< 2 Petro 3 >
1 Inu okondedwa, iyi ndi kalata yanga yachiwiri kwa inu. Ine ndalemba makalata onse awiri kuti ndikukumbutseni ndi kukutsitsimutsani ndi cholinga choti muzilingalira moyenera.
Píši vám už druhý dopis, moji milí přátelé. V obou jsem se snažil ve vás probouzet čisté smýšlení a připomínat vám skutečnosti, které jsou vám známy z poselství Božích proroků a vašich apoštolů, kteří vám přinesli slovo našeho Pána a Zachránce.
2 Ndikufuna kuti mukumbukire mawu amene anayankhulidwa kale ndi aneneri oyera mtima ndiponso lamulo limene Ambuye ndi Mpulumutsi wathu analipereka kudzera mwa atumwi.
3 Poyamba mudziwe kuti mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, adzanyoza ndi kutsata zilakolako zawo zoyipa.
Především vám chci připomenout, že v posledních dnech tohoto světa se objeví posměvači, kteří si budou žít po svém
4 Iwo adzati, “Kodi suja Ambuye analonjeza kuti adzabweranso? Nanga ali kuti? Lija nʼkale anamwalira makolo athu, koma zinthu zonse zili monga anazilengera poyamba paja.”
a budou se vysmívat: „Ježíš přece slíbil, že znovu přijde. Kde tedy je? Naši otcové již zemřeli a od stvoření světa se nic nezměnilo.“
5 Koma iwo akuyiwala dala kuti Mulungu atanena mawu, kumwamba kunakhalapo ndipo analenga dziko lapansi ndi madzi.
Úmyslně přehlížejí skutečnost, že nebe i zemi stvořil Bůh svým slovem. Přikázal a země vystoupila z vody.
6 Ndi madzinso achigumula, dziko lapansi la masiku amenewo linawonongedwa.
Opět poručil a voda celou zemi při potopě zachvátila.
7 Dziko la kumwamba ndi lapansi la masiku ano akulisunga ndi mawu omwewo kuti adzalitentha ndi moto. Akuzisunga mpaka tsiku limene adzaweruza ndi kuwononga anthu onse osapembedza Mulungu.
A nyní totéž Boží slovo uchovává náš svět až do dne, kdy bezbožní budou odsouzeni a zničeni ohněm.
8 Koma abale okondedwa, musayiwale chinthu chimodzi ichi: Kuti pamaso pa Ambuye tsiku limodzi lili ngati zaka 1,000, ndipo zaka 1,000 zili ngati tsiku limodzi!
Ale nezapomínejme, moji drazí přátelé, že pojem času u Pána je jiný než u nás. Pro něho může být jeden den jako tisíc let a tisíc let jako pouhý den.
9 Ambuye sazengereza kuchita zimene analonjeza, monga ena amaganizira. Iwo akukulezerani mtima, sakufuna kuti aliyense awonongeke, koma akufuna kuti aliyense alape.
Není to tak, jak si někteří myslí, že by se s naplněním svých slibů opozdil. Spíše má s námi velkou trpělivost. Nechce, aby byl někdo zničen, ale aby všichni zanechali své bezbožnosti a obrátili se k němu.
10 Koma tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala. Pa tsikuli zinthu zakumwamba zidzachoka ndi phokoso lalikulu. Zinthu zonse zidzawonongedwa ndi moto, ndipo dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzapsa.
Den soudu přijde tak náhle a nečekaně jako zloděj v noci. V ten den zmizí nebesa s děsivým rachotem, hmota se bude žárem rozkládat a země se vším, co je na ní, bude spálena.
11 Popeza kuti zinthu zonse zidzawonongedwa motere, kodi inu muyenera kukhala anthu otani? Muyenera kukhala moyo wachiyero ndi opembedza Mulungu
Když všechno má takto podlehnout zkáze, jak se na ten den připravíte? Nechte se vést Božím slovem a poddejte se Bohu.
12 pamene mukuyembekezera tsiku la Mulungu ndi kufulumiza kufika kwake. Pa tsiku limeneli zinthu zakumwamba zidzawonongedwa ndi moto, ndipo zidzasungunuka ndi kutentha.
Dokazujte, že na ten den čekáte a upřímně po něm toužíte. Je pravda, že v ten den nebesa shoří a hmota se rozplyne strašlivým žárem,
13 Koma ife tikudikira kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano, zimene Mulungu analonjeza, mʼmene chilungamo chidzakhalamo.
ale naše naděje se upíná k novému nebi a nové zemi, které nám Bůh přislíbil. Tam bude jen dobro.
14 Chomwecho okondedwa, popeza inu mukudikira zimenezi, chitani changu kuti mukhale wopanda chilema kuti mukhale pa mtendere ndi Iye.
Moji drazí, očekáváte-li tyto věci, usilujte o čistý život, protože jedině tak můžete jít vstříc Božímu soudu beze strachu.
15 Zindikirani kuti kuleza mtima kwa Ambuye kukutanthauza chipulumutso, monga momwe mʼbale wathu wokondedwa Paulo anakulemberaninso ndi nzeru zimene Mulungu anamupatsa.
Uvědomte si, že ve své trpělivosti vám Pán poskytuje čas ke spáse. O tom vám už psal náš drahý bratr Pavel s moudrostí, která mu byla dána Bohem.
16 Iye walemba chimodzimodzi makalata ake onse, kuyankhula za zinthu izi. Mʼmakalata ake mumakhala zinthu zina zovuta kuzimvetsa, zimene anthu osadziwa ndi osakhazikika amazipotoza, monga amachita ndi malemba ena onse, potero akudziwononga okha.
Mluví tak o tom ve všech svých dopisech. Je pravda, že jsou tam některé věci nesnadněji pochopitelné a těch se chytají nerozumní a nevyrovnaní lidé, kteří jeho dopisy překrucují.
17 Nʼchifukwa chake, abale okondedwa, popeza mukuzidziwa kale zimenezi, chenjerani kuti musatengeke ndi zolakwa za anthu osaweruzika, mungagwe ndi kuchoka pamalo otetezedwa.
Ale oni to činí i s ostatními částmi Písma, čímž přivolávají na sebe zkázu. Moji milovaní, varoval jsem vás, a tak si dejte pozor, aby ani vás tito bludaři nestrhli z pevného základu víry.
18 Koma kulani mu chisomo ndi mʼchidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Usilujte o duchovní růst a hlubší poznání Pána Ježíše Krista. Jemu patří všechna sláva již nyní i na věčnosti! Petr (aiōn )