< 2 Petro 2 >
1 Koma panalinso aneneri onama pakati pa Aisraeli, monga padzakhalanso aphunzitsi onyenga pakati panu. Iwo adzalowetsa mwamseri ziphunzitso zonama ndi zowononga, nadzakana Ambuye amene anawawombola, ndipo motero adzadziyitanira okha chiwonongeko mwadzidzidzi.
V Božím lidu se vyskytli i lživí proroci, jako se objeví i mezi vámi lživí učitelé. Vymyslí různé bludné nauky o Bohu. Dokonce budou zapírat Pána, který je vykoupil, ale tím na sebe přivodí rychlý a hrozný pád.
2 Ambiri adzatsata njira zawo zochititsa manyazi ndipo chifukwa cha iwowa, anthu adzanyoza njira ya choonadi.
Mnoho lidí se dá strhnout jejich zhoubným učením a tím zhanobí cestu pravdy.
3 Pofuna kupeza chuma, aphunzitsiwa adzakudyerani chuma chanu pokuwuzani nkhani zopeka. Chiweruzo chawo chinakonzedwa kale, ndipo chikuwadikira.
Ve své hrabivosti vám budou namlouvat různé výmysly, aby z vás těžili. Ale soud je jim v patách a jejich zkáza je blízká.
4 Pakuti Mulungu sanalekerere angelo atachimwa paja, koma anawaponya mʼndende, nawayika mʼmaenje amdima, kuwasunga kuti adzaweruzidwe. (Tartaroō )
Vždyť Bůh neušetřil ani anděly, kteří proti němu zhřešili, ale uvrhl je do temného vězení, kde očekávají den soudu. (Tartaroō )
5 Iye sanalekerere dziko lapansi kalelo, koma anapulumutsa Nowa, mlaliki wa chilungamo, ndi anthu ena asanu ndi awiri atadzetsa chigumula pa dziko lapansi kwa anthu akhalidwe losapembedza Mulunguyo.
Neušetřil ani svět před potopou; zachránil jenom kazatele spravedlnosti Noeho a sedm jiných.
6 Mulungu anaweruza mizinda ya Sodomu ndi Gomora nayiwononga ndi moto, kuti ikhale chitsanzo cha zimene zidzachitikira anthu osapembedza Mulungu.
Také města Sodomu a Gomoru obrátil v popel a odsoudil k zániku jako výstražný příklad do budoucnosti pro bezbožné.
7 Koma Iye anapulumutsa Loti, munthu wolungama, amene ankavutika ndi khalidwe lonyansa la anthu oyipa.
Zachránil však zbožného Lota, muže, který se trápil nad nemravným životem svých současníků.
8 (Pakuti munthu wolungamayo, pokhala pakati pawo tsiku ndi tsiku ankavutika mu mtima ndi makhalidwe awo oyipa amene ankawaona ndi kuwamva).
9 Tsono mutha kuona kuti Ambuye amadziwa kuwapulumutsa kwake pa mayesero anthu opembedza. Amadziwanso kusunga osalungama kuti alangidwe mpaka tsiku la chiweruzo.
Pán totiž dovede ochránit zbožné lidi, kteří se octli v pokušení, ale hříšné potrestá v den soudu – zvláště pak ty, kteří propadají svým hříšným vášním a pohrdají každou autoritou. Takoví lživí učitelé jsou pyšní, samolibí, opovážliví a nebojí se ani nadpozemských bytostí.
10 Makamaka amene amatsata zilakolako zonyansa zathupi nanyoza ulamuliro. Anthu amenewa ndi odzikuza, ndipo otsata chifuniro cha iwo eni, sasamala za munthu, saopa kuchitira chipongwe zolengedwa za mmwamba.
11 Komatu ngakhale angelo, amene ali akulu ndi amphamvu kuwaposa, sayankhula za chipongwe pobweretsa chiweruzo pa iwo kuchokera kwa Ambuye.
Přesto andělé, nesrovnatelně mocnější a silnější, je nekritizují a nehaní před Pánem.
12 Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ali ngati zirombo zopanda nzeru. Zirombo zolengedwa kuti zigwidwe ndi kuwonongedwa, ndipo ngati zirombozo adzawonongedwa.
Tito falešní učitelé jednají podle svých tělesných popudů. Stejně jako nerozumná zvířata, přírodou určená k polapení a záhubě, čeká i tyto falešné učitele stejný konec. Vysmívají se tomu, čemu nerozumějí;
13 Iwo adzalangidwa chifukwa cha zoyipa zimene anachita. Koma chimene chimawakomera ndi kumangochita zokondweretsa thupi masanasana. Iwo ali ngati mawanga ndi zilema. Podya nanu pamodzi amakondwera kuchita za chinyengo.
jejich hříšnost je přivede do záhuby a za svou špatnost budou pykat. Tito lidé uspokojují den za dnem jen svoji pudovost, jsou samá skvrna a hanba, když se s nimi sejdete u stolu, jsou nevázaně poživační.
14 Ndi maso awo odzaza ndi chigololo, salekeza kuchimwa. Amanyengerera anthu osakhazikika. Iwo ndi akatswiri pa dyera ndi chuma, ndipo ndi ana otembereredwa!
Jejich pohled na ženu je vždy plný smyslnosti a jejich touha po hříchu je nenasytná. Svádějí slabé lidi a propadli hrabivosti. Jsou to zplozenci prokletí.
15 Iwo anasiya njira yolungama ndipo anapatuka kutsata njira ya Baalamu mwana wa Beori, amene anakonda malipiro a chosalungama.
Opustili správnou cestu a zbloudili jako Bileám, syn Beórův, kterého ovládla představa, že by mohl získat peníze vykonáním nešlechetného činu.
16 Koma anadzudzulidwa chifukwa cha kulakwa kwakeko. Bulu, nyama imene siyankhula, inayankhula ngati munthu kuletsa misala ya mneneriyo.
Byl však usvědčen z chystané špatnosti: němá oslice promluvila lidským hlasem a zabránila mu v nemoudrém jednání.
17 Anthu amenewa ali ngati akasupe wopanda madzi, ndiponso ngati nkhungu yowuluzidwa ndi mphepo yamkuntho. Mulungu wawasungira mdima wandiweyani.
Tito lživí učitelé jsou neužiteční jako studně bez jediné kapky vody, nestálí jako mraky po vichřici; jsou určeni ke zkáze ve věčné temnotě. ()
18 Pakuti anayankhula mawu opanda pake ndi onyada, ndipo ndi zilakolako zoyipa za thupi amanyenga anthu amene angopulumuka kumene pakati pa anzawo oyipa.
Mluví nadutě o nesmyslných věcech a svou nemravností a nízkými vášněmi svádějí zpět do hříchu ty, kteří se rozhodli s hříchem skoncovat.
19 Amawalonjeza ufulu, pomwe iwo eni ndi akapolo a zizolowezi zowononga. Pajatu munthu amakhala kapolo wa chilichonse chimene chikumulamulira.
Slibují jim svobodu, ale sami jsou otrocky oddáni svým zvrácenostem. Vždyť člověk je otrokem toho, čemu podléhá.
20 Ngati anapulumuka ku zodetsa za dziko lapansi podziwa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu, pambuyo pake nagwidwanso ndi kugonjetsedwa ndi zomwezo, potsiriza adzakhala oyipa kuposa mmene analili poyamba.
Jestliže tedy ti, kdo poznáním Pána a Spasitele Ježíše Krista unikli svodům světa, znovu se do nich zapletou a podlehnou jim, dočkají se toho, že jejich konce budou horší než začátky.
21 Kukanakhala bwino akanapanda kudziwa njira ya chilungamo, koposa ndi kuyileka atadziwa lamulo loyera limene Mulungu anawapatsa.
Pro takové by bylo lepší, kdyby tu pravou cestu vůbec nepoznali, než když se po jejím poznání od Božího poselství odvrátili.
22 Kwa iwo miyambi iyi ndi yoona, “Galu wabwerera ku masanzi ake,” ndipo, “Nkhumba imene inasamba, yakunkhunizikanso mʼmatope.”
Na ně se hodí staré přísloví: „Pes se vrací k tomu, co vyzvracel“a „Umyté prase se znovu válí v blátě.“