< 2 Petro 2 >
1 Koma panalinso aneneri onama pakati pa Aisraeli, monga padzakhalanso aphunzitsi onyenga pakati panu. Iwo adzalowetsa mwamseri ziphunzitso zonama ndi zowononga, nadzakana Ambuye amene anawawombola, ndipo motero adzadziyitanira okha chiwonongeko mwadzidzidzi.
But also false prophetis weren in the puple, as in you schulen be maistris lieris, that schulen bringe in sectis of perdicioun; and thei denyen thilke Lord that bouyte hem, and bringen on hem silf hasti perdicioun.
2 Ambiri adzatsata njira zawo zochititsa manyazi ndipo chifukwa cha iwowa, anthu adzanyoza njira ya choonadi.
And many schulen sue her letcheries, bi whiche the weie of treuthe schal be blasfemyd;
3 Pofuna kupeza chuma, aphunzitsiwa adzakudyerani chuma chanu pokuwuzani nkhani zopeka. Chiweruzo chawo chinakonzedwa kale, ndipo chikuwadikira.
and thei schulen make marchaundie of you in coueytise bi feyned wordis. To whiche doom now a while ago ceessith not, and the perdicioun of hem nappith not.
4 Pakuti Mulungu sanalekerere angelo atachimwa paja, koma anawaponya mʼndende, nawayika mʼmaenje amdima, kuwasunga kuti adzaweruzidwe. (Tartaroō )
For if God sparide not aungels synnynge, but bitook hem to be turmentid, and to be drawun doun with boondis of helle in to helle, to be kept in to dom; (Tartaroō )
5 Iye sanalekerere dziko lapansi kalelo, koma anapulumutsa Nowa, mlaliki wa chilungamo, ndi anthu ena asanu ndi awiri atadzetsa chigumula pa dziko lapansi kwa anthu akhalidwe losapembedza Mulunguyo.
and sparide not the firste world, but kept Noe, the eiythe man, the biforgoere of riytwisnesse, and brouyte in the greet flood to the world of vnfeithful men;
6 Mulungu anaweruza mizinda ya Sodomu ndi Gomora nayiwononga ndi moto, kuti ikhale chitsanzo cha zimene zidzachitikira anthu osapembedza Mulungu.
and he droof in to poudre the citees of men of Sodom and of men of Gommor, and dampnede bi turnyng vpsedoun, and putte hem the ensaumple of hem that weren to doynge yuele;
7 Koma Iye anapulumutsa Loti, munthu wolungama, amene ankavutika ndi khalidwe lonyansa la anthu oyipa.
and delyuerid the iust Loth, oppressid of the wrong, and of the letcherouse conuersacioun of cursid men;
8 (Pakuti munthu wolungamayo, pokhala pakati pawo tsiku ndi tsiku ankavutika mu mtima ndi makhalidwe awo oyipa amene ankawaona ndi kuwamva).
for in siyt and hering he was iust, and dwellide amongst hem that fro dai in to dai turmentiden with wickid werkis a iust soule.
9 Tsono mutha kuona kuti Ambuye amadziwa kuwapulumutsa kwake pa mayesero anthu opembedza. Amadziwanso kusunga osalungama kuti alangidwe mpaka tsiku la chiweruzo.
For the Lord kan delyuere piteuouse men fro temptacioun, and kepe wickid men `in to the dai of dom to be turmentid;
10 Makamaka amene amatsata zilakolako zonyansa zathupi nanyoza ulamuliro. Anthu amenewa ndi odzikuza, ndipo otsata chifuniro cha iwo eni, sasamala za munthu, saopa kuchitira chipongwe zolengedwa za mmwamba.
but more hem that walken aftir the fleisch, in coueytinge of vnclennesse, and dispisen lordschiping, and ben boold, plesynge hem silf, and dreden not to bringe in sectis, blasfemynge; where aungels,
11 Komatu ngakhale angelo, amene ali akulu ndi amphamvu kuwaposa, sayankhula za chipongwe pobweretsa chiweruzo pa iwo kuchokera kwa Ambuye.
whanne thei ben more in strengthe and vertu, beren not `that was the execrable doom ayens hem.
12 Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ali ngati zirombo zopanda nzeru. Zirombo zolengedwa kuti zigwidwe ndi kuwonongedwa, ndipo ngati zirombozo adzawonongedwa.
But these ben as vnresonable beestis, kyndli in to takyng, and in to deth, blasfemynge in these thingis that thei knowen not, and schulen perische in her corrupcioun,
13 Iwo adzalangidwa chifukwa cha zoyipa zimene anachita. Koma chimene chimawakomera ndi kumangochita zokondweretsa thupi masanasana. Iwo ali ngati mawanga ndi zilema. Podya nanu pamodzi amakondwera kuchita za chinyengo.
and resseyue the hire of vnriytwisnesse. And thei gessen delicis of defouling and of wemme, to be likyngis of dai, flowynge in her feestis with delicis, doynge letcherie with you,
14 Ndi maso awo odzaza ndi chigololo, salekeza kuchimwa. Amanyengerera anthu osakhazikika. Iwo ndi akatswiri pa dyera ndi chuma, ndipo ndi ana otembereredwa!
and han iyen ful of auowtrie, and vnceessynge trespas, disseyuynge vnstidfast soulis, and han the herte excercisid to coueitise; the sones of cursyng,
15 Iwo anasiya njira yolungama ndipo anapatuka kutsata njira ya Baalamu mwana wa Beori, amene anakonda malipiro a chosalungama.
that forsaken the riyt weie, and erriden, suynge the weie of Balaam of Bosor, which louyde the hire of wickidnesse.
16 Koma anadzudzulidwa chifukwa cha kulakwa kwakeko. Bulu, nyama imene siyankhula, inayankhula ngati munthu kuletsa misala ya mneneriyo.
But he hadde repreuyng of his woodnesse; a doumb beest vndur yok, that spak with vois of man, that forbede the vnwisdom of the profete.
17 Anthu amenewa ali ngati akasupe wopanda madzi, ndiponso ngati nkhungu yowuluzidwa ndi mphepo yamkuntho. Mulungu wawasungira mdima wandiweyani.
These ben wellis with out watir, and mystis dryuun with `whirlinge wyndys, to whiche the thicke mijst of derknessis is reseruyd.
18 Pakuti anayankhula mawu opanda pake ndi onyada, ndipo ndi zilakolako zoyipa za thupi amanyenga anthu amene angopulumuka kumene pakati pa anzawo oyipa.
And thei speken in pryde of vanyte, and disseyuen in desiris of fleisch of letcherie hem, that scapen a litil.
19 Amawalonjeza ufulu, pomwe iwo eni ndi akapolo a zizolowezi zowononga. Pajatu munthu amakhala kapolo wa chilichonse chimene chikumulamulira.
Whiche lyuen in errour, and biheten fredom to hem, whanne thei ben seruauntis of corrupcioun. For of whom ony man is ouercomun, of hym also he is seruaunt.
20 Ngati anapulumuka ku zodetsa za dziko lapansi podziwa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu, pambuyo pake nagwidwanso ndi kugonjetsedwa ndi zomwezo, potsiriza adzakhala oyipa kuposa mmene analili poyamba.
For if men forsaken the vnclennessis of the world, bi the knowyng of oure Lord and sauyour Jhesu Crist, and eftsone ben wlappid in these, and ben ouercomun, the lattere thingis ben maad to hem worse than the formere.
21 Kukanakhala bwino akanapanda kudziwa njira ya chilungamo, koposa ndi kuyileka atadziwa lamulo loyera limene Mulungu anawapatsa.
For it was betere to hem to not knowe the weie of riytwisnesse, than to turne ayen aftir the knowyng, fro that hooli maundement that was bitakun to hem.
22 Kwa iwo miyambi iyi ndi yoona, “Galu wabwerera ku masanzi ake,” ndipo, “Nkhumba imene inasamba, yakunkhunizikanso mʼmatope.”
For thilke very prouerb bifelde to hem, The hound turnede ayen to his castyng, and a sowe is waischun in walwyng in fenne.