< 2 Samueli 14 >

1 Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
And he perceived Joab [the] son of Zeruiah that [the] heart of the king [was] towards Absalom.
2 Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
And he sent Joab Tekoa towards and he took from there a woman wise and he said to her play [the] mourner please and put on please garments of mourning and may not you anoint yourself oil and you will be like a woman this days many [who has been] mourning on a dead [person].
3 Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
And you will go to the king and you will speak to him according to the word this and he put Joab the words in mouth her.
4 Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
And she said the woman Tekoite to the king and she fell on face her [the] ground towards and she bowed down and she said save! O king.
5 Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
And he said to her the king what? [is] to you and she said indeed [am] a woman a widow I and he has died husband my.
6 Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
And [belonged] to maidservant your two sons and they struggled together [the] two of them in the field and there not [was] a deliverer between them and he struck him the one the one and he killed him.
7 Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
And there! it has risen up all the clan on maidservant your and they have said deliver up - [the] [one who] struck down brother his so we may put to death him for [the] life of brother his whom he killed and let us destroy also the heir and they will extinguish coal my which it is left to not (to establish *Q(K)*) for husband my a name and a remnant on [the] surface of the ground.
8 Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
And he said the king to the woman go to house your and I I will command on you.
9 Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
And she said the woman Tekoite to the king [be] on me O lord my the king the iniquity and on [the] house of father my and the king and throne his [be] innocent.
10 Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
And he said the king the [one who] speaks to you and you will bring him to me and not he will repeat again to touch you.
11 Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
And she said let him remember please the king Yahweh God your (from increasing *Q(k)*) [the] avenger of blood to destroy and not they will destroy son my and he said [by] [the] life of Yahweh if it will fall one of [the] hair[s] of son your [the] ground towards.
12 Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
And she said the woman let her speak please maidservant your to lord my the king a word and he said speak.
13 Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
And she said the woman and why? have you planned like this on [the] people of God and because has spoken the king the word this like a guilty [person] to not to bring back the king banished [son] his.
14 Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
For certainly we will die and [we are] like waters which are spilled [the] ground towards which not they will be gathered and not he takes away God life and he plans plans to not he will be cast out from him a banished [one].
15 “Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
And now when I have come to speak to the king lord my the word this that they have made afraid me the people and she said maidservant your let me speak please to the king perhaps he will do the king [the] word of maidservant his.
16 Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
For he will hear the king to deliver maidservant his from [the] hand of the man to destroy me and son my together from [the] inheritance of God.
17 “Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
And she said maidservant your may it become please [the] word of lord my the king rest for - like [the] angel of God [is] so lord my the king to hear good and bad and Yahweh God your may he be with you.
18 Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
And he answered the king and he said to the woman may not please you hide from me anything which I [am] asking you and she said the woman let him speak please lord my the king.
19 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
And he said the king ¿ [is] [the] hand of Joab with you in all this and she answered the woman and she said [by] [the] life of self your O lord my the king if there is - to go to [the] right and to go to [the] left from all that he has spoken lord my the king for servant your Joab he he commanded me and he he put in [the] mouth of maidservant your all the words these.
20 Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
In order to change [the] face of the matter he did servant your Joab the thing this and lord my [is] wise like [the] wisdom of [the] angel of God to know all that [is] in the land.
21 Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
And he said the king to Joab here! please I do the thing this and go bring back the young man Absalom.
22 Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
And he fell Joab to face his [the] ground towards and he bowed down and he blessed the king and he said Joab this day he knows servant your that I have found favor in view your O lord my the king that he has done the king [the] word of (servant your. *Q(K)*)
23 Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
And he arose Joab and he went Geshur towards and he brought Absalom Jerusalem.
24 Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
And he said the king he will turn to house his and face my not he will see and he turned Absalom to house his and [the] face of the king not he saw.
25 Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
And like Absalom not he was a man handsome in all Israel to praise exceedingly from [the] sole of foot his and to scalp his not it was in him a blemish.
26 Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
And when shaved he head his and it was from [the] end of days - to the days when he shaved for [it was] heavy on him and he shaved it and he weighed [the] hair of head his two hundred shekels by [the] weight of the king.
27 Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
And they were born to Absalom three sons and a daughter one and name her [was] Tamar she she was a woman beautiful of appearance.
28 Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
And he dwelt Absalom in Jerusalem two years days and [the] face of the king not he saw.
29 Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
And he sent Absalom to Joab to send him to the king and not he was willing to come to him and he sent again a second [time] and not he was willing to come.
30 Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
And he said to servants his see [the] portion of land of Joab [is] to hand my and [belongs] to him there barley go (and set on fire it *Q(K)*) with fire and they set on fire [the] servants of Absalom the portion of land with fire.
31 Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
And he arose Joab and he went to Absalom the house towards and he said to him why? have they set on fire servants your the portion of land which [belongs] to me with fire.
32 Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
And he said Absalom to Joab here! I sent to you - saying come here so let me send you to the king saying why? have I come from Geshur [was] good for me still I [was] there and therefore let me see [the] face of the king and if there in me [is] iniquity and he will kill me.
33 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.
And he went Joab to the king and he told to him and he summoned Absalom and he came to the king and he bowed down to him on face his [the] ground towards before the king and he kissed the king Absalom.

< 2 Samueli 14 >