< 2 Mafumu 1 >

1 Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
UMowabi wasevukela uIsrayeli emva kokufa kukaAhabi.
2 Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
UAhaziya wasesiwa eminxibeni yewindi ekamelweni lakhe eliphezulu eliseSamariya, wagula. Wathuma izithunywa, wathi kuzo: Hambani liyebuza kuBhali-Zebhubi unkulunkulu weEkhironi ukuthi ngizasila yini emkhuhlaneni lo.
3 Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
Kodwa ingilosi yeNkosi yathi kuElija umTishibi: Sukuma, wenyuke ukuhlangabeza izithunywa zenkosi yeSamariya, uthi kizo: Kungenxa yokuthi kakulaNkulunkulu yini koIsrayeli ukuthi lihambe liyebuza kuBhali-Zebhubi unkulunkulu weEkhironi?
4 Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
Ngakho-ke itsho njalo iNkosi: Umbheda owenyukele kuwo kawuyikwehla kuwo, ngoba uzakufa lokufa. UElija wasehamba.
5 Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
Lapho izithunywa sezibuyele kuyo, wathi kuzo: Kungani selibuyile?
6 Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
Zasezisithi kuyo: Umuntu wenyukile ukusihlangabeza, wathi kithi: Hambani libuyele enkosini elithumileyo, lithi kuyo: Itsho njalo iNkosi: Kungenxa yokuthi kakulaNkulunkulu koIsrayeli yini ukuthi uthumele ukubuza kuBhali-Zebhubi unkulunkulu weEkhironi? Ngakho umbheda owenyukele kuwo kawuyikwehla kuwo, ngoba sibili uzakufa.
7 Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
Yasisithi kuzo: Besinjani isimo salowomuntu owenyukele ukulihlangabeza, wakhuluma kini lamazwi?
8 Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
Basebesithi kuyo: Ubeyindoda eloboya, ebophe ngozwezwe lwesikhumba ekhalweni lwayo. Yasisithi: NguElija umTishibi.
9 Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
Inkosi yasithuma kuye induna yabangamatshumi amahlanu labangamatshumi amahlanu bayo. Yasisenyukela kuye; khangela-ke, wayehlezi engqongeni yentaba; yathi kuye: Muntu kaNkulunkulu, inkosi ithe: Yehla.
10 Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
UElija wasephendula wathi enduneni yabangamatshumi amahlanu: Uba-ke ngingumuntu kaNkulunkulu, kakwehle umlilo ovela emazulwini uqothule wena labangamatshumi amahlanu bakho. Wasusehla umlilo uvela emazulwini, wayiqothula yona labangamatshumi amahlanu bayo.
11 Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
Yasibuya ithuma kuye enye induna yabangamatshumi amahlanu labangamatshumi amahlanu bayo. Yasiphendula yathi kuye: Muntu kaNkulunkulu, itsho njalo inkosi: Yehla masinyane.
12 Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
UElija wasephendula wathi kubo: Uba ngingumuntu kaNkulunkulu, kakwehle umlilo ovela emazulwini uqothule wena labangamatshumi amahlanu bakho. Wasusehla umlilo kaNkulunkulu uvela emazulwini, wayiqothula yona labangamatshumi amahlanu bayo.
13 Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
Yasithuma futhi induna yabangamatshumi amahlanu besithathu labangamatshumi amahlanu bayo. Leyonduna yesithathu yabangamatshumi amahlanu yasisenyuka yeza yawa ngamadolo ayo phambi kukaElija, yamncenga yathi kuye: Muntu kaNkulunkulu, ake ibe ligugu impilo yami lempilo yalezi inceku zakho ezingamatshumi amahlanu emehlweni akho.
14 Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
Khangela, wehla umlilo uvela emazulwini, waqothula induna ezimbili zabangamatshumi amahlanu zokuqala labangamatshumi amahlanu azo; ngakho-ke kayibe ligugu impilo yami emehlweni akho.
15 Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
Ingilosi yeNkosi yasisithi kuElija: Yehla laye, ungamesabi. Wasesukuma, wehla laye waya enkosini;
16 Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
wathi kuyo: Itsho njalo iNkosi: Ngenxa yokuthi uthume izithunywa ukuyabuza kuBhali-Zebhubi, unkulunkulu weEkhironi, kungenxa yokuthi kakulaNkulunkulu koIsrayeli yini, ukubuza ilizwi lakhe? Ngakho-ke umbheda owenyukele kuwo kawuyikwehla kuwo, ngoba uzakufa lokufa.
17 Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
Wasesifa njengokwelizwi leNkosi uElija ayelikhulumile. UJehoramu wasesiba yinkosi esikhundleni sakhe, ngomnyaka wesibili kaJoramu indodana kaJehoshafathi inkosi yakoJuda, ngoba wayengelandodana.
18 Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
Ezinye-ke zezindaba zikaAhaziya, azenzayo, kazibhalwanga yini egwalweni lwemilando yamakhosi akoIsrayeli?

< 2 Mafumu 1 >