kuwawidwa mitima? Kodi udzawaletsa liti ankhondo ako kuthamangitsa abale awo?”
Alors Abner s'adressant à Joab lui dit: L'épée sera-t-elle donc toujours dévorante? Ne sais-tu pas qu'il ne résultera que misère? Combien de temps encore veux-tu ne pas dire au peuple de renoncer à poursuivre des frères?
27 Yowabu anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, ukanapanda kuyankhula, ankhondo anga akanapitiriza kuthamangitsa abale awo mpaka mmawa.”
Et Joab dit: Par la vie de Dieu! si tu n'avais pas parlé, c'est demain seulement que le peuple aurait été ramené de la poursuite de ses frères.
28 Chomwecho Yowabu analiza lipenga, ndipo ankhondo onse anayima. Iwo analeka kuthamangitsa Aisraeli kapena kumenyana nawo.
Puis Joab sonna de la trompette, et tout le peuple fit halte, et cessa de harceler Israël et ne continua pas la guerre.
29 Usiku wonsewo Abineri ndi ankhondo ake anayenda kudutsa Araba. Iwo anawoloka Yorodani, napitirira mpaka kudutsa dera lonse la Bitironi ndipo anafika ku Mahanaimu.
Cependant Abner et ses hommes employèrent toute cette même nuit à traverser la plaine, et ils passèrent le Jourdain et traversèrent tout le Bithron et gagnèrent Mahanaïm.
30 Choncho Yowabu anabwerera kuchokera kothamangitsa Abineri ndipo anasonkhanitsa ankhondo ake onse. Kupatula Asaheli, panali ankhondo khumi ndi anayi a Davide amene anasowa.
Et Joab renonçant à la poursuite d'Abner, rassembla tout le peuple; et des serviteurs de David il manquait dix-neuf hommes et Hasahel.
31 Koma ankhondo a Davide anapha ankhondo a fuko la Benjamini 360 amene anali ndi Abineri.
D'un autre côté les serviteurs de David avaient frappé dans Benjamin et la troupe d'Abner, trois cent soixante hommes, à mort.
32 Iwo anatenga Asaheli ndi kukamuyika mʼmanda a abambo ake ku Betelehemu. Ndipo Yowabu ndi ankhondo ake anayenda usiku wonse ndi kufika ku Hebroni kukucha.
Et ils emportèrent Hasahel et lui donnèrent la sépulture dans le tombeau de son père à Bethléhem. Et Joab et ses hommes marchèrent toute la nuit et avec le jour ils arrivaient à Hébron.

< 2 Samueli 2 >