< 2 Samueli 17 >

1 Ahitofele anati kwa Abisalomu, “Mundilole ndisankhe asilikali 12,000, ndinyamuke usiku womwe uno kuti ndithamangire Davide.
Řekl ještě Achitofel Absolonovi: Nechť medle vyberu dvanácte tisíc mužů, abych vstana, honil Davida noci této.
2 Ndipo ndikamuthira nkhondo atatopa ndiponso atataya mtima. Ndikamuchititsa mantha ndipo anthu onse amene ali naye akathawa. Ine ndikakantha mfumu yokhayo,
A dostihna ho, dokudž jest ustalý a zemdlené má ruce, předěsím jej, a uteče všecken lid, kterýž jest s ním, i zamorduji krále samého.
3 ndipo anthu onse ndidzabwera nawo kwa inu, ngati mkwati amene akubwerera kwa mwamuna wake. Imfa ya munthu mmodzi yekha idzakhalitsa anthu onse pa mtendere.”
A tak obrátím všecken lid k tobě; nebo jako bych je všecky obrátil, když zhyne ten muž, kteréhož ty hledáš. O lid ty se nic nestarej.
4 Malangizo awa anaoneka abwino kwa Abisalomu ndi kwa akuluakulu onse a Israeli.
I líbila se ta řeč Absolonovi i všechněm starším Izraelským.
5 Koma Abisalomu anati, “Muyitanenso Husai Mwariki kuti timve zimene iye adzanena.”
A však řekl Absolon: Zavolej sem hned Chusai Architského, abychom slyšeli, co i on mluviti bude.
6 Husai atabwera kwa iye, Abisalomu anati, “Ahitofele wapereka malangizo ake. Kodi tichite zimene wanena? Ngati sichoncho, tiwuze maganizo ako.”
Když pak přišel Chusai k Absolonovi, mluvil k němu Absolon, řka: Takto mluvil Achitofel. Máme-li učiniti vedlé řeči jeho, čili nic? Pověz ty.
7 Husai anayankha Abisalomu kuti, “Malangizo amene Ahitofele wapereka si abwino pa nthawi ino.
Tedy řekl Chusai Absolonovi: Neníť dobrá rada, kterouž dal Achitofel nyní.
8 Inu mukudziwa bwino abambo anu ali ndi ankhondo awo. Iwo ndi anthu ankhondo komanso ndi woopsa ngati chimbalangondo chimene chalandidwa ana ake. Kuwonjezera apa abambo anu ndi katswiri wa nkhondo. Iwo sanagone pamodzi ndi asilikali awo.
Dále mluvil Chusai: Ty víš o otci svém i mužích jeho, že jsou udatní, k tomu zjitření na mysli, jako nedvědice osiřelá v poli. Nadto otec tvůj jest muž válečný, kterýž nebude nocovati s lidem.
9 Onani, ngakhale tsopano lino abisala mʼphanga lina ku malo ena ake. Ngati iwo atayamba kuthira nkhondo asilikali anu, aliyense amene adzamve zimenezi adzati, ‘Gulu lalikulu lankhondo lotsatira Abisalomu laphedwa.’
Nýbrž nyní spíše v záloze stojí v nějaké jeskyni, aneb v některém jiném místě. I stalo by se, jestliže by kteří padli z těch tvých při začátku, že každý, kdož by o tom uslyšel, řekl by: Stala se porážka v lidu, kterýž postoupil po Absolonovi.
10 Tsono ngakhale msilikali wolimba mtima kwambiri, amene mtima wake uli ngati wa mkango, adzagwidwa ndi mantha aakulu pakuti Aisraeli akudziwa kuti abambo anu ndi ankhondo ndipo kuti iwo amene ali nawo ndi anthu olimba mtima.
A tak by i silných reků srdce, kteréž jest jako srdce lva, škodlivě osláblo; nebo ví všecken Izrael, že jest zmužilý otec tvůj, a silní ti, kteříž jsou s ním.
11 “Kotero ine ndikukulangizani kuti: Aisraeli onse, kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba; ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja, asonkhane kwa inu ndipo muwatsogolera kupita ku nkhondo.
Ale radím, abys, shromáždě k sobě všecken Izrael od Dan až do Bersabé, kterýž v množství jest jako písek při moři, ty sám životně vytáhl k boji.
12 Ndipo ife tidzapita kukamuthira nkhondo kulikonse kumene tikamupeze, ndipo ife tikamuthira nkhondo ngati mame pa nthaka. Palibe amene adzakhale wamoyo kaya iye kapena ankhondo ake.
A tak potáhneme proti němu, na kterém by koli místě nalezen býti mohl, a připadneme na něj, jako padá rosa na zemi; i nepozůstaneť z něho, totiž ze všech mužů, kteříž jsou při něm, ani jednoho.
13 Iye akakathawira mu mzinda, Aisraeli onse adzabweretsa zingwe ku mzindawo, ndipo ife tidzawugwetsera ku chigwa mpaka sipadzapezeka ngakhale kachidutswa.”
Jestliže by se pak shrnul do města, snesou všecken lid Izraelský k tomu městu provazy, a vtrhneme je až do potoka, tak aby tam ani kaménka nebylo lze najíti.
14 Abisalomu ndi ankhondo ena onse a Israeli anati, “Malangizo a Husai Mwariki ndi abwino kuposa a Ahitofele.” Pakuti Yehova anatsimikiza kutsutsa malangizo onse abwino a Ahitofele ndi cholinga choti zimuvute Abisalomu.
I řekl Absolon a všickni muži Izraelští: Lepšíť jest rada Chusai Architského, než rada Achitofelova. Hospodin zajisté to způsobil, aby zrušena byla rada Achitofelova, kteráž sic dobrá byla, aby tak uvedl Hospodin na Absolona zlé věci.
15 Husai anawuza ansembe Zadoki ndi Abiatara kuti, “Ahitofele analangiza Abisalomu ndi akuluakulu a Israeli zakuti, koma ine ndawalangiza kuchita zakutizakuti.
Oznámil pak to Chusai Sádochovi a Abiatarovi kněžím: Tak a tak radil Achitofel Absolonovi a starším Izraelským, ale já takto a takto jsem radil.
16 Tsopano tumizani wamthenga msangamsanga kuti akamuwuze Davide kuti, ‘Musakagone powolokera Yorodani ku chipululu koma mukawoloke. Mukapanda kutero, mfumu ndi anthu onse amene ali naye adzaphedwa.’”
Nyní tedy pošlete rychle a oznamte Davidovi, řkouce: Nezůstavej přes noc na rovinách pouště, ale přeprav se bez meškání, aby snad nebyl sehlcen král i všecken lid, kterýž jest s ním.
17 Yonatani ndi Ahimaazi amakhala ku Eni Rogeli. Tsono wantchito wamkazi ndiye amapita kukawawuza ndipo iwo amayenera kupita kukamuwuza mfumu Davide, pakuti iwowo sankayenera kuonekera polowa mu mzinda.
Jonata pak a Achimaas stáli u studnice Rogel. I šla tam děvečka a pověděla jim, aby oni jdouce, oznámili to králi Davidovi; nebo nesměli se ukázati aneb vjíti do města.
18 Koma mnyamata wina anawaona ndipo anakawuza Abisalomu. Kotero anthu awiriwo anachoka mofulumira ndipo anapita ku nyumba ya munthu wina ku Bahurimu. Iye anali ndi chitsime ku mpanda kwake ndipo iwo analowamo.
A však uzřel je služebník, a oznámil Absolonovi. Pročež odšedše oba rychle, vešli do domu muže v Bahurim, kterýž měl studnici na dvoře svém. I spustili se do ní.
19 Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.
A žena vzavši plachtu, rozestřela ji na vrch studnice, a nasypala na ni krup. A tak nebyla ta věc spatřína.
20 Anthu a Abisalomu atafika kwa mkaziyo pa nyumbapo anafunsa kuti, “Kodi Ahimaazi ndi Yonatani ali kuti?” Mkaziyo anawayankha kuti, “Awoloka mtsinje.” Anthuwo anafunafuna koma sanapeze munthu, kotero anabwerera ku Yerusalemu.
Nebo když přišli služebníci Absolonovi k ženě do domu a řekli: Kde jest Achimaas a Jonata? odpověděla jim žena: Přešliť jsou ten potok. Hledavše tedy a nic nenalezše, navrátili se do Jeruzaléma.
21 Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”
A když oni odešli, tito vystoupivše z studnice, šli a oznámili králi Davidovi a řekli jemu: Vstaňte a přepravte se rychle přes vodu, nebo toto radil proti vám Achitofel.
22 Kotero Davide ndi anthu onse amene anali nawo ananyamuka ndi kuwoloka Yorodani. Pofika mmamawa, panalibe munthu amene anatsala asanawoloke Yorodani!
Protož vstav David a všecken lid, kterýž byl s ním, přepravili se přes Jordán, prvé než se rozednilo; a nezůstal ani jeden, ješto by se nepřepravil přes Jordán.
23 Ahitofele ataona kuti malangizo ake sanatsatidwe, iye anakwera bulu wake napita ku mzinda wa kwawo ku nyumba yake. Iye anakonza mʼnyumba mwakemo ndi kudzimangirira. Kotero anafa nayikidwa mʼmanda a abambo ake.
Tedy Achitofel vida, že se nestalo vedlé rady jeho, osedlal osla, a vstav, odjel do domu svého, do města svého. A učiniv pořízení v čeledi své, oběsil se a umřel; i pochován jest v hrobě otce svého.
24 Davide anapita ku Mahanaimu, ndipo Abisalomu anawoloka Yorodani pamodzi ndi ankhondo ena onse a Israeli.
David pak byl již přišel do Mahanaim, když se Absolon přepravil přes Jordán, on i všecken lid Izraelský s ním.
25 Abisalomu anasankha Amasa kukhala mkulu wa ankhondo mʼmalo mwa Yowabu. Amasa anali mwana wa munthu wotchedwa Itira Mwisraeli amene anakwatira Abigayeli mwana wa Nahasi mlongo wake wa Zeruya, amayi ake a Yowabu.
A tu ustanovil Absolon Amazu místo Joába nad vojskem. (Byl pak Amaza syn muže, jehož jméno bylo Jetra Izraelský, kterýž všel k Abigail dceři Náchas, sestře Sarvie matky Joábovy.)
26 Aisraeli ndi Abisalomu anamanga zithando mʼdziko la Giliyadi.
I položil se Izrael a Absolon v zemi Galád.
27 Davide atafika ku Mahanaimu, Sobi mwana wa Nahasi wochokera ku Raba ku dziko la Amoni ndi Makiri mwana wa Amieli wochokera ku Lodebara, ndi Barizilai Mgiliyadi wochokera ku Rogelimu
Stalo se pak, když přišel David do Mahanaim, že Sobi syn Náchas z Rabbat synů Ammon, a Machir syn Amielův z Lodebar, a Barzillai Galádský z Rogelim,
28 anabweretsa zofunda, mabeseni ndi miphika. Iwo anabweretsanso kwa Davide ndi anthu ake zakudya izi: tirigu ndi barele, ufa ndi tirigu wokazinga, nyemba ndi mphodza,
Lůže, číše a nádoby hliněné, též pšenice, ječmene, mouky, krup, bobu, šocovice a pražmy,
29 uchi ndi chambiko, nkhosa ndi mafuta olimba a mkaka wangʼombe. Pakuti anati, “Anthuwa ali ndi njala ndipo atopa, alinso ndi ludzu muno mʼchipululu.”
Ano i medu, másla a ovcí i syrů kravských přinesli Davidovi a lidu, kterýž s ním byl, aby jedli. Nebo řekli: Lid ten jest hladovitý a ustalý, i žíznivý na té poušti.

< 2 Samueli 17 >