< 2 Samueli 10 >

1 Patapita nthawi, mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake Hanuni analowa ufumu mʼmalo mwake.
Iti saan a nagbayag, natay ti ari dagiti tattao a taga-Amnon, ket simmukat nga ari ti anakna a ni Hanun.
2 Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni,
Kinuna ni David, “Ipakitak ti kinasayaat kenni Hanun nga anak ni Naas, kas iti panangipakita iti amana iti kinasayaatna kaniak.” Isu nga imbaon ni David dagiti adipenna tapno liwliwaenda ni Hanun maipapan iti amana. Simrek dagiti adipen ni David iti daga dagiti tattao a taga-Ammon.
3 atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni mbuye wawo kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi Davide sanawatumize anthuwa kuti adzaone mzinda wanu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
Ngem imbaga dagiti pangulo dagiti tattao a taga-Ammon kenni Hanun nga apoda, “Mamatika kadi a raraemen ni David ti amam gapu ta nangibaon iti tattao a mangliwliwa kenka? Saan ngata a nangibaon ni David kadagiti adipenna kenka a mangkita ken mangsiim iti siudad tapno parmekenda daytoy?”
4 Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anameta munthu aliyense mbali imodzi ya ndevu zake, ndi kudula zovala zake pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera, ndipo anawabweza kwawo.
Isu nga impatiliw ni Hanun dagiti adipen ni David, impaahitna ti maysa a bangir dagiti barbasda, pinigisna dagiti pagan-anayda agingga iti patongda, ken pinagawidna ida.
5 Atamufotokozera Davide zimenezi, iye anatuma amithenga kukakumana ndi anthuwo chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
Idi inlawlawagda daytoy kenni David, nangibaon isuna iti mangsabat kadakuada, ta kasta unay ti bain dagiti lallaki. Kinuna ti ari, “Agtalinaedkayo idiay Jerico agingga nga umatiddog manen dagiti barbasyo ket agsublikayo.”
6 Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, anakapeza ankhondo oyenda pansi aganyu okwanira 20,000 kuchokera ku Asiriya wa ku Beti Rehobu ndi Aramu-Zoba, komanso ankhondo 1,000 kwa mfumu Maaka ndiponso ankhondo 22,000 ochokera ku Tobu.
Idi naammoan dagiti tattao a taga-Ammon a bimmangsitdan kenni David, nangibaonda iti mensahero ken tinangdananda dagiti Arameo iti Berehob ken Soba, 20, 000 a magmagna a soldado, ken ti ari ti Maaca nga addaan iti 1, 000 a tattaona, ken dagiti tattao a taga-Tob nga addaan iti 12, 000 pay a lallaki.
7 Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
Idi nangegan ni David daytoy, imbaonna ni Joab ken amin nga armada dagiti soldado.
8 Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene Aaramu a ku Aramu-Zoba ndi Rehobu ndi ankhondo a ku Tobu ndi Maaka anali kwa wokha ku malo wopanda mitengo.
Rimmuar dagiti Ammonita ket nagpuestoda a makigubat iti pagserrekan iti ruangan ti siudadda, kabayatan a dagiti Arameo a taga-Soba, taga-Rehob, ken dagiti lallaki a taga-Tob ken Maaca ket nakapuesto iti nalawa a tay-ak.
9 Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake, iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
Idi makita ni Joab dagiti nakapuesto a makigubat a naisaaden kenkuana iti sango ken likodanna, nangpili isuna kadagiti kalalaingan a mannakigubat ti Israel ket impuestona ida maibusor kadagiti Arameo.
10 Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
Intedna met dagiti nabatbati iti armada iti panangbilin ni Abisai a kabsatna ket pinagpuestona ida a maibusor iti armada ti Ammon.
11 Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse. Koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
Kinuna ni Joab, “No napigsa unay dagiti Arameo para kaniak, masapul ngarud a tulongannak, sika Abisai.” Ngem no napigsa unay ti armada ti Ammon para kenka, umayak ngarud ket tulonganka.
12 Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
Papigsaenyo ti pakinakemyo ken ipakitatayo a napigsatayo para kadagiti tattaotayo ken para kadagiti siudad iti Diostayo, ta aramiden ni Yahweh no ania ti naimbag para iti panggepna.”
13 Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
Isu a dimmarup ni Joab ken dagiti soldado ti armadana maibusor kadagiti Arameo, a napilitan a naglibas manipud iti armada ti Israel.
14 Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai ndi kulowa mu mzinda. Nkhondo itatha, Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
Idi makita ti armada ti Ammon a naglibas dagiti Arameo, naglibasda met manipud kenni Abisai ket nagsublida iti siudad. Kalpasanna, nagsubli ni Joab manipud kadagiti tattao a taga-Ammon ket nagsubli idiay Jerusalem.
15 Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anasonkhananso.
Ket idi nakita dagiti Arameo a parparmeken idan ti Israel, nagtitiponda manen.
16 Hadadezeri anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, iwo anapita ku Helamu motsogozedwa ndi Sobaki mkulu wa ankhondo a Hadadezeri.
Kalpasanna, nangibaon ni Adadezer para kadagiti bunggoy ti Arameo manipud pay iti ballasiw ti Karayan Eufrates. Napanda iti Helam, kaduada ni Sobac a pangulo iti armada ni Adadezer iti sangoda.
17 Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani ndipo anapita ku Helamu. Aaramu anayima mʼmizere yawo yankhondo kukakumana ndi Davide ndipo anamenyana naye.
Idi naipadamag daytoy kenni David, inummongna amin nga Israel, bimmalasiwda iti Jordan ket nakadanonda idiay Helam. Nagpuesto a makigubat dagiti Arameo maibusor kenni David ket ginubatda isuna.
18 Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 700 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Davide anaphanso Sobaki mtsogoleri wawo wankhondo ndipo anafera pomwepo.
Naglibas manipud iti Israel dagiti Arameo. Pinatay ni David iti 700 a soldado a nakakarwahe ken 40, 000 a nakakabalio a soldado. Nasugatan ni Sobac a pangulo iti armadada ket natay sadiay.
19 Mafumu onse amene anali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, iwo anachita mtendere ndi Aisraeli ndipo anakhala pansi pawo. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.
Idi nakita dagiti ari nga agserserbi kenni Adadezer a pinarmek idan ti Israel, nakikappiada ken nagpaiturayda iti Israel. Isu a mabutengen dagiti Arameo a tumulong pay kadagiti tattao ti Ammon.

< 2 Samueli 10 >