< 2 Samueli 10 >

1 Patapita nthawi, mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake Hanuni analowa ufumu mʼmalo mwake.
Och det begaf sig derefter, att Ammons barnas Konung blef död, och hans son Hanun vardt Konung i hans stad.
2 Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni,
Då sade David: Jag vill göra barmhertighet på Hanun, Nahas son, såsom hans fader hafver gjort barmhertighet med mig. Och sände bort och lät genom sina tjenare hugsvala honom öfver hans fader. Och Davids tjenare kommo i Ammons barnas land.
3 atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni mbuye wawo kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi Davide sanawatumize anthuwa kuti adzaone mzinda wanu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
Då sade de öfverste öfver Ammons barn till sin herra Hanun: Menar du, att David hedrar din fader för din ögon, att han hafver sändt hugsvalare till dig? Menar du icke, att han fördenskull hafver sändt sina tjenare till dig, att han skall utspana och bespeja staden, och förstöra honom?
4 Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anameta munthu aliyense mbali imodzi ya ndevu zake, ndi kudula zovala zake pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera, ndipo anawabweza kwawo.
Då tog Hanun Davids tjenare, och lät raka dem halft skägget af; och skar half kläden af på dem, allt intill bältet, och lät så gå dem.
5 Atamufotokozera Davide zimenezi, iye anatuma amithenga kukakumana ndi anthuwo chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
Då det vardt bådadt David, sände han emot dem; förty männerna voro ganska mycket skämde. Och Konungen lät säga dem: Blifver i Jericho tilldess edart skägg växer, och kommer så igen.
6 Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, anakapeza ankhondo oyenda pansi aganyu okwanira 20,000 kuchokera ku Asiriya wa ku Beti Rehobu ndi Aramu-Zoba, komanso ankhondo 1,000 kwa mfumu Maaka ndiponso ankhondo 22,000 ochokera ku Tobu.
Då nu Ammons barn sågo, att de voro illa luktande vordne för David, sände de bort, och lejde sig de Syrer af Rehobs hus, och de Syrer i Zoba, tjugutusend män fotfolk, och af Konung Maacha tusend män, och af Istob tolftusend män.
7 Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
Då David det hörde, sände han Joab med hela hären af krigsfolket.
8 Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene Aaramu a ku Aramu-Zoba ndi Rehobu ndi ankhondo a ku Tobu ndi Maaka anali kwa wokha ku malo wopanda mitengo.
Och Ammons barn drogo ut, och skickade sig till strid ut för stadsporten; men de Syrer af Zoba, af Rehob, af Istob, och af Maacha, voro allena i markene.
9 Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake, iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
Då nu Joab såg, att striden var ställd på honom både bak och före, utvalde han utaf alla de unga män i Israel, och skickade sig emot de Syrer.
10 Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
Och det andra folket lät han under sins broders hand Abisai, och han skickade sig emot de Ammons barn;
11 Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse. Koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
Och sade: Om de Syrer varda mig för mägtige, så kom mig till hjelp; om Ammons barn varda dig öfvermägtige, så vill jag komma dig till hjelp.
12 Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
Var vid god tröst, och låt oss stå fasta för vårt folk och för vår Guds städer; men Herren göre hvad honom täckes.
13 Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
Och Joab drog åstad med det folk, som när honom var, till att strida emot de Syrer; och de flydde för honom.
14 Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai ndi kulowa mu mzinda. Nkhondo itatha, Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
Och då Ammons barn sågo, att de Syrer flydde, flydde de ock för Abisai, och drogo in i staden. Så vände Joab om ifrån Ammons barn, och kom till Jerusalem.
15 Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anasonkhananso.
Och då de Syrer sågo, att de voro slagne för Israel, församlade de sig tillhopa.
16 Hadadezeri anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, iwo anapita ku Helamu motsogozedwa ndi Sobaki mkulu wa ankhondo a Hadadezeri.
Och HadarEser sände bort, och lät utkomma de Syrer på hinsidon älfven; och lät deras magt inkomma; och Sobach, HadarEsers härhöfvitsman, drog för dem.
17 Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani ndipo anapita ku Helamu. Aaramu anayima mʼmizere yawo yankhondo kukakumana ndi Davide ndipo anamenyana naye.
Då det vardt bådadt David, församlade han tillhopa hela Israel, och drog öfver Jordan, och kom till Helam; och de Syrer skickade sig emot David, till att strida med honom.
18 Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 700 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Davide anaphanso Sobaki mtsogoleri wawo wankhondo ndipo anafera pomwepo.
Men de Syrer flydde för Israel, och David slog ihjäl de Syrer sjuhundrad vagnar, och fyratiotusend resenärar; dertill slog han Sobach härhöfvitsmannen, så att han blef der död.
19 Mafumu onse amene anali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, iwo anachita mtendere ndi Aisraeli ndipo anakhala pansi pawo. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.
Då nu de Konungar, som voro under HadarEser, sågo att de slagne voro för Israel, gjorde de frid med Israel, och vordo dem underdånige; och de Syrer fruktade sig mer hjelpa Ammons barn.

< 2 Samueli 10 >