< 2 Samueli 19 >
1 Yowabu anawuzidwa kuti, “Mfumu ikulira maliro a Abisalomu.”
Or, on annonça à Joab que le roi pleurait, et qu’il se lamentait sur son fils.
2 Ndipo kwa asilikali onse chipambano cha tsiku limenelo chinasandulika maliro, chifukwa tsiku limenelo anthu anamva kuti mfumu ili pa chisoni chachikulu chifukwa cha mwana wake.
Et la victoire, en ce jour-là, fut changée en deuil pour tout le peuple: car le peuple en ce jour entendit qu’on disait: Le roi pleure sur son fils.
3 Ankhondo analowa mu mzinda mwakachetechete tsiku limenelo ngati momwe amalowera anthu mwamanyazi chifukwa athawa ku nkhondo.
Et le peuple évita ce jour-là d’entrer dans la ville, comme a coutume de l’éviter le peuple qui a été défait et qui s’enfuit de la bataille.
4 Mfumu inaphimba nkhope yake ndipo inalira mofuwula, “Iwe mwana wanga Abisalomu! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”
Or, le roi couvrit sa tête, et il criait à haute voix: Mon fils Absalom! Absalom mon fils! mon fils!
5 Kenaka Yowabu analowa mʼnyumba ya mfumu nafika kwa mfumuyo ndipo anati, “Lero mwachititsa manyazi asilikali anu onse, amene apulumutsa moyo wanu ndiponso moyo wa ana anu aamuna ndi aakazi, kudzanso moyo wa akazi anu ndi wa azikazi anu.
Joab donc, étant entré près du roi dans la maison, dit: Vous avez aujourd’hui répandu la confusion sur le visage de tous vos serviteurs, qui ont sauvé votre âme, et l’âme de vos fils et de vos filles, et l’âme de vos épouses et de vos femmes.
6 Inu mumakonda amene amadana nanu ndipo mumadana ndi amene amakukondani. Inuyo mwaonetsa lero poyera kuti simusamala za atsogoleri anu a nkhondo ndi asilikali awo. Ine ndikuona kuti inu mukanakondwera ngati Abisalomu akanakhala ndi moyo lero, tonsefe titafa.
Vous aimez ceux qui vous haïssent, et haïssez ceux qui vous aiment; et vous avez montré aujourd’hui que vous ne songez pas à vos officiers et à vos serviteurs; et je reconnais maintenant avec vérité que si votre fils Absalom vivait, et que nous eussions tous succombé, cela vous serait agréable.
7 Tsopano pitani mukawalimbikitse asilikali anu. Ine ndikulumbira mwa Yehova kuti ngati inu simupita palibe munthu amene adzatsale ali ndi inu polowa dzuwa. Ichi chidzakhala choyipa kwambiri kuposa zovuta zonse zimene zinakugwerani kuyambira muli mnyamata mpaka lero.”
Maintenant donc levez-vous, paraissez, et en leur parlant, contentez vos serviteurs: car je vous jure par le Seigneur que, si vous ne sortez, il n’en demeurera pas même un seul avec vous cette nuit; et ce sera pour vous pire que tous les maux qui sont venus sur vous depuis votre adolescence jusqu’à présent.
8 Kotero mfumu inanyamuka ndipo inakhala pa mpando wake pa chipata. Pamene asilikali anawuzidwa kuti, “Mfumu yakhala pa chipata,” onse anabwera kwa iye. Nthawi imeneyi nʼkuti Aisraeli atathawira ku nyumba zawo.
Le roi se leva donc et s’assit à la porte; et l’on annonça à tout le peuple que le roi était assis à la porte; et toute la multitude vint devant le roi; mais Israël s’enfuit dans ses tabernacles.
9 Pakati pa mafuko onse a Israeli, anthu amakangana ndipo amati, “Mfumu inatipulumutsa mʼmanja mwa adani anthu. Iye ndi amene anatilanditsa mʼdzanja la Afilisti. Koma tsopano wathawa mʼdziko muno chifukwa cha Abisalomu.
Et tout le peuple dans toutes les tribus d’Israël s’animait à l’envi, disant: Le roi nous a délivrés de la main de nos ennemis, lui-même nous a sauvés de la main des Philistins; et maintenant il fuit de son pays à cause d’Absalom.
10 Ndipo Abisalomu amene ife tinamudzoza kuti atilamulire wafa pa nkhondo. Tsono nʼchifukwa chiyani simukunena kanthu za kubweretsanso mfumu?”
Et Absalom, que nous avons oint pour être au-dessus de nous, est mort à la guerre. Jusqu’à quand garderez-vous le silence, et ne ramènerez-vous point le roi?
11 Mfumu Davide inatumiza uthenga uwu kwa ansembe Zadoki ndi Abiatara, “Funsani akuluakulu a Yuda, ‘Nʼchifukwa chiyani inu mukukhala otsiriza kuyitana mfumu ku nyumba yake yaufumu, pakuti zimene zikunenedwa mu Israeli yense zamveka kwa mfumu ndi onse amene akukhala nayo.
Or, le roi David envoya à Sadoc et à Abiathar, prêtres, disant: Parlez aux anciens de Juda, disant: Pourquoi venez vous les derniers pour ramener le roi dans sa maison? (Or, la parole de tout Israël était venue jusqu’au roi en sa maison.)
12 Inu ndinu abale anga enieni, mafupa anga ndi mnofu wanga. Nʼchifukwa chiyani inuyo mukukhala otsiriza kubweretsa mfumu?’
Vous êtes mes frères, vous êtes mon os et ma chair: pourquoi ramenez-vous le roi les derniers?
13 Ndipo munene kwa Amasa, ‘Kodi iwe si mʼbale wanga weniweni? Mulungu andilange, andilange kwambiri ngati kuyambira tsopano sukhala mtsogoleri wa ankhondo anga kulowa mʼmalo mwa Yowabu.’”
Et dites à Amasa: N’es-tu pas mon os et ma chair? Que Dieu me fasse ceci, et qu’il ajoute cela, si tu n’es le maître de la milice devant moi, en tout temps, à la place de Joab!
14 Davide anakopa mitima ya anthu onse a Yuda ndipo anthuwo anakhala ngati munthu mmodzi. Iwo anatumiza mawu kwa mfumu, “Bwererani inu ndi anthu anu onse.”
Et il s’attira le cœur de tous les hommes de Juda, comme le cœur d’un seul homme; et ils envoyèrent au roi, disant: Revenez, vous et tous vos serviteurs.
15 Kotero mfumu inabwerera ndipo inakafika mpaka ku Yorodani. Tsono anthu a ku Yuda anabwera ku Giligala kuti akakumane ndi mfumu ndi kumuwolotsa Yorodani.
Le roi donc retourna, et vint jusqu’au Jourdain; et tout Juda vint jusqu’à Galgala pour rencontrer le roi, et pour le conduire au-delà du Jourdain.
16 Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wa ku Bahurimu, anabwera mofulumira pamodzi ndi Ayuda kudzakumana ndi mfumu Davide.
Or Séméi, fils de Géra, fils de Jémini, de Bahurim, se hâta, et descendit avec les hommes de Juda, à la rencontre du roi David,
17 Iyeyo anali ndi anthu 1,000 a fuko la Benjamini pamodzi ndi Ziba, wantchito wa banja la Sauli ndi ana ake aamuna khumi ndi asanu ndi antchito ake makumi awiri. Iwo anathamangira ku Yorodani kumene kunali mfumu.
Avec mille hommes de Benjamin, et Siba, le serviteur de la maison de Saül; et ses quinze fils et vingt serviteurs étaient avec lui; et, traversant le Jourdain avant le roi,
18 Iwo anawoloka mtsinje kukatenga banja lonse la mfumu ndi kuchita zonse zimene mfumuyo imafuna. Pamene Simei mwana wa Gera anawoloka Yorodani, anagwa pansi chafufumimba pamaso pa mfumu,
Ils passèrent à gué, afin de conduire au-delà la maison du roi, et pour agir selon son commandement: or, Séméi, fils de Géra, prosterné devant le roi, lorsque déjà il avait passé le Jourdain,
19 ndipo anati, “Mbuye wanga musaganizire za kulakwa kwanga. Musakumbukire zolakwa zimene mtumiki wanu anakuchitirani tsiku limene mbuye wanga mfumu mumachoka mu Yerusalemu. Mfumu musazikumbukirenso zimenezi.
Lui dit: Mon seigneur, ne considérez point mon iniquité, et ne vous souvenez pas des injures de votre serviteur au jour, mon seigneur le roi, que vous êtes sorti de Jérusalem, et ne la mettez pas en votre cœur, ô roi;
20 Pakuti ine mtumiki wanu ndazindikira kuti ndachimwa. Koma lero ndabwera ngati woyamba wa nyumba ya Yosefe yonse kudzakumana nanu mbuye wanga mfumu.”
Car moi, votre serviteur, je connais mon péché, et c’est pourquoi aujourd’hui je suis venu le premier de toute la maison de Joseph, et je suis descendu à la rencontre de mon seigneur le roi.
21 Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati, “Kodi Simei saphedwa chifukwa cha ichi? Iye anatukwana wodzozedwa wa Yehova.”
Mais Abisaï, fils de Sarvia, répondant, dit: Est-ce que pour ces paroles, Séméi ne sera pas mis à mort, puisqu’il a maudit le christ du Seigneur?
22 Davide anayankha kuti, “Kodi inu ana a Zeruya, ndikuchitireni chiyani? Lero lino iwe wakhala mdani wanga! Kodi wina aphedwe lero mu Israeli? Kodi ine sindikudziwa kuti lero ndine mfumu mu Israeli?”
Et David répondit: Qu’importe à moi et à vous, fils de Sarvia? Pourquoi me devenez-vous aujourd’hui des ennemis? Est-ce donc aujourd’hui qu’un homme sera mis à mort en Israël? Est-ce que j’ignore que je suis devenu aujourd’hui roi sur Israël?
23 Ndipo mfumu inati kwa Simei, “Iwe Simei suphedwa.” Ndipo mfumuyo inalonjeza ndi lumbiro.
Et le roi dit à Séméi: Tu ne mourras point. Et il lui jura.
24 Mefiboseti, mdzukulu wa Sauli, nayenso anabwera kudzakumana ndi mfumu. Kuyambira tsiku limene mfumu inachoka mpaka tsiku limene inabwerera mu mtendere, iye sanasambe mapazi kaya kumeta ndevu kapena kuchapa zovala zake.
Miphiboseth aussi, fils de Saül, descendit à la rencontre du roi, les pieds non lavés et la barbe non rasée; et il n’avait point lavé ses vêtements depuis le jour que le roi était sorti jusqu’au jour de son retour en paix.
25 Pamene anafika kuchokera ku Yerusalemu kudzakumana ndi mfumu, mfumu inamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunapite nane Mefiboseti?”
Et lorsqu’il fut venu à la rencontre du roi à Jérusalem, le roi lui dit: Pourquoi n’es-tu pas venu avec moi, Miphiboseth?
26 Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga mfumu, pakuti ine wantchito wanu ndine wolumala. Ndinati, ‘Andikonzere chishalo cha bulu wanga ndipo ndidzakwera kuti ndipite ndi mfumu.’ Koma Ziba wantchito wanga anandilakwitsa.
Et, répondant, il dit: Mon seigneur le roi, mon serviteur m’a méprisé, et je lui ai dit, moi, votre serviteur, qu’il préparât mon âne, afin que montant dessus je m’en allasse avec le roi; car moi, votre serviteur, je suis boiteux.
27 Ndipo wayankhula zosinjirira za ine mtumiki wanu kwa inu mbuye wanga mfumu. Mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu ndipo chitani chimene chikukomerani.
Et de plus, il m’a accusé, moi, votre serviteur, devant vous, mon seigneur le roi. Mais vous, mon seigneurie roi, vous êtes comme un ange de Dieu; faites ce qui vous est agréable.
28 Zidzukulu zonse za agogo anga sizinayenera chilichonse koma imfa kuchokera kwa inu mbuye wanga mfumu, koma inu munapereka malo kwa mtumiki wanu pakati pa amene amadya pa tebulo lanu. Tsono ine ndili ndi chiyaninso kuti ndipitirize kudandaula kwa mfumu?”
Car toute la maison de mon père n’a mérité que la mort de mon seigneur le roi; cependant vous m’avez placé, moi, votre serviteur, parmi les convives de votre table. Quel sujet ai-je donc d’une juste plainte, et que puis-je encore réclamer du roi?
29 Mfumu inayankha kuti, “Uneneranji zambiri? Ine ndikulamula kuti iwe ndi Ziba mugawane minda.”
Le roi donc lui dit: Pourquoi parles-tu encore? ce que j’ai dit est arrêté: toi et Siba, partagez les possessions.
30 Mefiboseti anati kwa mfumu, “Muloleni atenge zonse, pakuti tsopano mbuye wanga mwafika kwanu mu mtendere.”
Et Miphiboseth répondit au roi: Qu’il prenne même tout, puisque mon seigneur le roi est revenu pacifiquement dans sa maison.
31 Barizilai Mgiliyadi anabweranso kuchokera ku Rogelimu kudzawoloka Yorodani ndi mfumu ndi kumuperekeza kuchokera kumeneko.
Berzellaï aussi, le Galaadite, descendant de Rogelim, conduisit le roi de l’autre côté du Jourdain, prêt à l’accompagner aussi au-delà du fleuve.
32 Tsono Barizilai anali wokalamba kwambiri, wa zaka makumi asanu ndi atatu. Iye ndi amene anapereka zinthu kwa mfumu pamene anali ku Mahanaimu pakuti anali wolemera kwambiri.
Or Berzellaï, le Galaadite, était très vieux, c’est-à-dire, octogénaire; ce fut lui qui fournit des vivres au roi, quand il demeurait dans le camp; car il fut un homme très riche.
33 Mfumu inati kwa Barizilai, “Woloka nane ndipo ukakhale ndi ine mu Yerusalemu ndipo ineyo ndidzakusamalira.”
C’est pourquoi le roi dit à Berzellaï: Viens avec moi, afin que tu vives en repos avec moi à Jérusalem.
34 Barizilai anayankha mfumu kuti, “Kodi zakhala zaka zingati zoti ndikhale ndi moyo, kuti ndipite ku Yerusalemu ndi mfumu?
Et Berzellaï répondit au roi: Quel est le nombre des jours de ma vie, pour que je monte avec le roi à Jérusalem?
35 Ine tsopano ndili ndi zaka 80. Kodi ndingathe kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa? Kodi mtumiki wanu angathe kuzindikira kukoma kwa zimene akudya ndi kumwa? Kodi ndingathe kumva kuyimba kwa amuna ndi akazi? Nʼchifukwa chiyani wantchito wanu akakhale ngati katundu kwa mbuye wanga mfumu?
Je suis octogénaire aujourd’hui. Mes sens ont-ils quelque vigueur, pour discerner le doux et l’amer? Ou le manger et le boire peuvent-ils donner du plaisir à votre serviteur? ou bien puis-je écouter encore la voix des chanteurs et des chanteuses? Pourquoi votre serviteur serait-il à charge à mon seigneur le roi?
36 Koma ine mtumiki wanu ndingoyenda pangʼono kuti ndiwoloke Yorodani pamodzi ndi mfumu. Amfumu mungandipatsirenji mphotho yotere?
Moi, votre serviteur, j’irai un peu au-delà du Jourdain avec vous; je n’ai pas besoin de ce changement.
37 Muloleni, mtumiki wanu abwerere, kuti ndikafere kwathu pafupi ndi manda a abambo ndi amayi anga. Koma nayu mtumiki wanu Kimuhamu. Muloleni iye awoloke nanu mbuye wanga mfumu. Mumuchitire chilichonse chimene chikukomereni!”
Mais je vous conjure, que je puisse, moi votre serviteur, retourner et mourir dans ma ville, et être enseveli près du sépulcre de mon père et de ma mère. Mais voici votre serviteur Chamaam, qu’il aille lui-même avec vous, mon seigneur le roi, et faites pour lui tout ce qui vous semble bon.
38 Mfumu inati, “Kimuhamu adzawoloka ndi ine, ndipo ndidzamuchitira iye chilichonse chimene chidzakondweretsa iwe. Ndipo chilichonse chimene udzandipempha ine ndidzakuchitira.”
C’est pourquoi le roi lui dit: Que Chamaam vienne avec moi, et je ferai pour lui tout ce qui te plaira, et tout ce que tu demanderas, je te raccorderai.
39 Kotero anthu onse anawoloka Yorodani ndipo kenaka mfumu inawoloka. Mfumu inapsompsona Barizilai ndi kumupatsa madalitso ndipo Barizilaiyo anabwerera kwawo.
Et lorsque tout le peuple et le roi eurent passé le Jourdain, le roi baisa Berzellaï et lui souhaita toute sorte de prospérités; et celui-ci s’en retourna en sa demeure.
40 Pamene mfumu inawolokera ku Giligala, Kimuhamu anawoloka naye. Ankhondo onse a Yuda ndi theka la ankhondo a Israeli onse anaperekeza mfumu.
Le roi donc passa à Galgala, et Chamaam avec lui: mais tout le peuple de Juda avait conduit le roi au-delà du fleuve, et la moitié seulement du peuple d’Israël s’y était trouvée.
41 Kenaka Aisraeli onse amabwera kwa mfumu nʼkumati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani abale athu, anthu a ku Ayuda, anakubani mfumu, nawoloka nanu Yorodani inu ndi banja lanu, pamodzi ndi anthu ake onse?”
C’est pourquoi tous les hommes d’Israël, accourant auprès du roi, lui dirent: Pourquoi nos frères, les hommes de Juda, vous ont-ils enlevé, et ont-ils conduit le roi et sa maison au-delà du Jourdain, et tous les hommes de David avec lui?
42 Ayuda onse anayankha Aisraeli kuti, “Ife timachita zimenezi chifukwa mfumu ndi mʼbale wathu. Nʼchifukwa chiyani inu mwapsa mtima ndi zimenezi? Kodi ife tinadya chakudya chilichonse cha mfumu? Kodi chilipo chimene ife tatenga kukhala chathu?”
Et chaque homme de Juda répondit aux hommes d’Israël: Parce que le roi m’est plus proche; pourquoi vous irritez-vous de cela? Est-ce que nous avons mangé quelque chose venant du roi? ou nous a-t-on donné des présents?
43 Aisraeli anayankha Ayuda kuti, “Ife ndi magawo khumi mwa mfumu imeneyi, ndipo kuwonjezera apo, ife tili ndi zinthu zambiri mwa Davide kuposa inu. Tsono nʼchifukwa chiyani mukutichita chipongwe? Kodi ife si amene tinayamba kunena za kubweretsa mfumu yathu?” Koma anthu a Yuda anayankha mwaukali kwambiri kupambana anthu a ku Israeli.
Et un homme d’Israël répondit aux hommes de Juda, et dit: Nous sommes auprès du roi dix fois plus, que vous; ainsi David nous appartient plus qu’à vous. Pourquoi nous avez-vous fait injure, et n’avons-nous pas été avertis les premiers pour ramener notre roi? Mais les hommes de Juda répondirent plus durement aux hommes d’Israël.