< 2 Samueli 17 >

1 Ahitofele anati kwa Abisalomu, “Mundilole ndisankhe asilikali 12,000, ndinyamuke usiku womwe uno kuti ndithamangire Davide.
Derpå sagde Akitofel til Absalon; " Lad mig udvælge 12000 Mand og bryde op i Nat og sætte efter David.
2 Ndipo ndikamuthira nkhondo atatopa ndiponso atataya mtima. Ndikamuchititsa mantha ndipo anthu onse amene ali naye akathawa. Ine ndikakantha mfumu yokhayo,
Når jeg overfalder ham, medens han er udmattet og modfalden, kan jeg indjage ham Skræk, og alle hans Folk vil flygte, så at jeg kan fælde Kongen uden at røre nogen anden;
3 ndipo anthu onse ndidzabwera nawo kwa inu, ngati mkwati amene akubwerera kwa mwamuna wake. Imfa ya munthu mmodzi yekha idzakhalitsa anthu onse pa mtendere.”
så bringer jeg hele Folket tilbage til dig, som en Brud vender tilbage til sin Mand. Du attrår jo dog kun en enkelt Mands Liv, og hele Folket vil da være uskadt!"
4 Malangizo awa anaoneka abwino kwa Abisalomu ndi kwa akuluakulu onse a Israeli.
Det Forslag tiltalte Absalon og alle Israels Ældste.
5 Koma Abisalomu anati, “Muyitanenso Husai Mwariki kuti timve zimene iye adzanena.”
Men Absalon sagde: "Kald dog også Arkiten Husjaj hid, for at vi også kan høre, hvad han råder til!"
6 Husai atabwera kwa iye, Abisalomu anati, “Ahitofele wapereka malangizo ake. Kodi tichite zimene wanena? Ngati sichoncho, tiwuze maganizo ako.”
Da Husjaj kom ind, sagde Absalon til ham: "Det og det har Akitofel sagt; skal vi følge hans Råd? Hvis ikke, så sig du din Mening!"
7 Husai anayankha Abisalomu kuti, “Malangizo amene Ahitofele wapereka si abwino pa nthawi ino.
Husjaj svarede Absalon: "Denne Gang er Akitofels Råd ikke godt!"
8 Inu mukudziwa bwino abambo anu ali ndi ankhondo awo. Iwo ndi anthu ankhondo komanso ndi woopsa ngati chimbalangondo chimene chalandidwa ana ake. Kuwonjezera apa abambo anu ndi katswiri wa nkhondo. Iwo sanagone pamodzi ndi asilikali awo.
Og Husjaj sagde fremdeles: "Du ved, at din Fader og hans Mænd er Helte, og bitre i Hu er de som en Bjørn på Marken, hvem Ungerne er taget fra; desuden er din Fader en rigtig Kriger, som ikke lægger sig til Hvile om Natten med Folkene.
9 Onani, ngakhale tsopano lino abisala mʼphanga lina ku malo ena ake. Ngati iwo atayamba kuthira nkhondo asilikali anu, aliyense amene adzamve zimenezi adzati, ‘Gulu lalikulu lankhondo lotsatira Abisalomu laphedwa.’
For Øjeblikket holder han sig sikkert skjult i en Kløft eller et andet Sted; falder der nu straks i Begyndelsen nogle af Folkene, vil det rygtes, og man vil sige, at Absalons Tilhængere har lidt Nederlag;
10 Tsono ngakhale msilikali wolimba mtima kwambiri, amene mtima wake uli ngati wa mkango, adzagwidwa ndi mantha aakulu pakuti Aisraeli akudziwa kuti abambo anu ndi ankhondo ndipo kuti iwo amene ali nawo ndi anthu olimba mtima.
og da bliver selv den tapre, hvis Mod er som Løvens, forsagt; thi hele Israel ved, at din Fader er en Helt og hans Ledsagere tapre Mænd.
11 “Kotero ine ndikukulangizani kuti: Aisraeli onse, kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba; ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja, asonkhane kwa inu ndipo muwatsogolera kupita ku nkhondo.
Mit Råd er derfor: Lad hele Israel fra Dan til Be'ersjeba samles om dig, talrigt som Sandet ved Havet, og drag selv med i deres Midte.
12 Ndipo ife tidzapita kukamuthira nkhondo kulikonse kumene tikamupeze, ndipo ife tikamuthira nkhondo ngati mame pa nthaka. Palibe amene adzakhale wamoyo kaya iye kapena ankhondo ake.
Støder vi så på ham et eller andet Sted, hvor han nu befinder sig, kan vi falde over ham som Dug over Jorden, og der skal ikke blive en eneste tilbage, hverken han eller nogen af alle hans Mænd;
13 Iye akakathawira mu mzinda, Aisraeli onse adzabweretsa zingwe ku mzindawo, ndipo ife tidzawugwetsera ku chigwa mpaka sipadzapezeka ngakhale kachidutswa.”
men kaster han sig ind i en By, skal hele Israel lægge Reb om den, og vi vil slæbe den ned i Dalen, så der ikke bliver Sten på Sten tilbage af den!" Da sagde Absalon og alle Israels Mænd: "Arkiten Husjajs Råd er bedre end Akitofels!"
14 Abisalomu ndi ankhondo ena onse a Israeli anati, “Malangizo a Husai Mwariki ndi abwino kuposa a Ahitofele.” Pakuti Yehova anatsimikiza kutsutsa malangizo onse abwino a Ahitofele ndi cholinga choti zimuvute Abisalomu.
HERREN havde nemlig sat sig for at gøre Akitofels gode Råd til Skamme, for at HERREN kunde bringe Ulykke over Absalon.
15 Husai anawuza ansembe Zadoki ndi Abiatara kuti, “Ahitofele analangiza Abisalomu ndi akuluakulu a Israeli zakuti, koma ine ndawalangiza kuchita zakutizakuti.
Derpå sagde Husjaj til Præsterne Zadok og Ebjatar: "Det og det Råd har Akitofel givet Absalon og Israels Ældste, og det og det Råd har jeg givet.
16 Tsopano tumizani wamthenga msangamsanga kuti akamuwuze Davide kuti, ‘Musakagone powolokera Yorodani ku chipululu koma mukawoloke. Mukapanda kutero, mfumu ndi anthu onse amene ali naye adzaphedwa.’”
Skynd eder nu at sende Bud til David og bring ham det Bud: Bliv ikke Natten over ved vadestederne på Jordansletten, men søg over på den anden Side, for at ikke Kongen og alle hans Folk skal gå til Grunde!"
17 Yonatani ndi Ahimaazi amakhala ku Eni Rogeli. Tsono wantchito wamkazi ndiye amapita kukawawuza ndipo iwo amayenera kupita kukamuwuza mfumu Davide, pakuti iwowo sankayenera kuonekera polowa mu mzinda.
Jonatan og Ahima'az stod ved Rogelkilden, hvorhen en Tjenestepige til Stadighed kom og bragte dem Melding, hvorefter de gik hen og bragte Kong David Melding; thi de turde ikke vise sig i Byen.
18 Koma mnyamata wina anawaona ndipo anakawuza Abisalomu. Kotero anthu awiriwo anachoka mofulumira ndipo anapita ku nyumba ya munthu wina ku Bahurimu. Iye anali ndi chitsime ku mpanda kwake ndipo iwo analowamo.
Men en ung Mand opdagede dem og meldte det til Absalon; så skyndte de sig begge bort og kom ind hos en Mand i Bahurim. Han havde en Brønd i Gården, og i den steg de ned;
19 Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.
Konen tog et Tæppe, bredte det ud over Brønden og hældte Korn derpå, så at man intet kunde opdage.
20 Anthu a Abisalomu atafika kwa mkaziyo pa nyumbapo anafunsa kuti, “Kodi Ahimaazi ndi Yonatani ali kuti?” Mkaziyo anawayankha kuti, “Awoloka mtsinje.” Anthuwo anafunafuna koma sanapeze munthu, kotero anabwerera ku Yerusalemu.
Nu kom Absalons Folk imod i Huset til Konen og spurgte: "Hvor er Ahima'az og Jonatan?" Konen svarede: "De gik over Vandbækken!" Så søgte de efter dem, men da de ikke fandt dem, vendte de tilbage til Jerusalem.
21 Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”
Så snart de var gået bort, steg de to op af Brønden og gik hen og bragte Kong David Melding; og de sagde til David: "Bryd op og skynd eder over på den anden Side af Vandet; thi det og det Råd kom Akitofel med angående eder!"
22 Kotero Davide ndi anthu onse amene anali nawo ananyamuka ndi kuwoloka Yorodani. Pofika mmamawa, panalibe munthu amene anatsala asanawoloke Yorodani!
Da brød David op med alle sine Folk og satte over Jordan; og ved Daggry manglede ikke en eneste, alle var de kommet over Jordan.
23 Ahitofele ataona kuti malangizo ake sanatsatidwe, iye anakwera bulu wake napita ku mzinda wa kwawo ku nyumba yake. Iye anakonza mʼnyumba mwakemo ndi kudzimangirira. Kotero anafa nayikidwa mʼmanda a abambo ake.
Men da Akitofel så, at hans Råd ikke blev fulgt, sadlede han sit Æsel og drog hjem til sin By; og efter at have beskikket sit Hus hængte han sig og døde. Han blev jordet i sin Faders Grav.
24 Davide anapita ku Mahanaimu, ndipo Abisalomu anawoloka Yorodani pamodzi ndi ankhondo ena onse a Israeli.
David havde nået Mahanajim, da Absalon tillige med alle Israels Mænd gik over Jordan.
25 Abisalomu anasankha Amasa kukhala mkulu wa ankhondo mʼmalo mwa Yowabu. Amasa anali mwana wa munthu wotchedwa Itira Mwisraeli amene anakwatira Abigayeli mwana wa Nahasi mlongo wake wa Zeruya, amayi ake a Yowabu.
Absalon havde i Joabs Sted sat Amasa over Hæren; Amasa var Søn af en Ismaelit ved Navn Jitra, som var gået ind til Abigajil, en Datter af Isaj og Søster til Joabs Moder Zeruja.
26 Aisraeli ndi Abisalomu anamanga zithando mʼdziko la Giliyadi.
Og Israel og Absalon slog Lejr i Gilead.
27 Davide atafika ku Mahanaimu, Sobi mwana wa Nahasi wochokera ku Raba ku dziko la Amoni ndi Makiri mwana wa Amieli wochokera ku Lodebara, ndi Barizilai Mgiliyadi wochokera ku Rogelimu
Men da David kom til Mahaoajim, bragte Sjobi, Nahasj's Søn fra Rabba i Ammon, Makir, Ammiels Søn fra Lodebar, og Gileaditen Barzillaj fra Rogelim
28 anabweretsa zofunda, mabeseni ndi miphika. Iwo anabweretsanso kwa Davide ndi anthu ake zakudya izi: tirigu ndi barele, ufa ndi tirigu wokazinga, nyemba ndi mphodza,
Senge, Tæpper, Skåle og Lerkar; og Hvede, Byg, Mel, ristet Korn, Bønner, Linser,
29 uchi ndi chambiko, nkhosa ndi mafuta olimba a mkaka wangʼombe. Pakuti anati, “Anthuwa ali ndi njala ndipo atopa, alinso ndi ludzu muno mʼchipululu.”
Honning, Surmælk, Småkvæg og Komælksost bragte de David og hans Folk til Føde; thi de tænkte: "Folkene er sultne, udmattede og tørstige i Ørkenen."

< 2 Samueli 17 >