< 2 Mafumu 9 >

1 Mneneri Elisa anayitanitsa mmodzi mwa ana a aneneri, namuwuza kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga botolo la mafuta mʼdzanja lako ndipo upite ku Ramoti Giliyadi.
and Elisha [the] prophet to call: call to to/for one from son: child [the] prophet and to say to/for him to gird loin your and to take: take vial [the] oil [the] this in/on/with hand your and to go: went Ramoth (Ramoth)-gilead
2 Ukakafika kumeneko, ukafunefune Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi. Ukapite kwa iye, ukamuchotse pakati pa anzake ndi kukamulowetsa mʼchipinda chamʼkati.
and to come (in): come there [to] and to see: see there Jehu son: child Jehoshaphat son: child Nimshi and to come (in): come and to arise: rise him from midst brother: compatriot his and to come (in): come [obj] him chamber in/on/with chamber
3 Ndipo ukatenge botololi ndi kuthira mafuta pa mutu wake ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ Kenaka ukatsekule chitseko ndi kuthawa ndipo usakachedwe!”
and to take: take vial [the] oil and to pour: pour upon head his and to say thus to say LORD to anoint you to/for king to(wards) Israel and to open [the] door and to flee and not to wait
4 Choncho mneneri wachinyamatayo anapita ku Ramoti Giliyadi.
and to go: went [the] youth [the] youth [the] prophet Ramoth (Ramoth)-gilead
5 Atafika ku Giliyadiko anapeza atsogoleri a ankhondo ali pa msonkhano. Iye anati, “Mtsogoleri, ine ndili ndi uthenga wanu.” Ndipo Yehu anafunsa kuti, “Uthengawo ndi wa yani pakati pathu?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndi wa inuyo, mtsogoleri.”
and to come (in): come and behold ruler [the] strength: soldiers to dwell and to say word to/for me to(wards) you [the] ruler and to say Jehu to(wards) who? from all our and to say to(wards) you [the] ruler
6 Yehu anayimirira nakalowa mʼnyumba. Pamenepo mneneriyo anakhuthulira mafuta pamutu pa Yehu ndipo ananena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndikukudzoza kukhala mfumu ya Israeli, anthu a Yehova.
and to arise: rise and to come (in): come [the] house: home [to] and to pour: pour [the] oil to(wards) head his and to say to/for him thus to say LORD God Israel to anoint you to/for king to(wards) people LORD to(wards) Israel
7 Uyenera kuwononga nyumba ya mbuye wako Ahabu ndipo ndidzabwezera imfa ya atumiki anga, aneneri ndiponso imfa ya atumiki ena onse a Yehova amene anaphedwa ndi Yezebeli.
and to smite [obj] house: household Ahab lord your and to avenge blood servant/slave my [the] prophet and blood all servant/slave LORD from hand: to Jezebel
8 Banja lonse la Ahabu lidzatheratu. Ndidzachotsa munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu kaya ndi kapolo kapena mfulu.
and to perish all house: household Ahab and to cut: eliminate to/for Ahab to urinate in/on/with wall and to restrain and to leave: release in/on/with Israel
9 Ndidzachititsa kuti banja la Ahabu lifanane ndi banja la Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati banja la Baasa mwana wa Ahiya.
and to give: make [obj] house: household Ahab like/as house: household Jeroboam son: child Nebat and like/as house: household Baasha son: child Ahijah
10 Kunena za Yezebeli, agalu adzamudya ku dera la Yezireeli ndipo palibe amene adzamuyike mʼmanda.’” Kenaka mneneriyo anatsekula chitseko nʼkuthawa.
and [obj] Jezebel to eat [the] dog in/on/with portion Jezreel and nothing to bury and to open [the] door and to flee
11 Yehu atatuluka kupita kumene kunali atsogoleri anzake, mmodzi mwa iwo anamufunsa kuti, “Kodi zonse zili bwino? Kodi munthu wamisala uja anabwera kudzatani kwa iwe?” Yehu anayankha kuti, “Iwe ukumudziwa munthu uja ndiponso ukudziwa zomwe amayankhula.”
and Jehu to come out: come to(wards) servant/slave lord his and to say to/for him peace: well-being why? to come (in): come [the] be mad [the] this to(wards) you and to say to(wards) them you(m. p.) to know [obj] [the] man and [obj] complaint his
12 Atsogoleri aja anati, “Ukunama! Tiwuze.” Yehu anati, “Zimene wandiwuza ndi izi: ‘Yehova akuti: Ine ndakudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’”
and to say deception to tell please to/for us and to say like/as this and like/as this to say to(wards) me to/for to say thus to say LORD to anoint you to/for king to(wards) Israel
13 Atsogoleri aja mofulumira anatenga zofunda zawo naziyala pansi pa makwerero kuti Yehu akhalepo. Kenaka analiza lipenga, nafuwula kuti, “Yehu ndiye mfumu!”
and to hasten and to take: take man: anyone garment his and to set: put underneath: under him to(wards) bone [the] step and to blow in/on/with trumpet and to say to reign Jehu
14 Choncho Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi, anachitira chiwembu Yoramu. (Nthawi imeneyi nʼkuti Yoramu ndi Aisraeli onse akuteteza Ramoti Giliyadi kwa Hazaeli mfumu ya ku Aramu,
and to conspire Jehu son: child Jehoshaphat son: child Nimshi to(wards) Joram and Joram to be to keep: guard in/on/with Ramoth (Ramoth)-gilead he/she/it and all Israel from face: before Hazael king Syria
15 koma nʼkuti Yoramu atabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene Aaramu anamuvulaza pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya ku Aramu.) Yehu anati, “Ngati mukugwirizana nazo zimenezi, wina aliyense asatuluke mu mzinda muno kupita kukafotokoza nkhaniyi ku Yezireeli.”
and to return: return Joram [the] king to/for to heal in/on/with Jezreel from [the] wound which to smite him Syrian in/on/with to fight he with Hazael king Syria and to say Jehu if there soul: myself your not to come out: come survivor from [the] city to/for to go: went (to/for to tell *Q(k)*) in/on/with Jezreel
16 Pamenepo Yehu anakwera galeta lake, napita ku Yezireeli, chifukwa Yoramu anali akupumula kumeneko ndipo Ahaziya, mfumu ya ku Yuda, nʼkuti ali komweko kudzamuona.
and to ride Jehu and to go: went Jezreel [to] for Joram to lie down: lay down there [to] and Ahaziah king Judah to go down to/for to see: see [obj] Joram
17 Mlonda amene ankayimirira pa nsanja yolondera mzinda wa Yezireeli ataona gulu lankhondo la Yehu likuyandikira, anafuwula kuti, “Ndikuona gulu lankhondo likubwera.” Yoramu analamula kuti, “Peza munthu wokwera kavalo, mutume kuti akakumane nawo ndi kuwafunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’”
and [the] to watch to stand: stand upon [the] tower in/on/with Jezreel and to see: see [obj] abundance Jehu in/on/with to come (in): come he and to say abundance I to see: see and to say Joram to take: take charioteer and to send: depart to/for to encounter: meet them and to say peace
18 Choncho munthu wokwera kavalo anapita kukakumana ndi Yehu ndipo anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.” Mlonda uja anakafotokoza kwa mfumu kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwerera.”
and to go: went to ride [the] horse to/for to encounter: meet him and to say thus to say [the] king peace and to say Jehu what? to/for you and to/for peace to turn: turn to(wards) after me and to tell [the] to watch to/for to say to come (in): come [the] messenger till they(masc.) and not to return: return
19 Choncho mfumu inatumanso munthu wina wachiwiri wokwera kavalo. Atafika kwa anthuwo iye anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”
and to send: depart to ride horse second and to come (in): come to(wards) them and to say thus to say [the] king peace and to say Jehu what? to/for you and to/for peace to turn: turn to(wards) after me
20 Mlonda uja anakanenanso kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwereranso. Kuyendako kukukhala ngati kwa Yehu mwana wa Nimisi, iye amayenda ngati munthu wamisala.”
and to tell [the] to watch to/for to say to come (in): come till to(wards) them and not to return: return and [the] driving like/as driving Jehu son: child Nimshi for in/on/with madness to lead
21 Yoramu analamula kuti, “Konzani galeta langa.” Ndipo atakonza galeta lake, Yoramu mfumu ya Israeli ndi Ahaziya mfumu ya ku Yuda anakwera nʼkutuluka mu mzindamo, aliyense atakwera galeta lake, kukakumana ndi Yehu. Iwo anakumana ndi Yehu pa munda umene unali wa Naboti, wa ku Yezireeli.
and to say Joram to bind and to bind chariot his and to come out: come Joram king Israel and Ahaziah king Judah man: anyone in/on/with chariot his and to come out: come to/for to encounter: meet Jehu and to find him in/on/with portion Naboth [the] Jezreelite
22 Yoramu ataona Yehu anafunsa kuti, “Yehu, kodi wabwera mwamtendere?” Yehu anayankha kuti, “Pangakhale bwanji mtendere pamene zopembedza mafano zonse zilipo ndiponso ufiti wa amayi ako Yezebeli uli ponseponse?”
and to be like/as to see: see Joram [obj] Jehu and to say peace Jehu and to say what? [the] peace till fornication Jezebel mother your and sorcery her [the] many
23 Yoramu anatembenuka, nathawa akufuwula kwa Ahaziya kuti, “Ahaziya, anthuwa atiwukira!”
and to overturn Joram hand his and to flee and to say to(wards) Ahaziah deceit Ahaziah
24 Pamenepo Yehu anakoka uta wake ndipo analasa Yoramu kumsana pakati pa mapewa. Muviwo unakalasa mtima wake ndipo anagwa pansi mʼgaleta lakelo.
and Jehu to fill hand: power his in/on/with bow and to smite [obj] Joram between arm his and to come out: issue [the] arrow from heart his and to bow in/on/with chariot his
25 Yehu anawuza Bidikara, mtsogoleri wa galeta lake kuti, “Munyamule ndipo ukamuponye mʼmunda umene unali wa Naboti wa ku Yezireeli, chifukwa kumbukira mmene iwe ndi ine tinkayenda pambuyo pa Ahabu abambo ake, kuti Yehova ananeneratu za iye kuti,
and to say to(wards) Bidkar (officer his *Q(K)*) to lift: raise to throw him in/on/with portion land: soil Naboth [the] Jezreelite for to remember I and you(m. s.) [obj] to ride pair after Ahab father his and LORD to lift: loud upon him [obj] [the] oracle [the] this
26 ‘Zoonadi dzulo ndinaona magazi a Naboti ndi magazi a ana ake, akutero Yehova, ndipo Ine ndidzakubwezera ndithu choyipa chimenechi pa munda womwe uno, akutero Yehova.’ Tsono munyamule ndipo ukamuponye mʼmundamo, potsatira zimene Yehova ananena.”
if: surely yes not [obj] blood Naboth and [obj] blood son: child his to see: see last night utterance LORD and to complete to/for you in/on/with portion [the] this utterance LORD and now to lift: raise to throw him in/on/with portion like/as word LORD
27 Ahaziya mfumu ya ku Yuda ataona zimene zinachitika, anathawira ku Beti Hagani. Yehu anamuthamangitsa, uku akufuwula kuti, “Mupheninso!” Iwo anamuvulaza ali mʼgaleta lakelo pa njira yopita ku Guri pafupi ndi Ibuleamu, koma iye anathawira ku Megido ndipo anakafera kumeneko.
and Ahaziah king Judah to see: see and to flee way: direction Beth (Haggan) (Beth)-haggan and to pursue after him Jehu and to say also [obj] him to smite him to(wards) [the] chariot in/on/with ascent Gur which with Ibleam and to flee Megiddo and to die there
28 Antchito ake anamunyamulira mʼgaleta kupita naye ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide.
and to ride [obj] him servant/slave his Jerusalem [to] and to bury [obj] him in/on/with tomb his with father his in/on/with city David
29 (Mʼchaka cha khumi ndi chimodzi cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu, Ahaziya anakhala mfumu ya ku Yuda).
and in/on/with year one ten year to/for Joram son: child Ahab to reign Ahaziah upon Judah
30 Kenaka Yehu anapita ku Yezireeli. Yezebeli atamva zimene zinachitika, anapaka zodzikometsera mʼmaso, naluka tsitsi lake, namasuzumira pa zenera.
and to come (in): come Jehu Jezreel [to] and Jezebel to hear: hear and to set: put in/on/with color eye her and be good [obj] head her and to look about/through/for [the] window
31 Pamene Yehu ankalowa pa chipata iye anafunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere, iwe Zimuri, munthu wopha mbuye wako?”
and Jehu to come (in): come in/on/with gate and to say peace Zimri to kill lord his
32 Yehu anakweza maso nayangʼana pa zenera, ndipo anafuwula kuti, “Kodi ndani ali mbali yanga? Ndani?” Anthu ofulidwa awiri kapena atatu anayangʼana Yehu pansipo.
and to lift: raise face: kindness his to(wards) [the] window and to say who? with me who? and to look to(wards) him two three eunuch
33 Yehu anawawuza kuti, “Muponyeni pansi!” Motero anamuponya pansi ndipo magazi ake ena anafalikira pa khoma ndi pa akavalo pamene ankamupondaponda.
and to say (to release her *Q(K)*) and to release her and to sprinkle from blood her to(wards) [the] wall and to(wards) [the] horse and to trample her
34 Yehu analowa mʼnyumba yaufumu ndipo anadya ndi kumwa. Kenaka iye anati, “Kamutoleni mkazi wotembereredwayo, ndipo kamuyikeni mʼmanda, popeza ndi mwana wa mfumu.”
and to come (in): come and to eat and to drink and to say to reckon: visit please [obj] [the] to curse [the] this and to bury her for daughter king he/she/it
35 Koma atapita kuti akamuyike mʼmanda, sanapeze kanthu kupatula chibade cha mutu wokha, mapazi ake ndi manja ake.
and to go: went to/for to bury her and not to find in/on/with her that if: except if: except [the] head and [the] foot and palm [the] hand
36 Choncho iwo anabwerera kwa Yehu ndi kukamufotokozera kuti, “Mawu amene Yehova anayankhula kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe ndi awa: Pa munda wa ku Yezireeli agalu adzadya mtembo wa Yezebeli.
and to return: return and to tell to/for him and to say word LORD he/she/it which to speak: speak in/on/with hand: by servant/slave his Elijah [the] Tishbite to/for to say in/on/with portion Jezreel to eat [the] dog [obj] flesh Jezebel
37 Mtembo wa Yezebeli udzakhala ngati zinyalala pa munda wa ku Yezireeli, kotero kuti palibe amene adzathe kunena kuti, ‘Uyu ndi Yezebeli.’”
(and to be *Q(k)*) carcass Jezebel like/as dung upon face: surface [the] land: country in/on/with portion Jezreel which not to say this Jezebel

< 2 Mafumu 9 >