< 2 Petro 1 >
1 Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
Simon Peter, a bondservant and Apostle of Jesus Christ: To those to whom there has been allotted the same precious faith as that which is ours through the righteousness of our God and of our Saviour Jesus Christ.
2 Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.
May more and more grace and peace be granted to you in a full knowledge of God and of Jesus our Lord,
3 Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake.
seeing that His divine power has given us all things that are needful for life and godliness, through our knowledge of Him who has appealed to us by His own glorious perfections.
4 Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.
It is by means of these that He has granted us His precious and wondrous promises, in order that through them you may, one and all, become sharers in the very nature of God, having completely escaped the corruption which exists in the world through earthly cravings.
5 Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru.
But for this very reason--adding, on your part, all earnestness-- along with your faith, manifest also a noble character: along with a noble character, knowledge;
6 Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu.
along with knowledge, self-control; along with self-control, power of endurance;
7 Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi.
along with power of endurance, godliness; along with godliness, brotherly affection; and along with brotherly affection, love.
8 Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu.
If these things exist in you, and continually increase, they prevent your being either idle or unfruitful in advancing towards a full knowledge of our Lord Jesus Christ.
9 Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.
For the man in whom they are lacking is blind and cannot see distant objects, in that he has forgotten that he has been cleansed from his old sins.
10 Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse.
For this reason, brethren, be all the more in earnest to make sure that God has called you and chosen you; for it is certain that so long as you practise these things, you will never stumble.
11 Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. (aiōnios )
And so a triumphant admission into the eternal Kingdom of our Lord and Saviour Jesus Christ will be freely granted to you. (aiōnios )
12 Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano.
For this reason I shall always persist in reminding you of these things, although you know them and are stedfast believers in truth which you already possess.
13 Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani,
But I think it right, so long as I remain in the body, my present dwelling-place, to arouse you by such reminders.
14 chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu.
For I know that the time for me to lay aside my body is now rapidly drawing near, even as our Lord Jesus Christ has revealed to me.
15 Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.
So on every possible occasion I will also do my best to enable you to recall these things after my departure.
16 Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake.
For when we made known to you the power and Coming of our Lord Jesus Christ, we were not eagerly following cleverly devised legends, but we had been eye-witnesses of His majesty.
17 Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.”
He received honour and glory from God the Father, and out of the wondrous glory words such as these were spoken to Him, "This is My dearly-loved Son, in whom I take delight."
18 Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.
And we ourselves heard these words come from Heaven, when we were with Him on the holy mountain.
19 Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu.
And in the written word of prophecy we have something more permanent; to which you do well to pay attention--as to a lamp shining in a dimly-lighted place--until day dawns and the morning star rises in your hearts.
20 Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha.
But, above all, remember that no prophecy in Scripture will be found to have come from the prophet's own prompting;
21 Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.
for never did any prophecy come by human will, but men sent by God spoke as they were impelled by the Holy Spirit.