< 2 Samueli 14 >

1 Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
UJowabi indodana kaZeruya wasenanzelela ukuthi inhliziyo yenkosi ikuAbisalomu.
2 Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
UJowabi wasethumela eThekhowa ukuthi alande khona owesifazana ohlakaniphileyo, wathi kuye: Ake uzitshaye olilayo, ake ugqoke izigqoko zokulila, ungazigcobi ngamafutha, kodwa ube njengowesifazana oselilele ofileyo insuku ezinengi.
3 Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
Ungene enkosini, ukhulume kuyo ngalindlela. UJowabi wasefaka amazwi emlonyeni wakhe.
4 Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
Lapho owesifazana umThekhowa ekhuluma enkosini, wathi mbo ngobuso bakhe emhlabathini, wakhothama, wathi: Siza, nkosi!
5 Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
Inkosi yasisithi kuye: Ulani? Yena wasesithi: Sibili, ngingumfazi ongumfelokazi, lendoda yami yafa.
6 Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
Njalo incekukazi yakho yayilamadodana amabili, alwa womabili egangeni; kwakungelamlamuli phakathi kwawo; enye yasitshaya enye, yayibulala.
7 Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
Khangela-ke, usendo lonke seluvukele incekukazi yakho, bathi: Nikela lowo owatshaya umfowabo wambulala, ukuthi simbulale ngenxa yempilo yomfowabo ambulalayo, sichithe lendlalifa. Ngalokho bacitshe ilahle lami eliseleyo, ukuze bangatshiyeli indoda yami ibizo lensali ebusweni bomhlaba.
8 Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
Inkosi yasisithi kowesifazana: Yana endlini yakho; mina-ke ngizalaya ngawe.
9 Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
Owesifazana umThekhowa wasesithi enkosini: Nkosi yami, nkosi, icala kalibe phezu kwami laphezu kwendlu kababa; kodwa inkosi lesihlalo sayo sobukhosi kube msulwa.
10 Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
Inkosi yasisithi: Okhuluma ulutho kuwe, umlethe kimi, njalo kayikuphinda akuthinte futhi.
11 Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
Wasesithi: Inkosi ake ikhumbule iNkosi uNkulunkulu wayo ukuthi umphindiseli wegazi angabe esachitha, hlezi bachithe indodana yami. Yasisithi: Kuphila kukaJehova, kakuyikuwela emhlabathini olulodwa unwele lwendodana yakho.
12 Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
Owesifazana wasesithi: Incekukazi yakho ake ikhulume ilizwi enkosini yami inkosi. Yasisithi: Khuluma.
13 Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
Owesifazana wasesithi: Pho, unakaneleni okunje ngabantu bakaNkulunkulu? Ngokukhuluma lindaba inkosi injengolecala, ngokuthi inkosi kayibuyisanga oxotshiweyo wayo.
14 Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
Ngoba kumele sife, sinjengamanzi achithekele emhlabathini angabuthwanga; kodwa uNkulunkulu kayikususa impilo, kodwa uzacabanga amacebo ukuthi angalahli kuye oxotshiweyo.
15 “Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
Ngakho-ke, njengoba ngizile ukukhuluma linto enkosini, inkosi yami, kungoba abantu bangesabisile; incekukazi yakho yasisithi: Khathesi ngizakhuluma lenkosi; mhlawumbe inkosi izakwenza ilizwi lencekukazi yayo.
16 Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
Ngoba inkosi izakuzwa, ukukhulula incekukazi yayo esandleni somuntu ofuna ukuchitha mina kanye lendodana yami elifeni likaNkulunkulu.
17 “Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
Incekukazi yakho yasisithi: Akuthi ilizwi lenkosi yami, inkosi, libe ngelokuthula, ngoba njengengilosi kaNkulunkulu, injalo inkosi yami, inkosi, ukuzwa okubi lokuhle. Ngakho iNkosi uNkulunkulu wakho kayibe lawe.
18 Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
Inkosi yasiphendula yathi kowesifazana: Ake ungangifihleli indaba engizayibuza kuwe. Owesifazana wasesithi: Ake ikhulume inkosi yami, inkosi.
19 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
Inkosi yasisithi: Isandla sikaJowabi silawe yini kukho konke lokhu? Owesifazana wasephendula wathi: Kuphila komphefumulo wakho, nkosi yami, nkosi, isibili kakho ongaya ngakwesokunene langakwesokhohlo asuke lakuyiphi into inkosi yami, inkosi, eyikhulumileyo; ngoba inceku yakho uJowabi, yona yangilaya, yiyo eyafunza incekukazi yakho wonke lamazwi.
20 Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
Inceku yakho uJowabi iyenzile linto ukuthi iphendule ukuma kwendaba. Njalo inkosi yami ihlakaniphile njengenhlakanipho yengilosi kaNkulunkulu, ukwazi konke okusemhlabeni.
21 Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
Inkosi yasisithi kuJowabi: Khangela khathesi, ngenzile lindaba; ngakho hamba ubuyise umfana uAbisalomu.
22 Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
UJowabi wasesithi mbo ngobuso emhlabathini, wakhothama, wayibusisa inkosi; uJowabi wasesithi: Lamuhla inceku yakho iyazi ukuthi ngithole umusa emehlweni akho, nkosi yami, nkosi, ngokuthi inkosi yenzile indaba yenceku yayo.
23 Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
Wasesuka uJowabi, waya eGeshuri, wamletha uAbisalomu eJerusalema.
24 Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
Inkosi yasisithi: Kaphendukele endlini yakhe, angaboni ubuso bami. Ngakho uAbisalomu waphendukela endlini yakhe, kabonanga ubuso benkosi.
25 Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
KoIsrayeli wonke-ke kwakungelamuntu onjengoAbisalomu ukudunyiswa kakhulu ngobuhle; kwakungelasici kuye kusukela kungaphansi yonyawo lwakhe kuze kufike enkanda yakhe.
26 Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
Nxa ephuca ikhanda lakhe - ngoba kwakusithi ekupheleni kwawo wonke umnyaka aliphuce, ngoba zazinzima kuye, ngakho waliphuca - walinganisa inwele zekhanda lakhe, amashekeli angamakhulu amabili ngesilinganiso senkosi.
27 Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
Kwasekuzalelwa uAbisalomu amadodana amathathu lendodakazi eyodwa, obizo layo lalinguTamari; wayengowesifazana omuhle ebukeka.
28 Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
UAbisalomu wasehlala eJerusalema iminyaka emibili epheleleyo, kabonanga ubuso benkosi.
29 Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
UAbisalomu wasethumela kuJowabi ukuthi amthume enkosini; kodwa kavumanga ukuza kuye. Waphinda wathumela ngokwesibili, kodwa kavumanga ukuza.
30 Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
Wasesithi ezincekwini zakhe: Bonani, isabelo sikaJowabi siseceleni kwesami, njalo ulebhali lapho; hambani lisithungele ngomlilo. Izinceku zikaAbisalomu zasezithungela isabelo ngomlilo.
31 Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
Wasesuka uJowabi weza kuAbisalomu endlini, wathi kuye: Izinceku zakho zithungeleleni isabelo esingesami ngomlilo?
32 Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
UAbisalomu wasesithi kuJowabi: Khangela, ngithumele kuwe ngisithi: Woza lapha, ukuze ngikuthume enkosini, ukuthi: Ngibuyeleni ngisuka eGeshuri? Bekukuhle kimi ukuthi ngabe ngilokhu ngikhonale. Ngakho-ke kangibone ubuso benkosi; njalo uba kulecala kimi, kayingibulale.
33 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.
Ngakho uJowabi weza enkosini, wayitshela; isimbizile uAbisalomu weza enkosini, wayikhothamela ngobuso bakhe emhlabathini, phambi kwenkosi; inkosi yasimanga uAbisalomu.

< 2 Samueli 14 >