< 2 Samueli 14 >

1 Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
А Јоав син Серујин опази да се срце царево обратило к Авесалому.
2 Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
И посла Јоав у Текују те дозва отуда жену лукаву, па јој рече: Учини се као да си у жалости, и обуци жалосне хаљине, и немој се намазати уљем, него буди као жена која одавна жали за мртвим.
3 Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
И отиди к цару, и говори му тако и тако. И научи је Јоав шта ће говорити.
4 Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
И кад отиде жена Текујанка к цару да говори, паде ничице на земљу и поклони се, и рече: Помагај царе!
5 Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
А цар јој рече: Шта ти је? А она рече: Удовица сам, умро ми је муж.
6 Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
А имаше слушкиња твоја два сина, па се свадише у пољу, а не беше никога да их развади, те један удари другог и уби га.
7 Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
И гле, сав дом уста на слушкињу твоју говорећи: Дај тог што је убио брата свог да га погубимо за душу брата његовог, ког је убио, и да истребимо наследника; и тако хоће да угасе искру која ми је остала, да не оставе име мужу мом ни остатак на земљи.
8 Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
А цар рече жени: Иди кући својој, а ја ћу наредити за те.
9 Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
А жена Текујанка рече цару: Царе господару! Нека на ме и на дом оца мог падне кривица, а цар и његов престо нека је прав.
10 Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
А цар рече: Ко узговори на те, доведи га к мени, и неће те се више дотаћи.
11 Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
А она рече: Нека се опомене цар Господа Бога свог, да се не умноже осветници који убијају, и да не убију сина мог. А он рече: Тако жив био Господ, ниједна длака с твог сина неће пасти на земљу.
12 Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
А жена рече: Да каже слушкиња твоја нешто цару господару. А он рече: Говори.
13 Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
А жена рече: А зашто си намислио такву ствар народу Божијем? Јер цар као да је крив говорећи тако, јер неће цар да дозове натраг оног ког је одагнао.
14 Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
Јер ћемо доиста помрети, и јесмо као вода која се проспе на земљу и више се не може скупити; јер му Бог није узео живот, него је наумио да одагнани не остане одагнан од њега.
15 “Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
И тако дођох да кажем ово цару господару свом, јер ме народ уплаши; зато рече слушкиња твоја: Да говорим цару, може бити да ће учинити цар шта слушкиња његова каже.
16 Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
Јер ће цар услишити и избавити слушкињу своју из руке оног који хоће да истреби мене и сина мог из наследства Божијег.
17 “Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
И слушкиња твоја рече: Реч цара господара мог биће ми утеха, јер је цар господар мој као анђео Божји, те слуша и добро и зло, и Господ ће Бог твој бити с тобом.
18 Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
А цар одговори и рече жени: Немој тајити од мене шта ћу те питати. А жена рече: Нека говори цар господар мој.
19 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
Тада цар рече: Да није Јоавов посао у свему томе што чиниш? А жена одговори и рече: Тако да је жива душа твоја, царе господару, не може се ни надесно ни налево од свега што каза цар господар мој; јер слуга твој Јоав заповедио ми је и научио слушкињу твоју све ово да говорим.
20 Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
Слуга је твој Јоав учинио, те сам овако извила беседу своју; али је господар мој мудар као анђео Божји, те зна све што бива на земљи.
21 Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
Тада рече цар Јоаву: Ево, ти си учинио то, иди, доведи натраг дете Авесалома.
22 Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
Тада паде Јоав лицем на земљу, и поклони се и благослови цара, и рече Јоав: Данас види слуга твој да сам нашао милост пред тобом, царе господару, кад је цар учинио шта му слуга његов рече.
23 Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
Потом се подиже Јоав и отиде у Гесур, и доведе натраг у Јерусалим Авесалома.
24 Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
И цар рече: Нека иде својој кући, а лице моје да не види. И отиде Авесалом својој кући, и не виде лице царево.
25 Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
А не беше човека тако лепа као Авесалом у свем Израиљу, да га тако хвале; од пете до темена не беше на њему мане.
26 Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
И кад би стригао главу (а имаше обичај сваке године стрићи је, јер му беше тешко), мерио би косу с главе своје, и биваше је двеста сикала царском мером.
27 Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
И родише се Авесалому три сина и једна кћи, којој беше име Тамара, и она беше лепа.
28 Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
И Авесалом оста целе две године у Јерусалиму, а лице царево не виде.
29 Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
Тада посла Авесалом по Јоава да га пошаље к цару; али он не хте доћи к њему; и посла опет други пут, али он не хте доћи.
30 Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
Тада рече слугама својим: Видите ли њиву Јоавову поред моје? На њој је јечам; идите и упалите је. И упалише слуге Авесаломове ону њиву.
31 Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
Тада се подиже Јоав, и дође к Авесалому у кућу, и рече му: Зашто слуге твоје упалише моју њиву?
32 Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
Авесалом рече Јоаву: Ето слао сам к теби говорећи: Ходи овамо да те пошаљем к цару да му кажеш: Зашто сам дошао из Гесура? Боље би било да сам још онде. Зато да видим лице царево; ако ли има каква кривица на мени, нека ме погуби.
33 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.
И отиде Јоав к цару, и каза му. И дозва Авесалома; а он дошавши к цару поклони се лицем до земље пред царем, и цар целива Авесалома.

< 2 Samueli 14 >