< 2 Samueli 13 >

1 Patapita nthawi, Amnoni mwana wa Davide anakonda Tamara, mlongo wa Abisalomu, mwana wa Davide, amene anali wokongola.
此後,還發生了一件事:達味的兒子阿貝沙隆有個妹妹,名叫塔瑪爾,很是美麗,達味的兒子阿默農很愛她。
2 Amnoni sankagona tulo mpaka anadwala chifukwa cha Tamara mlongo wakeyo, pakuti iye anali asanagonepo ndi mwamuna ndipo zimaoneka kuti zinali zosatheka kuti achite chilichonse kwa iye.
阿默農為了他妹妹塔瑪爾的緣故,竟憂愁悶成疾;因為她還是處女,所以在阿默農看來,對她行事幾乎不可能。
3 Koma Amnoni anali ndi mnzake dzina lake Yehonadabu mwana wamwamuna wa Simea, mʼbale wake wa Davide. Yonadabu anali munthu wochenjera kwambiri.
阿默農有個朋友,名叫約納達布,是達味的兄弟史默亞的兒子。約納達布是一個很狡滑的人。
4 Iye anafunsa Amnoni, “Nʼchifukwa chiyani iwe mwana wa mfumu, umaoneka wowonda mmawa uliwonse? Bwanji wosandiwuza?” Amnoni anamuyankha kuti, “Ine ndamukonda Tamara, mlongo wa mʼbale wanga Abisalomu.”
他向阿默農說:「太子,為什麼你一天一天如此萎靡不振﹖你不肯告訴我嗎﹖」阿默農回答說:「我愛上我兄弟阿貝沙隆的妹妹塔瑪爾」。
5 Yehonadabu anati, “Pita ukagone ndipo unamizire kudwala. Abambo ako akabwera kudzakuona, udzati kwa iwo, Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara abwere kuti adzandikonzere chakudya kuti ndidye. Adzandikonzere chakudyacho ine ndikumuona ndi kudya chili mʼmanja mwake.”
約納達布向他說:「你在躺床裝病,你父親來看你時,你就對他說:我很希望我的妹妹塔瑪爾來,給我準備食物,她要在我眼前準備,叫我看看著,並且由她手中取食。
6 Kotero Amnoni anagona nakhala ngati akudwala. Mfumu itabwera kudzamuona, Amnoni anati kwa iyo, “Ine ndikufuna mlongo wanga Tamara kuti abwere adzandipangire buledi wapamwamba ineyo ndikuona, kuti ndidye ali mʼmanja mwake.”
阿默農就臥床裝病,君王來看他時,阿默農向君王說:「求你叫我妹妹塔瑪爾來,在我前做兩塊餅,好叫我從她手中取食」。
7 Davide anatumiza mawu kwa Tamara ku nyumba yaufumu kuti, “Pita ku nyumba ya mlongo wako Amnoni ndipo ukamukonzere chakudya.”
達味就派人到塔瑪爾房中說:「請妳到妳哥哥房裏去,給他準備食物」。
8 Choncho Tamara anapitadi ku nyumba ya mlongo wake Amnoni kumalo kumene ankagona. Anakanda ufa, nawumba buledi Amunoniyo akuona ndipo anaphika bulediyo.
塔瑪爾到了她哥哥阿默農房裏,他正躺在床上。她取了麵,在他眼前和好,烤成餅。
9 Kenaka iye anatenga chiwaya ndipo anamupatsa bulediyo, koma iyeyo anakana. Amnoni anati “Uza aliyense atuluke muno.” Ndipo aliyense anatuluka.
她就拿過鍋來,在他面前將餅倒出,他卻推辭不吃。阿默農說:「妳叫眾人都由面前出去」。眾人就都由他面前出去了。
10 Kenaka Amnoni anati kwa Tamara, “Bweretsa chakudya kuno, ku chipinda changa chogona kuti ndidye chili mʼmanja mwako.” Ndipo Tamara anatenga buledi amene anapanga ndi kubwera naye kwa mlongo wake ku chipinda chake.
阿默農對塔瑪爾說:「妳給我把食物拿到內室來,好叫我由妳手中取食」。塔瑪爾拿著她做的餅,進了內室,送到她哥哥阿默農前。
11 Koma atabweretsa kwa iye kuti adye, anamugwira ndipo anati, “Bwera ugone nane, iwe mlongo wanga.”
她正遞給他時,他就抓住她說:「我的妹妹,來與我同寢! 」
12 Tamara anati kwa iye, “Ayi mlongo wanga! Usandikakamize. Zotere siziyenera kuchitika mu Israeli! Usachite chinthu choyipa chotere.
她回答說:「我的哥哥! 不可這樣,不要作賤我! 在以色列不應作這樣 木事,不要作這愚蠢的事!
13 Kodi ukuganiza bwanji za ine? Kodi manyazi anga ndidzawachotsa bwanji? Ndipo nanga iweyo? Udzakhalatu monga mmodzi mwa zitsiru zoyipitsitsa muno mu Israeli. Chonde kapemphe kwa mfumu. Sadzakuletsa kuti undikwatire.”
我帶著這恥辱到哪裏去呢﹖你在以色列也成了一個愚妄人。請你向君王說明,他決不會拒絕使我屬於你的! 」
14 Koma sanamvere zimene amanena Tamara ndipo popeza anali wamphamvu kuposa Tamarayo, iye anamugwirira.
他卻不肯聽她的話,又比她有力,就強姦了她。
15 Atatero Amnoni anadana naye kwambiri. Iyeyo anamuda kuposa momwe anamukondera. Amnoni anati, “Dzuka ndipo tuluka!”
事後,阿默農立即十分憎恨她,並且他如今對她的憎恨,遠超過以前對她的愛戀,就向她說:「起來,走吧! 」
16 Iye anayankha, “Ayi! Kundithamangitsa kukhala kulakwa kwakukulu kuposa zimene wachita kale kwa ine.” Koma anakana kumumvera.
她答說:「我的哥哥,那不可以。氮趕我走,比你對我所行的,更為無理! 」他卻石聽從她,
17 Amnoni anayitana wantchito wake ndipo anati, “Mutulutse mkazi uyu muno ndipo utseke chitseko akatuluka.”
就叫服侍自己的僕人來,向他說:「把這女人從我這裏趕出去! 她走後,隨鎖上門! 」
18 Choncho wantchito wakeyo anamutulutsa ndipo anatseka chitseko atatuluka. Tamara anali atavala mkanjo wokongoletsedwa kwambiri, pakuti ichi chinali chovala chimene ana aakazi a mfumu amene sanagonepo ndi mwamuna amavala.
她那時穿著彩色長衣,因為君王的女兒,在未出嫁以前,昔日都是如此裝束。他的僕人將她趕出去,隨後鎖上了門。
19 Tamara anatsira phulusa pamutu pake ndipo anangʼamba mkanjo wokongoletsedwa umene anavalawo. Iye anagwira manja ake kumutu ndipo anachoka, akulira mokweza pamene amapita.
塔瑪爾把灰撒在頭上,撕破自己所穿的彩色長衣,雙手抱著頭,一路邊哭邊走。
20 Mlongo wake Abisalomu anati, “Kodi Amnoni uja mlongo wako wagona nawe? Khala chete mlongo wanga. Iye uja ndi mlongo wako ndipo usazilabadire.” Choncho Tamara anakhala mʼnyumba ya Abisalomu mlongo wake ngati woferedwa.
她的哥哥阿貝沙隆問她說:「莫非妳的哥哥阿默農與妳同寢了﹖妹妹,暫且不要出聲,因為他是好的兄弟,不可把這事放在心上! 」塔瑪爾從此就憂悶不樂,住在她哥哥阿貝沙隆家裏。
21 Mfumu Davide itamva zimenezi, inakwiya kwambiri.
達味聽說了這一切事,十分生氣;怛他不願傷他兒子阿默農的心,因為他是長子,格外愛他。
22 Abisalomu sananene mawu aliwonse kwa Amnoni; abwino kapena oyipa. Iye anamuda Amunoniyo chifukwa anachititsa manyazi mlongo wake Tamara.
至於,無論好話歹話,一句也不向阿默農說。他惱恨阿默農,因為他污辱了他妹妹塔瑪爾。
23 Patapita zaka ziwiri, pamene wometa nkhosa za Abisalomu anali ku Baala-Hazori pafupi ndi malire a fuko la Efereimu, iye anayitana ana onse aamuna a mfumu kuti apite kumeneko.
過了兩年,當阿貝沙隆在厄弗辣因的巴耳哈祚爾剪羊毛的時節,阿貝沙隆邀請了君王所有的兒子。
24 Abisalomu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Ometa nkhosa za mtumiki wanu anabwera. Chonde mfumu ndi akuluakulu anu mubwere kudzakhala nane?”
阿貝沙隆來到君王前說:「看,你的僕人剪羊毛的時節,請君王帶著臣僕都到你僕人那裏去! 」
25 Mfumu inayankha kuti, “Ayi mwana wanga, tisapite tonsefe. Tidzakhala cholemetsa kwa iwe.” Ngakhale Abisalomu anayesetsa kuwumiriza mfumuyo, inakana kupita. Mʼmalo mwake inangomudalitsa Abisalomuyo.
君王回答阿貝沙隆說:「我兒,不必如此! 我們不必都去麻煩你」。他雖然懇求,君王仍不願去,只祝福了他。
26 Kenaka Abisalomu anati, “Ngati sizitero, chonde mulole mʼbale wanga Amnoni apite nane.” Mfumu inamufunsa kuti, “Apite nawe chifukwa chiyani?”
阿貝沙隆便說:「至少讓我的兄弟阿默農同我們一起去! 」君王回答說:「為什麼要他同你一起去﹖」
27 Koma Abisalomu anamuwumiriza, kotero analola kuti Amnoni pamodzi ndi ana onse a mfumu apite naye.
阿貝沙隆還是再三懇求,達味便派阿默農和君王所有的兒子,同他一起去了。阿貝沙隆擺設筳席,好像御筳。
28 Abisalomu analamula antchito ake kuti, “Tamverani! Amnoni akakaledzera ndi vinyo ndipo ine ndikakanena kuti, ‘Mukantheni Amnoni,’ pamenepo mukamuphe. Musakachite mantha. Kodi ine sindinakulamuleni? Mukhale amphamvu ndipo mulimbe mtima.”
阿貝沙隆吩咐僕人說:「你們要注意! 阿默農暢飲的時候,我向你們說:刺死阿默農! 你們就打死他,不要害怕,是我吩咐了你們,要大膽勇敢」。
29 Kotero antchito a Abisalomu anachita kwa Amnoni zimene Abisalomu anawalamula. Kenaka ana onse a mfumu anayimirira ndipo anakwera pa abulu awo nathawa.
阿貝沙隆的僕人,就照他所吩咐的,對阿默農做了。君王所有的兒子遂起來,各自騎上騾子逃跑了。
30 Ali mʼnjira, Davide anamva mphekesera yakuti, “Abisalomu wakantha ana onse a mfumu ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene watsala.”
他們還在路上,消息已傳到達味前說:「阿貝沙隆殺了君王所有的兒子,沒有一個幸免」。
31 Mfumu inayimirira, ningʼamba zovala zake ndi kugona pa dothi. Antchito ake onse anayimirira pomwepo atangʼamba zovala zawo.
君王便起來,撕裂了自己的衣服,俯伏在地;他身邊的臣僕,也都撕裂了自己的衣服。
32 Koma Yehonadabu mwana wa Simea, mʼbale wake wa Davide anati, “Mbuye wanga mfumu musaganize kuti wapha ana onse a mfumu; wafa ndi Amnoni yekha. Awa ndiwo akhala maganizo a Abisalomu kuyambira tsiku limene Amnoni anagwirira mlongo wake Tamara.
達味的兄弟史默亞的兒子說道:「我主不要想:所有的青年,君王所有兒子都被殺了;其實只有阿默農一人死了。自從阿默農污辱了他的妹妹塔瑪爾那日起,阿貝沙隆就決定了這事。
33 Mbuye wanga mfumu musavutike ndi maganizo ndi nkhani yoti ana onse a mfumu afa. Wafa ndi Amnoni yekha.”
主君王,且不要將這事放在心上,以為君王所有的兒子都死了,因為只有阿默農一人死了」。
34 Nthawi imeneyi nʼkuti Abisalomu atathawa. Tsono munthu amene amalondera anayangʼana ndipo anaona anthu ambiri pa msewu wa kumadzulo kwake, akubwera kutsetsereka phiri. Mlondayo anapita kukawuza mfumu kuti, “Ndikuona anthu pa njira ya Horonaimu, mʼmbali mwa phiri.”
逃走了。守衛的僕人舉目一望,看見在往曷洛納因山坡的路上,有一大群人下來。守衛的就去報告君王說:「我看見一群人,從曷洛納因山坡的路上下來了」。
35 Yehonadabu anati kwa mfumu, “Taonani ana a mfumu afika. Zachitika monga momwe mtumiki wanu ananenera.”
約納達布就向君王說:「看,執行的兒子回來了,正如你僕人所說的,現在實現了」。
36 Pamene amatsiriza kuyankhula, ana a mfumu analowa, akulira mofuwula. Mfumunso ndi antchito ake onse analira mokhudzidwa.
他剛說完這話,君王的兒子都來到了,放聲大哭;君王和眾臣僕也都號咷痛哭。
37 Abisalomu anathawa, napita kwa Talimai mwana wa Amihudi, mfumu ya ku Gesuri. Koma mfumu Davide inalira mwana wake tsiku ndi tsiku.
同時,阿貝沙隆逃到革叔爾王阿米胡得的兒子塔取買那裏去了。君王天天哀悼自己的兒子。
38 Abisalomu atathawa ndi kupita ku Gesuri, anakhala kumeneko zaka zitatu.
阿貝沙隆逃到革叔爾,在那裏住了三年。
39 Ndipo Davide anagwidwa ndi chifundo chofuna kumulondola Abisalomu pakuti anali atatonthozedwa pa imfa ya Amnoni.
此時,君王的心漸漸不再惱怒阿貝沙隆,對阿默農的死,也不再難過了。

< 2 Samueli 13 >