< 2 Samueli 13 >
1 Patapita nthawi, Amnoni mwana wa Davide anakonda Tamara, mlongo wa Abisalomu, mwana wa Davide, amene anali wokongola.
Or, il arriva après cela, qu’Amnon, fils de David, s’éprit d’amour pour la sœur d’Absalom, fils de David, femme très belle, du nom de Thamar;
2 Amnoni sankagona tulo mpaka anadwala chifukwa cha Tamara mlongo wakeyo, pakuti iye anali asanagonepo ndi mwamuna ndipo zimaoneka kuti zinali zosatheka kuti achite chilichonse kwa iye.
Et il l’aimait éperdument, à un tel point, qu’à cause de son amour il était malade, parce que comme elle était vierge, il lui paraissait difficile de rien faire déshonnêtement avec elle.
3 Koma Amnoni anali ndi mnzake dzina lake Yehonadabu mwana wamwamuna wa Simea, mʼbale wake wa Davide. Yonadabu anali munthu wochenjera kwambiri.
Or, Amnon avait un ami, du nom de Jonadab, fils de Semmaa, frère de David, homme très prudent,
4 Iye anafunsa Amnoni, “Nʼchifukwa chiyani iwe mwana wa mfumu, umaoneka wowonda mmawa uliwonse? Bwanji wosandiwuza?” Amnoni anamuyankha kuti, “Ine ndamukonda Tamara, mlongo wa mʼbale wanga Abisalomu.”
Lequel lui demanda: Pourquoi, fils du roi, maigris-tu ainsi chaque jour? pourquoi ne me le dis-tu point? Et Amnon lui répondit: J’aime Thamar, la sœur de mon frère Absalom.
5 Yehonadabu anati, “Pita ukagone ndipo unamizire kudwala. Abambo ako akabwera kudzakuona, udzati kwa iwo, Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara abwere kuti adzandikonzere chakudya kuti ndidye. Adzandikonzere chakudyacho ine ndikumuona ndi kudya chili mʼmanja mwake.”
Jonadab lui dit: Couche-toi sur ton lit et feins une maladie; et lorsque ton père viendra pour te visiter, dis-lui: Que Thamar, ma sœur, vienne, je vous prie, afin qu’elle me donne de la nourriture, et qu’elle me fasse un mets, pour que je mange de sa main.
6 Kotero Amnoni anagona nakhala ngati akudwala. Mfumu itabwera kudzamuona, Amnoni anati kwa iyo, “Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara kuti abwere adzandipangire buledi wapamwamba ineyo ndikuona, kuti ndidye ali mʼmanja mwake.”
C’est pourquoi Amnon se coucha, et commença à feindre d’être malade; et lorsque le roi fut venu pour le visiter, Amnon dit au roi: Que Thamar, ma sœur, vienne, je vous conjure, afin qu’elle fasse sous mes yeux deux petits bouillons, et que je prenne de la nourriture de sa main.
7 Davide anatumiza mawu kwa Tamara ku nyumba yaufumu kuti, “Pita ku nyumba ya mlongo wako Amnoni ndipo ukamukonzere chakudya.”
David donc envoya à la maison de Thamar, disant: Venez à la maison d’Amnon, votre frère, et faites-lui un mets.
8 Choncho Tamara anapitadi ku nyumba ya mlongo wake Amnoni kumalo kumene ankagona. Anakanda ufa, nawumba buledi Amunoniyo akuona ndipo anaphika bulediyo.
Et Thamar vint à la maison d’Amnon, son frère; celui-ci était couché; et elle, prenant de la farine, la pétrit, et la délayant, elle fit cuire sous ses yeux deux petits bouillons.
9 Kenaka iye anatenga chiwaya ndipo anamupatsa bulediyo, koma iyeyo anakana. Amnoni anati “Uza aliyense atuluke muno.” Ndipo aliyense anatuluka.
Et prenant ce quelle avait fait cuire, elle le versa et le posa devant lui, et il ne voulut pas en manger; et Amnon dit: Faites retirer tout le monde. Et lorsqu’on eut fait retirer tout le monde,
10 Kenaka Amnoni anati kwa Tamara, “Bweretsa chakudya kuno, ku chipinda changa chogona kuti ndidye chili mʼmanja mwako.” Ndipo Tamara anatenga buledi amene anapanga ndi kubwera naye kwa mlongo wake ku chipinda chake.
Amnon dit à Thamar: Porte le mets dans la chambre, afin que je le mange de ta main. Thamar donc prit les deux petits bouillons qu’elle avait faits, et les porta à Amnon son frère dans la chambre.
11 Koma atabweretsa kwa iye kuti adye, anamugwira ndipo anati, “Bwera ugone nane, iwe mlongo wanga.”
Et lorsqu’elle lui eut présenté le mets, il la saisit, et dit: Viens, repose avec moi, ma sœur.
12 Tamara anati kwa iye, “Ayi mlongo wanga! Usandikakamize. Zotere siziyenera kuchitika mu Israeli! Usachite chinthu choyipa chotere.
Thamar lui répondit: Non, mon frère, ne me fais pas violence; car cela n’est pas permis en Israël; ne fais pas cette folie.
13 Kodi ukuganiza bwanji za ine? Kodi manyazi anga ndidzawachotsa bwanji? Ndipo nanga iweyo? Udzakhalatu monga mmodzi mwa zitsiru zoyipitsitsa muno mu Israeli. Chonde kapemphe kwa mfumu. Sadzakuletsa kuti undikwatire.”
Car moi, je ne pourrai supporter mon opprobre, et toi, tu seras comme un des insensés en Israël; mais plutôt parle au roi, et il ne me refusera pas à toi.
14 Koma sanamvere zimene amanena Tamara ndipo popeza anali wamphamvu kuposa Tamarayo, iye anamugwirira.
Or, il ne voulut point acquiescer à ses prières, mais plus fort, il lui fit violence, et il reposa avec elle.
15 Atatero Amnoni anadana naye kwambiri. Iyeyo anamuda kuposa momwe anamukondera. Amnoni anati, “Dzuka ndipo tuluka!”
Aussitôt Amnon la prit en très grande haine, de sorte que la haine dont il la haïssait était plus grande que l’amour dont il l’avait aimée auparavant. Aussi Amnon lui dit: Lève-toi et va-t’en.
16 Iye anayankha, “Ayi! Kundithamangitsa kukhala kulakwa kwakukulu kuposa zimene wachita kale kwa ine.” Koma anakana kumumvera.
Thamar lui répondit: Le mal que tu fais maintenant en me chassant, est plus grand que celui que tu as fait auparavant. Et il ne voulut pas l’écouter;
17 Amnoni anayitana wantchito wake ndipo anati, “Mutulutse mkazi uyu muno ndipo utseke chitseko akatuluka.”
Mais, ayant appelé le jeune homme qui le servait, il dit: Eloigne celle-là de moi, fais-la sortir, et ferme la porte après elle.
18 Choncho wantchito wakeyo anamutulutsa ndipo anatseka chitseko atatuluka. Tamara anali atavala mkanjo wokongoletsedwa kwambiri, pakuti ichi chinali chovala chimene ana aakazi a mfumu amene sanagonepo ndi mwamuna amavala.
Thamar était vêtue d’une robe traînante, car c’est de cette sorte de vêtements que les filles du roi, qui étaient vierges, faisaient usage. C’est pourquoi son serviteur la mit dehors, et ferma la porte derrière elle.
19 Tamara anatsira phulusa pamutu pake ndipo anangʼamba mkanjo wokongoletsedwa umene anavalawo. Iye anagwira manja ake kumutu ndipo anachoka, akulira mokweza pamene amapita.
Thamar, répandant de la cendre sur sa tête, déchirant sa robe traînante, et les mains posées sur sa tête, allait marchant et criant.
20 Mlongo wake Abisalomu anati, “Kodi Amnoni uja mlongo wako wagona nawe? Khala chete mlongo wanga. Iye uja ndi mlongo wako ndipo usazilabadire.” Choncho Tamara anakhala mʼnyumba ya Abisalomu mlongo wake ngati woferedwa.
Or, Absalom, son frère, lui demanda: Est-ce qu’Amnon, ton frère, a dormi avec toi? Mais maintenant, ma sœur, garde le silence, c’est ton frère; n’afflige pas ton cœur pour cela. C’est pourquoi Thamar demeura, se desséchant, dans la maison d’Absalom, son frère.
21 Mfumu Davide itamva zimenezi, inakwiya kwambiri.
Mais lorsque le roi David eut appris ces choses, il fut très centriste, et il ne voulut point contrister l’esprit d’Amnon, son fils, car il le chérissait, parce qu’il était son premier-né.
22 Abisalomu sananene mawu aliwonse kwa Amnoni; abwino kapena oyipa. Iye anamuda Amunoniyo chifukwa anachititsa manyazi mlongo wake Tamara.
Or, Absalom ne dit rien à Amnon, ni mal, ni bien; car Absalom haïssait Amnon, parce qu’il avait violé Thamar, sa sœur.
23 Patapita zaka ziwiri, pamene wometa nkhosa za Abisalomu anali ku Baala-Hazori pafupi ndi malire a fuko la Efereimu, iye anayitana ana onse aamuna a mfumu kuti apite kumeneko.
Mais il arriva, après un intervalle de deux ans, qu’on tondait les brebis d’Absalom, à Baalhasor près d’Ephraïm; et Absalom appela tous les fils du roi.
24 Abisalomu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Ometa nkhosa za mtumiki wanu anabwera. Chonde mfumu ndi akuluakulu anu mubwere kudzakhala nane?”
Et il vint vers le roi, et lui dit: Voilà qu’on tond les brebis de votre serviteur, je prie le roi qu’il vienne avec ses serviteurs chez son serviteur.
25 Mfumu inayankha kuti, “Ayi mwana wanga, tisapite tonsefe. Tidzakhala cholemetsa kwa iwe.” Ngakhale Abisalomu anayesetsa kuwumiriza mfumuyo, inakana kupita. Mʼmalo mwake inangomudalitsa Abisalomuyo.
Et le roi répondit à Absalom: Non, mon fils, ne demande pas que nous venions tous, et que nous te gênions. Mais, comme Absalom le pressait, et qu’il ne voulait pas y aller, il le bénit.
26 Kenaka Abisalomu anati, “Ngati sizitero, chonde mulole mʼbale wanga Amnoni apite nane.” Mfumu inamufunsa kuti, “Apite nawe chifukwa chiyani?”
Alors Absalom lui dit: Si vous ne voulez pas venir, je vous prie qu’au moins Amnon, mon frère, vienne avec nous. Et le roi lui répondit: Il n’est pas nécessaire qu’il aille avec toi.
27 Koma Abisalomu anamuwumiriza, kotero analola kuti Amnoni pamodzi ndi ana onse a mfumu apite naye.
C’est pourquoi Absalom lui fit des instances, et David laissa aller avec lui Amnon et tous les fils du roi. Or, Absalom avait préparé un festin comme un festin de roi.
28 Abisalomu analamula antchito ake kuti, “Tamverani! Amnoni akakaledzera ndi vinyo ndipo ine ndikakanena kuti, ‘Mukantheni Amnoni,’ pamenepo mukamuphe. Musakachite mantha. Kodi ine sindinakulamuleni? Mukhale amphamvu ndipo mulimbe mtima.”
Et Absalom avait ordonné à ses serviteurs, disant: Faites attention, lorsqu’Amnon sera troublé par le vin, et que je vous dirai: Frappez-le, et le tuez; ne craignez point; car c’est moi qui vous l’ordonne. Fortifiez-vous, et soyez des hommes courageux.
29 Kotero antchito a Abisalomu anachita kwa Amnoni zimene Abisalomu anawalamula. Kenaka ana onse a mfumu anayimirira ndipo anakwera pa abulu awo nathawa.
Les serviteurs d’Absalom firent donc contre Amnon, comme leur avait ordonné Absalom. Et tous les fils du roi se levant montèrent chacun sur leur mule, et s’enfuirent.
30 Ali mʼnjira, Davide anamva mphekesera yakuti, “Abisalomu wakantha ana onse a mfumu ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene watsala.”
Et comme ils poursuivaient encore leur chemin, le bruit en vint jusqu’à David; on dit: Absalom a tué tous les fils du roi; il n’en est pas resté même un seul.
31 Mfumu inayimirira, ningʼamba zovala zake ndi kugona pa dothi. Antchito ake onse anayimirira pomwepo atangʼamba zovala zawo.
C’est pourquoi le roi se leva, et déchira ses vêtements, et tomba sur la terre; et tous ses serviteurs qui étaient près de lui déchirèrent leurs vêtements.
32 Koma Yehonadabu mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anati, “Mbuye wanga mfumu musaganize kuti wapha ana onse a mfumu; wafa ndi Amnoni yekha. Awa ndiwo akhala maganizo a Abisalomu kuyambira tsiku limene Amnoni anagwirira mlongo wake Tamara.
Or, Jonadab, fils de Semmaa, frère de David, prenant la parole, dit: Que mon seigneur le roi ne croie pas que tous les jeunes hommes fils du roi aient été tués: Amnon seul est mort, parce qu’il avait été mis dans la bouche d’Absalom, depuis le jour qu’il fit violence à Thamar, sa sœur.
33 Mbuye wanga mfumu musavutike ndi maganizo ndi nkhani yoti ana onse a mfumu afa. Wafa ndi Amnoni yekha.”
Maintenant donc, que mon seigneur le roi ne mette point cela en son esprit, disant: Tous les fils du roi ont été tués, puisqu’Amnon seul est mort.
34 Nthawi imeneyi nʼkuti Abisalomu atathawa. Tsono munthu amene amalondera anayangʼana ndipo anaona anthu ambiri pa msewu wa kumadzulo kwake, akubwera kutsetsereka phiri. Mlondayo anapita kukawuza mfumu kuti, “Ndikuona anthu pa njira ya Horonaimu, mʼmbali mwa phiri.”
Mais Absalom s’enfuit, et la jeune sentinelle leva ses yeux, et regarda; et voilà qu’un peuple nombreux venait par un chemin détourné du côté de la montagne.
35 Yehonadabu anati kwa mfumu, “Taonani ana a mfumu afika. Zachitika monga momwe mtumiki wanu ananenera.”
Or. Jonadab dit au roi: Voici les fils du roi qui viennent: selon la parole de votre serviteur, ainsi il est arrivé.
36 Pamene amatsiriza kuyankhula, ana a mfumu analowa, akulira mofuwula. Mfumunso ndi antchito ake onse analira mokhudzidwa.
Et lorsqu’il eut cessé de parler, parurent les fils du roi; et, entrant, ils élevèrent leurs voix et pleurèrent; mais le roi aussi et tous ses serviteurs pleurèrent d’un très grand pleur.
37 Abisalomu anathawa, napita kwa Talimai mwana wa Amihudi, mfumu ya ku Gesuri. Koma mfumu Davide inalira mwana wake tsiku ndi tsiku.
Ainsi Absalom fuyant s’en alla auprès de Tholomaï, fils d’Ammiud, roi de Gessur. David pleura donc son fils, tous les jours.
38 Abisalomu atathawa ndi kupita ku Gesuri, anakhala kumeneko zaka zitatu.
Or Absalom, lorsqu’il se fut enfui, et qu’il fut venu à Gessur, fut là pendant trois ans.
39 Ndipo Davide anagwidwa ndi chifundo chofuna kumulondola Abisalomu pakuti anali atatonthozedwa pa imfa ya Amnoni.
Et le roi David cessa de poursuivre Absalom, parce qu’il s’était consolé de la mort d’Amnon.