< 2 Samueli 11 >
1 Nthawi ya mphukira, nthawi imene mafumu amapita ku nkhondo, Davide anatumiza Yowabu ndi ankhondo a mfumu pamodzi ndi gulu lonse lankhondo la Aisraeli. Iwo anawononga Aamoni ndi kuzungulira mzinda wa Raba. Koma Davide anatsala ku Yerusalemu.
And it came to pass, at the return of the same season of the year, at the time when kings go forth, that David sent Joab, and his servants with him, and all Israel; and they destroyed the children of 'Ammon, and besieged Rabbah. But David remained behind at Jerusalem.
2 Tsiku lina cha kumadzulo Davide anadzuka pa bedi lake ndipo ankayenda pamwamba pa nyumba yake. Ali pa dengapo anaona mkazi akusamba. Mkaziyo anali wokongola kwambiri.
And it happened at evening-tide, that David arose from off his couch, and walked upon the roof of the king's house: and he saw from the roof a woman bathing herself; and the woman was of a very beautiful appearance.
3 Ndipo Davide anatuma munthu wina kuti akafufuze za iye. Munthuyo anati, “Kodi uyu si Batiseba, mwana wa Eliamu, mkazi wa Uriya Mhiti?”
And David sent and inquired after the woman; and some one said, Behold, this is Beth-sheba', the daughter of Eli'am, the wife of Uriyah the Hittite.
4 Ndipo Davide anatumiza amithenga kwa iye kukamuyitana. Batiseba anabwera kwa Davide ndipo anagona naye. (Nʼkuti mkaziyu atayeretsedwa ku masiku ake osamba). Kenaka anabwerera ku nyumba yake.
And David sent messengers, and took her; and she came in unto him, and he lay with her, and she had just purified herself from her uncleanness; and she returned unto her house.
5 Mkaziyo anakhala woyembekezera ndipo anatumiza mawu kwa Davide kunena kuti, “Ine ndine woyembekezera.”
And the woman conceived; and she sent and told David, and said, I am with child.
6 Ndipo Davide anatumiza mawu awa kwa Yowabu: “Nditumizire Uriya Mhiti.” Ndipo Yowabu anamutumiza kwa Davide.
And David sent to Joab, Send unto me Uriyah the Hittite. And Joab sent Uriyah to David.
7 Uriya atafika kwa Davide, Davide anamufunsa za momwe analili Yowabu, za asilikali ndi momwe nkhondo inkayendera.
And when Uriyah was come unto him, David asked after the well-being of Joab, and after the well-being of the people, and how the war prospered.
8 Kenaka Davide anati kwa Uriya, “Pita ku nyumba yako ukapumule.” Choncho Uriya anachoka ku nyumba yaufumu, ndipo mfumuyo inatumiza mphatso kwa Uriya.
And David said to Uriyah, Go down to thy house, and wash thy feet. And Uriyah went forth out of the king's house, and there followed him a mess of food from the king.
9 Koma Uriya anagona pa chipata cha nyumba yaufumu pamodzi ndi antchito onse a mbuye wake ndipo sanapite ku nyumba yake.
But Uriyah laid himself down at the door of the king's house with all the servants of his lord, and went not down to his house.
10 Davide atawuzidwa kuti, “Uriya sanapite ku nyumba yake.” Iye anafunsa kuti, “Kodi iwe sunachokera kutali? Nʼchifukwa chiyani sunapite ku nyumba yako?”
And they told David, saying, Uriyah is not gone down unto his house: and David said unto Uriyah, Art thou not come from a journey? why then art thou not gone down unto thy own house?
11 Uriya anayankha Davide kuti, “Bokosi la Chipangano ndi Israeli ndiponso Yuda akukhala mʼmatenti, ndipo mbuye wanga Yowabu ndi ankhondo anu mbuye wanga amanga misasa pa mtetete. Ine ndingapite bwanji ku nyumba yanga kukadya ndi kumwa ndiponso kugona ndi mkazi wanga? Pali inu wamoyo, ine sindidzachita chinthu chimenechi.”
Then said Uriyah unto David, The ark, and Israel, and Judah abide in booths; and my Lord Joab and the servants of my Lord are encamped in the open field: and should I alone go unto my house, to eat and to drink, and to lie with my wife? as thou livest, and as thy soul liveth, I will not do this thing.
12 Ndipo Davide anati kwa iye, “Ukhale konkuno tsiku lina limodzi, ndipo mawa ndikulola kuti upite.” Kotero Uriya anakhala mu Yerusalemu tsiku limenelo ndi tsiku linalo.
And David said unto Uriyah, Tarry here also this day, and tomorrow will I send thee off. So Uriyah remained in Jerusalem on that day and the following.
13 Davide anayitana Uriya nadya ndi kumwa naye, ndipo Davide anamuledzeretsa. Koma madzulo Uriya anapita kukagona pa mphasa pamodzi ndi antchito a mbuye wake. Iye sanapite ku nyumba yake.
And David invited him, and he ate and drank before him, and he made him drunken; and he went out in the evening to lie down on his resting-place with the servants of his lord; but to his house he did not go down.
14 Mmawa Davide analemba kalata kwa Yowabu ndipo anayitumiza ndi Uriya.
And it came to pass in the morning, that David wrote a letter to Joab, and sent it by the hand of Uriyah.
15 Mʼkalatayo analembamo kuti, “Uriya mumuyike patsogolo penipeni, pamene pali nkhondo yoopsa. Ndipo mumusiye yekha kuti akanthidwe ndi kufa.”
And he wrote in the letter, saying, Set Uriyah in front, opposite to the hottest fight, and then withdraw from behind him, that he may be smitten and die.
16 Kotero Yowabu atawuzinga mzindawo, anamuyika Uriya pamalo pamene amadziwa kuti pali asilikali amphamvu.
And it came to pass, when Joab was enclosing the city, that he placed Uriyah toward the spot of which he knew that valiant men were there.
17 Ankhondo a mu mzindawo atabwera kudzamenyana ndi Yowabu, anthu ena a gulu la ankhondo la Davide anaphedwa ndipo Uriya Mhiti uja anaphedwanso.
And the men of the city went out and fought with Joab; and there fell some of the people, of the servants of David, and there died also Uriyah the Hittite.
18 Yowabu anatumiza wamthenga kwa Davide kukafotokoza mwatsatanetsatane za nkhondoyo.
Then did Joab send, and told unto David all the events of the war.
19 Iye anamulangiza wa mthengayo kuti, “Pamene ukatsiriza kufotokozera mfumu za ku nkhondozi,
And he charged the messenger, saying, When thou hast finished telling all the events of the war to the king,
20 mfumu ikapsa mtima, ndipo akakakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani munapita pafupi ndi mzindawo kukamenya nkhondo? Inu simunadziwe kuti atha kukuponyerani mivi kuchokera pa khoma?
And it happen that the king's wrath arise, and he say unto thee, Wherefore did you approach unto the city to fight? knew ye not, that they would shoot down from off the wall?
21 Kodi anapha Abimeleki mwana wa Yerubeseti ndani? Kodi mkazi sanamuponyere mphero kuchokera pa khoma? Kotero kuti anakafera ku Tebezi. Nʼchifukwa chiyani munafika pafupi ndi khoma?’ Ngati iye akafunsa zimenezi, iwe ukanene kwa iye kuti, ‘Mtumiki wanunso Uriya Mhiti wafa.’”
Who smote Abimelech the son of Yerubbesheth? did not a woman throw down upon him a piece of an upper mill-stone from off the wall so that he died at Thebez? why did ye approach unto the wall? then must thou say, Also thy servant Uriyah the Hittite is dead.
22 Mthengayo ananyamuka, ndipo atafika anamuwuza Davide zonse zimene Yowabu anamutuma kuti akanene.
And the messenger went, and came and told unto David all for which Joab had sent him.
23 Mthengayo anati kwa Davide, “Anthuwo anatiposa mphamvu ndipo anabwera kudzalimbana nafe poyera, koma ife tinawabwezera ku chipata cha mzindawo.
And the messenger said unto David, Because the men overpowered us and came out against us into the field; but we set upon them, as far as the entrance of the gate.
24 Ndipo anthu oponya mivi anatiponyera kuchokera pa khoma, anthu ena a mfumu afa. Kuwonjezera apo, mtumiki wanu Uriya Mhiti wafanso.”
And the archers then shot at thy servants from off the wall; and there died some of the servants of the king, and also thy servant Uriyah the Hittite is dead.
25 Davide anamuwuza mthengayo kuti, “Ukanene izi kwa Yowabu: ‘Zimenezi zisakukhumudwitse; lupanga limapha wina nthawi zinanso wina. Limbikitsa nkhondo pa mzindawo ndipo uwuwononge!’ Ukanene zimenezi pomulimbikitsa Yowabu.”
Then said David to the messenger, Thus shalt thou say to Joab, Let this thing not be displeasing in thy eyes; for at times this, at other times the other will the sword devour; continue firmly in thy war against the city, and overthrow it: and thus do thou encourage him.
26 Mkazi wa Uriya atamva kuti mwamuna wake wafa, analira maliro.
And when the wife of Uriyah heard that Uriyah her husband had died, she mourned for her lord.
27 Nthawi yolira maliro itatha, Davide anamubweretsa ku nyumba yake, ndipo anakhala mkazi wake nabala mwana wamwamuna. Koma Yehova sanakondwe ndi zimene Davide anachitazo.
And when the [time of] mourning was past, David sent and took her to his house, and she became his wife; and she bore him a son. But the thing which David had done was displeasing in the eyes of the Lord.