< 2 Mafumu 9 >

1 Mneneri Elisa anayitanitsa mmodzi mwa ana a aneneri, namuwuza kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga botolo la mafuta mʼdzanja lako ndipo upite ku Ramoti Giliyadi.
A KAHEA aku la o Elisai ke kaula i kekahi o na haumana a ka poe kaula, i aku la ia ia, E kaei oe i kou puhaka, a lawe i keia hue aila ma kou lima, a e hele aku i Ramota-Gileada.
2 Ukakafika kumeneko, ukafunefune Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi. Ukapite kwa iye, ukamuchotse pakati pa anzake ndi kukamulowetsa mʼchipinda chamʼkati.
A hiki oe ilaila, e imi aku oe ilaila ia Iehu, ko keiki a Iehosapata, ke keiki a Nimesi, a komo aku oe, a hooku ia ia mai waena mai o kona poe hoahanau, a hookomo ia ia i ke keena maloko.
3 Ndipo ukatenge botololi ndi kuthira mafuta pa mutu wake ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ Kenaka ukatsekule chitseko ndi kuthawa ndipo usakachedwe!”
Alaila e lawe oe i ka hue aila, a e ninini maluna o kona poo, a e i aku, Ke olelo mai nei o Iehova peneia, Ua poni aku au ia oe i alii maluna o ka Iseraela. Alaila e wehe ae oe i ka puka, a holo aku, mai kali oe.
4 Choncho mneneri wachinyamatayo anapita ku Ramoti Giliyadi.
A hele aku la ke kanaka ui i Ramota-Gileada, he kaula hoi ua kanaka ui la.
5 Atafika ku Giliyadiko anapeza atsogoleri a ankhondo ali pa msonkhano. Iye anati, “Mtsogoleri, ine ndili ndi uthenga wanu.” Ndipo Yehu anafunsa kuti, “Uthengawo ndi wa yani pakati pathu?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndi wa inuyo, mtsogoleri.”
A hiki aku ia, aia hoi, e noho ana na luna o ke kaua; i aku la ia, Ho wahi olelo ka'u ia oe, e ka luna. I mai la o Iehu, Ia wai o makou a pau? I aku la ia, Ia oe, e ka luna.
6 Yehu anayimirira nakalowa mʼnyumba. Pamenepo mneneriyo anakhuthulira mafuta pamutu pa Yehu ndipo ananena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndikukudzoza kukhala mfumu ya Israeli, anthu a Yehova.
Ku ae la ia a komo iloko o ka hale; a ninini iho la ia i ka aila maluna o kona poo. a i aku la ia ia, Ke olelo mai nei o Iehova ke Akua o ka Iseraela, Ua poni aku au ia oe i alii maluna o na kanaka o Iehova, maluna o ka Iseraela.
7 Uyenera kuwononga nyumba ya mbuye wako Ahabu ndipo ndidzabwezera imfa ya atumiki anga, aneneri ndiponso imfa ya atumiki ena onse a Yehova amene anaphedwa ndi Yezebeli.
A e pepehi aku oe i ko ka hale o Ahaba kou haku, i hoopai aku ai au i ko koko o ka'u poe kauwa, o na kaula, a me ke koko o na kauwa a pau a Iehova ma ka lima o Iezebela.
8 Banja lonse la Ahabu lidzatheratu. Ndidzachotsa munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu kaya ndi kapolo kapena mfulu.
A e pau auanei ko ka hale a pau o Ahaba; a oki aku au i na kane a pau no Ahaba, a o ka mea i paa, a me ka mea i paa ole iloko o ka Iseraela.
9 Ndidzachititsa kuti banja la Ahabu lifanane ndi banja la Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati banja la Baasa mwana wa Ahiya.
A e hana like aku au i ko ka hale o Ahaba me ko ka hale o Ieroboama ke keiki a Nebata, a me ko ka hale o Baasa, ke keiki a Ahiia.
10 Kunena za Yezebeli, agalu adzamudya ku dera la Yezireeli ndipo palibe amene adzamuyike mʼmanda.’” Kenaka mneneriyo anatsekula chitseko nʼkuthawa.
A e ai na ilio ia Iezebela ma ka aina i Iezereela, aohe mea nana ia e kanu. A wehe ae la ia i ka puka, a holo aku la.
11 Yehu atatuluka kupita kumene kunali atsogoleri anzake, mmodzi mwa iwo anamufunsa kuti, “Kodi zonse zili bwino? Kodi munthu wamisala uja anabwera kudzatani kwa iwe?” Yehu anayankha kuti, “Iwe ukumudziwa munthu uja ndiponso ukudziwa zomwe amayankhula.”
Alaila puka iwaho o Iehu i na kauwa a kona haku, a ninau mai kekahi ia ia, He pono anei? No ke aha la i hele mai ai keia hehena i ou la? I aku la ia ia lakou, Ua ike oukou i ke kanaka, a me kana olelo.
12 Atsogoleri aja anati, “Ukunama! Tiwuze.” Yehu anati, “Zimene wandiwuza ndi izi: ‘Yehova akuti: Ine ndakudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’”
I aku la lakou ia ia, He wahahee; e hai mai oe ia makou ano. I mai la ia, Me neia, me neia kana i olelo mai ai ia'u, i mai la, Ke i mai nei o Iehova peneia, Ua poni aku au ia oe i alii maluna o ka Iseraela.
13 Atsogoleri aja mofulumira anatenga zofunda zawo naziyala pansi pa makwerero kuti Yehu akhalepo. Kenaka analiza lipenga, nafuwula kuti, “Yehu ndiye mfumu!”
Alaila wikiwiki lakou, a lawe ae la kela kanaka keia kanaka i kona aahu, a waiho malalo iho ona maluna o ke alapii, a puhi i na pu, i aku la, E alii ana o Iehu.
14 Choncho Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi, anachitira chiwembu Yoramu. (Nthawi imeneyi nʼkuti Yoramu ndi Aisraeli onse akuteteza Ramoti Giliyadi kwa Hazaeli mfumu ya ku Aramu,
A kipi iho la o Iehu ke keiki a Iehosapata, ke keiki a Nimesi, ia Iorama. (A o Iorama e kiai ana ia ma Ramota-Gileada, oia, a me ka Iseraela a pau, no Hazaela ke alii o Suria.
15 koma nʼkuti Yoramu atabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene Aaramu anamuvulaza pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya ku Aramu.) Yehu anati, “Ngati mukugwirizana nazo zimenezi, wina aliyense asatuluke mu mzinda muno kupita kukafotokoza nkhaniyi ku Yezireeli.”
A ua hoi aku o Iorama ke alii ma Iezereela e hoolaia i kona eha a ko Suria i hana eha ai ia ia, i kona manawa i kaua aku ai ia Hazaela ke alii o Suria.) A i aku la o Iehu, Ina oukou e manao, mai puka aku e pakele kekahi mai ke kulanakauhale aku e hele ia e hai aku ma Iezereela.
16 Pamenepo Yehu anakwera galeta lake, napita ku Yezireeli, chifukwa Yoramu anali akupumula kumeneko ndipo Ahaziya, mfumu ya ku Yuda, nʼkuti ali komweko kudzamuona.
A holo aku la o Iehu ma ka halekaa, a hele aku la i Iezereela; no ka mea, e waiho ana o Iorama malaila. A ua iho mai o Ahazia, ke alii o ka Iuda, e ike ia Iorama.
17 Mlonda amene ankayimirira pa nsanja yolondera mzinda wa Yezireeli ataona gulu lankhondo la Yehu likuyandikira, anafuwula kuti, “Ndikuona gulu lankhondo likubwera.” Yoramu analamula kuti, “Peza munthu wokwera kavalo, mutume kuti akakumane nawo ndi kuwafunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’”
A e ku ana ke kanaka kiai maluna o ka hale kiai ma Iezereela, a ike aku la ia i ka poe nui o Iehu i kona hele ana mai, i aku la ia, Ke ike nei au i ka poe nui. I mai la o Iorama, e lawe oe i ka hooholelio, a e hoouna aku e halawai me lakou, a e ninau aku ia, He aloha anei?
18 Choncho munthu wokwera kavalo anapita kukakumana ndi Yehu ndipo anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.” Mlonda uja anakafotokoza kwa mfumu kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwerera.”
A holo aku la kekahi maluna o ka lio e halawai me ia, a i aku la, Ke olelo mai nei ke alii peneia, He aloha anei? I aku la o Iehu, Heaha kau i ke aloha? e huli ae oe mahope o'u. A hai aku la ke kanaka kiai, i aku la, Hele aku la ke elele io lakou la, aole i hoi hou mai.
19 Choncho mfumu inatumanso munthu wina wachiwiri wokwera kavalo. Atafika kwa anthuwo iye anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”
A hoouna hou aku la ia i ka lua maluna o ka lio a hiki aku la ia io lakou la, i aku la, Ke olelo mai nei ke alii peneia, He aloha anei? I aku la o Iehu, Heaha kau i ke aloha? E huli ae oe mahope o'u.
20 Mlonda uja anakanenanso kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwereranso. Kuyendako kukukhala ngati kwa Yehu mwana wa Nimisi, iye amayenda ngati munthu wamisala.”
A hai aku la ke kiai, i aku la, Ua hele aku ia io lakou la, aole i hoi hou mai; a o ka holo ana, ua like me ka holo ana o Iehu ke keiki a Nimesi, no ka mea, ke holo la ia e like me ka hehena huhu.
21 Yoramu analamula kuti, “Konzani galeta langa.” Ndipo atakonza galeta lake, Yoramu mfumu ya Israeli ndi Ahaziya mfumu ya ku Yuda anakwera nʼkutuluka mu mzindamo, aliyense atakwera galeta lake, kukakumana ndi Yehu. Iwo anakumana ndi Yehu pa munda umene unali wa Naboti, wa ku Yezireeli.
I aku o Iorama, E hoomakaukau; a hoomakaukauia iho la kona halekaa. A hele aku la o Iorama ke alii o ka Iseraela, a o Ahazia ke alii o ka Iuda, o kela keia ma kona halekaa iho, a hele aku e halawai me Iehu, a loaa ia lakou ia ma ka aina o Nabota no Iezereela.
22 Yoramu ataona Yehu anafunsa kuti, “Yehu, kodi wabwera mwamtendere?” Yehu anayankha kuti, “Pangakhale bwanji mtendere pamene zopembedza mafano zonse zilipo ndiponso ufiti wa amayi ako Yezebeli uli ponseponse?”
A i ka manawa i ike ai o Iorama ia Iehu, i aku la ia, He aloha anei, e Iehu? Ninau mai la ia, Heaha ke aloha i ka manawa i nui loa ai na hoomanakii o Iezebela kou makuwahine, a me ka anaana ana?
23 Yoramu anatembenuka, nathawa akufuwula kwa Ahaziya kuti, “Ahaziya, anthuwa atiwukira!”
A huli ae la o Iorama, a holo aku la, a i aku la ia Ahazia, He kipi, e Ahazia.
24 Pamenepo Yehu anakoka uta wake ndipo analasa Yoramu kumsana pakati pa mapewa. Muviwo unakalasa mtima wake ndipo anagwa pansi mʼgaleta lakelo.
A lawe o Iehu i ke kikoo ma kona lima, a pana aku la ia Iorama mawaena o kona mau lima, a puka aku la ka pua ma kona puuwai, a haule iho la ia maloko o kona halekaa.
25 Yehu anawuza Bidikara, mtsogoleri wa galeta lake kuti, “Munyamule ndipo ukamuponye mʼmunda umene unali wa Naboti wa ku Yezireeli, chifukwa kumbukira mmene iwe ndi ine tinkayenda pambuyo pa Ahabu abambo ake, kuti Yehova ananeneratu za iye kuti,
Alaila i aku la oia ia Bidekara i kona luna, E kaikai, a hoolei aku ia ia iloko o ka aina kihapai o Nabota no Iezereela; no ka mea, e hoomanao oe i ka wa a kaua elua i holo pu ai, mamuli o Ahaba kona makuakane, ua kau mai o Iehova i keia mea kaumaha maluna iho ona.
26 ‘Zoonadi dzulo ndinaona magazi a Naboti ndi magazi a ana ake, akutero Yehova, ndipo Ine ndidzakubwezera ndithu choyipa chimenechi pa munda womwe uno, akutero Yehova.’ Tsono munyamule ndipo ukamuponye mʼmundamo, potsatira zimene Yehova ananena.”
Ua ike io no au inehinei i ke koko o Nabota, a me ke koko o kana mau keiki, wahi a Iehova; a e hoopai aka au ia oe ma keia aina, wahi a Iehova. Ano hoi, e lawe, a e hoolei aku ia ia iloko o ua aina la, e like me ka olelo a Iehova.
27 Ahaziya mfumu ya ku Yuda ataona zimene zinachitika, anathawira ku Beti Hagani. Yehu anamuthamangitsa, uku akufuwula kuti, “Mupheninso!” Iwo anamuvulaza ali mʼgaleta lakelo pa njira yopita ku Guri pafupi ndi Ibuleamu, koma iye anathawira ku Megido ndipo anakafera kumeneko.
A ike aku la o Ahazia ke alii o ka Iuda, alaila holo aku la ia ma ke ala o ka hale ma ke kihapai. A hahai aku la o Iehu mahope ona, a i aku la ia, E pepehi aku ia ia hoi ma ka halekaa i ka pii ana ma Gura, e kokoke ana i Ibeleama. A holo aku la ia i Megido, a make iho la ilaila.
28 Antchito ake anamunyamulira mʼgaleta kupita naye ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide.
A lawe aku la kana poe kauwa ia ia maloko o ka halekaa i Ierusalema, a kanu iho la ia ia iloko o ka halelua me kona poe kupuna ma ke kulanakauhale o Davida.
29 (Mʼchaka cha khumi ndi chimodzi cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu, Ahaziya anakhala mfumu ya ku Yuda).
I ka umikumamakahi o ka makahiki o Iorama ke keiki a Ahaba, hoomaka iho la o Ahazia e noho alii maluna o ka Iuda.
30 Kenaka Yehu anapita ku Yezireeli. Yezebeli atamva zimene zinachitika, anapaka zodzikometsera mʼmaso, naluka tsitsi lake, namasuzumira pa zenera.
A hiki aku la o Iehu i Iezereela, lohe ae la o Iezebela; a pena iho la ia i kona maka, a hooponopono i kona poo, a nana mai la ma ka pukamakani.
31 Pamene Yehu ankalowa pa chipata iye anafunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere, iwe Zimuri, munthu wopha mbuye wako?”
A komo aku la o Iehu ma ka pukapa, ninau mai la keia, I maluhia anei o Zimeri, nana i pepehi kona haku?
32 Yehu anakweza maso nayangʼana pa zenera, ndipo anafuwula kuti, “Kodi ndani ali mbali yanga? Ndani?” Anthu ofulidwa awiri kapena atatu anayangʼana Yehu pansipo.
A nana aku la ia iluna ma ka pukamakani, i aku la, Owai ka mea ma o'u nei? Owai? A nana mai la ia ia elua a ekolu paha mau luna hale.
33 Yehu anawawuza kuti, “Muponyeni pansi!” Motero anamuponya pansi ndipo magazi ake ena anafalikira pa khoma ndi pa akavalo pamene ankamupondaponda.
I aku la ia, E hoolei mai ia ia ilalo. A hoolei iho la lakou ia ia ilalo, a helelei iho kekahi o kona koko ma ka papohaku, a maluna o na lio: a hehiia iho la ia malalo o na wawae.
34 Yehu analowa mʼnyumba yaufumu ndipo anadya ndi kumwa. Kenaka iye anati, “Kamutoleni mkazi wotembereredwayo, ndipo kamuyikeni mʼmanda, popeza ndi mwana wa mfumu.”
A komo aku la ia maloko, a ai iho la ia, a inu hoi, a i aku la, E hele, e nana aku ano i keia mea i hoinoia, a e kanu aku ia ia, no ka mea, he kaikamahine ia a kekahi alii.
35 Koma atapita kuti akamuyike mʼmanda, sanapeze kanthu kupatula chibade cha mutu wokha, mapazi ake ndi manja ake.
A hele aku la lakou e kanu ia ia, aole i loaa ia lakou kekahi mea ona, o ka puniu wale no, a me na wawae, a me na poho lima.
36 Choncho iwo anabwerera kwa Yehu ndi kukamufotokozera kuti, “Mawu amene Yehova anayankhula kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe ndi awa: Pa munda wa ku Yezireeli agalu adzadya mtembo wa Yezebeli.
No ia mea, hoi mai lakou, hai aku ia ia. I mai la ia, O keia ka olelo a Iehova ana i olelo mai ai, ma kana kauwa, ma Elia no Tiseba, i ka i ana'e, Ma ka aina i Iezereela e ai iho ai na ilio i ka io o Iezebela.
37 Mtembo wa Yezebeli udzakhala ngati zinyalala pa munda wa ku Yezireeli, kotero kuti palibe amene adzathe kunena kuti, ‘Uyu ndi Yezebeli.’”
A e like auanei ke kupapau o Iezebela me ka lepo maluna o ke kula o ka aina i Iezereela; nolaila, aole lakou e olelo ae, O Iezebela keia.

< 2 Mafumu 9 >