< 2 Samueli 12 >

1 Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
Protož poslal Hospodin Nátana k Davidovi. Kterýž přišed k němu, řekl jemu: Dva muži byli v městě jednom, jeden bohatý a druhý chudý.
2 Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
Bohatý měl ovec i volů velmi mnoho,
3 koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
Chudý pak neměl nic, kromě jednu ovečku malou, kterouž byl koupil a choval, až i odrostla při něm a při dětech jeho tolikéž. Chléb jeho jedla a z číše jeho pila, a v lůnu jeho spávala, a tak byla mu jako za dceru.
4 “Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
Když pak přišel pocestný k tomu bohatému člověku, líto mu bylo vzíti z ovcí aneb z volů svých, což by připravil pocestnému, kterýž k němu přišel, ale vzav ovečku toho chudého člověka, připravil ji muži, kterýž byl přišel k němu.
5 Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
Tedy rozhněval se David na muže toho náramně a řekl Nátanovi: Živť jest Hospodin, že hoden jest smrti muž, kterýž to učinil.
6 Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
Ovečku také tu zaplatí čtvernásobně, proto že učinil věc tu, a nelitoval ho.
7 Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
I řekl Nátan Davidovi: Ty jsi ten muž! Takto praví Hospodin Bůh Izraelský: Já jsem tě pomazal, abys králem byl nad Izraelem, a vytrhl jsem tebe z ruky Saulovy.
8 Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
A dal jsem tobě dům pána tvého, i ženy pána tvého v lůno tvé, dalť jsem také dům Izraelský a Judský, a bylo-liť by to málo, byl bych přidal mnohem více.
9 Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
Pročež jsi sobě zlehčil slovo Hospodinovo, čině to, což se nelíbí jemu? Uriáše Hetejského zabil jsi mečem, a manželku jeho pojals sobě za ženu, samého pak zamordoval jsi mečem Ammonitských.
10 Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
Protož nyní neodejdeť meč z domu tvého až na věky, proto že jsi pohrdl mnou, a vzal jsi manželku Uriáše Hetejského, aby byla žena tvá.
11 “Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
Takto praví Hospodin: Aj, já vzbudím proti tobě zlé z domu tvého, a vezma ženy tvé před očima tvýma, dám je bližnímu tvému, kterýž spáti bude s ženami tvými, an na to každý hledí.
12 Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
A ačkoli ty učinil jsi to tajně, já však učiním to zjevně přede vším Izraelem a všechněm známě.
13 Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
Tedy řekl David Nátanovi: Zhřešilť jsem Hospodinu. Zase řekl Nátan Davidovi: Tentýž Hospodin přenesl hřích tvůj, neumřeš.
14 Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
Ale však, poněvadž jsi tou věcí dal příčinu nepřátelům Hospodinovým, aby se rouhali, protož ten syn, kterýž se narodil tobě, jistotně umře.
15 Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
Potom odšel Nátan do domu svého. V tom Hospodin ranil dítě, kteréž byla porodila manželka Uriášova Davidovi, tak že pochybili o něm.
16 Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
I modlil se David Bohu za to dítě a postil se, a všed, ležel přes noc na zemi.
17 Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
A ačkoli starší domu jeho přišli k němu, aby ho zdvihli z země, on však nechtěl, aniž s nimi co jedl.
18 Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
Stalo se pak dne sedmého, že umřelo dítě. I nesměli služebníci Davidovi toho oznámiti jemu, že by umřelo dítě; nebo pravili: Aj, když ještě bylo dítě živo, mluvili jsme jemu, a nechtěl slyšeti hlasu našeho, což pak když jemu díme: Umřelo dítě. Ovšem to tíže ponese.
19 Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
Ale vida David, an služebníci jeho k sobě šepcí, srozuměl, že by umřelo dítě. I řekl David služebníkům svým: Co již umřelo dítě? Kteříž řekli: Umřelo.
20 Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
Tedy vstav David s země, umyl se a pomazal se, a změnil roucho své, a všed do domu Hospodinova, pomodlil se. Potom vrátiv se do domu svého, rozkázal sobě dáti jísti a jedl.
21 Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
Služebníci pak jeho řekli jemu: Co jsi to učinil? Pro dítě, když živo bylo, postils se a plakal, ale jakž dítě umřelo, vstal jsi a přijal jsi pokrm.
22 Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
Kterýžto řekl: Pokudž ještě dítě živo bylo, postil jsem se a plakal, nebo jsem řekl: Kdo ví? Můžeť se smilovati nade mnou Hospodin, aby živo bylo dítě.
23 Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
Nyní pak, poněvadž umřelo, proč se mám postiti? Zdaliž budu moci zase je vzkřísiti? Jáť půjdu k němu, ale ono se nenavrátí ke mně.
24 Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
Potom David potěšiv Betsabé manželky své, všel k ní a spal s ní. I porodila syna, a nazval jméno jeho Šalamoun, a Hospodin miloval jej.
25 Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
Protož poslal byl Nátana proroka, a nazval jméno jeho Jedidiah pro Hospodina.
26 Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
Bojoval pak Joáb proti Rabba Ammonitských, a vzal město královské.
27 Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
A poslav posly k Davidovi, řekl: Dobýval jsem Rabba a vzal jsem město vod.
28 Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
Protož nyní sebera ostatek lidu, polož se proti městu a vezmi je, abych já nevzal města toho, a bylo by mně připisováno vítězství nad ním.
29 Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
Tedy sebrav David všecken lid, vytáhl proti Rabba, kteréhož dobýval a vzal je.
30 Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
A sňal korunu krále jejich s hlavy jeho, kteráž vážila centnéř zlata, a bylo v ní kamení drahé, a vstavena byla na hlavu Davidovu. Vyvezl též kořisti města velmi veliké.
31 ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.
Lid pak, kterýž v něm byl, vyvedl a dal jej pod pily a pod brány železné a pod sekery železné, a vehnal je do peci cihelné. A tak činil všechněm městům Ammonitským. Potom navrátil se David se vším lidem do Jeruzaléma.

< 2 Samueli 12 >