< 2 Samueli 16 >

1 Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.
Da David var kommet lidt på den anden Side af Bjergets Top, Kom Mefibosjets Tjener Ziba ham i Møde med et Par opsadlede Æsler, som bar 200 Brød, 100 Rosinkager, 100 Frugter og en Dunk Vin.
2 Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?” Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”
Da sagde Kongen til Ziba: "Hvad vil du med det?" Og Ziba svarede: "Æslerne er bestemt til Ridedyr for Kongens Hus, Brødene og Frugterne til Spise for Folkene og Vinen til Drikke for dem, der bliver trætte i Ørkenen!"
3 Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?” Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’”
Så sagde Kongen: '"Hvor er din Herres Søn?" Ziba svarede Kongen: "Han blev i Jerusalem; thi han tænkte: Nu vil Israels Hus give mig min Faders Kongedømme tilbage!"
4 Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.” Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”
Da sagde Kongen til Ziba: "Dig skal hele Mefibosjets Ejendom tilhøre!" Og Ziba sagde: "Jeg bøjer mig dybt! Måtte jeg finde Nåde for min Herre Kongens Øjne!"
5 Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera.
Men da Kong David kom til Bahurim, se, da kom en Mand ved Navn Simei, Geras Søn, af samme Slægt som Sauls Hus, gående ud af Byen, alt imedens han udstødte Forbandelser,
6 Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake.
og han kastede Sten efter David og alle Kong Davids Folk, skønt alle Krigerne og alle Kærnetropperne gik på begge Sider af ham.
7 Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe!
Og Simei forbandede ham med de Ord: "Bort, bort med dig, din Blodhund, din Usling!
8 Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”
HERREN har nu bragt alt Sauls Hus's Blod over dig, han, i hvis Sted du blev Konge, og HERREN har nu givet din Søn Absalon Kongedømmet; nu har Ulykken ramt dig. for, i du er en Blodhund!"
9 Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”
Da sagde Abisjaj, Zerujas Søn, til Kongen: "Hvorfor skal den døde Hund have Lov at forbande min Herre Kongen? Lad mig gå hen og hugge Hovedet af ham!"
10 Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’”
Men Kongen svarede: "Hvad har jeg med eder at gøre, Zerujasønner! Når han forbander, og når HERREN har budt ham at forbande David, hvem tør da sige: Hvorfor gør du det?"
11 Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero.
Og David sagde til Abisjaj og alle sine Folk: "Når min egen Søn, som er udgået af min Lænd, står mig efter Livet, hvad kan man da ikke vente af denne Benjaminit! Lad ham kun forbande, når HERREN har budt ham det!
12 Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”
Måske vil HERREN se til mig i min Nød og gøre mig godt til Gengæld for hans Forbandelse i Dag!"
13 Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi.
Derpå gik David med sine Mænd hen ad Vejen, medens Simei fulgte ham oppe på Bjergskråningen og stadig udstødte Forbandelser, slog med Sten og kastede Støv efter ham.
14 Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.
Således kom Kongen og alle Krigerne, som fulgte ham, udmattede til Jordan og hvilede ud der.
15 Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye.
Imidlertid var Absalon draget ind i Jerusalem med alle Israels Mænd, og Akitofel var hos ham.
16 Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
Da nu Arkiten Husjaj, Davids Ven, kom til Absalon, sagde han til ham: "Kongen leve, Kongen leve!"
17 Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”
Absalon sagde til Husjaj: "Er det sådan, du viser din Ven Godhed? Hvorfor fulgte du ikke din Ven?"
18 Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse.
Husjaj svarede Absalon: "Nej, den, som HERREN og dette Folk og alle Israels Mænd har valgt, i hans Tjeneste vil jeg træde, og hos ham vil jeg blive!
19 Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”
Og desuden: Hvem er det, jeg tjener? Mon ikke hans Søn? Som jeg har tjent din Fader, vil jeg tjene dig!"
20 Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”
Absalon sagde så til Akitofel: "Kom med eders Råd! Hvad skal vi gøre?"
21 Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.”
Akitofel svarede Absalon: "Gå ind til din Faders Medhustruer, som han har ladet blive tilbage for at se efter Huset; så kan hele Israel skønne, at du har lagt dig for Had hos din Fader, og alle de, der har sluttet sig til dig, vil få nyt Mod!"
22 Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.
Absalons Telt blev så rejst på Taget, og Absalon gik ind til sin Faders Medhustruer i hele Israels Påsyn.
23 Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.
Det Råd, Akitofel gav i de Tider, gjaldt nemlig lige så meget, som når man adspurgte Gud; så meget gjaldt ethvert Råd af Akitofel både hos David og Absalon.

< 2 Samueli 16 >