< 2 Samueli 13 >

1 Patapita nthawi, Amnoni mwana wa Davide anakonda Tamara, mlongo wa Abisalomu, mwana wa Davide, amene anali wokongola.
Forsothe it was doon aftir these thingis, that Amon, the sone of Dauid, louyde the faireste sistir, Thamar bi name, of Absolon, sone of Dauid.
2 Amnoni sankagona tulo mpaka anadwala chifukwa cha Tamara mlongo wakeyo, pakuti iye anali asanagonepo ndi mwamuna ndipo zimaoneka kuti zinali zosatheka kuti achite chilichonse kwa iye.
And Amon perischide greetli for hir, so that he was sijk for `the loue of hir. For whanne she was a virgyn, it semyde hard to hym, that he schulde do ony thing vnonestli with hir.
3 Koma Amnoni anali ndi mnzake dzina lake Yehonadabu mwana wamwamuna wa Simea, mʼbale wake wa Davide. Yonadabu anali munthu wochenjera kwambiri.
Forsothe a freend, Jonadab bi name, sone of Semmaa, brother of Dauid, `was to Amon; Jonadab was a ful prudent man.
4 Iye anafunsa Amnoni, “Nʼchifukwa chiyani iwe mwana wa mfumu, umaoneka wowonda mmawa uliwonse? Bwanji wosandiwuza?” Amnoni anamuyankha kuti, “Ine ndamukonda Tamara, mlongo wa mʼbale wanga Abisalomu.”
Which seide to Amon, Sone of the kyng, whi art thou maad feble so bi leenesse bi alle daies? whi schewist thou not to me? And Amon seide to him, Y loue Thamar, the sister of my brother Absolon.
5 Yehonadabu anati, “Pita ukagone ndipo unamizire kudwala. Abambo ako akabwera kudzakuona, udzati kwa iwo, Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara abwere kuti adzandikonzere chakudya kuti ndidye. Adzandikonzere chakudyacho ine ndikumuona ndi kudya chili mʼmanja mwake.”
And Jonadab answeride to hym, Li thou on thi bed, and feyne thou sikenesse; and whanne thi fadir cometh, that he visyte thee, seie thou to hym, Y preye, come Thamar, my sister, that sche yyue mete to me, and make a seew, that Y ete of hir hond.
6 Kotero Amnoni anagona nakhala ngati akudwala. Mfumu itabwera kudzamuona, Amnoni anati kwa iyo, “Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara kuti abwere adzandipangire buledi wapamwamba ineyo ndikuona, kuti ndidye ali mʼmanja mwake.”
Therfor Amon lay doun, and `bigan as to be sijk. And whanne the kyng hadde come to visite him, Amon seide to the kyng, Y biseche, come Thamar, my sistir, that sche make twei soupyngis bifor my iyen, and that Y take of hir hond meete maad redi.
7 Davide anatumiza mawu kwa Tamara ku nyumba yaufumu kuti, “Pita ku nyumba ya mlongo wako Amnoni ndipo ukamukonzere chakudya.”
Therfor Dauid sente to the hows of Thamar, and seide, Come thou in to the hows of Amon, thi brother, and make thou seew to hym.
8 Choncho Tamara anapitadi ku nyumba ya mlongo wake Amnoni kumalo kumene ankagona. Anakanda ufa, nawumba buledi Amunoniyo akuona ndipo anaphika bulediyo.
And Thamar cam in to the hows of Amon, hir brother. Sotheli he lai; and sche took mele, and medlide, and made moist bifor hise iyen, and sethide soupyngis;
9 Kenaka iye anatenga chiwaya ndipo anamupatsa bulediyo, koma iyeyo anakana. Amnoni anati “Uza aliyense atuluke muno.” Ndipo aliyense anatuluka.
and sche took that, that sche hadde sode, and helde out, and settide byfor hym, and he nolde ete. And Amon seide, Putte ye out alle men fro me. And whanne thei hadden put out alle men,
10 Kenaka Amnoni anati kwa Tamara, “Bweretsa chakudya kuno, ku chipinda changa chogona kuti ndidye chili mʼmanja mwako.” Ndipo Tamara anatenga buledi amene anapanga ndi kubwera naye kwa mlongo wake ku chipinda chake.
Amon seide to Thamar, Bere the mete in to the closet, that Y ete of thin hond. Therfor Thamar took the soupingis whiche sche hadde maad, and brouyte in to Amon, hir brother, in the closet.
11 Koma atabweretsa kwa iye kuti adye, anamugwira ndipo anati, “Bwera ugone nane, iwe mlongo wanga.”
And whanne sche hadde proferid mete to hym, he took hir, and seide, Come thou, my sistir, li thou with me.
12 Tamara anati kwa iye, “Ayi mlongo wanga! Usandikakamize. Zotere siziyenera kuchitika mu Israeli! Usachite chinthu choyipa chotere.
And sche answeride to hym, My brother, nyle thou, nyle thou oppresse me, for this is not leueful in Israel; nyle thou do this foli.
13 Kodi ukuganiza bwanji za ine? Kodi manyazi anga ndidzawachotsa bwanji? Ndipo nanga iweyo? Udzakhalatu monga mmodzi mwa zitsiru zoyipitsitsa muno mu Israeli. Chonde kapemphe kwa mfumu. Sadzakuletsa kuti undikwatire.”
For Y schal not mow bere my schenschip, and thou schalt be as oon of the vnwise men in Israel; but rather speke thou to the kyng, and he schal not denye me to thee.
14 Koma sanamvere zimene amanena Tamara ndipo popeza anali wamphamvu kuposa Tamarayo, iye anamugwirira.
Sotheli he nolde assente to hir preieris; but he was strengere in myytis, and oppresside hir, and lay with hir.
15 Atatero Amnoni anadana naye kwambiri. Iyeyo anamuda kuposa momwe anamukondera. Amnoni anati, “Dzuka ndipo tuluka!”
And `Amon hadde hir hateful bi ful grete haterede, so that the hatrede was gretter, bi which he hatide hir, than the loue bi which he louyde hir bifor. And Amon seide to hir, Rise thou, and go.
16 Iye anayankha, “Ayi! Kundithamangitsa kukhala kulakwa kwakukulu kuposa zimene wachita kale kwa ine.” Koma anakana kumumvera.
And sche answeride to hym, This yuel is more which thou doist now ayens me, and puttist me out, than that, that thou didist bifore. And he nolde here hir; but whanne the child was clepide,
17 Amnoni anayitana wantchito wake ndipo anati, “Mutulutse mkazi uyu muno ndipo utseke chitseko akatuluka.”
that mynystride to hym, he seide, Putte thou out this womman fro me, and close thou the dore aftir hir.
18 Choncho wantchito wakeyo anamutulutsa ndipo anatseka chitseko atatuluka. Tamara anali atavala mkanjo wokongoletsedwa kwambiri, pakuti ichi chinali chovala chimene ana aakazi a mfumu amene sanagonepo ndi mwamuna amavala.
And sche was clothid with a coote doun to the heele; for the kyngis douytris virgyns vsiden siche clothis. Therfor the mynystre of Amon puttide hir out, and closide the dore aftir hir.
19 Tamara anatsira phulusa pamutu pake ndipo anangʼamba mkanjo wokongoletsedwa umene anavalawo. Iye anagwira manja ake kumutu ndipo anachoka, akulira mokweza pamene amapita.
And sche spreynte aische to hir heed, whanne the coote to `the heele was to-rent, and whanne the hondis weren put on hir heed, and sche yede entrynge and criynge.
20 Mlongo wake Abisalomu anati, “Kodi Amnoni uja mlongo wako wagona nawe? Khala chete mlongo wanga. Iye uja ndi mlongo wako ndipo usazilabadire.” Choncho Tamara anakhala mʼnyumba ya Abisalomu mlongo wake ngati woferedwa.
Forsothe Absolon, hir brother, seide to hir, Whether Amon, thi brothir, hath leyn with thee? But `now, sister, be stille; he is thi brother, and turmente not thin herte for this thing. Therfor Thamar dwellide morenynge in the hows of Absolon, hir brothir.
21 Mfumu Davide itamva zimenezi, inakwiya kwambiri.
Forsothe whanne `kyng Dauid hadde herd these wordis, he was ful sori, and he nolde make sore the spyrit of Amon, his sone; for he louyde Amon, for he was the firste gendrid `to hym.
22 Abisalomu sananene mawu aliwonse kwa Amnoni; abwino kapena oyipa. Iye anamuda Amunoniyo chifukwa anachititsa manyazi mlongo wake Tamara.
Forsothe Absolon spak not to Amon, nether yuel nether good; for Absolon hatide Amon, for he hadde defoulid Thamar, his sistir.
23 Patapita zaka ziwiri, pamene wometa nkhosa za Abisalomu anali ku Baala-Hazori pafupi ndi malire a fuko la Efereimu, iye anayitana ana onse aamuna a mfumu kuti apite kumeneko.
Forsothe it was doon aftir the tyme of twei yeer, that the scheep of Absolon weren shorun in Baalasor, which is bisidis Effraym. And Absolon clepide alle the sones of the kyng.
24 Abisalomu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Ometa nkhosa za mtumiki wanu anabwera. Chonde mfumu ndi akuluakulu anu mubwere kudzakhala nane?”
And he cam to the kyng, and seide to hym, Lo! the scheep of thi seruaunt ben schorun; Y preye, come the king with hise seruauntis to his seruaunt.
25 Mfumu inayankha kuti, “Ayi mwana wanga, tisapite tonsefe. Tidzakhala cholemetsa kwa iwe.” Ngakhale Abisalomu anayesetsa kuwumiriza mfumuyo, inakana kupita. Mʼmalo mwake inangomudalitsa Abisalomuyo.
And the kyng seide to Absolon, Nyle thou, my sone, nyle thou preye, that alle we come, and greeue thee. Forsothe whanne he constreynede Dauid, and he nolde go, he blesside Absolon.
26 Kenaka Abisalomu anati, “Ngati sizitero, chonde mulole mʼbale wanga Amnoni apite nane.” Mfumu inamufunsa kuti, “Apite nawe chifukwa chiyani?”
And Absolon seide to Dauid, If thou nylt come, Y byseche, come nameli Amon, my brother, with vs. And the kyng seide to hym, It is no nede, that he go with thee.
27 Koma Abisalomu anamuwumiriza, kotero analola kuti Amnoni pamodzi ndi ana onse a mfumu apite naye.
Therfor Absolon constreynede hym; and he delyuerede with him Amon, and alle the sones of the kyng. And Absolon hadde maad a feeste as the feeste of a kyng.
28 Abisalomu analamula antchito ake kuti, “Tamverani! Amnoni akakaledzera ndi vinyo ndipo ine ndikakanena kuti, ‘Mukantheni Amnoni,’ pamenepo mukamuphe. Musakachite mantha. Kodi ine sindinakulamuleni? Mukhale amphamvu ndipo mulimbe mtima.”
Sotheli Absolon comaundide to hise children, and seide, Aspie ye, whanne Amon is drunkun of wyn, and Y seie to you, Smyte ye, and sle hym. Nyle ye drede, for Y am that comaunde to you; be ye strengthid, and be ye stronge men.
29 Kotero antchito a Abisalomu anachita kwa Amnoni zimene Abisalomu anawalamula. Kenaka ana onse a mfumu anayimirira ndipo anakwera pa abulu awo nathawa.
Therfor the children of Absolon diden ayens Amon, as Absolon hadde comaundide to hem; and alle the sones of the kyng risiden, and stieden ech on his mule, and fledden.
30 Ali mʼnjira, Davide anamva mphekesera yakuti, “Abisalomu wakantha ana onse a mfumu ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene watsala.”
And whanne thei yeden yit in the weie, fame cam to the kyng, and seide, Absolon hath kild alle the sones of the king, and `nameli not oon lefte of hem.
31 Mfumu inayimirira, ningʼamba zovala zake ndi kugona pa dothi. Antchito ake onse anayimirira pomwepo atangʼamba zovala zawo.
Therfor the kyng roos, and to-rente hise clothis, and felde doun on the erthe; and alle hise seruauntis that stoden nyy to hym, to-renten her clothis.
32 Koma Yehonadabu mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anati, “Mbuye wanga mfumu musaganize kuti wapha ana onse a mfumu; wafa ndi Amnoni yekha. Awa ndiwo akhala maganizo a Abisalomu kuyambira tsiku limene Amnoni anagwirira mlongo wake Tamara.
Sotheli Jonadab, sone of Semmaa, brother of Dauid, answeride and seide, My lord the kyng, gesse not, that alle the children, and sones of the kyng, ben slayn; Amon aloone is deed, for he was set in hatrede to Absolon, fro the day in which he oppresside Thamar, his sistir.
33 Mbuye wanga mfumu musavutike ndi maganizo ndi nkhani yoti ana onse a mfumu afa. Wafa ndi Amnoni yekha.”
Now therfor, my lord the kyng, set not this word on his herte, and seie, Alle the sones of the kyng ben slayn; for Amon aloone is deed.
34 Nthawi imeneyi nʼkuti Abisalomu atathawa. Tsono munthu amene amalondera anayangʼana ndipo anaona anthu ambiri pa msewu wa kumadzulo kwake, akubwera kutsetsereka phiri. Mlondayo anapita kukawuza mfumu kuti, “Ndikuona anthu pa njira ya Horonaimu, mʼmbali mwa phiri.”
Forsothe Absolon fledde. And a child aspiere reiside hise iyen, and bihelde, and lo! myche puple cam bi a weye out of the comyn weie bi the side of the hil.
35 Yehonadabu anati kwa mfumu, “Taonani ana a mfumu afika. Zachitika monga momwe mtumiki wanu ananenera.”
And Jonadab seide to the kyng, Lo! the sones of the kyng comen; bi the word of thi seruaunt, so it is doon.
36 Pamene amatsiriza kuyankhula, ana a mfumu analowa, akulira mofuwula. Mfumunso ndi antchito ake onse analira mokhudzidwa.
And whanne he hadde ceessid to speke, also the sones of the kyng apperiden; and thei entriden, and reisiden her vois, and wepten; but also the kyng and alle his seruauntis wepten bi ful greet wepyng.
37 Abisalomu anathawa, napita kwa Talimai mwana wa Amihudi, mfumu ya ku Gesuri. Koma mfumu Davide inalira mwana wake tsiku ndi tsiku.
Forsothe Absolon fledde, and yede to Tholmai, sone of Amyur, the kyng of Gessur. Therfor Dauid biweilide his sone Amon in many daies.
38 Abisalomu atathawa ndi kupita ku Gesuri, anakhala kumeneko zaka zitatu.
Forsothe Absolon, whanne he hadde fled, and hadde come in to Gessur, was there thre yeer.
39 Ndipo Davide anagwidwa ndi chifundo chofuna kumulondola Abisalomu pakuti anali atatonthozedwa pa imfa ya Amnoni.
And Dauid ceesside to pursue Absolon, for he was coumfortid on the deeth of Amon.

< 2 Samueli 13 >