< 2 Samueli 2 >

1 Patapita nthawi, Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite ku umodzi mwa mizinda ya Yuda?” Yehova anayankha kuti, “Pita.” Davide anafunsanso kuti, “Kodi ndipite kuti?” Yehova anayankha kuti, “Ku Hebroni.”
And it came to pass after this that David inquired of Jehovah, saying, Shall I go up into one of the cities of Judah? And Jehovah said to him, Go up. And David said, Whither shall I go up? And he said, Unto Hebron.
2 Choncho Davide anapita kumeneko ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wamasiye uja wa Nabala wa ku Karimeli.
So David went up thither, and his two wives also, Ahinoam the Jizreelitess, and Abigail the wife of Nabal the Carmelite.
3 Davide anatenganso anthu amene anali nawo aliyense ndi banja lake, ndipo anakakhala ku midzi ya ku Hebroni.
And his men that were with him did David bring up, every man with his household; and they dwelt in the cities of Hebron.
4 Kenaka amuna a ku Yuda anabwera ku Hebroni ndipo kumeneko anadzoza Davide kukhala mfumu ya fuko la Yuda. Davide atawuzidwa kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi ndi amene anayika mʼmanda Sauli,
And the men of Judah came, and there they anointed David king over the house of Judah. And they told David, saying, It is the men of Jabesh-Gilead that have buried Saul.
5 iye anatuma amithenga kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti akayankhule nawo kuti, “Yehova akudalitseni poonetsa kukoma mtima kwanu kwa Sauli mbuye wanu pomuyika mʼmanda.
And David sent messengers to the men of Jabesh-Gilead, and said to them, Blessed be ye of Jehovah, that ye have shewn this kindness to your lord, to Saul, and have buried him!
6 Tsopano Yehova akuonetseni kukoma mtima ndi kukhulupirika kwake ndipo inenso ndidzakukomerani mtima chifukwa munachita zimenezi.
And now Jehovah shew kindness and faithfulness to you; and I also will requite you this good, because ye have done this thing.
7 Tsopano khalani amphamvu ndi olimba mtima, pakuti Sauli mbuye wanu wafa, ndipo fuko la Yuda landidzoza kukhala mfumu yawo.”
And now let your hands be strong, and be ye valiant; for your master Saul is dead, and also the house of Judah have anointed me king over them.
8 Pa nthawi imeneyi Abineri mwana wa Neri, wolamulira ankhondo a Sauli, anatenga Isi-Boseti mwana wa Sauli ndi kubwera naye ku Mahanaimu.
And Abner the son of Ner, captain of Saul's host, took Ishbosheth the son of Saul, and brought him over to Mahanaim;
9 Iye anamuyika kuti akhale mfumu yoyangʼanira Giliyadi, Asuri ndi Yezireeli, pamodzi ndi Efereimu, Benjamini ndi Israeli yense.
and made him king over Gilead, and over the Asshurites, and over Jizreel, and over Ephraim, and over Benjamin, and over all Israel.
10 Isi-Boseti mwana wa Sauli anali wa zaka makumi anayi pamene anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira zaka ziwiri. Koma fuko la Yuda linatsatira Davide.
Ishbosheth Saul's son was forty years old when he began to reign over Israel, and he reigned two years. However, the house of Judah followed David.
11 Davide anakhala mfumu ku Hebroni akulamulira fuko la Yuda, kwa zaka zisanu ndi chimodzi ndi miyezi isanu ndi umodzi.
And the time that David was king in Hebron over the house of Judah was seven years and six months.
12 Abineri mwana wa Neri, pamodzi ndi ankhondo a Isi-Boseti mwana wa Sauli, anachoka ku Mahanaimu ndi kupita ku Gibiyoni.
And Abner the son of Ner, and the servants of Ishbosheth the son of Saul, went out from Mahanaim to Gibeon.
13 Yowabu mwana wa Zeruya pamodzi ndi ankhondo a Davide anapita ndi kukakumana nawo ku dziwe la ku Gibiyoni. Gulu lina linakhala mbali ina ya dziwelo pamene gulu lina linakhala mbali inayo.
And Joab the son of Zeruiah, and the servants of David, went out. And they met together by the pool of Gibeon; and they sat down, these on the one side of the pool, and those on the other side of the pool.
14 Kenaka Abineri anati kwa Yowabu, “Tiye tibweretse ena mwa anyamata athu kuti amenyane patsogolo pathupa.” Yowabu anayankha, “Chabwino, amenyane.”
And Abner said to Joab, Let the young men now arise and make sport before us. And Joab said, Let them arise.
15 Kotero anayimirira ndipo anawawerenga: anyamata khumi ndi awiri a fuko la Benjamini ndi Isi-Boseti mwana wa Sauli ndiponso anyamata khumi ndi awiri a Davide.
And they arose and went over by number, twelve for Benjamin, and for Ishbosheth the son of Saul, and twelve of the servants of David.
16 Tsono aliyense anagwira mutu wa mnzake namubaya mnzakeyo mʼnthiti ndi mpeni ndipo onse anagwera pansi limodzi. Kotero malo amenewo ku Gibiyoni amatchedwa Helikati Hazurimu.
And they caught every one his fellow by the head, and [thrust] his sword in his fellow's side, and they fell down together. And that place was called Helkath-hazzurim, which is by Gibeon.
17 Tsiku limeneli nkhondo yake inali yoopsa kwambiri, ndipo Abineri ndi ankhondo a Israeli anagonjetsedwa ndi ankhondo a Davide.
And the battle that day was very severe; and Abner and the men of Israel were routed before the servants of David.
18 Ana atatu aamuna a Zeruya, Yowabu, Abisai ndi Asaheli anali komweko. Koma Asaheli anali waliwiro ngati insa.
And there were three sons of Zeruiah there, Joab, and Abishai, and Asahel. Now Asahel was swift of foot, as one of the gazelles that are in the field.
19 Iye anathamangitsa Abineri ndipo sanakhotere kumanja kapena kumanzere pamene amamutsatira.
And Asahel pursued after Abner; and in going he turned not to the right hand nor to the left from behind Abner.
20 Abineri anayangʼana mʼmbuyo ndipo anafunsa, “Kodi ndiwe Asaheli?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
Then Abner looked behind him, and said, Art thou Asahel? And he said, I am.
21 Ndipo Abineri anati kwa iye, “Khotera kumanja kapena kumanzere: tsatira mmodzi mwa anyamatawa ndipo umulande zida zake.” Koma Asaheli sanasiye kumuthamangitsa.
And Abner said to him, Turn thee aside, to thy right hand or to thy left, and lay hold of one of the young men, and take for thyself his armour. But Asahel would not turn aside from following him.
22 Abineri anamuchenjezanso Asaheli, “Siya kuthamangitsa ine! Kodi ndikukanthe chifukwa chiyani? Kodi ndikaonana naye bwanji mʼbale wako Yowabu?”
And Abner said again to Asahel, Turn thee aside from following me: why should I smite thee to the ground? how then should I hold up my face to Joab thy brother?
23 Koma iye anakana kuleka kumuthamangitsa. Choncho Abineri anabaya Asaheli mʼmimba ndi msonga ya mkondo wake ndipo mkondowo unatulukira mbali ina. Iye anagwa ndi kufera pamalo pomwepo. Ndipo munthu aliyense amayima akafika pamalo pamene anagwera ndi kufa.
But he refused to turn aside; therefore Abner with the hinder end of the spear smote him in the belly, so that the spear came out behind him; and he fell down there, and died in the same place. And it came to pass, that as many as came to the place where Asahel fell down and died stood still.
24 Koma Yowabu ndi Abisai anathamangitsa Abineri, ndipo dzuwa likulowa, anafika ku phiri la Ama, pafupi ndi Giya pa njira yopita ku chipululu cha ku Gibiyoni.
And Joab and Abishai pursued after Abner; and the sun went down when they came to the hill of Ammah, which is before Giah on the way to the wilderness of Gibeon.
25 Pamenepo anthu a fuko la Benjamini anasonkhana kudzathandiza Abineri. Iwo anapanga gulu ndipo anayima pamwamba pa phiri.
And the children of Benjamin gathered themselves together after Abner, and became one troop, and stood on the top of a hill.
26 Abineri anayitana Yowabu, “Kodi tipitirize kumenyana mpaka kalekale? Kodi sukuzindikira kuti mathero ake kudzakhala kuwawidwa mitima? Kodi udzawaletsa liti ankhondo ako kuthamangitsa abale awo?”
And Abner called to Joab, and said, Shall the sword devour for ever? knowest thou not that it will be bitterness in the latter end? and how long shall it be ere thou bid the people return from following their brethren?
27 Yowabu anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, ukanapanda kuyankhula, ankhondo anga akanapitiriza kuthamangitsa abale awo mpaka mmawa.”
And Joab said, [As] God liveth, unless thou hadst spoken, surely then in the morning the people had gone up every one from following his brother.
28 Chomwecho Yowabu analiza lipenga, ndipo ankhondo onse anayima. Iwo analeka kuthamangitsa Aisraeli kapena kumenyana nawo.
And Joab blew the trumpet, and all the people stood still, and pursued after Israel no more, neither did they fight any more.
29 Usiku wonsewo Abineri ndi ankhondo ake anayenda kudutsa Araba. Iwo anawoloka Yorodani, napitirira mpaka kudutsa dera lonse la Bitironi ndipo anafika ku Mahanaimu.
And Abner and his men walked all that night through the plain, and passed over the Jordan, and went through all Bithron, and they came to Mahanaim.
30 Choncho Yowabu anabwerera kuchokera kothamangitsa Abineri ndipo anasonkhanitsa ankhondo ake onse. Kupatula Asaheli, panali ankhondo khumi ndi anayi a Davide amene anasowa.
And Joab returned from following Abner, and gathered all the people together; and there lacked of David's servants nineteen men, and Asahel.
31 Koma ankhondo a Davide anapha ankhondo a fuko la Benjamini 360 amene anali ndi Abineri.
And the servants of David had smitten of Benjamin, and of Abner's men, three hundred and sixty men, who had died.
32 Iwo anatenga Asaheli ndi kukamuyika mʼmanda a abambo ake ku Betelehemu. Ndipo Yowabu ndi ankhondo ake anayenda usiku wonse ndi kufika ku Hebroni kukucha.
And they took up Asahel, and buried him in the sepulchre of his father, which was in Bethlehem. And Joab and his men went all night, and they came to Hebron at break of day.

< 2 Samueli 2 >