< 2 Samueli 17 >

1 Ahitofele anati kwa Abisalomu, “Mundilole ndisankhe asilikali 12,000, ndinyamuke usiku womwe uno kuti ndithamangire Davide.
Још рече Ахитофел Авесалому: Да одаберем дванаест хиљада људи па да идем и терам Давида ноћас.
2 Ndipo ndikamuthira nkhondo atatopa ndiponso atataya mtima. Ndikamuchititsa mantha ndipo anthu onse amene ali naye akathawa. Ine ndikakantha mfumu yokhayo,
Па ћу га стигнути док је уморан и изнемоглих руку; и уплашићу га, те ће побећи сав народ што је с њим, па ћу убити цара самог.
3 ndipo anthu onse ndidzabwera nawo kwa inu, ngati mkwati amene akubwerera kwa mwamuna wake. Imfa ya munthu mmodzi yekha idzakhalitsa anthu onse pa mtendere.”
И обратићу сав народ к теби; јер за оним кога тражиш стоји да се сви врате к теби; тада ће се сав народ умирити.
4 Malangizo awa anaoneka abwino kwa Abisalomu ndi kwa akuluakulu onse a Israeli.
И то се учини добро Авесалому и свим старешинама Израиљевим.
5 Koma Abisalomu anati, “Muyitanenso Husai Mwariki kuti timve zimene iye adzanena.”
Али рече Авесалом: Дозовите и Хусаја Архијанина да чујемо шта ће и он рећи.
6 Husai atabwera kwa iye, Abisalomu anati, “Ahitofele wapereka malangizo ake. Kodi tichite zimene wanena? Ngati sichoncho, tiwuze maganizo ako.”
А кад дође Хусај к Авесалому, рече му Авесалом говорећи: Тако и тако рече Ахитофел; хоћемо ли чинити како он рече или нећемо? Кажи ти.
7 Husai anayankha Abisalomu kuti, “Malangizo amene Ahitofele wapereka si abwino pa nthawi ino.
А Хусај рече Авесалому: Није добар савет што је сада саветовао Ахитофел.
8 Inu mukudziwa bwino abambo anu ali ndi ankhondo awo. Iwo ndi anthu ankhondo komanso ndi woopsa ngati chimbalangondo chimene chalandidwa ana ake. Kuwonjezera apa abambo anu ndi katswiri wa nkhondo. Iwo sanagone pamodzi ndi asilikali awo.
Још рече Хусај: Ти знаш оца свог и људе његове да су храбри и да су љута срца као медведица кад јој отму медведиће у пољу; сврх тога, твој је отац ратник, неће ноћити с народом.
9 Onani, ngakhale tsopano lino abisala mʼphanga lina ku malo ena ake. Ngati iwo atayamba kuthira nkhondo asilikali anu, aliyense amene adzamve zimenezi adzati, ‘Gulu lalikulu lankhondo lotsatira Abisalomu laphedwa.’
Гле, он се је сада сакрио у какву јаму или на друго како место. Па ако у први мах који од ових погину, ко год чује сваки ће рећи: Побијен је народ који приста за Авесаломом.
10 Tsono ngakhale msilikali wolimba mtima kwambiri, amene mtima wake uli ngati wa mkango, adzagwidwa ndi mantha aakulu pakuti Aisraeli akudziwa kuti abambo anu ndi ankhondo ndipo kuti iwo amene ali nawo ndi anthu olimba mtima.
А тада ће најхрабрији, у којих је срце као срце лавово, клонути, јер сав Израиљ зна да је твој отац јунак и да су храбри који су с њим.
11 “Kotero ine ndikukulangizani kuti: Aisraeli onse, kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba; ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja, asonkhane kwa inu ndipo muwatsogolera kupita ku nkhondo.
Зато ја саветујем да скупиш к себи све Израиљце од Дана до Вирсавеје да их буде као песка на мору, па ти главом иди у бој.
12 Ndipo ife tidzapita kukamuthira nkhondo kulikonse kumene tikamupeze, ndipo ife tikamuthira nkhondo ngati mame pa nthaka. Palibe amene adzakhale wamoyo kaya iye kapena ankhondo ake.
Тада ћемо поћи на њ, где би се год налазио, и напашћемо на њ као што роса пада на земљу, да му не остане ниједан од свих људи што су с њим.
13 Iye akakathawira mu mzinda, Aisraeli onse adzabweretsa zingwe ku mzindawo, ndipo ife tidzawugwetsera ku chigwa mpaka sipadzapezeka ngakhale kachidutswa.”
Ако ли утече у град, сав народ израиљски нека донесе ужа под онај град, па ћемо га свући у поток, да се ни камен не нађе онде.
14 Abisalomu ndi ankhondo ena onse a Israeli anati, “Malangizo a Husai Mwariki ndi abwino kuposa a Ahitofele.” Pakuti Yehova anatsimikiza kutsutsa malangizo onse abwino a Ahitofele ndi cholinga choti zimuvute Abisalomu.
Тада рече Авесалом и сви Израиљци: Бољи је савет Хусаја Архијанина него савет Ахитофелов. Јер Господ беше наредио да се разбије савет Ахитофелов, који беше бољи, да би Господ навукао зло на Авесалома.
15 Husai anawuza ansembe Zadoki ndi Abiatara kuti, “Ahitofele analangiza Abisalomu ndi akuluakulu a Israeli zakuti, koma ine ndawalangiza kuchita zakutizakuti.
Потом рече Хусај свештеницима Садоку и Авијатару: Тако и тако саветова Ахитофел Авесалома и старешине Израиљеве, а ја саветовах тако и тако.
16 Tsopano tumizani wamthenga msangamsanga kuti akamuwuze Davide kuti, ‘Musakagone powolokera Yorodani ku chipululu koma mukawoloke. Mukapanda kutero, mfumu ndi anthu onse amene ali naye adzaphedwa.’”
Него брже пошаљите, те јавите Давиду и реците: Немој ноћас ноћити у пољу у пустињи, него пређи преко, да не буде прождрт цар и сав народ што је с њим.
17 Yonatani ndi Ahimaazi amakhala ku Eni Rogeli. Tsono wantchito wamkazi ndiye amapita kukawawuza ndipo iwo amayenera kupita kukamuwuza mfumu Davide, pakuti iwowo sankayenera kuonekera polowa mu mzinda.
А Јонатан и Ахимас стајаху код студенца Рогила, и дође једна слушкиња и каза им, да би отишли те јавили цару Давиду; јер се не смеху показати ни ући у град.
18 Koma mnyamata wina anawaona ndipo anakawuza Abisalomu. Kotero anthu awiriwo anachoka mofulumira ndipo anapita ku nyumba ya munthu wina ku Bahurimu. Iye anali ndi chitsime ku mpanda kwake ndipo iwo analowamo.
Али их виде један момак, те каза Авесалому; а они обојица брже отидоше, и дођоше у Ваурим у кућу једног човека који имаше на двору студенац, те се спустише у њ.
19 Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.
И жена узе и разастре поњаву поврх студенца, и поврх ње разасу прекрупу. И тако се не дозна.
20 Anthu a Abisalomu atafika kwa mkaziyo pa nyumbapo anafunsa kuti, “Kodi Ahimaazi ndi Yonatani ali kuti?” Mkaziyo anawayankha kuti, “Awoloka mtsinje.” Anthuwo anafunafuna koma sanapeze munthu, kotero anabwerera ku Yerusalemu.
Јер дођоше слуге Авесаломове к оној жени у кућу, и рекоше јој: Где је Ахимас и Јонатан? А жена им рече: Отидоше преко потока. Тако траживши и не нашавши вратише се у Јерусалим.
21 Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”
А кад отидоше, они изађоше из студенца, и отидоше те јавише цару Давиду, и рекоше му: Устаните и пређите брже преко воде; јер је тако и тако саветовао Ахитофел на вас.
22 Kotero Davide ndi anthu onse amene anali nawo ananyamuka ndi kuwoloka Yorodani. Pofika mmamawa, panalibe munthu amene anatsala asanawoloke Yorodani!
Тада уста Давид и сав народ што беше с њим, и пређоше преко Јордана пре зоре, не оста ниједан да не пређе преко Јордана.
23 Ahitofele ataona kuti malangizo ake sanatsatidwe, iye anakwera bulu wake napita ku mzinda wa kwawo ku nyumba yake. Iye anakonza mʼnyumba mwakemo ndi kudzimangirira. Kotero anafa nayikidwa mʼmanda a abambo ake.
Ахитофел пак видећи где се не учини како он саветова, оседла свог магарца, па се подиже и отиде кући својој, у свој град, и наредивши за своју кућу обеси се те умре, и би погребен у гробу оца свог.
24 Davide anapita ku Mahanaimu, ndipo Abisalomu anawoloka Yorodani pamodzi ndi ankhondo ena onse a Israeli.
А Давид дође у Маханајим; Авесалом пак пређе преко Јордана и сав Израиљ што беше с њим.
25 Abisalomu anasankha Amasa kukhala mkulu wa ankhondo mʼmalo mwa Yowabu. Amasa anali mwana wa munthu wotchedwa Itira Mwisraeli amene anakwatira Abigayeli mwana wa Nahasi mlongo wake wa Zeruya, amayi ake a Yowabu.
И постави Авесалом Амасу над војском, на место Јоавово; а Амаса беше син неког човека по имену Итре Израиљца, који облежа Авигеју кћер Насову, сестру Серује матере Јоавове.
26 Aisraeli ndi Abisalomu anamanga zithando mʼdziko la Giliyadi.
И стаде у логор Израиљ с Авесаломом у земљи Галадовој.
27 Davide atafika ku Mahanaimu, Sobi mwana wa Nahasi wochokera ku Raba ku dziko la Amoni ndi Makiri mwana wa Amieli wochokera ku Lodebara, ndi Barizilai Mgiliyadi wochokera ku Rogelimu
А кад дође Давид у Маханајим, Совије син Насов из Раве синова Амонових и Махир син Амилов из Лодевара и Варзелај од Галада из Рогелима.
28 anabweretsa zofunda, mabeseni ndi miphika. Iwo anabweretsanso kwa Davide ndi anthu ake zakudya izi: tirigu ndi barele, ufa ndi tirigu wokazinga, nyemba ndi mphodza,
Донесоше постеље и чаша и судова земљаних и пшенице и јечма и брашна и прекрупе и боба и лећа и пржених зрна,
29 uchi ndi chambiko, nkhosa ndi mafuta olimba a mkaka wangʼombe. Pakuti anati, “Anthuwa ali ndi njala ndipo atopa, alinso ndi ludzu muno mʼchipululu.”
И меда и масла и оваца и сира крављег; донесоше Давиду и народу што беше с њим да једу. Јер говораху: Народ је гладан и уморан и жедан у тој пустињи.

< 2 Samueli 17 >