< 2 Mafumu 9 >

1 Mneneri Elisa anayitanitsa mmodzi mwa ana a aneneri, namuwuza kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga botolo la mafuta mʼdzanja lako ndipo upite ku Ramoti Giliyadi.
Or le prophète Élisée appela un des enfants des prophètes, et lui dit: Ceins tes reins, prends ce petit vase d’huile en ta main et va à Ramoth-Galaad.
2 Ukakafika kumeneko, ukafunefune Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi. Ukapite kwa iye, ukamuchotse pakati pa anzake ndi kukamulowetsa mʼchipinda chamʼkati.
Et lorsque tu seras arrivé là, tu verras Jéhu, fils de Josaphat, fils de Namsi; et, étant entré, tu le feras sortir du milieu de ses frères, et tu l’introduiras dans une chambre secrète.
3 Ndipo ukatenge botololi ndi kuthira mafuta pa mutu wake ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ Kenaka ukatsekule chitseko ndi kuthawa ndipo usakachedwe!”
Et tenant le petit vase d’huile, tu la répandras sur sa tête, et tu diras: Voici ce que dit le Seigneur: Je t’ai oint roi sur Israël. Et tu ouvriras la porte, et tu t’enfuiras, et tu ne resteras pas là.
4 Choncho mneneri wachinyamatayo anapita ku Ramoti Giliyadi.
Le jeune homme, serviteur du prophète, s’en alla donc à Ramoth-Galaad,
5 Atafika ku Giliyadiko anapeza atsogoleri a ankhondo ali pa msonkhano. Iye anati, “Mtsogoleri, ine ndili ndi uthenga wanu.” Ndipo Yehu anafunsa kuti, “Uthengawo ndi wa yani pakati pathu?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndi wa inuyo, mtsogoleri.”
Et il y entra: or, voilà que les princes de l’armée étaient assis; et il dit à Jéhu: J’ai un mot pour vous, ô prince. Et Jéhu demanda: Pour qui d’entre nous tous? Et celui-ci répondit: Pour vous, ô prince.
6 Yehu anayimirira nakalowa mʼnyumba. Pamenepo mneneriyo anakhuthulira mafuta pamutu pa Yehu ndipo ananena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndikukudzoza kukhala mfumu ya Israeli, anthu a Yehova.
Alors il se leva, et il entra dans sa chambre, et le jeune homme répandit l’huile sur sa tête, et dit: Voici ce que dit le Seigneur, Dieu d’Israël: Je t’ai oint roi sur le peuple du Seigneur, Israël,
7 Uyenera kuwononga nyumba ya mbuye wako Ahabu ndipo ndidzabwezera imfa ya atumiki anga, aneneri ndiponso imfa ya atumiki ena onse a Yehova amene anaphedwa ndi Yezebeli.
Et tu frapperas la maison d’Achab, ton seigneur, et je vengerai le sang de mes serviteurs, les prophètes, et le sang de tous les serviteurs du Seigneur, de la main de Jézabel.
8 Banja lonse la Ahabu lidzatheratu. Ndidzachotsa munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu kaya ndi kapolo kapena mfulu.
Et je perdrai toute la maison d’Achab, et je tuerai d’Achab, celui qui urine contre une muraille, celui qui est renfermé, et celui qui est le dernier dans Israël.
9 Ndidzachititsa kuti banja la Ahabu lifanane ndi banja la Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati banja la Baasa mwana wa Ahiya.
Et je rendrai la maison d’Achab comme la maison de Jéroboam, fils de Nabath, et comme la maison de Baasa, fils d’Ahia.
10 Kunena za Yezebeli, agalu adzamudya ku dera la Yezireeli ndipo palibe amene adzamuyike mʼmanda.’” Kenaka mneneriyo anatsekula chitseko nʼkuthawa.
Et Jézabel elle-même, les chiens la mangeront dans la campagne de Jezrahel, et il n’y aura personne qui l’ensevelisse. Et il ouvrit la porte et s’enfuit.
11 Yehu atatuluka kupita kumene kunali atsogoleri anzake, mmodzi mwa iwo anamufunsa kuti, “Kodi zonse zili bwino? Kodi munthu wamisala uja anabwera kudzatani kwa iwe?” Yehu anayankha kuti, “Iwe ukumudziwa munthu uja ndiponso ukudziwa zomwe amayankhula.”
Mais Jéhu sortit vers les serviteurs de son maître, qui lui demandèrent: Tout va-t-il bien? Pourquoi cet insensé est-il venu vers vous? Jéhu leur dit: Vous connaissez cet homme et ce qu’il a pu dire.
12 Atsogoleri aja anati, “Ukunama! Tiwuze.” Yehu anati, “Zimene wandiwuza ndi izi: ‘Yehova akuti: Ine ndakudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’”
Mais ceux-ci répondirent: C’est quelque chose de faux, mais au moins racontez-le nous. Jéhu leur dit: Il m’a dit ceci et cela, et il a ajouté: Voici ce que dit le Seigneur: Je t’ai oint roi sur Israël.
13 Atsogoleri aja mofulumira anatenga zofunda zawo naziyala pansi pa makwerero kuti Yehu akhalepo. Kenaka analiza lipenga, nafuwula kuti, “Yehu ndiye mfumu!”
C’est pourquoi ils se hâtèrent, et chacun prenant son manteau, ils le mirent sous les pieds de Jéhu, pour représenter un tribunal; puis ils sonnèrent de la trompette, et dirent: Jéhu est roi.
14 Choncho Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi, anachitira chiwembu Yoramu. (Nthawi imeneyi nʼkuti Yoramu ndi Aisraeli onse akuteteza Ramoti Giliyadi kwa Hazaeli mfumu ya ku Aramu,
Jéhu, fils de Josaphat, fils de Namsi, conspira donc contre Joram: or Joram avait assiégé Ramoth-Galaad, lui et tout Israël, contre Hazaël, roi de Syrie;
15 koma nʼkuti Yoramu atabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene Aaramu anamuvulaza pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya ku Aramu.) Yehu anati, “Ngati mukugwirizana nazo zimenezi, wina aliyense asatuluke mu mzinda muno kupita kukafotokoza nkhaniyi ku Yezireeli.”
Et il était revenu pour se guérir à Jezrahel d’une blessure, parce que les Syriens l’avaient blessé, lorsqu’il combattait contre Hazaël, roi de Syrie; et Jéhu dit: S’il vous plaît, que personne ne sorte, fuyant de la ville, afin qu’il n’aille et ne l’annonce à Jezrahel.
16 Pamenepo Yehu anakwera galeta lake, napita ku Yezireeli, chifukwa Yoramu anali akupumula kumeneko ndipo Ahaziya, mfumu ya ku Yuda, nʼkuti ali komweko kudzamuona.
Et il monta et partit pour Jezrahel; car Joram était là malade; et Ochozias, roi de Juda, était descendu pour visiter Joram.
17 Mlonda amene ankayimirira pa nsanja yolondera mzinda wa Yezireeli ataona gulu lankhondo la Yehu likuyandikira, anafuwula kuti, “Ndikuona gulu lankhondo likubwera.” Yoramu analamula kuti, “Peza munthu wokwera kavalo, mutume kuti akakumane nawo ndi kuwafunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’”
La sentinelle donc qui était sur la tour de Jezrahel, vit la troupe de Jéhu qui venait, et dit: J’aperçois une troupe, et Joram dit: Prends un chariot et envoie à leur rencontre, et que celui qui ira dise: Tout va-t-il bien?
18 Choncho munthu wokwera kavalo anapita kukakumana ndi Yehu ndipo anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.” Mlonda uja anakafotokoza kwa mfumu kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwerera.”
Celui donc qui était monté sur le char, alla à la rencontre de Jéhu, et dit: Voici ce que dit le roi: Tout est-il en paix? Et Jéhu répondit: Qu’importe à toi et à la paix? passe, et suis-moi. La sentinelle l’annonça aussi, disant: Le messager est allé vers eux, et il ne revient point.
19 Choncho mfumu inatumanso munthu wina wachiwiri wokwera kavalo. Atafika kwa anthuwo iye anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”
Joram envoya encore un second chariot avec des chevaux; et le messager alla vers eux, et dit: Voici ce que dit le roi: Est-ce la paix? Et Jéhu répondit: Qu’importe à toi et à la paix? Passe, et suis-moi.
20 Mlonda uja anakanenanso kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwereranso. Kuyendako kukukhala ngati kwa Yehu mwana wa Nimisi, iye amayenda ngati munthu wamisala.”
Or la sentinelle l’annonça, disant: Il est allé jusqu’à eux, et il ne revient point; mais la démarche de quelqu’un qui vient, est comme la démarche de Jéhu, fils de Namsi; car il marche avec précipitation.
21 Yoramu analamula kuti, “Konzani galeta langa.” Ndipo atakonza galeta lake, Yoramu mfumu ya Israeli ndi Ahaziya mfumu ya ku Yuda anakwera nʼkutuluka mu mzindamo, aliyense atakwera galeta lake, kukakumana ndi Yehu. Iwo anakumana ndi Yehu pa munda umene unali wa Naboti, wa ku Yezireeli.
Et Joram dit: Attelle mon char. Et l’on attela son char, et Joram, roi d’Israël, sortit, et Ochozias, roi de Juda, chacun dans son char, et ils sortirent à la rencontre de Jéhu, et le trouvèrent dans le champ de Naboth, le Jezrahélite.
22 Yoramu ataona Yehu anafunsa kuti, “Yehu, kodi wabwera mwamtendere?” Yehu anayankha kuti, “Pangakhale bwanji mtendere pamene zopembedza mafano zonse zilipo ndiponso ufiti wa amayi ako Yezebeli uli ponseponse?”
Et lorsque Joram eut vu Jéhu, il dit: Est-ce la paix, Jéhu? Mais celui-ci répondit: Quelle est cette paix? Les fornications de Jézabel votre mère et ses enchantements nombreux subsistent encore.
23 Yoramu anatembenuka, nathawa akufuwula kwa Ahaziya kuti, “Ahaziya, anthuwa atiwukira!”
Or Joram tourna sa main, et, fuyant, il dit à Ochozias: C’est un piège, Ochozias.
24 Pamenepo Yehu anakoka uta wake ndipo analasa Yoramu kumsana pakati pa mapewa. Muviwo unakalasa mtima wake ndipo anagwa pansi mʼgaleta lakelo.
Mais Jéhu tendit son arc de sa main et frappa Joram entre les épaules; et la flèche sortit par son cœur, et aussitôt il tomba sur son char.
25 Yehu anawuza Bidikara, mtsogoleri wa galeta lake kuti, “Munyamule ndipo ukamuponye mʼmunda umene unali wa Naboti wa ku Yezireeli, chifukwa kumbukira mmene iwe ndi ine tinkayenda pambuyo pa Ahabu abambo ake, kuti Yehova ananeneratu za iye kuti,
Alors Jéhu dit à Badacer, chef de l’armée: Prends-le et jette-le dans le champ de Naboth, le Jezrahélite; car je me souviens, quand moi et toi, assis sur un char, nous suivions Achab, son père, que le Seigneur leva sur lui ce fardeau, disant:
26 ‘Zoonadi dzulo ndinaona magazi a Naboti ndi magazi a ana ake, akutero Yehova, ndipo Ine ndidzakubwezera ndithu choyipa chimenechi pa munda womwe uno, akutero Yehova.’ Tsono munyamule ndipo ukamuponye mʼmundamo, potsatira zimene Yehova ananena.”
Je jure, si pour le sang de Naboth et pour le sang de ses fils, que j’ai vu hier verser, dit le Seigneur, je ne te rends point la pareille dans ce champ, dit le Seigneur. Maintenant donc, prends-le, et jette-le dans le champ, selon la parole du Seigneur.
27 Ahaziya mfumu ya ku Yuda ataona zimene zinachitika, anathawira ku Beti Hagani. Yehu anamuthamangitsa, uku akufuwula kuti, “Mupheninso!” Iwo anamuvulaza ali mʼgaleta lakelo pa njira yopita ku Guri pafupi ndi Ibuleamu, koma iye anathawira ku Megido ndipo anakafera kumeneko.
Or Ochozias, roi de Juda, ayant vu cela, s’enfuit par le chemin de la maison du jardin, et Jéhu le poursuivit et dit: Même celui-là, frappez-le sur son char. Et ils le frappèrent à la montée de Gaver, qui est près de Jéblaam, et Ochozias s’enfuit à Mageddo et mourut là.
28 Antchito ake anamunyamulira mʼgaleta kupita naye ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide.
Et ses serviteurs le placèrent sur son char, et le portèrent à Jérusalem, et l’ensevelirent dans le sépulcre avec ses pères dans la cité de David.
29 (Mʼchaka cha khumi ndi chimodzi cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu, Ahaziya anakhala mfumu ya ku Yuda).
La onzième année de Joram, fils d’Achab, Ochozias régna sur Juda,
30 Kenaka Yehu anapita ku Yezireeli. Yezebeli atamva zimene zinachitika, anapaka zodzikometsera mʼmaso, naluka tsitsi lake, namasuzumira pa zenera.
Et Jéhu vint à Jezrahel. Or Jézabel, ayant appris son arrivée, peignit ses yeux avec du noir et orna sa tête, puis elle regarda par la fenêtre
31 Pamene Yehu ankalowa pa chipata iye anafunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere, iwe Zimuri, munthu wopha mbuye wako?”
Jéhu qui entrait à la porte, et dit: Est-ce que la paix peut être avec Zambri qui a tué son maître?
32 Yehu anakweza maso nayangʼana pa zenera, ndipo anafuwula kuti, “Kodi ndani ali mbali yanga? Ndani?” Anthu ofulidwa awiri kapena atatu anayangʼana Yehu pansipo.
Et Jéhu leva sa face vers la fenêtre, et demanda: Qui est celle-là? Et deux ou trois eunuques se penchèrent vers lui.
33 Yehu anawawuza kuti, “Muponyeni pansi!” Motero anamuponya pansi ndipo magazi ake ena anafalikira pa khoma ndi pa akavalo pamene ankamupondaponda.
Et Jéhu leur dit: Précipitez-la en bas. Et ils la précipitèrent, et la muraille fut arrosée de son sang, et la corne des chevaux la foula.
34 Yehu analowa mʼnyumba yaufumu ndipo anadya ndi kumwa. Kenaka iye anati, “Kamutoleni mkazi wotembereredwayo, ndipo kamuyikeni mʼmanda, popeza ndi mwana wa mfumu.”
Et lorsque Jéhu fut entré pour boire et pour manger, il dit: Allez, et voyez cette maudite, et ensevelissez-la, parce qu’elle est fille de roi.
35 Koma atapita kuti akamuyike mʼmanda, sanapeze kanthu kupatula chibade cha mutu wokha, mapazi ake ndi manja ake.
Et lorsqu’ils furent allés pour l’ensevelir, ils ne trouvèrent que le crâne, les pieds et l’extrémité des mains.
36 Choncho iwo anabwerera kwa Yehu ndi kukamufotokozera kuti, “Mawu amene Yehova anayankhula kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe ndi awa: Pa munda wa ku Yezireeli agalu adzadya mtembo wa Yezebeli.
Et étant revenus, ils l’annoncèrent à Jéhu. Or Jéhu dit: C’est la parole du Seigneur, qu’il a prononcée par son serviteur Élie, le Tesbite, disant: Dans la campagne de Jezrahel, les chiens mangeront la chair de Jézabel,
37 Mtembo wa Yezebeli udzakhala ngati zinyalala pa munda wa ku Yezireeli, kotero kuti palibe amene adzathe kunena kuti, ‘Uyu ndi Yezebeli.’”
Et la chair de Jézabel sera comme un fumier sur la face de la terre, dans la campagne de Jezrahel; et tous ceux qui passeront diront: Est-ce là cette Jézabel?

< 2 Mafumu 9 >