< 2 Samueli 19 >
1 Yowabu anawuzidwa kuti, “Mfumu ikulira maliro a Abisalomu.”
I oznámeno jest Joábovi: Aj, král pláče a naříká pro Absolona.
2 Ndipo kwa asilikali onse chipambano cha tsiku limenelo chinasandulika maliro, chifukwa tsiku limenelo anthu anamva kuti mfumu ili pa chisoni chachikulu chifukwa cha mwana wake.
Pročež obrátilo se to vysvobození toho dne v kvílení všemu lidu; nebo slyšel lid v ten den, že bylo praveno: Zámutek má král pro syna svého.
3 Ankhondo analowa mu mzinda mwakachetechete tsiku limenelo ngati momwe amalowera anthu mwamanyazi chifukwa athawa ku nkhondo.
A tak kradl se lid toho dne, vcházeje do města, jako se krade lid, když se stydí, utíkaje z boje.
4 Mfumu inaphimba nkhope yake ndipo inalira mofuwula, “Iwe mwana wanga Abisalomu! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”
Král pak zakryl tvář svou, a křičel král hlasem velikým: Synu můj Absolone, Absolone synu můj, synu můj!
5 Kenaka Yowabu analowa mʼnyumba ya mfumu nafika kwa mfumuyo ndipo anati, “Lero mwachititsa manyazi asilikali anu onse, amene apulumutsa moyo wanu ndiponso moyo wa ana anu aamuna ndi aakazi, kudzanso moyo wa akazi anu ndi wa azikazi anu.
Tedy všed Joáb k králi do domu, řekl: Zahanbil jsi dnes tváři všech služebníků svých, kteříž vysvobodili život tvůj dnes, a život synů tvých i dcer tvých, a život žen tvých i život ženin tvých,
6 Inu mumakonda amene amadana nanu ndipo mumadana ndi amene amakukondani. Inuyo mwaonetsa lero poyera kuti simusamala za atsogoleri anu a nkhondo ndi asilikali awo. Ine ndikuona kuti inu mukanakondwera ngati Abisalomu akanakhala ndi moyo lero, tonsefe titafa.
Miluje ty, kteříž tě mají v nenávisti, a v nenávisti maje ty, kteříž tě milují; nebos dokázal dnes, že sobě nevážíš hejtmanů a služebníků. Shledalť jsem to zajisté dnes, že kdyby byl Absolon živ zůstal, bychom pak všickni dnes byli pobiti, tedy dobře by se tobě to líbilo.
7 Tsopano pitani mukawalimbikitse asilikali anu. Ine ndikulumbira mwa Yehova kuti ngati inu simupita palibe munthu amene adzatsale ali ndi inu polowa dzuwa. Ichi chidzakhala choyipa kwambiri kuposa zovuta zonse zimene zinakugwerani kuyambira muli mnyamata mpaka lero.”
Protož nyní vstana, vyjdi, a mluv ochotně k služebníkům svým; nebo přisahámť skrze Hospodina, jestliže nevyjdeš, žeť nezůstane žádný s tebou této noci, a toť bude tobě horší, nežli všecky zlé věci, kteréž na tebe přišly od mladosti tvé až dosavad.
8 Kotero mfumu inanyamuka ndipo inakhala pa mpando wake pa chipata. Pamene asilikali anawuzidwa kuti, “Mfumu yakhala pa chipata,” onse anabwera kwa iye. Nthawi imeneyi nʼkuti Aisraeli atathawira ku nyumba zawo.
A tak vstav král, posadil se v bráně. I povědíno bylo všemu lidu těmito slovy: Aj, král sedí v bráně. I přišel všecken lid před oblíčej krále, ale lid Izraelský byl zutíkal jeden každý do svých stanů.
9 Pakati pa mafuko onse a Israeli, anthu amakangana ndipo amati, “Mfumu inatipulumutsa mʼmanja mwa adani anthu. Iye ndi amene anatilanditsa mʼdzanja la Afilisti. Koma tsopano wathawa mʼdziko muno chifukwa cha Abisalomu.
Tedy všecken lid hádal se vespolek ve všech pokoleních Izraelských, a pravili: Král vytrhl nás z ruky nepřátel našich, a tentýž vytrhl nás z ruky Filistinských, a teď nyní utekl z země před Absolonem.
10 Ndipo Abisalomu amene ife tinamudzoza kuti atilamulire wafa pa nkhondo. Tsono nʼchifukwa chiyani simukunena kanthu za kubweretsanso mfumu?”
Absolon pak, kteréhož jsme pomazali sobě, zahynul v boji. Nyní tedy, proč zanedbáváte přivésti zase krále?
11 Mfumu Davide inatumiza uthenga uwu kwa ansembe Zadoki ndi Abiatara, “Funsani akuluakulu a Yuda, ‘Nʼchifukwa chiyani inu mukukhala otsiriza kuyitana mfumu ku nyumba yake yaufumu, pakuti zimene zikunenedwa mu Israeli yense zamveka kwa mfumu ndi onse amene akukhala nayo.
Protož král David poslal k Sádochovi a Abiatarovi kněžím, s těmito slovy: Mluvte k starším Judským, řkouce: Proč máte býti poslední v uvedení zase krále do domu jeho? (Nebo řeč všeho lidu Izraelského donesla se krále o uvedení jeho do domu jeho.)
12 Inu ndinu abale anga enieni, mafupa anga ndi mnofu wanga. Nʼchifukwa chiyani inuyo mukukhala otsiriza kubweretsa mfumu?’
Bratří moji jste, kost má a tělo mé jste; proč tedy máte býti poslední v uvedení zase krále?
13 Ndipo munene kwa Amasa, ‘Kodi iwe si mʼbale wanga weniweni? Mulungu andilange, andilange kwambiri ngati kuyambira tsopano sukhala mtsogoleri wa ankhondo anga kulowa mʼmalo mwa Yowabu.’”
A Amazovi také rcete: Zdaliž ty nejsi kost má a tělo mé? Toto ať mi učiní Bůh a toto přidá, jestliže nebudeš hejtmanem vojska přede mnou po všecky dny na místo Joába.
14 Davide anakopa mitima ya anthu onse a Yuda ndipo anthuwo anakhala ngati munthu mmodzi. Iwo anatumiza mawu kwa mfumu, “Bwererani inu ndi anthu anu onse.”
I naklonil srdce všech mužů Judských, jako muže jednoho, aby poslali k králi, řkouce: Navratiž se ty i všickni služebníci tvoji.
15 Kotero mfumu inabwerera ndipo inakafika mpaka ku Yorodani. Tsono anthu a ku Yuda anabwera ku Giligala kuti akakumane ndi mfumu ndi kumuwolotsa Yorodani.
Tedy navrátil se král, a přišel až k Jordánu. Lid pak Judský byl přišel do Galgala, aby se bral vstříc králi, a převedl jej přes Jordán.
16 Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wa ku Bahurimu, anabwera mofulumira pamodzi ndi Ayuda kudzakumana ndi mfumu Davide.
Pospíšil také Semei syn Gery, syna Jemini, kterýž byl z Bahurim, a vyšel s lidem Judským vstříc králi Davidovi.
17 Iyeyo anali ndi anthu 1,000 a fuko la Benjamini pamodzi ndi Ziba, wantchito wa banja la Sauli ndi ana ake aamuna khumi ndi asanu ndi antchito ake makumi awiri. Iwo anathamangira ku Yorodani kumene kunali mfumu.
A tisíc mužů bylo s ním z Beniamin. Síba také služebník domu Saulova, s patnácti syny svými, a dvadceti služebníků jeho s ním, přepravili se přes Jordán před krále.
18 Iwo anawoloka mtsinje kukatenga banja lonse la mfumu ndi kuchita zonse zimene mfumuyo imafuna. Pamene Simei mwana wa Gera anawoloka Yorodani, anagwa pansi chafufumimba pamaso pa mfumu,
I přeplavili lodí, aby převezli čeled královskou a učinili, což by se jemu líbilo. Semei pak syn Gerův padl před králem, když se přepraviti měl přes Jordán.
19 ndipo anati, “Mbuye wanga musaganizire za kulakwa kwanga. Musakumbukire zolakwa zimene mtumiki wanu anakuchitirani tsiku limene mbuye wanga mfumu mumachoka mu Yerusalemu. Mfumu musazikumbukirenso zimenezi.
A řekl králi: Nepočítej mi pán můj nepravosti, a nezpomínej, co neprávě učinil služebník tvůj toho dne, když vyšel pán můj král z Jeruzaléma, aby to měl skládati král v srdci svém.
20 Pakuti ine mtumiki wanu ndazindikira kuti ndachimwa. Koma lero ndabwera ngati woyamba wa nyumba ya Yosefe yonse kudzakumana nanu mbuye wanga mfumu.”
Neboť zná služebník tvůj, že zhřešil, a aj, přišel jsem dnes prvé, než kdo ze vší čeledi Jozefovy, abych vyšel vstříc pánu svému králi.
21 Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati, “Kodi Simei saphedwa chifukwa cha ichi? Iye anatukwana wodzozedwa wa Yehova.”
I odpověděl Abizai syn Sarvie a řekl: A což nebude zabit Semei, proto že zlořečil pomazanému Hospodinovu?
22 Davide anayankha kuti, “Kodi inu ana a Zeruya, ndikuchitireni chiyani? Lero lino iwe wakhala mdani wanga! Kodi wina aphedwe lero mu Israeli? Kodi ine sindikudziwa kuti lero ndine mfumu mu Israeli?”
Ale David řekl: Co vám do toho, synové Sarvie, že jste mi dnes odporní? Dnes-liž má zabit býti někdo v Izraeli? Nebo zdaliž nevím, že dnes jsem králem nad Izraelem.
23 Ndipo mfumu inati kwa Simei, “Iwe Simei suphedwa.” Ndipo mfumuyo inalonjeza ndi lumbiro.
Tedy řekl král k Semei: Neumřeš. I přisáhl mu král.
24 Mefiboseti, mdzukulu wa Sauli, nayenso anabwera kudzakumana ndi mfumu. Kuyambira tsiku limene mfumu inachoka mpaka tsiku limene inabwerera mu mtendere, iye sanasambe mapazi kaya kumeta ndevu kapena kuchapa zovala zake.
Mifibozet také vnuk Saulův vyjel vstříc králi. (Neošetřoval pak byl noh svých, ani brady nespravoval, ani šatů svých nepral od toho dne, jakž byl odšel král, až do dne, když se navrátil v pokoji.)
25 Pamene anafika kuchokera ku Yerusalemu kudzakumana ndi mfumu, mfumu inamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunapite nane Mefiboseti?”
A když přišel do Jeruzaléma, vyšel vstříc králi. I řekl jemu král: Proč jsi neodšel se mnou, Mifibozete?
26 Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga mfumu, pakuti ine wantchito wanu ndine wolumala. Ndinati, ‘Andikonzere chishalo cha bulu wanga ndipo ndidzakwera kuti ndipite ndi mfumu.’ Koma Ziba wantchito wanga anandilakwitsa.
Kterýž odpověděl: Pane můj králi, služebník můj oklamal mne. Řekltě byl zajisté služebník tvůj: Osedlám sobě osla, abych vsedna na něj, bral se s králem, proto že jest kulhavý služebník tvůj.
27 Ndipo wayankhula zosinjirira za ine mtumiki wanu kwa inu mbuye wanga mfumu. Mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu ndipo chitani chimene chikukomerani.
I osočil služebníka tvého u pána mého krále, ale pán můj král jest jako anděl Boží, učiniž tedy, cožť se dobrého vidí.
28 Zidzukulu zonse za agogo anga sizinayenera chilichonse koma imfa kuchokera kwa inu mbuye wanga mfumu, koma inu munapereka malo kwa mtumiki wanu pakati pa amene amadya pa tebulo lanu. Tsono ine ndili ndi chiyaninso kuti ndipitirize kudandaula kwa mfumu?”
Nebo všickni z domu otce mého byli jsme hodni smrti před pánem mým králem, a však jsi zasadil služebníka svého mezi ty, kteříž jedí chléb stolu tvého. K čemuž bych více právo měl, a oč se více na krále domlouval?
29 Mfumu inayankha kuti, “Uneneranji zambiri? Ine ndikulamula kuti iwe ndi Ziba mugawane minda.”
Jemuž řekl král: Proč šíříš řeč svou? Vyřklť jsem. Ty a Síba rozdělte se statkem.
30 Mefiboseti anati kwa mfumu, “Muloleni atenge zonse, pakuti tsopano mbuye wanga mwafika kwanu mu mtendere.”
Ještě řekl Mifibozet králi: Třebas nechť všecko vezme, když se jen navrátil pán můj král v pokoji do domu svého.
31 Barizilai Mgiliyadi anabweranso kuchokera ku Rogelimu kudzawoloka Yorodani ndi mfumu ndi kumuperekeza kuchokera kumeneko.
Ano i Barzillai Galádský vyšel z Rogelim, a přepravil se s králem přes Jordán, aby ho zprovodil za Jordán.
32 Tsono Barizilai anali wokalamba kwambiri, wa zaka makumi asanu ndi atatu. Iye ndi amene anapereka zinthu kwa mfumu pamene anali ku Mahanaimu pakuti anali wolemera kwambiri.
Byl pak Barzillai velmi starý, maje osmdesáte let, kterýž opatroval krále stravou, když obýval v Mahanaim; nebo byl člověk bohatý velmi.
33 Mfumu inati kwa Barizilai, “Woloka nane ndipo ukakhale ndi ine mu Yerusalemu ndipo ineyo ndidzakusamalira.”
I řekl král k Barzillai: Poď se mnou, a chovati tě budu při sobě v Jeruzalémě.
34 Barizilai anayankha mfumu kuti, “Kodi zakhala zaka zingati zoti ndikhale ndi moyo, kuti ndipite ku Yerusalemu ndi mfumu?
Ale Barzillai odpověděl králi: Jacíž jsou dnové věku mého, abych šel s králem do Jeruzaléma?
35 Ine tsopano ndili ndi zaka 80. Kodi ndingathe kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa? Kodi mtumiki wanu angathe kuzindikira kukoma kwa zimene akudya ndi kumwa? Kodi ndingathe kumva kuyimba kwa amuna ndi akazi? Nʼchifukwa chiyani wantchito wanu akakhale ngati katundu kwa mbuye wanga mfumu?
V osmdesáti letech jsem dnes. Zdaliž mohu rozeznati mezi dobrým a zlým? Zdaliž okušením rozezná služebník tvůj, co bych jedl a co bych pil? Zdaliž poslouchati mohu již hlasu zpěváků a zpěvakyní? Proč by tedy služebník tvůj déle býti měl břemenem pánu svému králi?
36 Koma ine mtumiki wanu ndingoyenda pangʼono kuti ndiwoloke Yorodani pamodzi ndi mfumu. Amfumu mungandipatsirenji mphotho yotere?
Maličko ještě půjde služebník tvůj za Jordán s králem; nebo proč by mi se takovou odplatou král odplacovati měl?
37 Muloleni, mtumiki wanu abwerere, kuti ndikafere kwathu pafupi ndi manda a abambo ndi amayi anga. Koma nayu mtumiki wanu Kimuhamu. Muloleni iye awoloke nanu mbuye wanga mfumu. Mumuchitire chilichonse chimene chikukomereni!”
Nechť se navrátí, prosím, služebník tvůj, ať umru v městě svém, kdež jest hrob otce mého a matky mé. Aj, služebník tvůj Chimham půjde se pánem mým králem, jemuž učiníš, cožť se dobrého viděti bude.
38 Mfumu inati, “Kimuhamu adzawoloka ndi ine, ndipo ndidzamuchitira iye chilichonse chimene chidzakondweretsa iwe. Ndipo chilichonse chimene udzandipempha ine ndidzakuchitira.”
I řekl král: Dobře, nechť jde se mnou Chimham, a učiním jemu, což se tobě za dobré viděti bude; nadto čehožkoli požádáš ode mne, toť učiním.
39 Kotero anthu onse anawoloka Yorodani ndipo kenaka mfumu inawoloka. Mfumu inapsompsona Barizilai ndi kumupatsa madalitso ndipo Barizilaiyo anabwerera kwawo.
A když se přepravil všecken lid přes Jordán, král také přepravil se. I políbil král Barzillai a požehnal ho, kterýžto navrátil se na místo své.
40 Pamene mfumu inawolokera ku Giligala, Kimuhamu anawoloka naye. Ankhondo onse a Yuda ndi theka la ankhondo a Israeli onse anaperekeza mfumu.
A tak bral se král do Galgala a Chimham s ním; všecken také lid Judský provázeli krále, též i polovice lidu Izraelského.
41 Kenaka Aisraeli onse amabwera kwa mfumu nʼkumati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani abale athu, anthu a ku Ayuda, anakubani mfumu, nawoloka nanu Yorodani inu ndi banja lanu, pamodzi ndi anthu ake onse?”
A aj, všickni muži Izraelští přišedše k králi, řekli jemu: Proč jsou tě ukradli bratří naši, muži Juda, a převedli krále a čeled jeho přes Jordán, i všecky muže Davidovy s ním?
42 Ayuda onse anayankha Aisraeli kuti, “Ife timachita zimenezi chifukwa mfumu ndi mʼbale wathu. Nʼchifukwa chiyani inu mwapsa mtima ndi zimenezi? Kodi ife tinadya chakudya chilichonse cha mfumu? Kodi chilipo chimene ife tatenga kukhala chathu?”
I odpověděli všickni muži Judští mužům Izraelským: Proto že král jest příbuzný náš. A proč se hněváte o to? Zdaliž nás za to král pokrmy opatroval? Zdaliž nám jaké dary dal?
43 Aisraeli anayankha Ayuda kuti, “Ife ndi magawo khumi mwa mfumu imeneyi, ndipo kuwonjezera apo, ife tili ndi zinthu zambiri mwa Davide kuposa inu. Tsono nʼchifukwa chiyani mukutichita chipongwe? Kodi ife si amene tinayamba kunena za kubweretsa mfumu yathu?” Koma anthu a Yuda anayankha mwaukali kwambiri kupambana anthu a ku Israeli.
Odpovídajíce pak muži Izraelští mužům Judským, řekli: Deset dílů máme v králi, a protož i v Davidovi máme více nežli vy. Pročež tedy málo jste nás sobě vážili? Zdaliž jsme my prvé o to nemluvili, abychom zase přivedli krále svého? Ale tvrdší byla řeč mužů Judských nad řeč mužů Izraelských.