< 2 Samueli 17 >

1 Ahitofele anati kwa Abisalomu, “Mundilole ndisankhe asilikali 12,000, ndinyamuke usiku womwe uno kuti ndithamangire Davide.
Ахитофел каза още на Авесалома: Да избера сега дванадесет хиляди мъже, и да стана да преследвам Давида още тая нощ.
2 Ndipo ndikamuthira nkhondo atatopa ndiponso atataya mtima. Ndikamuchititsa mantha ndipo anthu onse amene ali naye akathawa. Ine ndikakantha mfumu yokhayo,
Ще налетя върху него като е уморен и ръцете му ослабнали, и ще го уплаша; и всичките люде, що са с него, ще побягнат, и ще поразя само царя.
3 ndipo anthu onse ndidzabwera nawo kwa inu, ngati mkwati amene akubwerera kwa mwamuna wake. Imfa ya munthu mmodzi yekha idzakhalitsa anthu onse pa mtendere.”
Така ще възвърна всичките люде към тебе, защото убиването на мъжа, когото ти търсиш, значи възвръщането на всичките; всичките люде ще се помирят.
4 Malangizo awa anaoneka abwino kwa Abisalomu ndi kwa akuluakulu onse a Israeli.
И тая дума бе угодна на Авесалома и на всичките Израилеви старейшини.
5 Koma Abisalomu anati, “Muyitanenso Husai Mwariki kuti timve zimene iye adzanena.”
Тогава рече Авесолом: Повикай сега и архиеца Хусай, и нека чуем какво ще каже и той.
6 Husai atabwera kwa iye, Abisalomu anati, “Ahitofele wapereka malangizo ake. Kodi tichite zimene wanena? Ngati sichoncho, tiwuze maganizo ako.”
И когато Хусей влезе при Авесалома, Авесалом му говори, казвайки: Така е говорил Ахитофел. Да постъпим ли според неговия съвет? ако не, говори ти.
7 Husai anayankha Abisalomu kuti, “Malangizo amene Ahitofele wapereka si abwino pa nthawi ino.
И Хусей каза на Авесалома: Не е добър съветът, който Ахитофел даде тоя път.
8 Inu mukudziwa bwino abambo anu ali ndi ankhondo awo. Iwo ndi anthu ankhondo komanso ndi woopsa ngati chimbalangondo chimene chalandidwa ana ake. Kuwonjezera apa abambo anu ndi katswiri wa nkhondo. Iwo sanagone pamodzi ndi asilikali awo.
Хусей рече още: Ти знаеш баща си и неговите мъже, че са силни мъже, и че са преогорчени в душа, както мечка лишена от малките си в полето; и баща ти, като военен мъж, няма да пренощува с людете;
9 Onani, ngakhale tsopano lino abisala mʼphanga lina ku malo ena ake. Ngati iwo atayamba kuthira nkhondo asilikali anu, aliyense amene adzamve zimenezi adzati, ‘Gulu lalikulu lankhondo lotsatira Abisalomu laphedwa.’
ето, сега скрит в някой трап или в някое друго място, и когато нападне някой от тия свои люде в началото на сражението, всеки, който чуе ще рече: Поражение става между людете, които следват Авесалома.
10 Tsono ngakhale msilikali wolimba mtima kwambiri, amene mtima wake uli ngati wa mkango, adzagwidwa ndi mantha aakulu pakuti Aisraeli akudziwa kuti abambo anu ndi ankhondo ndipo kuti iwo amene ali nawo ndi anthu olimba mtima.
Тогава даже юначният, чието сърце е като лъвско сърце, съвсем ще премре; защото целият Израил знаеше, че баща ти е юнак, и че ония, които са с него, са храбри мъже.
11 “Kotero ine ndikukulangizani kuti: Aisraeli onse, kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba; ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja, asonkhane kwa inu ndipo muwatsogolera kupita ku nkhondo.
Аз съветвам по-добре да се събере при тебе целият Израил, от Дан до Вирсавее, по множество както пясъка край морето, и ти лично да идеш в боя.
12 Ndipo ife tidzapita kukamuthira nkhondo kulikonse kumene tikamupeze, ndipo ife tikamuthira nkhondo ngati mame pa nthaka. Palibe amene adzakhale wamoyo kaya iye kapena ankhondo ake.
Така ще налетим върху него в някое място, където се намери, и ще го нападнем, както пада росата на земята, тъй щото от него и от всичките човеци, които са с него, няма да оставим ни един.
13 Iye akakathawira mu mzinda, Aisraeli onse adzabweretsa zingwe ku mzindawo, ndipo ife tidzawugwetsera ku chigwa mpaka sipadzapezeka ngakhale kachidutswa.”
Или, ако прибегне в някой град, тогава целият Израил ще донесе до оня град въжета, та ще го завлечем до потока, тъй щото да не остане там ни едно камъче.
14 Abisalomu ndi ankhondo ena onse a Israeli anati, “Malangizo a Husai Mwariki ndi abwino kuposa a Ahitofele.” Pakuti Yehova anatsimikiza kutsutsa malangizo onse abwino a Ahitofele ndi cholinga choti zimuvute Abisalomu.
Тогава Авесалом и всичките Израилеви мъже казаха: Съветът на архиеца Хусей е по-добър от съвета на Ахитофела. (Защото Господ беше рекъл да осуети добрия Ахитофелов съвет, за да нанесе Господ зло на Авесалома).
15 Husai anawuza ansembe Zadoki ndi Abiatara kuti, “Ahitofele analangiza Abisalomu ndi akuluakulu a Israeli zakuti, koma ine ndawalangiza kuchita zakutizakuti.
Тогава Хусей каза на свещениците Садоха и Авиатара: Така и така съветва Ахитофел Авесалома и Израилевите старейшини; а така и така съветвах аз.
16 Tsopano tumizani wamthenga msangamsanga kuti akamuwuze Davide kuti, ‘Musakagone powolokera Yorodani ku chipululu koma mukawoloke. Mukapanda kutero, mfumu ndi anthu onse amene ali naye adzaphedwa.’”
Сега, прочее, пратете скоро да известят на Давида, казвайки: Не оставай тая нощ при бродовете в пустинята, но непременно да преминеш Иордан, за да не погинат царят и всичките люде, които са с него.
17 Yonatani ndi Ahimaazi amakhala ku Eni Rogeli. Tsono wantchito wamkazi ndiye amapita kukawawuza ndipo iwo amayenera kupita kukamuwuza mfumu Davide, pakuti iwowo sankayenera kuonekera polowa mu mzinda.
А Иоанатан и Ахимаас стояха при извора Рогил, защото не смееха да влизат явно в града: затова, една слугиня отиде да им извести това, и те отидоха та известиха на цар Давида.
18 Koma mnyamata wina anawaona ndipo anakawuza Abisalomu. Kotero anthu awiriwo anachoka mofulumira ndipo anapita ku nyumba ya munthu wina ku Bahurimu. Iye anali ndi chitsime ku mpanda kwake ndipo iwo analowamo.
А един момък ги видя и обади на Авесалома; но двамата отидоха бърже та влязоха в къщата на един човек във Ваурим, който имаше кладенец в двора си, и спуснаха се в него.
19 Mkazi wake anatenga chophimba ndipo anachiyika pamwamba pa chitsimecho nawazapo tirigu. Palibe amene anadziwa chilichonse za izi.
И жена му взе една покривка та я простря върху отвора на кладенеца, и насипа върху нея чукано жито, така щото нищо не се позна.
20 Anthu a Abisalomu atafika kwa mkaziyo pa nyumbapo anafunsa kuti, “Kodi Ahimaazi ndi Yonatani ali kuti?” Mkaziyo anawayankha kuti, “Awoloka mtsinje.” Anthuwo anafunafuna koma sanapeze munthu, kotero anabwerera ku Yerusalemu.
И когато Авесаломовите слуги дойдоха при жената в къщата и казаха: Где са Ахимаас и Ионатан? Жената им рече: Преминах водния поток. И те ги потърсиха, но като не ги намериха, върнаха се в Ерусалим.
21 Anthu aja atapita, awiriwo anatuluka mʼchitsimemo ndipo anapita kukawuza mfumu Davide nati kwa iye, “Nyamukani, muwoloke mtsinje msangamsanga. Ahitofele wapereka malangizo akutiakuti kutsutsana nanu.”
А след заминаването им, ония излязоха от кладенеца и отидоха та известиха на цар Давида. Рекоха на Давида: Станете преминете скоро водата, защото Ахитофел така съветва против вас.
22 Kotero Davide ndi anthu onse amene anali nawo ananyamuka ndi kuwoloka Yorodani. Pofika mmamawa, panalibe munthu amene anatsala asanawoloke Yorodani!
Тогава Давид и всичките люде, що бяха с него, станаха та преминаха Иордан; до зори не остана ни един, който не беше преминал Иордан.
23 Ahitofele ataona kuti malangizo ake sanatsatidwe, iye anakwera bulu wake napita ku mzinda wa kwawo ku nyumba yake. Iye anakonza mʼnyumba mwakemo ndi kudzimangirira. Kotero anafa nayikidwa mʼmanda a abambo ake.
А Ахитофел, като видя, че съветът му не се възприе, оседла осела си и стана та отиде у дома си, в своя град; и като нареди домашните си работи, обеси се. Така умря; и погребан бе в бащиния си гроб.
24 Davide anapita ku Mahanaimu, ndipo Abisalomu anawoloka Yorodani pamodzi ndi ankhondo ena onse a Israeli.
Тогава Давид дойде в Механаим; а Авесалом премина Иордан, той и всичките Израилеви мъже с него.
25 Abisalomu anasankha Amasa kukhala mkulu wa ankhondo mʼmalo mwa Yowabu. Amasa anali mwana wa munthu wotchedwa Itira Mwisraeli amene anakwatira Abigayeli mwana wa Nahasi mlongo wake wa Zeruya, amayi ake a Yowabu.
И Авесалом постави Амаса за военачалник вместо Иоава. А Амаса бе син на един човек на име Итра, израилтянин, който беше влязъл при Авигея Наасовата дъщеря, сестра на Саруия Иоавовата майка).
26 Aisraeli ndi Abisalomu anamanga zithando mʼdziko la Giliyadi.
И Израил и Авесалом разположиха стана си в галаадската земя.
27 Davide atafika ku Mahanaimu, Sobi mwana wa Nahasi wochokera ku Raba ku dziko la Amoni ndi Makiri mwana wa Amieli wochokera ku Lodebara, ndi Barizilai Mgiliyadi wochokera ku Rogelimu
А когато дойде Давид в Маханаим, Совей Наасовият син, от Рава на амонците, и Махир Амииловият син, от Ло-девар, и галаадецът Верзелай, от Рогелим,
28 anabweretsa zofunda, mabeseni ndi miphika. Iwo anabweretsanso kwa Davide ndi anthu ake zakudya izi: tirigu ndi barele, ufa ndi tirigu wokazinga, nyemba ndi mphodza,
донесоха постелки, легени и пръстени съдове, жито, ечемик, брашно, пържено жито, боб, леща и други печени храни,
29 uchi ndi chambiko, nkhosa ndi mafuta olimba a mkaka wangʼombe. Pakuti anati, “Anthuwa ali ndi njala ndipo atopa, alinso ndi ludzu muno mʼchipululu.”
мед, масло, овци и говеждо сирене на Давида и на людете с него за да ядат; защото рекоха: Людете са гладни и изнемощели и жадни в пустинята.

< 2 Samueli 17 >