< 2 Mafumu 9 >
1 Mneneri Elisa anayitanitsa mmodzi mwa ana a aneneri, namuwuza kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga botolo la mafuta mʼdzanja lako ndipo upite ku Ramoti Giliyadi.
Profeten Elisa kaldte en af Profetsønnerne til sig og sagde til ham: »Omgjord dine Lænder, tag denne Flaske Olie med og drag til Ramot i Gilead.
2 Ukakafika kumeneko, ukafunefune Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi. Ukapite kwa iye, ukamuchotse pakati pa anzake ndi kukamulowetsa mʼchipinda chamʼkati.
Naar du kommer derhen, opsøg saa Jehu, Nimsjis Søn Josjafats Søn; gaa hen og faa ham til at staa op fra sine Fæller og før ham ind i det inderste Hammer;
3 Ndipo ukatenge botololi ndi kuthira mafuta pa mutu wake ndipo ukanene kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’ Kenaka ukatsekule chitseko ndi kuthawa ndipo usakachedwe!”
tag saa Olieflasken og gyd Olien ud over hans Hoved med de Ord: Saa siger HERREN: Jeg salver dig til Konge over Israel! Derefter skal du lukke Døren op og flygte ufortøvet!«
4 Choncho mneneri wachinyamatayo anapita ku Ramoti Giliyadi.
Den unge Mand, Profetens Tjener, drog saa til Ramot i Gilead;
5 Atafika ku Giliyadiko anapeza atsogoleri a ankhondo ali pa msonkhano. Iye anati, “Mtsogoleri, ine ndili ndi uthenga wanu.” Ndipo Yehu anafunsa kuti, “Uthengawo ndi wa yani pakati pathu?” Mneneriyo anayankha kuti, “Ndi wa inuyo, mtsogoleri.”
og da han kom derhen, traf han Hærførerne siddende sammen. Han sagde da: »Jeg har et Ærinde til dig, Hærfører!« Jehu spurgte: »Til hvem af os?« Han svarede: »Til dig, Hærfører!«
6 Yehu anayimirira nakalowa mʼnyumba. Pamenepo mneneriyo anakhuthulira mafuta pamutu pa Yehu ndipo ananena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndikukudzoza kukhala mfumu ya Israeli, anthu a Yehova.
Saa rejste han sig og gik ind i Huset; der gød han Olien ud over hans Hoved og sagde til ham: »Saa siger HERREN, Israels Gud: Jeg salver dig til Konge over HERRENS Folk, over Israel!
7 Uyenera kuwononga nyumba ya mbuye wako Ahabu ndipo ndidzabwezera imfa ya atumiki anga, aneneri ndiponso imfa ya atumiki ena onse a Yehova amene anaphedwa ndi Yezebeli.
Du skal hugge din Herre Akabs Hus ned, saa jeg faar Hævn over Jesabel for mine Tjenere Profeternes og alle HERRENS Tjeneres Blod.
8 Banja lonse la Ahabu lidzatheratu. Ndidzachotsa munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu kaya ndi kapolo kapena mfulu.
Hele Akabs Hus skal omkomme, jeg vil udrydde hvert mandligt Væsen, hver og en af Akabs Slægt i Israel;
9 Ndidzachititsa kuti banja la Ahabu lifanane ndi banja la Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati banja la Baasa mwana wa Ahiya.
jeg vil handle med Akabs Hus som med Jeroboams, Nebats Søns, og Ba'sjas, Ahijas Søns, Hus.
10 Kunena za Yezebeli, agalu adzamudya ku dera la Yezireeli ndipo palibe amene adzamuyike mʼmanda.’” Kenaka mneneriyo anatsekula chitseko nʼkuthawa.
Og Jesabel skal Hundene æde paa Jizre'els Mark, og ingen skal jorde hende!« Derpaa lukkede han Døren op og flygtede.
11 Yehu atatuluka kupita kumene kunali atsogoleri anzake, mmodzi mwa iwo anamufunsa kuti, “Kodi zonse zili bwino? Kodi munthu wamisala uja anabwera kudzatani kwa iwe?” Yehu anayankha kuti, “Iwe ukumudziwa munthu uja ndiponso ukudziwa zomwe amayankhula.”
Da Jehu kom ud til sin Herres Folk, spurgte de ham: »Hvorledes staar det til? Hvad vilde den gale Mand hos dig?« Han svarede: »I kender jo den Mand og hans Snak!«
12 Atsogoleri aja anati, “Ukunama! Tiwuze.” Yehu anati, “Zimene wandiwuza ndi izi: ‘Yehova akuti: Ine ndakudzoza iwe kukhala mfumu ya Israeli.’”
Men de sagde: »Udflugter! Sig os det nu!« Da sagde han: »Saaledes sagde han til mig: Saa siger HERREN: Jeg salver dig til Konge over Israel!«
13 Atsogoleri aja mofulumira anatenga zofunda zawo naziyala pansi pa makwerero kuti Yehu akhalepo. Kenaka analiza lipenga, nafuwula kuti, “Yehu ndiye mfumu!”
Øjeblikkelig tog de da hver sin Kappe og lagde under ham paa selve Trappen, og de stødte i Hornet og udraabte Jehu til Konge.
14 Choncho Yehu mwana wa Yehosafati, mwana wa Nimisi, anachitira chiwembu Yoramu. (Nthawi imeneyi nʼkuti Yoramu ndi Aisraeli onse akuteteza Ramoti Giliyadi kwa Hazaeli mfumu ya ku Aramu,
Saaledes stiftede Jehu, Nimsjis Søn Josjafats Søn, en Sammensværgelse mod Joram. Joram havde med hele Israel forsvaret Ramot i Gilead mod Kong Hazael af Aram;
15 koma nʼkuti Yoramu atabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene Aaramu anamuvulaza pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya ku Aramu.) Yehu anati, “Ngati mukugwirizana nazo zimenezi, wina aliyense asatuluke mu mzinda muno kupita kukafotokoza nkhaniyi ku Yezireeli.”
men Kong Joram var vendt tilbage for i Jizre'el at søge Helbredelse for de Saar, Aramæerne havde tilføjet ham, da han kæmpede med Kong Hazael af Aram. Da sagde Jehu: »Vil I som jeg, saa lad ikke en eneste slippe ud af Byen og bringe Bud til Jizre'el.«
16 Pamenepo Yehu anakwera galeta lake, napita ku Yezireeli, chifukwa Yoramu anali akupumula kumeneko ndipo Ahaziya, mfumu ya ku Yuda, nʼkuti ali komweko kudzamuona.
Derpaa steg Jehu til Vogns og kørte til Jizre'el; thi der laa Joram syg, og Kong Ahazja af Juda var rejst ned for at se til ham.
17 Mlonda amene ankayimirira pa nsanja yolondera mzinda wa Yezireeli ataona gulu lankhondo la Yehu likuyandikira, anafuwula kuti, “Ndikuona gulu lankhondo likubwera.” Yoramu analamula kuti, “Peza munthu wokwera kavalo, mutume kuti akakumane nawo ndi kuwafunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’”
Da Vægteren, som stod paa Taarnet i Jizre'el, saa Støvskyen efter Jehu, sagde han: »Jeg ser en Støvsky!« Da sagde Joram: »Tag en Rytter og send ham ud imod dem, for at han kan spørge, om de kommer med Fred!«
18 Choncho munthu wokwera kavalo anapita kukakumana ndi Yehu ndipo anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.” Mlonda uja anakafotokoza kwa mfumu kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwerera.”
Saa red Rytteren ham i Møde og sagde: »Saaledes siger Kongen: Kommer du med Fred?« Jehu svarede: »Hvad vedkommer det dig, om det er med Fred? Omkring, følg mig!« Vægteren meldte: »Sendebudet har naaet dem, men han kommer ikke tilbage!«
19 Choncho mfumu inatumanso munthu wina wachiwiri wokwera kavalo. Atafika kwa anthuwo iye anati, “Mfumu ikufunsa kuti, ‘Kodi mukubwera mwamtendere?’” Yehu anayankha kuti, “Kodi iwe nkhani ya mtendere yakukhudza bwanji? Tiye, zinditsata pambuyo panga.”
Saa sendte han en anden Rytter ud; og da han var kommet hen til dem, sagde han: »Saaledes siger Kongen: Kommer du med Fred?« Jehu svarede: »Hvad vedkommer det dig, om jeg kommer med Fred? Omkring, følg mig!«
20 Mlonda uja anakanenanso kuti, “Wamthenga uja wakafika kwa anthuwo koma sakubwereranso. Kuyendako kukukhala ngati kwa Yehu mwana wa Nimisi, iye amayenda ngati munthu wamisala.”
Vægteren meldte: »Han har naaet dem, men han kommet ikke tilbage. Og de har en Fart paa, som var det Jehu, Nimsjis Søn, thi han farer af Sted som rasende.«
21 Yoramu analamula kuti, “Konzani galeta langa.” Ndipo atakonza galeta lake, Yoramu mfumu ya Israeli ndi Ahaziya mfumu ya ku Yuda anakwera nʼkutuluka mu mzindamo, aliyense atakwera galeta lake, kukakumana ndi Yehu. Iwo anakumana ndi Yehu pa munda umene unali wa Naboti, wa ku Yezireeli.
Da sagde Joram: »Spænd for!« Og da der var spændt for, kørte Kong Joram af Israel og Kong Ahazja af Juda ud hver i sin Vogn. De kørte Jehu i Møde og traf ham ved Jizre'eliten Nabots Mark.
22 Yoramu ataona Yehu anafunsa kuti, “Yehu, kodi wabwera mwamtendere?” Yehu anayankha kuti, “Pangakhale bwanji mtendere pamene zopembedza mafano zonse zilipo ndiponso ufiti wa amayi ako Yezebeli uli ponseponse?”
Da Joram fik Øje paa Jehu, spurgte han: »Kommer du med Fred, Jehu?« Men han svarede: »Hvad! Skulde jeg komme med Fred, saa længe det ikke har Ende med din Moder Jesabels Bolen og hendes mange Trolddomskunster!«
23 Yoramu anatembenuka, nathawa akufuwula kwa Ahaziya kuti, “Ahaziya, anthuwa atiwukira!”
Da drejede Joram omkring og flygtede, idet han raabte til Ahazja: »Svig, Ahazja!«
24 Pamenepo Yehu anakoka uta wake ndipo analasa Yoramu kumsana pakati pa mapewa. Muviwo unakalasa mtima wake ndipo anagwa pansi mʼgaleta lakelo.
Men Jehu greb sin Bue og skød Joram i Ryggen, saa at Pilen gik igennem Hjertet, og han sank sammen i Vognen;
25 Yehu anawuza Bidikara, mtsogoleri wa galeta lake kuti, “Munyamule ndipo ukamuponye mʼmunda umene unali wa Naboti wa ku Yezireeli, chifukwa kumbukira mmene iwe ndi ine tinkayenda pambuyo pa Ahabu abambo ake, kuti Yehova ananeneratu za iye kuti,
og Jehu sagde til sin Høvedsmand Bidkar: »Tag og kast ham hen paa Jizre'eliten Nabots Mark, thi det rinder mig i Hu, hvorledes jeg og du kørte sammen bag efter hans Fader Akab, dengang HERREN fremsatte dette Udsagn imod ham:
26 ‘Zoonadi dzulo ndinaona magazi a Naboti ndi magazi a ana ake, akutero Yehova, ndipo Ine ndidzakubwezera ndithu choyipa chimenechi pa munda womwe uno, akutero Yehova.’ Tsono munyamule ndipo ukamuponye mʼmundamo, potsatira zimene Yehova ananena.”
Sandelig, Nabots og hans Sønners Blod saa jeg i Gaar, lyder det fra HERREN, og jeg bringer Gengældelse over dig her paa denne Mark, lyder det fra HERREN! Tag derfor og kast ham hen paa Marken efter HERRENS Ord!«
27 Ahaziya mfumu ya ku Yuda ataona zimene zinachitika, anathawira ku Beti Hagani. Yehu anamuthamangitsa, uku akufuwula kuti, “Mupheninso!” Iwo anamuvulaza ali mʼgaleta lakelo pa njira yopita ku Guri pafupi ndi Ibuleamu, koma iye anathawira ku Megido ndipo anakafera kumeneko.
Da Kong Ahazja at Juda saa det, flygtede han ad Vejen til Bet-Hagan; men Jehu satte efter ham og raabte: »Ogsaa ham!« Og i Gurpasset, i Nærheden af Jibleam, skød de ham ned i Vognen. Han undslap til Megiddo, men der døde han.
28 Antchito ake anamunyamulira mʼgaleta kupita naye ku Yerusalemu ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide.
Hans Folk førte ham til Jerusalem og jordede ham i hans Grav hos hans Fædre i Davidsbyen.
29 (Mʼchaka cha khumi ndi chimodzi cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu, Ahaziya anakhala mfumu ya ku Yuda).
I Akabs Søn Jorams ellevte Regeringsaar blev Ahazja Konge over Juda.
30 Kenaka Yehu anapita ku Yezireeli. Yezebeli atamva zimene zinachitika, anapaka zodzikometsera mʼmaso, naluka tsitsi lake, namasuzumira pa zenera.
Jehu kom nu til Jizre'el. Saa snart Jesabel hørte det, sminkede hun sine Øjne og smykkede sit Hoved og bøjede sig ud af Vinduet;
31 Pamene Yehu ankalowa pa chipata iye anafunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere, iwe Zimuri, munthu wopha mbuye wako?”
og da Jehu kørte ind igennem Porten, raabte hun: »Kommer du med Fred, Zimri Kongemorder?«
32 Yehu anakweza maso nayangʼana pa zenera, ndipo anafuwula kuti, “Kodi ndani ali mbali yanga? Ndani?” Anthu ofulidwa awiri kapena atatu anayangʼana Yehu pansipo.
Men han saa op til Vinduet og sagde: »Hvem holder med mig? Hvem?« Saa var der et Par Hofmænd, som saa ud efter ham,
33 Yehu anawawuza kuti, “Muponyeni pansi!” Motero anamuponya pansi ndipo magazi ake ena anafalikira pa khoma ndi pa akavalo pamene ankamupondaponda.
og han raabte: »Styrt hende ned!« Saa styrtede de hende ned, og Blodet sprøjtede op paa Muren og paa Hestene, og de traadte hende ned.
34 Yehu analowa mʼnyumba yaufumu ndipo anadya ndi kumwa. Kenaka iye anati, “Kamutoleni mkazi wotembereredwayo, ndipo kamuyikeni mʼmanda, popeza ndi mwana wa mfumu.”
Derpaa gik han ind og spiste og drak. Saa sagde han: »Tag jer af hende, den forbandede, og jord hende, hun var jo dog en Kongedatter!«
35 Koma atapita kuti akamuyike mʼmanda, sanapeze kanthu kupatula chibade cha mutu wokha, mapazi ake ndi manja ake.
Men da de gik ud for at jorde hende, fandt de ikke andet af hende end Hjerneskallen, Fødderne og Hænderne.
36 Choncho iwo anabwerera kwa Yehu ndi kukamufotokozera kuti, “Mawu amene Yehova anayankhula kudzera mwa mtumiki wake Eliya wa ku Tisibe ndi awa: Pa munda wa ku Yezireeli agalu adzadya mtembo wa Yezebeli.
Og de kom tilbage og meldte ham det; da sagde han: »Det er det Ord, HERREN talede ved sin Tjener Tisjbiten Elias: Paa Jizre'els Mark skal Hundene æde Jesabels Legeme!
37 Mtembo wa Yezebeli udzakhala ngati zinyalala pa munda wa ku Yezireeli, kotero kuti palibe amene adzathe kunena kuti, ‘Uyu ndi Yezebeli.’”
og Jesabels Lig skal blive som Gødning paa Ageren paa Jizre'els Mark, saa ingen kan sige: Dette er Jesabel!«