< 2 Petro 1 >
1 Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
Simon Peter, slave and apostle of Jesus Christ, to those who have obtained with us the same kind of faith in the righteousness of our God and Savior, Jesus Christ:
2 Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.
may grace and peace be multiplied to you through a real knowledge of God and of our Lord Jesus,
3 Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake.
in that His divine power has granted to us all things pertaining to life and godliness, through the real knowledge of the One who called us by glory and excellence,
4 Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.
through which He has granted to us such precious and extraordinary promises, so that through these you may become partakers of a divine nature, having escaped the depravity that is in the world because of lust.
5 Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru.
So for this very reason, making every effort, to your faith add excellence, and to the excellence knowledge,
6 Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu.
and to the knowledge self-control, and to the self-control perseverance, and to the perseverance godliness,
7 Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi.
and to the godliness brotherly affection, and to the brotherly affection love.
8 Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu.
Because with these things existing and increasing in you, it makes you to be neither useless nor unfruitful in the real knowledge of our Lord Jesus Christ.
9 Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.
For he who lacks these things is blind, being so myopic, having forgotten the cleansing from his past sins.
10 Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse.
Therefore, brothers, you should be all the more diligent to make your calling and election sure, for if you do these things you will never stumble.
11 Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. (aiōnios )
Because in this way you will be granted the abundant entrance into the unending kingdom of our Lord and Savior, Jesus Christ. (aiōnios )
12 Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano.
So then, I will not neglect to keep reminding you about these things, though you know and are established in the present truth.
13 Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani,
Yes, I think it right to stir you up by a reminder, as long as I am in this ‘tent’,
14 chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu.
knowing that the shedding of my ‘tent’ is imminent, just as our Lord Jesus Christ has made clear to me.
15 Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.
Moreover I will take pains to provide a reminder of these things for you to have, as needed, after my exit.
16 Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake.
Now then, we did not follow craftily devised fables when we made known to you the power and coming of our Lord Jesus Christ; rather we were attentive eyewitnesses of His majesty
17 Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.”
—because He received from God the Father honor and glory when that Voice was directed to Him by the Magnificent Glory, “This is my Son, the beloved, in whom I am always well pleased”—
18 Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.
yes, we heard this Voice being uttered from heaven when we were with Him on the holy mountain.
19 Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu.
And so we have the most reliable prophetic Word, to which you do well to pay attention as to a lamp shining in a dark place, until the day dawns and the morning star rises in your hearts;
20 Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha.
knowing this first, that no Prophecy of Scripture comes to be from private release;
21 Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.
for no Prophecy ever came by the will of man, rather holy men of God spoke as they were carried along by the Holy Spirit.