< 2 Samueli 18 >
1 Davide anasonkhanitsa anthu amene anali naye ndipo anasankha atsogoleri ena olamulira ankhondo 1,000 ndi ena olamulira ankhondo 100.
Potom David pobroji narod što bijaše s njim i postavi nad njima tisućnike i stotnike.
2 Davide anatumiza asilikaliwo atawagawa patatu: gulu loyamba limalamulidwa ndi Yowabu, gulu lachiwiri limalamulidwa ndi Abisai ndipo gulu lachitatu limalamulidwa ndi Itai Mgiti. Mfumu inawuza asilikaliwo kuti, “Inenso ndipita nanu ndithu.”
Zatim podijeli vojsku na tri skupine: jednu trećinu predade Joabu, drugu trećinu Abišaju, sinu Sarvijinu, bratu Joabovu, a treću trećinu Itaju iz Gata. Tada David reče narodu: “I ja ću s vama u rat.”
3 Koma anthuwo anati, “Inu musapite nafe. Ngati tidzathamangitsidwa, iwowo sadzasamala za ife. Ngakhale theka la ife litafa, iwo sadzasamalako. Koma inuyo ndinu ofunika kuposa asilikali 10,000. Nʼkwabwino kwambiri kuti inu muzititumizira chithandizo kuchokera ku mzindako.”
Ali se narod usprotivi: “Ne smiješ ti ići. Jer ako mi i pobjegnemo, neće nitko na to obraćati pažnju, ili ako nas i pola izgine, neće se na to obraćati pažnja; ali ti sam vrijediš kao nas deset tisuća. Osim toga, bolje je da budeš pripravan da nam iz grada pomogneš.”
4 Mfumu inayankha kuti, “Ine ndichita chimene chili chokukomerani.” Kotero mfumu inayima pambali pa chipata pamene ankhondo onse amayenda mʼmagulu a anthu 100 ndi a 1,000.
A kralj im odgovori: “Učinit ću sve što vam se čini dobro.” I kralj stade kod vrata dok je vojska izlazila po stotinama i tisućama.
5 Mfumu inalamulira Yowabu, Abisai ndi Itai kuti, “Mumukomere mtima Abisalomu chifukwa cha ine.” Ndipo asilikali onse anamva pamene mfumu imalamula izi za Abisalomu kwa wolamulira aliyense.
A Joabu, Abišaju i Itaju dade zapovijed: “Čuvajte mi mladića Abšaloma!” I sav je narod čuo da je kralj tako zapovjedio svim vojvodama za Abšaloma.
6 Ankhondo anayenda kupita kukachita nkhondo ndi Israeli, ndipo nkhondo inachitika mʼnkhalango ya Efereimu.
Tako vojska iziđe za boj spremna pred Izraela i bitka se zametnu u Efrajimovoj šumi.
7 Aisraeli anagonjetsedwa kumeneko ndi ankhondo a Davide. Tsiku limenelo anaphedwa anthu okwanira 20,000.
Izraelsku vojsku potukoše Davidovi ljudi; i velik poraz bijaše u onaj dan: dvadeset tisuća mrtvih.
8 Nkhondo inafalikira ku madera onse akumidzi ndipo anthu akufa chifukwa cha zoopsa za mʼnkhalango anali ambiri tsiku limenelo kuposa akufa ndi lupanga.
Boj se proširio po svemu onom kraju i više je ljudi onoga dana progutala šuma nego mač.
9 Tsono zinachitika kuti Abisalomu anakumana ndi asilikali a Davide. Iye anali atakwera bulu ndipo pamene buluyo amadutsa pansi pa nthambi zambiri za mtengo wa thundu, mutu wa Abisalomu unakodwa mu mtengomo. Iye anasiyidwa atatsakamira mʼmalele, pamene bulu amene anakwerapoyo amapitirira.
Abšalom slučajno zapade u ruke Davidovim ljudima. Abšalom je jahao na mazgi, a mazga naiđe pod grane velika hrasta, tako te je Abšalomu glava zapela o grane i on osta viseći između neba i zemlje, dok je mazga ispod njega otišla dalje.
10 Mmodzi mwa asilikali ataona zimenezi, anamuwuza Yowabu kuti, “Ine ndamuona Abisalomu ali lende mu mtengo wa thundu.”
Vidje to neki čovjek i javi Joabu govoreći: “Upravo sam vidio Abšaloma gdje visi o jednom hrastu.”
11 Yowabu anati kwa munthu amene anamuwuza zimenezi, “Ukuti chiyani! Unamuona? Nʼchifukwa chiyani sunamukanthire pansi pomwepo? Ndipo ine ndikanakupatsa ndalama za siliva khumi ndi lamba wausilikali.”
A Joab odvrati čovjeku koji mu je to javio: “Kad si ga vidio, zašto ga na mjestu nisi sastavio sa zemljom? Moja bi onda bila dužnost da ti dam deset srebrnih šekela i jedan pojas!”
12 Koma munthuyo anayankha kuti, “Ngakhale atandipatsa mʼmanja mwanga ndalama zasiliva 1,000, sindingatambasule dzanja langa kupha mwana wa mfumu. Ife tikumva, mfumu inalamula inu Abisai ndiponso Itai kuti, ‘Mutetezeni mnyamatayo Abisalomu chifukwa cha ine!’
Ali čovjek odgovori Joabu: “I kad bi mi na dlan izbrojio tisuću srebrnih šekela, ne bih digao ruku na kraljeva sina! Čuli smo na svoje uši kako je kralj zapovjedio tebi, Abišaju i Itaju govoreći: 'Čuvajte mi mladića Abšaloma!'
13 Ndipo sindikanayika moyo wanga pa chiswe pakuti palibe chimene chimabisika pamaso pa mfumu komanso inu simukanditeteza.”
Da sam podmuklo napao na njega izlažući opasnosti svoj život - jer kralju ništa ne ostaje skriveno - onda bi se ti držao po strani.”
14 Yowabu anati, “Ine sinditayanso nthawi ndi iwe.” Ndipo anatenga mikondo itatu mʼmanja mwake ndipo anabaya pamtima pa Abisalomu, Abisalomuyo akanali ndi moyo pa mtengo wa thundu.
A Joab odvrati: “Neću ja ovdje dangubiti s tobom!” I uze tri sulice u ruke i zabode ih u srce Abšalomu, koji je bio još živ viseći o hrastu.
15 Ndipo anthu khumi onyamula zida za Yowabu anazungulira Abisalomu, kumubaya ndi kumupha.
Nato priđe deset momaka, štitonoša Joabovih, i dotukoše Abšaloma i usmrtiše.
16 Kenaka Yowabu analiza lipenga ndipo asilikali analeka kuthamangitsa Israeli pakuti Yowabu anawaletsa.
Tada Joab zapovjedi da zatrube u rog, i vojska prestade progoniti Izraela jer je Joab zaustavio vojsku.
17 Iwo anatenga Abisalomu ndi kumuponya mʼdzenje lalikulu mʼchipululumo ndipo anawunjikapo miyala ikuluikulu. Nthawiyi Aisraeli onse anathawa kupita ku nyumba zawo.
Potom uzeše Abšaloma, baciše ga u duboku jamu usred šume i navaljaše na nj veliku gomilu kamenja. Izraelci pak pobjegoše svaki svome šatoru.
18 Abisalomu ali ndi moyo anadzimangira chipilala mʼchigwa cha mfumu, pakuti ankaganiza kuti, “Ine ndilibe mwana wamwamuna amene adzakhale chikumbutso changa.” Chipilalacho anachitchula dzina lake lomwe ndipo mpaka lero chimatchedwa chipilala cha Abisalomu.
Abšalom bijaše još za života postavio sebi spomenik u Kraljevoj dolini jer mišljaše: “Nemam sina koji bi sačuvao spomen mome imenu.” I nazvao je taj spomenik po svome imenu te se još i danas zove “Abšalomov spomenik”.
19 Tsono Ahimaazi mwana wa Zadoki anati, “Ndiloleni ndithamange ndi kukapereka uthenga kwa mfumu kuti Yehova wayipulumutsa mʼdzanja la adani ake.”
Ahimaas, Sadokov sin, reče Joabu: “Idem javiti kralju veselu vijest da mu je Jahve pribavio pravdu izbavivši ga iz ruku njegovih neprijatelja.”
20 Yowabu anamuwuza iye kuti, “Iwe si amene uti ukanene zimenezi lero. Ukapereka uthenga nthawi ina, koma usatero lero, chifukwa mwana wa mfumu wafa.”
Ali mu Joab reče: “Ne možeš danas biti glasnik vesele vijesti, nego ćeš to biti koji drugi dan; danas ne možeš javiti dobru vijest jer je poginuo kraljev sin.”
21 Kenaka Yowabu anawuza Mkusi kuti, “Pita ukawuze mfumu zimene waona.” Mkusiyo anawerama pamaso pa Yowabu ndipo anathamanga kupita.
Zatim Joab zapovjedi Etiopljaninu: “Idi javi kralju što si vidio!” Etiopljanin se pokloni Joabu i otrča.
22 Ahimaazi mwana wa Zadoki ananenanso kwa Yowabu kuti, “Zivute zitani, chonde mundilole kuti ndipite pambuyo pa Mkusiyo.” Koma Yowabu anayankha kuti, “Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukufuna kupita? Ulibe nkhani yoti ukalandire nayo mphotho.”
A Sadokov sim Ahimaas opet zamoli Joaba: “Dogodilo se što mu drago, dopusti da otrčim i ja za Etiopljaninom.” A Joab upita: “Zašto bi trčao, sine moj, kad ti ta vesela vijest neće pribaviti nagrade?”
23 Iye anati, “Zivute zitani ine ndikufuna kuti ndipite.” Choncho Yowabu anati “Pita!” Ndipo Ahimaazi anathamanga kudzera njira ya ku chigwa ndipo anamupitirira Mkusi uja.
A on ponovi: “Dogodilo se što mu drago, trčat ću!” A Joab mu odvrati: “Trči!” I Ahimaas otrča putem kroz ravnicu i preteče Etiopljanina.
24 Nthawi imeneyo nʼkuti Davide atakhala pakati pa zipata ziwiri, chakubwalo ndi chamʼkati. Mlonda anakwera pa khoma nakayimirira pa denga la chipata. Anati atayangʼana, anaona munthu akuthamanga yekhayekha.
David je upravo sjedio među dvojim gradskim vratima, a stražar se bio uspeo na krov iznad vrata. Podigavši oči, stražar ugleda čovjeka kako trči sam.
25 Mlonda uja anapita kwa mfumu ndipo anafotokoza. Mfumu inati, “Ngati ali yekha ali ndi nkhani yabwino” Ndipo munthuyo anayandikira.
Stražar povika i javi kralju, a kralj mu reče: “Ako je sam, nosi dobar glas na ustima.” Čovjek je dolazio sve bliže.
26 Mlonda uja anaonanso munthu wina akuthamanga, ndipo anayitana woyangʼanira pa chipata, “Taona, munthu winanso akuthamanga ali yekha!” Mfumu inati, “Iye akubweretsanso nkhani yabwino.”
Uto stražar ugleda drugoga čovjeka gdje trči. I povika stražar koji je bio nad vratima: “Evo još jednoga čovjeka koji trči sam!” A kralj odvrati: “I taj nosi dobar glas.”
27 Mlonda uja anati, “Munthu akuthamanga patsogoloyo, kathamangidwe kake kakufanafana ndi mmene amathamangira Ahimaazi, mwana wa Zadoki.” Mfumu inati, “Ameneyo ndi munthu wabwino, ndipo akubwera ndi nkhani yabwino.”
Stražar nastavi: “Prepoznajem trk prvoga čovjeka: trči kao Sadokov sin Ahimaas.” A kralj odvrati: “To je dobar čovjek, dolazi s dobrim glasom.”
28 Ndipo Ahimaazi anafuwula kwa mfumu, “Zonse zili bwino!” Iye anagwada pamaso pa mfumu nkhope yake atagunditsa pansi ndipo anati, “Yehova Mulungu wathu alemekezedwe! Iye wapereka mʼdzanja lathu anthu amene anawukira inu mbuye wanga mfumu.”
Ahimaas se približi kralju i pozdravi ga: “Zdravo!” Baci se licem na zemlju pred kraljem i nastavi: “Blagoslovljen Jahve, tvoj Bog, koji je napustio ljude što su digli ruku na moga gospodara i kralja!”
29 Mfumu inafunsa, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Ahimaazi anayankha, “Pamene Yowabu amati azindituma ine mtumiki wanu ndinaona chipiringu cha anthu, koma sindikudziwa chinali chiyani.”
A kralj upita: “Je li spašen mladić Abšalom?” A Ahimaas odgovori: “Vidio sam veliku vrevu kad je kraljev sluga Joab slao tvoga slugu, ali ne znam što je bilo.”
30 Mfumu inati, “Ima apo ndipo udikire.” Kotero iye anapita pa mbali nayima pamenepo.
Kralj mu reče: “Odstupi i stani tamo!” On odstupi i stade.
31 Kenaka Mkusi uja anafika ndipo anati, “Mbuye wanga mfumu imvani nkhani yabwino! Yehova wakupulumutsani inu lero kwa onse amene anakuwukirani.”
Uto stiže Etiopljanin i progovori: “Neka moj gospodar kralj primi veselu vijest. Jahve ti je danas pribavio pravdu izbavivši te iz ruku svih onih koji su ustali na tebe.”
32 Mfumu inafunsa Mkusiyo kuti, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Mkusiyo anayankha kuti, “Adani anu mbuye wanga mfumu, pamodzi ndi anthu onse amene amakuwukirani, ziwaonekere zomwe zamuonekera mnyamatayo.”
A kralj upita Etiopljanina: “Je li spašen mladić Abšalom?” A Etiopljanin odgovori: “Neka neprijatelji moga gospodara i kralja i svi koji se dižu na tebe u zloj namjeri - prođu kao taj mladić!”
33 Mfumu inanthunthumira. Inapita ku chipinda cha mmwamba cha pa chipata kukalira. Pamene imapita, inkati: “Iwe mwana wanga Abisalomu! Mwana wanga! Mwana wanga Abisalomu! Zikanakhala bwino ndikanafa ndine mʼmalo mwako! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”
Kralj zadrhta, pope se u gornju odaju nad vratima i zaplaka; jecajući govoraše ovako: “Sine Abšalome, sine moj! Sine moj Abšalome! Oh, da sam ja umro mjesto tebe! Abšalome, sine moj, sine moj!”