< 2 Samueli 14 >
1 Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
And Joab the son of Sarvia, understanding that the king’s heart was turned to Absalom,
2 Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
Sent to Thecua, and fetched from thence a wise woman: and said to her: Feign thyself to be a mourner, and put on mourning apparel, and be not anointed with oil, that thou mayest be as a woman that had a long time been mourning for one dead.
3 Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
And thou shalt go in to the king, and shalt speak to him in this manner. And Joab put the words in her mouth.
4 Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
And when the woman of Thecua was come in to the king, she fell before him upon the ground, and worshipped, and said: Save me, O king.
5 Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
And the king said to her: What is the matter with thee? She answered: Alas, I am a widow woman: for my husband is dead.
6 Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
And thy handmaid had two sons: and they quarrelled with each other in the field, and there was none to part them: and the one struck the other, and slew him.
7 Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
And behold the whole kindred rising against thy handmaid, saith: Deliver him that hath slain his brother, that we may kill him for the life of his brother, whom he slew, and that we may destroy the heir: and they seek to quench my spark which is left, and will leave my husband no name, nor remainder upon the earth.
8 Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
And the king said to the woman: Go to thy house, and I will give charge concerning thee.
9 Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
And the woman of Thecua said to the king: Upon me, my lord, be the iniquity, and upon the house of my father: but may the king and his throne be guiltless.
10 Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
And the king said: If any one shall say ought against thee, bring him to me, and be shall not touch thee any more.
11 Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
And she said: Let the king remember the Lord his God, that the next of kin be not multiplied to take revenge, and that they may not kill my son. And he said: As the Lord liveth, there shall not one hair of thy son fall to the earth.
12 Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
Then the woman said: Let thy handmaid speak one word to my lord the king. And he said: Speak.
13 Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
And the woman said: Why hast thou thought such a thing against the people of God, and why hath the king spoken this word, to sin, and not bring home again his own exile?
14 Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
We all die, and like waters that return no more, we fall down into the earth: neither will God have a soul to perish, but recalleth, meaning that he that is cast off should not altogether perish.
15 “Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
Now therefore I am come, to speak this word to my lord the king before the people. And thy handmaid said: I will speak to the king, it maybe the king will perform the request of his handmaid.
16 Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
And the king hath hearkened to me to deliver his handmaid out of the hand of all that would destroy me and my son together out of the inheritance of God.
17 “Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
Then let thy handmaid say, that the word of the Lord the king be made as a sacrifice. For even as an angel of God, so is my lord the king, that he is neither moved with blessing nor cursing: wherefore the Lord thy God is also with thee.
18 Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
And the king answering, said to the woman: Hide not from me the thing that I ask thee. And the woman said to him: Speak, my lord the king.
19 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
And the king said: Is not the hand of Joab with thee in all this? The woman answered, and said: By the health of thy soul, my lord, O king, it is neither on the left hand, nor on the right, in all these things which my lord the king hath spoken: for thy servant Joab, he commanded me, and he put all these words into the mouth of thy handmaid.
20 Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
That I should come about with this form of speech, thy servant Joab, commanded this: but thou, my lord, O king, art wise, according to the wisdom of ail angel of God, to understand all things upon earth.
21 Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
And the king said to Joab: Behold I am appeased and have granted thy request: Go therefore and fetch back the boy Absalom.
22 Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
And Joab falling down to the ground upon his face, adored, and blessed the king: and Joab said: This day thy servant hath understood, that I have found grace in thy sight, my lord, O king: for thou hast fulfilled the request of thy servant.
23 Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
Then Joab arose and went to Gessur, and brought Absalom to Jerusalem.
24 Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
But the king said: Let him return into his house, and let him not see my face. So Absalom returned into his house, and saw not the king’s face.
25 Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
But in all Israel there was not a man so comely, and so exceedingly beautiful as Absalom: from the sole of the foot to the crown of his head there was no blemish in him.
26 Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
And when he polled his hair (now he was polled once a year, because his hair was burdensome to him) he weighed the hair of his head at two hundred sicles, according to the common weight.
27 Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
And there were born to Absalom three sons: and one daughter, whose, name was Thamar, and she was very beautiful.
28 Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
And Absalom dwelt two years in Jerusalem, and saw not the king’s face.
29 Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
He sent therefore to Joab, to send him to the king: but he would not come to him. And when he had sent the second time, and he would not come to him,
30 Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
He said to his servants: You know the field of Joab near my field, that hath a crop of barley: go now and set it on fire. So the servants of Absalom set the corn on fire. And Joab’s servants coming with their garments rent, said: The servants of Absalom have set part of the field on fire.
31 Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
Then Joab arose, and came to Absalom to his house, and said: Why have thy servants set my corn on fire?
32 Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
And Absalom answered Joab: I sent to thee beseeching thee to come to me, that I might send thee to the king, to say to him: Wherefore am I come from Gessur? it had been better for me to be there: I beseech thee therefore that I may see the face of the king: and if he be mindful of my iniquity, let him kill me.
33 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.
So Joab going in to the king, told him all: and Absalom was called for, and he went in to the king: and prostrated himself on the ground before him: and the king kissed Absalom.