< 2 Samueli 14 >

1 Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
Joab, fils de Tseruja, s'aperçut que le cœur du roi était tourné vers Absalom.
2 Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
Joab envoya à Tekoa et y fit venir une femme sage, à qui il dit: « Je t'en prie, agis comme une personne en deuil, mets des vêtements de deuil, je t'en prie, et ne t'oins pas d'huile, mais sois comme une femme qui a pleuré longtemps un mort.
3 Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
Va vers le roi et parle-lui ainsi. » Joab mit les mots dans sa bouche.
4 Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
Lorsque la femme de Tekoa a parlé au roi, elle s'est prosternée à terre, s'est montrée respectueuse et a dit: « Au secours, ô roi! »
5 Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
Le roi lui dit: « Qu'est-ce qui te prend? » Elle répondit: « En vérité, je suis veuve, et mon mari est mort.
6 Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
Ton serviteur avait deux fils; ils se sont battus ensemble dans les champs, et il n'y avait personne pour les séparer; mais l'un a frappé l'autre et l'a tué.
7 Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
Voici que toute la famille s'est soulevée contre ton serviteur, et ils disent: « Délivrez celui qui a frappé son frère, afin que nous le tuions pour la vie de son frère qu'il a tué, et que nous fassions aussi périr l'héritier ». Ainsi, ils éteindraient mon charbon qui reste, et ne laisseraient à mon mari ni nom ni reste sur la surface de la terre. »
8 Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
Le roi dit à la femme: « Va dans ta maison, et je donnerai un ordre à ton sujet. »
9 Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
La femme de Tekoa dit au roi: « Mon seigneur, ô roi, que l'iniquité retombe sur moi et sur la maison de mon père, et que le roi et son trône soient sans reproche. »
10 Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
Le roi dit: « Si quelqu'un te dit quelque chose, amène-le moi, et il ne t'ennuiera plus. »
11 Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
Et elle dit: « Je te prie, que le roi se souvienne de Yahvé, ton Dieu, afin que le vengeur du sang ne détruise plus, de peur qu'on ne fasse périr mon fils. » Il a dit: « Yahvé est vivant, aucun cheveu de ton fils ne tombera sur la terre. »
12 Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
Alors la femme dit: « Je te prie de laisser ton serviteur dire un mot à mon seigneur le roi. » Il a dit: « Dis-le. »
13 Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
La femme dit: « Pourquoi donc as-tu imaginé une telle chose contre le peuple de Dieu? Car en prononçant cette parole, le roi est comme un coupable, en ce que le roi ne ramène pas son banni.
14 Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
Car nous devons mourir, et nous sommes comme de l'eau répandue sur le sol, qui ne peut être recueillie; et Dieu n'ôte pas la vie, mais il conçoit des moyens, afin que celui qui est banni ne soit pas exclu de lui.
15 “Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
Maintenant, si je suis venu pour dire cette parole à mon seigneur le roi, c'est parce que le peuple m'a fait peur. Ton serviteur a dit: « Je vais maintenant parler au roi; il se peut que le roi exauce la demande de son serviteur ».
16 Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
Car le roi écoutera, pour délivrer son serviteur de la main de l'homme qui voulait nous faire périr, moi et mon fils, hors de l'héritage de Dieu.
17 “Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
Ton serviteur dit: « Que la parole de mon seigneur le roi apporte le repos, car comme un ange de Dieu, mon seigneur le roi sait discerner le bien et le mal. Que Yahvé, ton Dieu, soit avec toi. »
18 Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
Alors le roi répondit à la femme: « Je t'en prie, ne me cache rien de ce que je te demande. » La femme dit: « Que mon seigneur le roi parle maintenant. »
19 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
Le roi dit: « La main de Joab est-elle avec toi dans tout cela? » La femme répondit: « Aussi vrai que ton âme est vivante, mon seigneur le roi, personne ne peut se détourner à droite ou à gauche de ce que mon seigneur le roi a dit; car ton serviteur Joab m'a pressée, et il a mis toutes ces paroles dans la bouche de ta servante.
20 Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
Ton serviteur Joab a fait cela pour changer la face de l'affaire. Mon seigneur est sage, selon la sagesse d'un ange de Dieu, pour connaître toutes les choses qui sont sur la terre. »
21 Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
Le roi dit à Joab: « Voici, j'ai accordé cette chose. Va donc, et ramène le jeune homme Absalom. »
22 Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
Joab tomba à terre sur sa face, fit preuve de respect et bénit le roi. Joab dit: « Ton serviteur sait aujourd'hui que j'ai trouvé grâce à tes yeux, mon seigneur, ô roi, puisque le roi a exécuté la demande de son serviteur. »
23 Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
Joab se leva, alla à Gueschur, et amena Absalom à Jérusalem.
24 Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
Le roi dit: « Qu'il retourne dans sa maison, mais qu'il ne voie pas mon visage. » Absalom retourna donc dans sa maison, et ne vit pas le visage du roi.
25 Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
Or, dans tout Israël, il n'y avait personne qui fût aussi loué qu'Absalom pour sa beauté. Depuis la plante de son pied jusqu'au sommet de sa tête, il n'y avait en lui aucun défaut.
26 Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
Lorsqu'il se coupait les cheveux de sa tête (c'était à la fin de chaque année qu'il les coupait; comme ils étaient lourds pour lui, il les coupait), il pesait les cheveux de sa tête à deux cents sicles, selon le poids du roi.
27 Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
Trois fils naquirent à Absalom, et une fille, dont le nom était Tamar. C'était une femme qui avait un beau visage.
28 Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
Absalom vécut deux années entières à Jérusalem, et il ne vit pas le visage du roi.
29 Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
Absalom envoya alors chercher Joab, pour l'envoyer auprès du roi, mais celui-ci ne voulut pas venir à lui. Il envoya encore une seconde fois, mais il ne voulut pas venir.
30 Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
Il dit alors à ses serviteurs: « Voici, le champ de Joab est près du mien, et il y a de l'orge. Allez-y et mettez-y le feu. » Les serviteurs d'Absalom mirent donc le feu au champ.
31 Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
Alors Joab se leva et vint chez Absalom, dans sa maison, et lui dit: « Pourquoi tes serviteurs ont-ils mis le feu à mon champ? »
32 Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
Absalom répondit à Joab: « Voici, je t'ai envoyé dire: Viens ici, afin que je t'envoie dire au roi: « Pourquoi suis-je venu de Gueshur? Il vaudrait mieux que j'y sois encore. Maintenant, que je voie la face du roi, et s'il y a en moi de l'iniquité, qu'il me fasse mourir ».
33 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.
Joab se rendit auprès du roi et lui en fit part. Après avoir appelé Absalom, il vint auprès du roi et se prosterna à terre, face contre terre, devant le roi; et le roi embrassa Absalom.

< 2 Samueli 14 >