< 2 Samueli 13 >

1 Patapita nthawi, Amnoni mwana wa Davide anakonda Tamara, mlongo wa Abisalomu, mwana wa Davide, amene anali wokongola.
And it came to pass after this, that Amnon the son of David loved the sister of Absalom the son of David, who was very beautiful, and her name was Thamar.
2 Amnoni sankagona tulo mpaka anadwala chifukwa cha Tamara mlongo wakeyo, pakuti iye anali asanagonepo ndi mwamuna ndipo zimaoneka kuti zinali zosatheka kuti achite chilichonse kwa iye.
And he was exceedingly fond of her, so that he fell sick for the love of her: for as she was a virgin, he thought it hard to do any thing dishonestly with her.
3 Koma Amnoni anali ndi mnzake dzina lake Yehonadabu mwana wamwamuna wa Simea, mʼbale wake wa Davide. Yonadabu anali munthu wochenjera kwambiri.
Now Amnon had a friend, named Jonadab the son of Semmaa the brother of David, a very wise man:
4 Iye anafunsa Amnoni, “Nʼchifukwa chiyani iwe mwana wa mfumu, umaoneka wowonda mmawa uliwonse? Bwanji wosandiwuza?” Amnoni anamuyankha kuti, “Ine ndamukonda Tamara, mlongo wa mʼbale wanga Abisalomu.”
And he said to him: Why dost thou grow so lean from day to day, O son of the king? why dost thou not tell me the reason of it? And Amnon said to him: I am in love with Thamar the sister of my brother Absalom.
5 Yehonadabu anati, “Pita ukagone ndipo unamizire kudwala. Abambo ako akabwera kudzakuona, udzati kwa iwo, Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara abwere kuti adzandikonzere chakudya kuti ndidye. Adzandikonzere chakudyacho ine ndikumuona ndi kudya chili mʼmanja mwake.”
And Jonadab said to him: Lie down upon thy bed, and feign thyself sick: and when thy father shall come to visit thee, say to him: Let my sister Thamar, I pray thee, come to me, to give me to eat, and to make me a mess, that I may eat it at her hand.
6 Kotero Amnoni anagona nakhala ngati akudwala. Mfumu itabwera kudzamuona, Amnoni anati kwa iyo, “Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara kuti abwere adzandipangire buledi wapamwamba ineyo ndikuona, kuti ndidye ali mʼmanja mwake.”
So Amnon lay down, and made as if he were sick: and when the king came to visit him, Amnon said to the king: I pray thee let my sister Thamar come, and make in my sight two little messes, that I may eat at her hand.
7 Davide anatumiza mawu kwa Tamara ku nyumba yaufumu kuti, “Pita ku nyumba ya mlongo wako Amnoni ndipo ukamukonzere chakudya.”
Then David sent home to Thamar, saying: Come to the house of thy brother Amnon, and make him a mess.
8 Choncho Tamara anapitadi ku nyumba ya mlongo wake Amnoni kumalo kumene ankagona. Anakanda ufa, nawumba buledi Amunoniyo akuona ndipo anaphika bulediyo.
And Thamar came to the house of Amnon her brother: but he was laid down: and she took meal and tempered it: and dissolving it in his sight she made little messes.
9 Kenaka iye anatenga chiwaya ndipo anamupatsa bulediyo, koma iyeyo anakana. Amnoni anati “Uza aliyense atuluke muno.” Ndipo aliyense anatuluka.
And taking what she had boiled, she poured it out, and set it before him, but he would not eat: and Amnon said: Put out all persons from me. And when they had put all persons out,
10 Kenaka Amnoni anati kwa Tamara, “Bweretsa chakudya kuno, ku chipinda changa chogona kuti ndidye chili mʼmanja mwako.” Ndipo Tamara anatenga buledi amene anapanga ndi kubwera naye kwa mlongo wake ku chipinda chake.
Amnon said to Thamar: Bring the mess into the chamber, that I may eat at thy hand. And Thamar took the little messes which she had made, and brought them in to her brother Amnon in the chamber.
11 Koma atabweretsa kwa iye kuti adye, anamugwira ndipo anati, “Bwera ugone nane, iwe mlongo wanga.”
And when she had presented him the meat, he took hold of her, and said: Come lie with me, my sister.
12 Tamara anati kwa iye, “Ayi mlongo wanga! Usandikakamize. Zotere siziyenera kuchitika mu Israeli! Usachite chinthu choyipa chotere.
She answered him: Do not so, my brother, do not force me: for no such thing must be done in Israel. Do not thou this folly.
13 Kodi ukuganiza bwanji za ine? Kodi manyazi anga ndidzawachotsa bwanji? Ndipo nanga iweyo? Udzakhalatu monga mmodzi mwa zitsiru zoyipitsitsa muno mu Israeli. Chonde kapemphe kwa mfumu. Sadzakuletsa kuti undikwatire.”
For I shall not be able to bear my shame, and thou shalt be as one of the fools in Israel: but rather speak to the king, and he will not deny me to thee.
14 Koma sanamvere zimene amanena Tamara ndipo popeza anali wamphamvu kuposa Tamarayo, iye anamugwirira.
But he would not hearken to her prayers, but being stronger overpowered her and lay with her.
15 Atatero Amnoni anadana naye kwambiri. Iyeyo anamuda kuposa momwe anamukondera. Amnoni anati, “Dzuka ndipo tuluka!”
Then Amnon hated her with an exceeding great hatred: so that the hatred wherewith he hated her was greater than the love with which he had loved her before, And Amnon said to her: Arise, and get thee gone.
16 Iye anayankha, “Ayi! Kundithamangitsa kukhala kulakwa kwakukulu kuposa zimene wachita kale kwa ine.” Koma anakana kumumvera.
She answered him: This evil which now thou dost against me, in driving me away, is greater than that which thou didst before. And he would not hearken to her:
17 Amnoni anayitana wantchito wake ndipo anati, “Mutulutse mkazi uyu muno ndipo utseke chitseko akatuluka.”
But calling the servants that ministered to him, he said: Thrust this woman out from me: and shut the door after her.
18 Choncho wantchito wakeyo anamutulutsa ndipo anatseka chitseko atatuluka. Tamara anali atavala mkanjo wokongoletsedwa kwambiri, pakuti ichi chinali chovala chimene ana aakazi a mfumu amene sanagonepo ndi mwamuna amavala.
And she was clothed with along robe: for the king’s daughters that were virgins, used such kind of garments. Then his servant thrust her out: and shut the door after her.
19 Tamara anatsira phulusa pamutu pake ndipo anangʼamba mkanjo wokongoletsedwa umene anavalawo. Iye anagwira manja ake kumutu ndipo anachoka, akulira mokweza pamene amapita.
And she put ashes on her head, and rent her long robe and laid her hands upon her head, and went on crying.
20 Mlongo wake Abisalomu anati, “Kodi Amnoni uja mlongo wako wagona nawe? Khala chete mlongo wanga. Iye uja ndi mlongo wako ndipo usazilabadire.” Choncho Tamara anakhala mʼnyumba ya Abisalomu mlongo wake ngati woferedwa.
And Absalom her brother said to her: Hath thy brother Amnon lain with thee? but now, sister, hold thy peace, he is thy brother: and afflict not thy heart for this thing. So Thamar remained pining away in the house of Absalom her brother.
21 Mfumu Davide itamva zimenezi, inakwiya kwambiri.
And when king David heard of these things he was exceedingly grieved: and he would not afflict the spirit of his son Amnon, for he loved him, because he was his firstborn.
22 Abisalomu sananene mawu aliwonse kwa Amnoni; abwino kapena oyipa. Iye anamuda Amunoniyo chifukwa anachititsa manyazi mlongo wake Tamara.
But Absalom spoke not to Amnon neither good nor evil: for Absalom hated Amnon because he had ravished his sister Thamar.
23 Patapita zaka ziwiri, pamene wometa nkhosa za Abisalomu anali ku Baala-Hazori pafupi ndi malire a fuko la Efereimu, iye anayitana ana onse aamuna a mfumu kuti apite kumeneko.
And it came to pass after two years, that the sheep of Absalom were shorn in Baalhasor, which is near Ephraim: and Absalom invited all the king’s sons:
24 Abisalomu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Ometa nkhosa za mtumiki wanu anabwera. Chonde mfumu ndi akuluakulu anu mubwere kudzakhala nane?”
And he came to the king, and said to him: Behold thy servant’s sheep are shorn. Let the king, I pray, with his servants come to his servant.
25 Mfumu inayankha kuti, “Ayi mwana wanga, tisapite tonsefe. Tidzakhala cholemetsa kwa iwe.” Ngakhale Abisalomu anayesetsa kuwumiriza mfumuyo, inakana kupita. Mʼmalo mwake inangomudalitsa Abisalomuyo.
And the king said to Absalom: Nay, my son, do not ask that we should all come, and be chargeable to thee. And when he pressed him, and he would not go, he blessed him.
26 Kenaka Abisalomu anati, “Ngati sizitero, chonde mulole mʼbale wanga Amnoni apite nane.” Mfumu inamufunsa kuti, “Apite nawe chifukwa chiyani?”
And Absalom said: If thou wilt not come, at least let my brother Amnon, I beseech thee, come with us. And the king said to him: It is not necessary that he should go with thee.
27 Koma Abisalomu anamuwumiriza, kotero analola kuti Amnoni pamodzi ndi ana onse a mfumu apite naye.
But Absalom pressed him, so that he let Amnon and all the king’s sons go with him. And Absalom made a feast as it were the feast of a king.
28 Abisalomu analamula antchito ake kuti, “Tamverani! Amnoni akakaledzera ndi vinyo ndipo ine ndikakanena kuti, ‘Mukantheni Amnoni,’ pamenepo mukamuphe. Musakachite mantha. Kodi ine sindinakulamuleni? Mukhale amphamvu ndipo mulimbe mtima.”
And Absalom had commanded his servants, saying: Take notice when Amnon shall be drunk with wine, and when I shall say to you: Strike him, and kill him, fear not: for it is I that command you: take courage, and be valiant men.
29 Kotero antchito a Abisalomu anachita kwa Amnoni zimene Abisalomu anawalamula. Kenaka ana onse a mfumu anayimirira ndipo anakwera pa abulu awo nathawa.
And the servants of Absalom did to Amnon as Absalom had commanded them. And all the king’s sons arose and got up every man upon his mule, and fled.
30 Ali mʼnjira, Davide anamva mphekesera yakuti, “Abisalomu wakantha ana onse a mfumu ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene watsala.”
And while they were yet in the way, a rumour came to David, saying: Absalom hath slain all the king’s sons, and there is not one of them left.
31 Mfumu inayimirira, ningʼamba zovala zake ndi kugona pa dothi. Antchito ake onse anayimirira pomwepo atangʼamba zovala zawo.
Then the king rose up, and rent his garments: and fell upon the ground, and all his servants, that stood about him, rent their garments.
32 Koma Yehonadabu mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anati, “Mbuye wanga mfumu musaganize kuti wapha ana onse a mfumu; wafa ndi Amnoni yekha. Awa ndiwo akhala maganizo a Abisalomu kuyambira tsiku limene Amnoni anagwirira mlongo wake Tamara.
But Jonadab the son of Semmaa David’s brother answering, said: Let not my lord the king think that all the king’s sons are slain: Amnon only is dead, for he was appointed by the mouth of Absalom from the day that he ravished his sister Thamar.
33 Mbuye wanga mfumu musavutike ndi maganizo ndi nkhani yoti ana onse a mfumu afa. Wafa ndi Amnoni yekha.”
Now therefore let not my lord the king take this thing into his heart, saying: All the king’s sons are slain: for Amnon only is dead.
34 Nthawi imeneyi nʼkuti Abisalomu atathawa. Tsono munthu amene amalondera anayangʼana ndipo anaona anthu ambiri pa msewu wa kumadzulo kwake, akubwera kutsetsereka phiri. Mlondayo anapita kukawuza mfumu kuti, “Ndikuona anthu pa njira ya Horonaimu, mʼmbali mwa phiri.”
But Absalom fled away: and the young man that kept the watch, lifted up his eyes and looked, and behold there came much people by a by-way on the side of the mountain.
35 Yehonadabu anati kwa mfumu, “Taonani ana a mfumu afika. Zachitika monga momwe mtumiki wanu ananenera.”
And Jonadab said to the king: Behold the king’s sons are come: as thy servant said, so it is.
36 Pamene amatsiriza kuyankhula, ana a mfumu analowa, akulira mofuwula. Mfumunso ndi antchito ake onse analira mokhudzidwa.
And when he made an end of speaking, the king’s sons also appeared: and coming in they lifted up their voice, and wept: and the king also and all his servants wept very much.
37 Abisalomu anathawa, napita kwa Talimai mwana wa Amihudi, mfumu ya ku Gesuri. Koma mfumu Davide inalira mwana wake tsiku ndi tsiku.
But Absalom fled, and went to Tholomai the son of Ammiud the king of Gessur. And David mourned for his son every day.
38 Abisalomu atathawa ndi kupita ku Gesuri, anakhala kumeneko zaka zitatu.
And Absalom after he was fled, and come into Gessur, was there three years.
39 Ndipo Davide anagwidwa ndi chifundo chofuna kumulondola Abisalomu pakuti anali atatonthozedwa pa imfa ya Amnoni.
And king David ceased to pursue after Absalom, because he was comforted concerning the death of Amnon.

< 2 Samueli 13 >