< 2 Samueli 10 >

1 Patapita nthawi, mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake Hanuni analowa ufumu mʼmalo mwake.
А после тога умре цар синова Амонових, и зацари се Анун син његов на његово место.
2 Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni,
И рече Давид: Да учиним милост Ануну сину Насовом, као што је отац његов мени учинио милост. И посла Давид да га потеши за оцем преко слуга својих. И дођоше слуге Давидове у земљу синова Амонових.
3 atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni mbuye wawo kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi Davide sanawatumize anthuwa kuti adzaone mzinda wanu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
А кнезови синова Амонових рекоше Ануну господару свом: Мислиш да је Давид зато послао људе да те потеше, што је рад учинити част оцу твом? А није зато послао Давид к теби слуге своје да промотри град и уходи, па после да га раскопа?
4 Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anameta munthu aliyense mbali imodzi ya ndevu zake, ndi kudula zovala zake pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera, ndipo anawabweza kwawo.
Тада Анун ухвати слуге Давидове, и обрија им браде до пола и одсече им хаљине по поле, до задњице, и оправи их натраг.
5 Atamufotokozera Davide zimenezi, iye anatuma amithenga kukakumana ndi anthuwo chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
А кад то јавише Давиду, он посла пред њих, јер људи беху грдно осрамоћени, и поручи им цар: Седите у Јерихону докле вам нарасте брада, па онда дођите натраг.
6 Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, anakapeza ankhondo oyenda pansi aganyu okwanira 20,000 kuchokera ku Asiriya wa ku Beti Rehobu ndi Aramu-Zoba, komanso ankhondo 1,000 kwa mfumu Maaka ndiponso ankhondo 22,000 ochokera ku Tobu.
Тада синови Амонови видећи где се омразише с Давидом, послаше синови Амонови, те најмише Сираца од Вет-Реова и Сираца од Сове двадесет хиљада пешака, и у цара од Махе хиљаду људи, и од Ис-Това дванаест хиљада људи.
7 Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
А Давид кад то чу, посла Јоава са свом храбром војском својом.
8 Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene Aaramu a ku Aramu-Zoba ndi Rehobu ndi ankhondo a ku Tobu ndi Maaka anali kwa wokha ku malo wopanda mitengo.
И Изиђоше синови Амонови, и уврсташе се пред вратима, а Сирци из Сове и из Реова и људи из Ис-Това и из Махе беху за себе у пољу.
9 Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake, iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
И Јоав видећи намештену војску према себи спред и озад, узе одабране из све војске израиљске, и намести их према Сирцима;
10 Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
А остали народ предаде Ависају брату свом да их намести према синовима Амоновим.
11 Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse. Koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
И рече: Ако Сирци буду јачи од мене, дођи ми у помоћ; ако ли синови Амонови буду јачи од тебе, ја ћу доћи теби у помоћ.
12 Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
Буди храбар, и држимо се храбро за свој народ и за градове Бога свог; а Господ нека учини шта му је по вољи.
13 Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
Тада Јоав и народ који беше с њим примакоше се да ударе на Сирце, али они побегоше испред њега.
14 Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai ndi kulowa mu mzinda. Nkhondo itatha, Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
А синови Амонови видећи где побегоше Сирци, побегоше и они испред Ависаја, и уђоше у свој град. И врати се Јоав од синова Амонових, и дође у Јерусалим.
15 Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anasonkhananso.
Али Сирци кад видеше где их надбише Израиљци, скупише се опет.
16 Hadadezeri anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, iwo anapita ku Helamu motsogozedwa ndi Sobaki mkulu wa ankhondo a Hadadezeri.
И Адад-Езер посла, те доведе Сирце испреко реке, који дођоше у Елам; а Совак, војвода Адад-Езеров иђаше пред њима.
17 Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani ndipo anapita ku Helamu. Aaramu anayima mʼmizere yawo yankhondo kukakumana ndi Davide ndipo anamenyana naye.
Кад то јавише Давиду, он скупи све Израиљце, и пређе преко Јордана и дође у Елам; и Сирци се наместише против Давида и побише се с Давидом.
18 Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 700 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Davide anaphanso Sobaki mtsogoleri wawo wankhondo ndipo anafera pomwepo.
Али побегоше Сирци испред Израиља, и поби Давид Сираца седам стотина и четрдесет хиљада коњика; и Совака војводу њиховог уби, те погибе онде.
19 Mafumu onse amene anali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, iwo anachita mtendere ndi Aisraeli ndipo anakhala pansi pawo. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.
И кад видеше сви цареви, слуге Адад-Езерове, да их разби Израиљ, учинише мир с Израиљем, и служаху им, и Сирци не смеше више помагати синовима Амоновим.

< 2 Samueli 10 >