< 2 Samueli 1 >

1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
Kalpasan ti pannakatay ni Saul, nagsubli ni David manipud iti panangrautna kadagiti Amalekita ket nagtalinaed isuna iti dua nga aldaw idiay Siklag.
2 Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
Iti maikatlo nga aldaw, adda maysa a lalaki a simmangpet manipud iti kampo ni Saul a napisang ti badona ken adda rugit iti ulona. Idi simmangpet isuna iti ayan ni David, ket nagpakleb isuna iti daga.
3 Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
Kinuna ni David kenkuana, “Sadino ti naggapuam?” Simmungbat isuna, “Naglibasak manipud iti kampo ti Israel,”
4 Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
Kinuna ni David kenkuana, “Pangngaasim ta ibagam kaniak no ania ti napasamak.” Simmungbat isuna, “Naglibas dagiti tattao manipud iti gubat. Adu ti napasag ken adu dagiti natay. Natay met da Saul kenni Jonatan nga anakna.”
5 Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
Kinuna ni David iti agtutubo, “Kasanom nga ammo a natay da Saul ken Jonatan nga anakna?”
6 Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
Simmungbat ti agtutubo, “Nairana nga addaak idiay bantay Gilboa, ket adda sadiay ni Saul nga agsadsadag iti gayangna, ket asidegen dagiti karwahe ken kumakabalio a kabusor a mangtiliw kenkuana.
7 Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
Kimmita Saul iti aglawlaw ket nakitanak ket inayabannak. Simmungbatak, 'Adtoyak.'
8 Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
Kinunana kaniak, 'Siasinoka?' Sinungbatak isuna, 'Maysaak nga Amalekita.'
9 “Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
Kinunana kaniak, 'Pangngaasim ta umasidegka kaniak ket patayennak, ta tengngelnak ti nakaro a panagsagaba, ngem sibibiagak pay laeng.'
10 “Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
Isu nga imasidegak kenkuana ket pinatayko isuna, gapu ta ammok a saanen nga agbiag kalpasan a mapasag isuna. Ket innalak ti korona nga adda iti ulona ken ti pulseras nga adda iti takkiagna, ket inyegko dagitoy ditoy kenka, apok.”
11 Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
Ket, pinisang ni David dagiti pagan-anayna, ken kasta met ti inaramid dagiti amin a lallaki a kaduana.
12 Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
Nagladingit, nagsangit ken nagayunarda agingga iti rabii para kenni Saul, para kenni Jonatan nga anakna, para kadagiti tattao ni Yahweh ken para iti balay ti Israel gapu ta napasagda babaen iti kampilan.
13 Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
Kinuna ni David iti agtutubo, “Taga-anoka?” Simmungbat isuna, “Anaknak ti maysa a ganggannaet iti daytoy a daga, maysaak nga Amalekita.”
14 Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
Kinuna ni David kenkuana, “Apay a saanka a nagbuteng a nangpatay iti ari a pinulotan ni Yahweh babaen iti bukodmo nga ima?”
15 Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
Inayaban ni David iti maysa kadagiti agtutubo ket kinunana “Inka ket patayen isuna.” Isu a napan dinuyok dayta a lalaki ti Amalekita, ket natay ti Amalekita.
16 Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
Ket kinuna ni David iti natay nga Amalekita, adda iti ulom ti bukodmo a dara gapu ta ti bukodmo a ngiwat ti nangpaneknek iti maibusor kenka ket kinunam, 'Pinatayko ti ari a pinulotan ni Yahweh.'”
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
Kalpasanna, kinanta ni David daytoy a dung-aw maipapan kada Saul ken Jonatan nga anakna.
18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
Imbilinna kadagiti tattao nga isuroda daytoy a Kanta ti Bai kadagiti lallaki a putot ti Juda, a naisurat iti Libro ti Jasar.
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
“Ti dayagmo, Israel, ket natayen, napapatay kadagiti bantaymo! Kasano a napasag ti maingel!
20 “Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
Saanmo nga ibagbaga daytoy idiay Gat, saanmo nga iwarwaragawag daytoy kadagiti kalsada iti Askelon, tapno saan a makapagrag-o dagiti babbai a putot dagiti Filisteo, tapno saan a makapagrambak dagiti babbai a putot dagiti saan a nakugit.
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
Banbantay ti Gilboa, awan koma kadakayo ti linnaaw wenno tudo, wenno talon a mangmangted kadagiti bukbukel nga aggpaay a daton, ta sadiay ket narugitan ti kalasag ti maingel. Ti kalasag ni Saul a saanen a napulotan iti lana.
22 “Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
Manipud iti dara dagidiay napapatay, manipud kadagiti bagi dagiti maingel, saanen a nagsubli ti bai ni Jonatan, ken saan a nagsubli nga awan naaramidan ti kampilan ni Saul.
23 “Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
Ni Saul ken Jonatan ket maay-ayat ken managparabur iti panagbiag, ken iti ipapatayda ket saanda a nagsina. Nasigsiglatda ngem kadagiti agila, napigpigsada ngem kadagiti leon.
24 “Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
Dakayo a babbai nga annak ti Israel, sangitanyo ni Saul, a nangkawes kadakayo iti napintas nga eskarlata, a nangarkos iti balitok kadagiti pagan-anaayyo.
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
Anian a pannakapasag ti maingel iti paggugubatan! Napapatay ni Jonatan kadagiti nangangato a lugarmo.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
Maladigitanak unay para kenka Jonatan a kabsatko. Napategka unay kaniak. Nakaskasdaaw ti ayatmo kaniak, nalablabes ngem iti panagayat dagiti babbai.
27 “Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”
Anian a pannakapasag ti maingel, ken ti pannakapukaw dagiti igam a panggubat!”

< 2 Samueli 1 >