< 2 Petro 1 >

1 Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
Simon Peter, Jesu Kristi Tjener og Apostel, til dem, der have fået samme dyrebare Tro som vi ved vor Guds og Frelsers Jesu Kristi Retfærdighed:
2 Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.
Nåde og Fred vorde eder mangfoldig til Del i Erkendelse af Gud og vor Herre Jesus.
3 Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake.
Såsom hans guddommelige Magt har skænket os alt, hvad der hører til Liv og Gudfrygtighed ved Erkendelsen af ham, som kaldte os ved sin Herlighed og Kraft,
4 Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.
hvorved han har skænket os de største og dyrebare Forjættelser, for at I ved disse skulle få Del i guddommelig Natur, når I undfly Fordærvelsen i Verden, som har sin Grund i Begær,
5 Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru.
så anvender just derfor al Flid på i eders Tro at udvise Dyd og i Dyden Kundskab
6 Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu.
og i Kundskaben Afholdenhed og i Afholdenheden Udholdenhed og i Udholdenheden Gudsfrygt
7 Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi.
og i Gudsfrygten Broderkærlighed og i Broderkærligheden Kærlighed.
8 Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu.
Thi når dette findes hos eder og er i Tiltagen, lader det eder ikke stå ørkesløse eller ufrugtbare i Erkendelsen af vor Herre Jesus Kristus;
9 Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.
den nemlig, som ikke har dette, er blind, svagsynet, idet han har glemt Renselsen fra sine fordums Synder.
10 Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse.
Derfor, Brødre! gører eder des mere Flid for at befæste eders Kaldelse og Udvælgelse; thi når I gøre dette, skulle I ingen Sinde støde an.
11 Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. (aiōnios g166)
Thi så skal der rigelig gives eder Indgang i vor Herres og Frelsers Jesu Kristi evige Rige. (aiōnios g166)
12 Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano.
Derfor vil jeg ikke forsømme altid at påminde eder om delte, ihvorvel I vide det og ere befæstede i den Sandhed, som er til Stede hos os.
13 Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani,
Men jeg anser det for ret at vække eder ved Påmindelse, så længe jeg er i dette Telt,
14 chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu.
da jeg ved, at Aflæggelsen af mit Telt kommer brat, således som jo vor Herre Jesus Kristus har givet mig til Kende.
15 Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.
Og jeg vil også gøre mig Flid for, at I til enhver Tid efter min Bortgang kunne drage eder dette i Minde.
16 Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake.
Thi vi have ikke fulgt klogtigt opdigtede Fabler, da vi kundgjorde eder vor Herres Jesu Kristi Kraft og Tilkommelse, men vi have været Øjenvidner til hans Majestæt,
17 Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.”
nemlig da han fik Ære og Herlighed af Gud Fader, idet en sådan Røst lød til ham fra den majestætiske Herlighed: "Denne er min Søn, den elskede, i hvem jeg har Velbehag."
18 Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.
Og vi hørte denne Røst lyde fra Himmelen, da vi vare med ham på det hellige Bjerg.
19 Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu.
Og des mere stadfæstet have vi det profetiske Ord, hvilket I gøre vel i at agte på som på et Lys, der skinner på et mørkt Sted, indtil Dagen bryder frem, og Morgenstjernen oprinder i eders Hjerter,
20 Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha.
idet I fornemmelig mærke eder dette, at ingen Profeti i Skriften beror på egen Tydning.
21 Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.
Thi aldrig er nogen Profeti bleven fremført ved et Menneskes Villie; men drevne af den Helligånd talte hellige Guds Mænd.

< 2 Petro 1 >