< 2 Samueli 16 >

1 Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.
Kwathi uDavida esehambe ibanga elifitshane ngale kwenqongo, wabona uZibha, isikhonzi sikaMefibhoshethi, elindele ukumhlangabeza, elodwendwe lwabobabhemi ababotshelwe izihlalo bethwele izinkwa ezingamakhulu amabili, ikhulu lamakhekhe ezithelo ezonyisiweyo, ikhulu lamakhekhe omkhiwa kanye lomgodla wewayini.
2 Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?” Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”
Inkosi yabuza uZibha yathi, “Ukuletheleni lokhu na?” UZibha waphendula wathi, “Obabhemi ngabendlu yenkosi ukuba bagade, izinkwa lezithelo ngokwabantu ukuba badle, iwayini ngelokuqaqabula labo abaphela amandla enkangala.”
3 Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?” Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’”
Inkosi yasibuza yathi, “Indodana yendodana yenkosi yakho ingaphi na?” UZibha wathi kuyo, “Ihlezi eJerusalema, ngoba icabanga ithi, ‘Lamhla indlu ka-Israyeli izangibuyisela umbuso kababamkhulu.’”
4 Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.” Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”
Inkosi yasisithi kuZibha, “Konke okwakungokuka Mefibhoshethi khathesi sekungokwakho.” UZibha wathi, “Ngikhothama ngokuzithoba. Sengathi ngingathola umusa emehlweni akho mhlekazi wami, nkosi.”
5 Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera.
Kwathi Inkosi uDavida efika eBhahurimi, umuntu wosendo lunye labendlu kaSawuli, waphuma evela lapho. Ibizo lakhe lalinguShimeyi indodana kaGera, njalo waphuma esethuka.
6 Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake.
Wajikijela uDavida lezikhulu zonke zenkosi ngamatshe, lanxa amabutho wonke labalindi abakhethiweyo babengakwesokudla lakwesokhohlo kukaDavida.
7 Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe!
Ekuthukeni kwakhe uShimeyi wathi, “Phuma, phuma, wena wegazi, wena sixhwali!
8 Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”
UThixo usephindisele kuwe ngenxa yegazi lonke owalichithayo kwabendlu kaSawuli, wena osubusa esikhundleni sakhe. UThixo umbuso usewunike indodana yakho u-Abhisalomu. Wena usudilikile ngoba ungumuntu wegazi!”
9 Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”
Lapho-ke u-Abhishayi indodana kaZeruya wathi enkosini, “Kungani inja efileyo le ithuka inkosi yami? Ngivumelani ngiyequma ikhanda layo.”
10 Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’”
Kodwa inkosi yathi, “Kuyini okulihlanganisa lami, lina madodana kaZeruya? Nxa ethuka ngenxa yokuthi uThixo uthe kuye, ‘Mthuke uDavida,’ ngubani ongabuza ukuthi, ‘Lokhu ukwenzelani na?’”
11 Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero.
UDavida wasesithi ku-Abhishayi lakuzo zonke izikhulu zakhe, “Indodana yami, eyinyama yami, izama ukungibulala. Pho umBhenjamini lo-ke! Myekeleni enjalo; yekelani athuke, ngoba uThixo umtshele ukuba enze njalo.
12 Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”
Engxenye uThixo uzalubona usizi lwami angibuyisele okuhle ngenxa yokuthukwa engikwenziwayo lamhla.”
13 Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi.
Ngakho uDavida labantu bonke waqhubeka elandela umgwaqo uShimeyi yena ehamba eyame intaba maqondana laye, ehamba elokhu ethuka njalo emjikijela ngamatshe emthela langengcekeza.
14 Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.
Inkosi labantu bayo bafika lapho ababesiya khona sebediniwe. Kulapho abaphumula khona.
15 Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye.
Ngalesosikhathi, u-Abhisalomu labantu bonke bako-Israyeli bafika eJerusalema, lo-Ahithofeli wayelaye.
16 Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
Lapho-ke uHushayi umʼArikhi, umngane kaDavida, waya ku-Abhisalomu wathi kuye, “Impilo ende nkosi! Impilo ende nkosi!”
17 Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”
U-Abhisalomu wabuza uHushayi wathi, “Lolu yilo uthando olutshengisa umngane wakho na? Kungani ungahambanga lomngane wakho na?”
18 Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse.
UHushayi wathi ku-Abhisalomu, “Hayi, lowo okhethwe nguThixo, langabantu laba, labantu bonke bako-Israyeli ngizakuba ngowakhe, njalo ngizahlala laye.
19 Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”
Phezu kwalokho, ngubani engingamkhonza na? Akumelanga ngikhonze indodana na? Njengoba ngakhonza uyihlo, kanjalo ngizakukhonza.”
20 Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”
U-Abhisalomu wasesithi ku-Ahithofeli, “Ake useluleke. Kuyini esingakwenza na?”
21 Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.”
U-Ahithofeli waphendula wathi, “Lala labafazi bakayihlo abaseceleni abatshiya belinde isigodlo. Lapho-ke u-Israyeli wonke uzakuzwa ukuthi wena usuzenze waba liphunga elibi emakhaleni kayihlo, njalo izandla zabantu bonke abalawe zizaqiniswa.”
22 Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.
Ngakho u-Abhisalomu bamisela ithente phezu kophahla lwendlu, walala labafazi bakayise beceleni u-Israyeli wonke ekhangele.
23 Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.
Ngalezonsuku iseluleko sika-Ahithofeli, sasifana lesalowo obuze uNkulunkulu. Lokho kwaba yiyo indlela uDavida lo-Abhisalomu abakhangela ngayo zonke izeluleko zika-Ahithofeli.

< 2 Samueli 16 >