< 2 Samueli 14 >

1 Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
Now Joab, the son of Zeruiah, understood that the heart of the king had been turned toward Absalom,
2 Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
so he sent to Tekoa, and he brought from there a wise woman. And he said to her: “Feign that you are in mourning, and put on the clothing of one who mourns. And do not anoint yourself with oil, so that you may be like a woman who is still grieving for someone who died some time ago.
3 Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
And you shall enter to the king, and you shall speak words to him in this manner.” Then Joab put the words in her mouth.
4 Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
And so, when the woman of Tekoa had entered to the king, she fell before him on the ground, and she reverenced, and she said, “Save me, O king.”
5 Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
And the king said to her, “What problem do you have?” And she responded: “Alas, I am a woman who is a widow. For my husband has died.
6 Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
And your handmaid had two sons. And they quarreled against one another in the field. And there was no one there who would be able to stop them. And one struck the other, and killed him.
7 Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
And behold, the whole family, rising up against your handmaid, said: ‘Deliver him who struck down his brother, so that we may kill him for the life of his brother, whom he killed, and so that we may do away with the heir.’ And they are seeking to extinguish my spark that is left, so that there may not survive a name for my husband, nor a remnant upon the earth.”
8 Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
And the king said to the woman, “Go to your own house, and I will make a decree on your behalf.”
9 Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
And the woman of Tekoa said to the king: “May the iniquity be upon me, my lord, and upon the house of my father. But may the king and his throne be innocent.”
10 Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
And the king said, “Whoever will contradict you, bring him to me, and he will never touch you again.”
11 Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
And she said, “Let the king remember the Lord his God, so that close blood relatives may not be multiplied in order to take revenge, and so that they may by no means kill my son.” And he said, “As the Lord lives, not one hair from your son shall fall to the ground.”
12 Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
Then the woman said, “Let your handmaid speak a word to my lord the king.” And he said, “Speak.”
13 Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
And the woman said: “Why have you thought such a thing against the people of God, and why has the king spoken this word, so that he sins and does not lead back the one whom he rejected?
14 Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
We are all dying, and we are all like waters that flow into the ground and do not return. God does not will to lose a soul. Instead, he renews his efforts, thinking that what has been rejected might not perish altogether.
15 “Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
Therefore, now I have come to speak this word to my lord the king, in the presence of the people. And your handmaid said: I will speak to the king, for perhaps there may be some way for the king to accomplish the word of his handmaid.
16 Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
And the king listened, and he freed his handmaid from the hand of all who were willing to take away me and my son together, from the inheritance of God.
17 “Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
Therefore, let your handmaid speak, so that the word of my lord the king may be like a sacrifice. For even like an Angel of God, so is my lord the king, so that he is moved by neither a blessing, nor a curse. Then too, the Lord your God is with you.”
18 Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
And in response, the king said to the woman, “You shall not conceal from me a word of what I ask you.” And the woman said to him, “Speak, my lord the king.”
19 Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
And the king said, “Is not the hand of Joab with you in all this?” And the woman answered and said: “By the welfare of your soul, my lord the king, it is neither to the left, nor to the right, in all these things that my lord the king has spoken. For your servant Joab himself instructed me, and he himself placed all these words in the mouth of your handmaid.
20 Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
Thus did I turn to this figure of speech, because your servant Joab instructed it. But you, my lord the king, are wise, just as an Angel of God has wisdom, so that you understand all that is upon the earth.”
21 Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
And the king said to Joab: “Behold, your word has succeeded in appeasing me. Therefore, go and call back the boy Absalom.”
22 Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
And falling to the ground upon his face, Joab reverenced, and he blessed the king. And Joab said: “Today your servant has understood that I have found grace in your sight, my lord the king. For you have accomplished the word of your servant.”
23 Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
Then Joab rose up, and he went away to Geshur. And he brought Absalom into Jerusalem.
24 Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
But the king said, “Let him return to his own house, but let him not see my face.” And so, Absalom returned to his own house, but he did not see the face of the king.
25 Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
Now in all of Israel, there was no man so handsome, and so very stately as Absalom. From the sole of the foot to the top of the head, there was no blemish in him.
26 Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
And when he shaved off his hair, for he shaved it off once a year, because his long hair was burdensome to him, he weighed the hair of his head at two hundred shekels, by the public weights.
27 Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
Then three sons were born to Absalom, and one daughter, of elegant form, whose name was Tamar.
28 Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
And Absalom remained for two years in Jerusalem, and he did not see the face of the king.
29 Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
And so, he sent to Joab, so that he might send him to the king. But he refused to come to him. And when he had sent a second time, and he had refused to come to him,
30 Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
he said to his servants: “You know that the field of Joab, the one that is near my field, has a harvest of barley. Therefore, go and set it on fire.” And so, the servants of Absalom set fire to the grain field. And the servants of Joab, arriving with their garments torn, said, “The servants of Absalom have set fire to part of the field!”
31 Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
And Joab rose up, and he went to Absalom at his house, and he said, “Why have your servants set fire to my grain field?”
32 Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
And Absalom responded to Joab: “I sent to you, begging that you might come to me, and that I might send you to the king, and that you might say to him: ‘Why was I brought from Geshur? It would have been better for me to be there.’ I beg you, therefore, that I may see the face of the king. And if he is mindful of my iniquity, let him put me to death.”
33 Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.
And so, Joab, entering to the king, reported everything to him. And Absalom was summoned. And he entered to the king, and he reverenced on the face of the earth. And the king kissed Absalom.

< 2 Samueli 14 >