< 2 Samueli 15 >

1 Patapita nthawi, Abisalomu anadzipezera galeta ndi akavalo pamodzi ndi amuna makumi asanu amene amathamanga patsogolo pake.
Sabara gah ılğevç'uyle qiyğa, Avşalomee cus dəv'əyn daşk'a, balkanar, xhots'al cune ögil g'adaxhvanasda insan t'abal ha'a.
2 Iye amadzuka mmamawa ndi kuyima pa njira yopita ku chipata cha mzinda. Munthu wina aliyense akakhala ndi zodandaula zopita nazo kwa mfumu kuti akaweruze, Abisalomu amamuyitana iye ndi kumufunsa kuti, “Kodi ukuchokera ku limodzi mwa mafuko a Israeli?”
Mana miç'eer çakra suğots'u, şaharne akkabışisqa əlyhəəne yəqqəniy ulyoyzarna. Mançe cone yı'q'nee gipxhına gaf paççahee məhkama alğehecenva vüqqən insanar ı'lğəəmee, mang'vee manbı cusqa qopt'ul, qiyghan ıxha: – Ğu nene şahareençene? Mane insaneeyid alidghıniy qele ıxha, vuc sa neneme İzrailyne nasıleençena vorna.
3 Kenaka Abisalomu amanena kwa iye kuti, “Taona, madandawulo ako ndi abwino ndi oyenera, koma palibe woyimira mfumu woti akumvere.”
Avşalomee mane insanık'le inəxüd eyhe ıxha: – Yiğna iş yugnab, qopkunab vuxheeyib, paççahısnee val k'ırı alixhxhesda insan deşda.
4 Ndipo Abisalomu amawonjezera kunena kuti, “Ine ndikanangosankhidwa kukhala woweruza mʼdziko muno bwenzi munthu aliyense amene ali ndi madandawulo kapena milandu akubwera kwa ine ndipo ndikanaonetsetsa kuti chilungamo chachitika.”
Avşalomee meed eyhe ıxha: – İne ölkayna haakim zıcarxhiy hı'ına. Manke zı, vuşuyiy zasqa məhkamee he'eva arı, mang'une işiqa qorkuraniy ilyakkas.
5 Ndipo nthawi zonse amati munthu akasendera pafupi ndi kumugwandira, Abisalomu amatambalitsa dzanja lake, kumuyimiritsa munthuyo ndi kupsompsona.
Vuşumecar k'yozarasva Avşalomusqa qexhemee, mang'vee xıl hotku, mana insan cusqa ts'ıts'ı'ı, ubba ha'a ıxha.
6 Abisalomu amachitira izi Aisraeli onse amene amabwera kwa mfumu kuti adzaweruzidwe ndipo Abisalomuyo anagwira mtima anthu a mu Israeli.
Avşalomee məxüd paççahısqa məhkama ha'asva vüqqəne gırgıne İzrailybışikcad ha'a ıxha. Məxüb mang'vee İzrailybı culqa saa'a vuxha.
7 Patapita zaka zinayi Abisalomu anati kwa mfumu, “Loleni ndipite ku Hebroni kuti ndikakwaniritse lonjezo limene ndinachita kwa Yehova.
Yoq'ulle sen ılğeç'uyle qiyğa, Avşalomee paççahık'le eyhen: – Hucoona ixhes, hasre zı Xevronqa hark'ın, Rəbbis cuvab huvuyn kar ha'as.
8 Pamene mtumiki wanu amakhala ku Gesuri ku Aramu, anachita lonjezo ili: ‘Ngati Yehova adzandibweretsadi ku Yerusalemu, ndidzapembedza Yehovayo mu Hebroni.’”
Zı, yiğna nukar, Aramne cigabışeene Geşurne şaharee axvamee, k'ınniy g'assır: «Rəbbee zı İyerusalimqa sak'al he'ee, zı Mang'us ı'bəədat ha'as Xevronqa ı'qqəs».
9 Mfumu inati kwa iye, “Pita mu mtendere” Kotero iye anapita ku Hebroni.
Paççahee mang'uk'le «Yugna yəq vuxhenava» eyhe. Avşalomur Xevronqa ayk'an.
10 Ndipo Abisalomu anatuma amithenga ake mwamseri kwa mafuko onse a Israeli kukanena kuti, “Mukangomva kulira kwa malipenga pamenepo munene kuti, ‘Abisalomu ndiye mfumu mu Hebroni.’”
Avşalomee dyugulenba gırgıne İzrailyne nasılbışeeqa cun insanar g'axuvu, maabınbışik'le eyhen: – Gaçeençe qı'ğəəne süttyun ses g'ayxhımee, «Avşalom Xevron paççah ıxhava» eyhe.
11 Anthu 200 ochokera mu Yerusalemu anapita naye Abisalomu. Iwo anayitanidwa monga alendo ndipo anapita osadziwa chilichonse pa nkhaniyi.
İyerusalimğançe Avşalomuka sacigee q'öd vəş insan ayk'an. Manbı məttıne yik'eka mang'uqab qihna əlyhəə vuxha. Manbışis nişikecab xabar vuxha deş.
12 Pamene Abisalomu amapereka nsembe, iye anayitanitsanso Ahitofele Mgiloni, mlangizi wa Davide, wa ku Gilo, kotero kuwukiraku kunakula kwambiri, ndipo anthu otsatira Abisalomu anapitirira kuchuluka.
Avşalomee q'urbanbı allya'amee, mang'vee Davudna muşaavir Giloonçena Axitofel cune şahareençe, Giloonçe, cusqa qoyt'al. Avşalomne suralqa ı'lğəənbı yiğ-yiğıle geeb qeebaxhe vuxha. Manbışis Davudne yı'q'əle qeepxhes vukkan vuxha.
13 Munthu wina anabweretsa uthenga ndi kudzamuwuza Davide kuti, “Mitima ya Aisraeli onse ili pa Abisalomu.”
Sa insan Davudusqa arı, mang'uk'le eyhen: – İzrailybışin yik'bı Avşalomulqa vod satk'ıl.
14 Ndipo Davide anati kwa akuluakulu ake amene anali mu Yerusalemu. “Bwerani! Tiyeni tithawe, mwina palibe adzapulumuke kwa Abisalomu. Tiyeni tichoke msanga, mwina iye adzabwera msanga ndi kutipitirira, nʼkuwononga ife ndi mzinda wathu ndi lupanga.”
Davudee İyerusalimeene cune gırgıne insanaaşik'le eyhen: – İnçe heepxas! Deşxheene, Avşalomne xılençe yişde neng'ussecar g'attixhanas əxəs deş. Zaraba vuxhe əlyhəəs. Deşxheene, mana şaka avarq'ıl, yişde vuk'lelqa yiğbı exas, şaharıb g'ılıncike alğaahas.
15 Akuluakulu a mfumu anamuyankha kuti, “Antchito anu ndi okonzeka kuchita chilichonse chimene mbuye wathu mfumu mukufuna kuchita.”
Paççahne insanaaşe eyhen: – Şi yiğın nukarar vob, hasre ğu, yişde xərıng'vee, eyhen ixhecen.
16 Mfumu inanyamuka pamodzi ndi banja lake lonse. Koma iye anasiya azikazi khumi kuti azisamalira nyumba yaufumu.
Paççahıqab qihna mang'un gırgın xaabınbı qığeebaç'enbı. Mang'vee saccu yits'ıyre caariye xaaqa ilyaakasva g'alyaa'a.
17 Kotero mfumu inanyamuka pamodzi ndi anthu onse oyitsatira, ndipo anayima pamalo pena chapatalipo.
Paççahıqad qihna gırgın milletcad qığeç'u, şahareençe qığəəne xaasqamee qadı, ulyoyzaran.
18 Ankhondo ake onse anayamba kuyenda pamaso pa Davide, ndipo Akereti ndi Apeleti, pamodzinso ndi Agiti okwanira 600 amene anamutsata kuchokera ku Gati, nawonso anayenda pamaso pake.
Gırgın mang'un insanar Keretbışika, Peletbışika, yixhıd vəş Gateençe cuqab qihna qabıyne Gatbışika sacigee, cune ögiyle ılğeebaç'e.
19 Mfumu inati kwa Itai Mgiti, “Nʼchifukwa chiyani iwe ukupita ndi ife? Bwerera ndipo ukakhale ndi mfumu Abisalomu. Iwe ndiwe mlendo munthu wothawa kwawo.
Paççahee Gatğançene İttayk'le eyhen: – Ğu nya'a şaka ı'qqə? Sak'le, ixhesde paççahıka Avşalomuka axve. Ğu menne cigeençe g'e'eşşu qarına vor.
20 Wangobwera dzulo lomweli, lero ndikutenge kuti uziyendayenda ndi ife, pamene ine sindikudziwa kumene ndikupita? Bwerera, ndipo tenga abale ako. Chifundo ndi kukhulupirika zikhale nawe.”
Ğu inyaqa həşdebışee qarı. G'iyna zı ğu zaka əlyhəəsne alikke? Zak'le zı nyaqa əlyəsvacar ats'a deş. Ğumee sak'le, yiğın insanarıb vaka quvke. Hasre Rəbbee Cuna badal dyooxhena yugvalla vak'le haagvecen!
21 Koma Itai anayankha mfumu kuti, “Pali Yehova wamoyo, kulikonse kumene mbuye wanga mfumu mudzakhala, kaya ndi moyo kapena imfa, mtumiki wanu adzakhala komweko.”
İttayee paççahıs alidghıniy qele: – Vorne Rəbbilqaniy yizde xərıng'une paççahne canılqan k'ın ixhen, ğu, yizda paççah, nyaa'ar ixhee, zınar qik'u ixheeyir, üç'ür ixheeyir, maa'ar ixhes.
22 Davide anati kwa Itai, “Tiye pita nafe” Kotero Itai Mgiti anayenda pamodzi ndi anthu ake ndi mabanja amene anali naye.
Davudee İttayk'le eyhen: – Qora manke ögilqa ılğeç'e, ögee hoora. Gatğançene İttaykan gırgın mang'un insanar, cone k'anebın gırgın uşaxar qabı, ılğeebaç'enbı.
23 Anthu onse a madera ozungulira analira mofuwula pamene anthu onsewo amadutsa. Mfumunso inawoloka chigwa cha Kidroni, ndipo anthu onse anayenda kulowera ku chipululu.
Paççahın insanar əlyhəəmee, ölkeebın gırgın insanar okur aletçu gyaaşenbı. Paççahee Qidronna q'adaal ılğevç'umee, mang'ukan gırgın milletcad sahrayne suralqa ayk'an.
24 Zadoki anali nawonso, ndipo Alevi onse amene anali naye ananyamula Bokosi la Chipangano la Mulungu. Iwo anayika pansi Bokosi la Mulungulo ndipo Abiatara ankapereka nsembe mpaka pamene anthu onse anamaliza kutuluka mu mzinda.
Maa'ar Tsadokır ıxhana. Mang'une k'ane Leviyke g'abıynbı vuxhaynbı. Manbışe Allahıka mugaavilenana q'utye quvkekka vuxha. Allahna q'utye manbışe ç'iyelqa giviyxhe. Evyataree gırgın millet şahareençe qığeç'esmee q'urbanbı allya'a.
25 Kenaka mfumu inati kwa Zadoki, “Tenga Bokosi la Mulungu ubwerere nalo mu mzinda. Ngati ndidzapeza chifundo pamaso pa Yehova, adzandibweretsa kuti ndilionenso ndi malo ake okhalamo.
Paççahee Tsadokuk'le eyhen: – Allahna q'utye şahareeqa savk'al hee'e. Zı Rəbbine ulesqa yugra qaree, Mang'vee meer zı yı'q'əlqa sak'al hı'ı, Cuna q'utyeyiy Cuna çadır zak'le hagvasın.
26 Koma iye anati, ‘Akapanda kukondwera nane,’ chabwino, andichite chimene chimukomere.”
De'eş, «ğu Zas ıkkanna deşurva» uvheene, hasre zak Cus hucooyiy ıkkan he'ecen. Zı Mang'une xıle vorna.
27 Mfumu inatinso kwa wansembe Zadoki, “Kodi siwe mlosi? Bwerera mu mzinda mwamtendere pamodzi ndi mwana wako Ahimaazi ndi Yonatani mwana wa Abiatara. Iwe ndi Abiatara tengani ana anu awiri.
Paççahee kaahin Tsadokuk'le eyhen: – İlekke, hucooyiy eyxhe. Ğunayiy yiğna dix Axima'ats, Evyatarne duxayka Yonatanıka sacigee hexxan hidi'ı şahareeqa savk'le. Ğunar, Evyatareeyib q'öyursana vuşun dixbı şoka vukkee.
28 Ine ndidzadikira powolokera Yorodani ku chipululu mpaka nditalandira mawu ochokera kwa iwe ondiwuza mmene zilili zinthu.”
Zı şoke xabar qavaalesmee, İordanne damayle ılğəəne cigee, sahree ixhes.
29 Kotero Zadoki ndi Abiatara ananyamula Bokosi la Mulungu lija nabwerera nalo ku Yerusalemu, ndipo anakakhala kumeneko.
Tsadokeeyiy Evyataree Allahna q'utye İyerusalimeeqa savaak'al haa'a. Cona q'öyursanab İyerusalimee axva.
30 Koma Davide anapitirira ndi kukakwera phiri la Olivi akupita nalira. Anafunda kumutu koma sanavale nsapato. Anthu onse amene anali naye anafundanso kumutu, ndipo nawonso amalira pamene amapita.
Davud Zeytunne suvalqa geşşe-geşşe ılqeç'e. Mang'vee vuk'lelqa kar atçu eyxhe, g'elilqamee kar ali'ı ıxha deş. Mang'uka sacigee suvalqa ı'lqəənbıb vuk'lelqa kar atçu gyaaşe-gyaaşe ılqeebaç'e.
31 Tsono Davide anamva kuti, “Ahitofele ali pakati pa anthu owukira pamodzi ndi Abisalomu.” Choncho Davide anapemphera, “Inu Yehova, musandutse uphungu wa Ahitofele ukhale uchitsiru.”
Şavaame «Axitofel Avşalomne k'ane vorva, g'elil qeepxhaynbışde suralirva» xabar hoole. Davudee Rəbbis düə haa'a: – Ya Rəbb, zı Vake heqqa, Axitofelin mı'sləhətbı nişiscad karaı'dəənbı he'e.
32 Davide atafika pamwamba pa phiri pomwe anthu ankapembedzerapo Mulungu, Husai Mwariki anadzakumana naye atangʼamba mkanjo wake ndi kudzithira fumbi kumutu.
Davud milletın Allahıs ı'bəədat ha'ane suvane q'omaqa hirxhılymee, Arkibışda Xuşay mana g'aces arayle. Mang'vee culqa abına ver haagvasva tanalinbı qıt'axxa'a, vuk'ulelqa nyaq'v kyaa'a.
33 Davide anati kwa iye, “Ngati iwe upite ndi ine, udzakhala chondilemetsa.
Davudee mang'uk'le eyhen: – Ğunar zaka sacigee əlyhəəsxhee, ğu zas dağamra ixhes.
34 Koma ngati ubwerera ku mzinda ndi kukanena kwa Abisalomu kuti, ‘Inu mfumu ine ndidzakhala wantchito wanu.’ Mʼmbuyomu ndinali wantchito wa abambo anu koma tsopano ndidzakhala wantchito wanu. Ukatero udzandithandiza kulepheretsa malangizo a Ahitofele.
İnekke yugun, ğu şahareeqa sak'ı, Avşalomuk'le eyhe: «Paççah, zınar yiğna nukar ixhes. Şenke nəxübiy yiğne dekkıs nukariyvalla hav'u, həşdeb vas haa'as». Məxüd vasse zas kumag ha'as əxə. Vasse Axitofelin mı'sləhətbı alyt'ik'al ha'as əxə.
35 Kodi ansembe, Zadoki ndi Abiatara, sakukhala nawe kumeneko? Ukawawuze zonse zimene umamva mʼnyumba yaufumu.
Kaahin Tsadokiy kaahin Evyatar maa'ab vaka vuxhes. Paççahne sarayee g'ayxhiyn gırgın kar, ğu kaahinaaşilqa Tsadokılqayiy Evyatarılqa hixhar ha'as.
36 Ana awo awiri, Ahimaazi wa Zadoki, ndi Yonatani mwana wa Abiatara ali nawo pamodzi, uzikawatuma kwa ine ndi china chilichonse chimene ukamve.”
Manbışda q'öyre dix – Tsadokna dix Axima'ats, Evyatarna dix Yonatan – manbışde k'ane vob. Şok'le g'ayxhiyn gırgın manbışde xıleka zalqa hixhar he'e.
37 Ndipo Husai bwenzi la Davide anafika ku Yerusalemu pamene Abisalomu amalowa mu mzinda.
Avşalom İyerusalimeeqa ı'kkəəmee, Davudna hambaz Xuşayır şahareeqa ikkeç'e.

< 2 Samueli 15 >