< 2 Samueli 12 >
1 Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
Og Herren sendte Nathan til David, og der han kom ind til ham, da sagde han til ham: Der var to Mænd i en Stad, en rig og en fattig.
2 Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
Den rige havde smaat Kvæg og stort Kvæg, saare meget.
3 koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
Men den fattige havde aldeles intet uden et lidet Faar, som han havde købt og fødte op, og det var blevet stort hos ham tillige med hans Børn; det aad af hans Brød og drak af hans Bæger og laa i hans Skød, og det var ham som en Datter.
4 “Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
Men der en Vandringsmand kom til den rige Mand, da nænnede han ikke at tage af sit smaa Kvæg og af sit store Kvæg for at lave noget til den vejfarende Mand, som kom til ham; men han tog den fattige Mands Faar og lavede det til den Mand, som var kommen til ham.
5 Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
Da optændtes Davids Vrede saare imod den Mand, og han sagde til Nathan: Saa vist som Herren lever, den Mand er et Dødsens Barn, som det gjorde.
6 Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
Og han skal betale det Faar firdobbelt, fordi han gjorde denne Gerning, og fordi han ikke viste Skaansel.
7 Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
Da sagde Nathan til David: Du er Manden! Saa sagde Herren, Israels Gud: Jeg salvede dig til Konge over Israel, og jeg udfriede dig af Sauls Haand,
8 Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
og jeg gav dig din Herres Hus og din Herres Hustruer i dit Skød og gav dig Israels og Judas Hus, og dersom det var for lidet, da vilde jeg lagt dig saadant og saadant til.
9 Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
Hvorfor har du foragtet Herrens Ord, at du gjorde det, som er ondt for hans Øjne? Hethiteren Uria har du slaget med Sværdet, og hans Hustru har du taget dig til Hustru; men ham har du slaget ihjel ved Ammons Børns Sværd.
10 Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
Saa skal nu Sværdet ikke vige fra dit Hus evindeligt, fordi du foragtede mig og tog Hethiteren Urias Hustru, at hun skulde være dig til en Hustru.
11 “Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
Saa sagde Herren: Se, jeg rejser Ulykke over dig fra dit eget Hus og tager dine Hustruer for dine Øjne og giver din Næste dem, at han skal ligge hos dine Hustruer for den klare Sol.
12 Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
Thi du har gjort det i Løndom; men jeg vil gøre denne Gerning for al Israel og for Solens Lys.
13 Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
Da sagde David til Nathan: Jeg har syndet imod Herren. Og Nathan sagde til David: Herren har ogsaa forladt dig din Synd, du skal ikke dø.
14 Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
Dog, fordi du ved denne Gerning har givet Herrens Fjender Lejlighed til at spotte, skal ogsaa den Søn, som dig er født, visselig dø.
15 Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
Saa gik Nathan til sit Hus, og Herren slog Barnet, som Urias Hustru havde født David, at det blev sygt.
16 Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
Og David søgte Gud for Drengen, og David fastede meget og gik ind og blev Natten over og laa paa Jorden.
17 Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
Da opstode de ældste af hans Hus for ham og vilde rejse ham op fra Jorden; men han vilde ikke og aad ikke Brød med dem.
18 Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
Og det skete paa den syvende Dag, da døde Barnet, og Davids Tjenere frygtede for at give ham til Kende, at Barnet var død; thi de sagde: Se, der Barnet var levende, talede vi til ham, og han hørte ikke paa vor Røst, hvorledes skulle vi da sige til ham: Barnet er død? thi det maatte gøre ham ondt.
19 Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
Men David saa, at hans Tjenere hviskede, og David forstod, at Barnet var død; og David sagde til sine Tjenere: Er Barnet død? og de sagde: Det er død.
20 Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
Da stod David op fra Jorden og toede sig og salvede sig og omskiftede sine Klæder og gik ind i Herrens Hus og bad; og der han kom til sit Hus, da begærede han Mad, og de satte Mad for ham, og han aad.
21 Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
Da sagde hans Tjenere til ham: Hvad er det for en Ting, som du har gjort? du fastede og græd for Barnet, da det levede, men da Barnet er død, staar du op og æder Brød?
22 Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
Og han sagde: Der Barnet endnu levede, fastede og græd jeg; thi jeg sagde: Hvo ved? Herren tør vorde mig naadig, at Barnet maa leve.
23 Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
Men nu det er død, hvorfor skal jeg da faste? kan jeg endnu hente det tilbage? jeg farer til det, men det kommer ikke tilbage til mig.
24 Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
Derefter trøstede David Bathseba sin Hustru og gik ind til hende og laa hos hende, og hun fødte en Søn, og han kaldte hans Navn Salomo, men ham elskede Herren;
25 Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
og han sendte Bud ved Nathan, Profeten, og denne kaldte hans Navn Jedid-Ja, for Herrens Skyld.
26 Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
Men Joab stred imod Ammons Børns Rabba og indtog Kongestaden.
27 Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
Og Joab sendte Bud til David og lod sige: Jeg har stridt imod Rabba og har ogsaa indtaget Vandstaden.
28 Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
Saa saml du nu det øvrige Folk, og belejr Staden, og indtag den, at ikke jeg skal indtage Staden, og jeg skulde blive navnkundig deraf.
29 Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
Saa samlede David alt Folket og drog til Rabba og stred imod den og indtog den.
30 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
Og han tog deres Konges Krone fra hans Hoved; den havde en Vægt af et Centner Guld og var besat med Ædelstene, og den kom over Davids Hoved, og han udførte af Staden saare meget Bytte.
31 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
Men Folket, som var derudi, førte han ud og lagde dem under Save og Tærskeslæder af Jern og under Økser af Jern og lod dem gaa igennem Teglovnen; og saaledes gjorde han ved alle Ammons Børns Stæder. Siden vendte David og alt Folket tilbage til Jerusalem.