< 2 Samueli 1 >

1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
And it was after [the] death of Saul and David he returned from defeating Amalek and he remained David in Ziklag days two.
2 Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
And it was - on the day third and there! a man [was] coming from the camp from with Saul and garments his [were] torn and earth [was] on head his and it was when came he to David and he fell [the] ground towards and he bowed down.
3 Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
And he said to him David where? from this are you coming and he said to him from [the] camp of Israel I have escaped.
4 Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
And he said to him David what? was it the word tell please to me and he said that it has fled the people from the battle and also [surely] a multitude has fallen of the people and they have died and also Saul and Jonathan son his they have died.
5 Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
And he said David to the young man who had told to him how? do you know that he has died Saul and Jonathan son his.
6 Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
And he said the young man - who had told to him [surely] by chance I found myself on [the] mountain of Gilboa and there! Saul [was] leaning on spear his and there! the chariotry and [the] owners of the horses they overtook him.
7 Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
And he turned behind him and he saw me and he called to me and I said here [am] I.
8 Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
And he said to me who? [are] you (and I said *Q(K)*) to him [am] an Amalekite I.
9 “Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
And he said to me stand please over me and kill me for it has seized me dizziness for all still life my [is] in me.
10 “Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
And I stood over him and I killed him for I knew that not he will live after had fallen he and I took the crown - which [was] on head his and an armlet which [was] on arm his and I brought them to lord my here.
11 Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
And he took hold David (on garments his *Q(K)*) and he tore them and also all the men who [were] with him.
12 Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
And they mourned and they wept and they fasted until the evening on Saul and on Jonathan son his and on [the] people of Yahweh and on [the] house of Israel for they had fallen by the sword.
13 Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
And he said David to the young man who had told to him where? from this [are] you and he said [am the] son of a man a sojourner an Amalekite I.
14 Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
And he said to him David how? not were you afraid to stretch out hand your to destroy [the] [one] anointed of Yahweh.
15 Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
And he called David to one from the young men and he said draw near fall on him and he struck down him and he died.
16 Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
And he said to him David (blood your *Q(K)*) [be] on head your for own mouth your it has testified against you saying I I killed [the] [one] anointed of Yahweh.
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
And he lamented David the lamentation this on Saul and on Jonathan son his.
18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
And he said to teach [the] descendants of Judah Bow here! [it is] written on [the] scroll of the Jashar.
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
The beauty O Israel on high places your [is] slain how! they have fallen [the] mighty [ones].
20 “Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
May not you tell in Gath may not you bear news in [the] streets of Ashkelon lest they should rejoice [the] daughters of [the] Philistines lest they should exult [the] daughters of the uncircumcised.
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
O mountains in Gilboa may not dew and may not rain [be] on you and fields of contributions for there it was defiled [the] shield of [the] mighty [ones] [the] shield of Saul not [was] anointed with oil.
22 “Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
From [the] blood of [those] slain from [the] fat of [the] mighty [ones] [the] bow of Jonathan not it turned back backwards and [the] sword of Saul not it returned empty.
23 “Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
Saul and Jonathan lovable and pleasant in lives their and in death their not they were separated more than eagles they were swift more than lions they were strong.
24 “Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
O daughters of Israel because of Saul weep who clothed you scarlet with luxuries who brought up ornament[s] of gold on clothing your.
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
How! they have fallen [the] mighty [ones] in [the] middle of the battle Jonathan on high places your [is] slain.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
It is distress to me on you O brother my Jonathan you were pleasant to me very it was wonderful love your to me more than [the] love of women.
27 “Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”
How! they have fallen [the] mighty [ones] and they have perished [the] weapons of war.

< 2 Samueli 1 >