< 2 Samueli 2 >

1 Patapita nthawi, Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite ku umodzi mwa mizinda ya Yuda?” Yehova anayankha kuti, “Pita.” Davide anafunsanso kuti, “Kodi ndipite kuti?” Yehova anayankha kuti, “Ku Hebroni.”
And it came to pass after this, that David asked counsel of the Lord, saying, Shall I go up into one of the cities of Judah? And the Lord said unto him, Go up. And David said, Whither shall I go up? And he said, Unto Hebron.
2 Choncho Davide anapita kumeneko ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wamasiye uja wa Nabala wa ku Karimeli.
So David went up thither, and his two wives also, Achino'am the Yizre'elitess, and Abigayil, Nabal's wife, the Carmelite.
3 Davide anatenganso anthu amene anali nawo aliyense ndi banja lake, ndipo anakakhala ku midzi ya ku Hebroni.
And his men that were with him did David bring up, every man with his household; and they dwelt in the cities of Hebron.
4 Kenaka amuna a ku Yuda anabwera ku Hebroni ndipo kumeneko anadzoza Davide kukhala mfumu ya fuko la Yuda. Davide atawuzidwa kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi ndi amene anayika mʼmanda Sauli,
And then came the men of Judah, and they anointed there David as king over the house of Judah. And they told David, saying, The men of Yabesh-gil'ad were those that buried Saul.
5 iye anatuma amithenga kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti akayankhule nawo kuti, “Yehova akudalitseni poonetsa kukoma mtima kwanu kwa Sauli mbuye wanu pomuyika mʼmanda.
And David thereupon sent messengers unto the men of Yabesh-gil'ad, and said unto them, Blessed be ye of the Lord, that ye have done this kindness unto your Lord, unto Saul, and have buried him.
6 Tsopano Yehova akuonetseni kukoma mtima ndi kukhulupirika kwake ndipo inenso ndidzakukomerani mtima chifukwa munachita zimenezi.
And now may the Lord deal with you in kindness and truth: and as for me also, I will requite you this good deed, because ye have done this thing.
7 Tsopano khalani amphamvu ndi olimba mtima, pakuti Sauli mbuye wanu wafa, ndipo fuko la Yuda landidzoza kukhala mfumu yawo.”
And now let your hands be strengthened, and be ye valiant men; for your lord Saul is dead; and also me have the house of Judah anointed as king over them.
8 Pa nthawi imeneyi Abineri mwana wa Neri, wolamulira ankhondo a Sauli, anatenga Isi-Boseti mwana wa Sauli ndi kubwera naye ku Mahanaimu.
But Abner, the son of Ner, the captain of the army of Saul, took Ish-bosheth the son of Saul, and brought him over to Machanayim;
9 Iye anamuyika kuti akhale mfumu yoyangʼanira Giliyadi, Asuri ndi Yezireeli, pamodzi ndi Efereimu, Benjamini ndi Israeli yense.
And made him king over Gil'ad, and over the Ashurites, and over Yizre'el, and over Ephraim, and over Benjamin, and over all Israel.
10 Isi-Boseti mwana wa Sauli anali wa zaka makumi anayi pamene anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira zaka ziwiri. Koma fuko la Yuda linatsatira Davide.
Forty years old was Ish-bosheth the son of Saul, when he became king over Israel, and two years he reigned. But the house of Judah followed David.
11 Davide anakhala mfumu ku Hebroni akulamulira fuko la Yuda, kwa zaka zisanu ndi chimodzi ndi miyezi isanu ndi umodzi.
And the number of days that David was king in Hebron over the house of Judah was seven years and six months.
12 Abineri mwana wa Neri, pamodzi ndi ankhondo a Isi-Boseti mwana wa Sauli, anachoka ku Mahanaimu ndi kupita ku Gibiyoni.
And there went out Abner the son of Ner, and the servants of Ish-bosheth the son of Saul, from Machanayim to Gib'on.
13 Yowabu mwana wa Zeruya pamodzi ndi ankhondo a Davide anapita ndi kukakumana nawo ku dziwe la ku Gibiyoni. Gulu lina linakhala mbali ina ya dziwelo pamene gulu lina linakhala mbali inayo.
And Joab the son of Zeruyah and the servants of David also went out, and they met together by the pool of Gib'on: and they sat down, these on the one side of the pool, and the others on the other side of the pool.
14 Kenaka Abineri anati kwa Yowabu, “Tiye tibweretse ena mwa anyamata athu kuti amenyane patsogolo pathupa.” Yowabu anayankha, “Chabwino, amenyane.”
And Abner said to Joab, Do let the young men rise up and play before us. And Joab said, They may rise up.
15 Kotero anayimirira ndipo anawawerenga: anyamata khumi ndi awiri a fuko la Benjamini ndi Isi-Boseti mwana wa Sauli ndiponso anyamata khumi ndi awiri a Davide.
Then they rose up and went over by number: twelve for Benjamin, and for Ish-bosheth the son of Saul, and twelve of the servants of David.
16 Tsono aliyense anagwira mutu wa mnzake namubaya mnzakeyo mʼnthiti ndi mpeni ndipo onse anagwera pansi limodzi. Kotero malo amenewo ku Gibiyoni amatchedwa Helikati Hazurimu.
And they grasped every one his fellow by the head, and thrust his sword in his fellow's side; and they fell down together: wherefore that place was called Chelkath-hazzurim, which is by Gib'on.
17 Tsiku limeneli nkhondo yake inali yoopsa kwambiri, ndipo Abineri ndi ankhondo a Israeli anagonjetsedwa ndi ankhondo a Davide.
And the battle was exceedingly fierce on that day; and Abner with the men of Israel was beaten, before the servants of David.
18 Ana atatu aamuna a Zeruya, Yowabu, Abisai ndi Asaheli anali komweko. Koma Asaheli anali waliwiro ngati insa.
And there were at that place three sons of Zeruyah, Joab, and Abishai, and 'Asahel: and 'Asahel was as fleet of foot as any roe in the field.
19 Iye anathamangitsa Abineri ndipo sanakhotere kumanja kapena kumanzere pamene amamutsatira.
And 'Asahel pursued after Abner; and he turned not in going to the right hand or to the left from following Abner.
20 Abineri anayangʼana mʼmbuyo ndipo anafunsa, “Kodi ndiwe Asaheli?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
And Abner turned round and said, Art thou 'Asahel? And he answered, I am.
21 Ndipo Abineri anati kwa iye, “Khotera kumanja kapena kumanzere: tsatira mmodzi mwa anyamatawa ndipo umulande zida zake.” Koma Asaheli sanasiye kumuthamangitsa.
And Abner said to him, Turn thee aside to thy right hand or to thy left, and lay hold for thyself on one of the young men, and take thyself his armor. But 'Asahel would not turn aside from following him.
22 Abineri anamuchenjezanso Asaheli, “Siya kuthamangitsa ine! Kodi ndikukanthe chifukwa chiyani? Kodi ndikaonana naye bwanji mʼbale wako Yowabu?”
And Abner repeated again to say unto 'Asahel, Turn thee aside from following me: wherefore should I smite thee to the ground? and how should I then lift up my face to Joab thy brother?
23 Koma iye anakana kuleka kumuthamangitsa. Choncho Abineri anabaya Asaheli mʼmimba ndi msonga ya mkondo wake ndipo mkondowo unatulukira mbali ina. Iye anagwa ndi kufera pamalo pomwepo. Ndipo munthu aliyense amayima akafika pamalo pamene anagwera ndi kufa.
But he refused to turn aside; and Abner smote him with the hinder end of the spear under the fifth rib, so that the spear came out behind him; and he fell down there, and died on the spot: and it came to pass, that all who came to the place where 'Asahel had fallen down and died remained standing still.
24 Koma Yowabu ndi Abisai anathamangitsa Abineri, ndipo dzuwa likulowa, anafika ku phiri la Ama, pafupi ndi Giya pa njira yopita ku chipululu cha ku Gibiyoni.
But Joab and Abishai pursued after Abner: and the sun went down when they were come to the hill of Ammah, that lieth before Giach on the way to the wilderness of Gib'on.
25 Pamenepo anthu a fuko la Benjamini anasonkhana kudzathandiza Abineri. Iwo anapanga gulu ndipo anayima pamwamba pa phiri.
And the children of Benjamin assembled themselves together behind Abner, and formed one solid body, and posted themselves on the top of a certain hill.
26 Abineri anayitana Yowabu, “Kodi tipitirize kumenyana mpaka kalekale? Kodi sukuzindikira kuti mathero ake kudzakhala kuwawidwa mitima? Kodi udzawaletsa liti ankhondo ako kuthamangitsa abale awo?”
And Abner called to Joab, and said, Shall for everlasting the sword devour? knowest thou not that it will be bitter in the end? and how long shall it be, ere thou wilt bid the people to return from pursuing their brethren?
27 Yowabu anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, ukanapanda kuyankhula, ankhondo anga akanapitiriza kuthamangitsa abale awo mpaka mmawa.”
And Joab said, As God liveth, unless thou hadst spoken, surely then already in the morning would the people have gone away every one from pursuing his brother.
28 Chomwecho Yowabu analiza lipenga, ndipo ankhondo onse anayima. Iwo analeka kuthamangitsa Aisraeli kapena kumenyana nawo.
So Joab blew the cornet, and all the people remained standing still, and pursued no more after Israel, and they continued no more to fight.
29 Usiku wonsewo Abineri ndi ankhondo ake anayenda kudutsa Araba. Iwo anawoloka Yorodani, napitirira mpaka kudutsa dera lonse la Bitironi ndipo anafika ku Mahanaimu.
And Abner and his men walked through the plain all that night, and they passed over the Jordan, and went through all Bithron, and they came to Machanayim.
30 Choncho Yowabu anabwerera kuchokera kothamangitsa Abineri ndipo anasonkhanitsa ankhondo ake onse. Kupatula Asaheli, panali ankhondo khumi ndi anayi a Davide amene anasowa.
And Joab returned from pursuing Abner; and he gathered all the people together; and there were missed of David's servants nineteen men and 'Asahel.
31 Koma ankhondo a Davide anapha ankhondo a fuko la Benjamini 360 amene anali ndi Abineri.
But the servants of David had smitten [many] of Benjamin, and of Abner's men: three hundred and sixty men died.
32 Iwo anatenga Asaheli ndi kukamuyika mʼmanda a abambo ake ku Betelehemu. Ndipo Yowabu ndi ankhondo ake anayenda usiku wonse ndi kufika ku Hebroni kukucha.
And they took up 'Asahel, and buried him in the sepulchre of his father, which was in Beth-lechem. And Joab and his men went all that night, and the day broke on them at Hebron.

< 2 Samueli 2 >