< 2 Mafumu 8 >
1 Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.”
И глагола Елиссей к жене, еяже воскреси сына, глаголя: востани и иди ты и дом твой, и обитай идеже аще можеши обитати, яко призва Господь глад на землю, и приидет на землю седмь лет.
2 Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.
И воста жена, и сотвори но глаголу Елиссееву, и пойде сама и дом ея, и обита на земли иноплеменничи седмь лет.
3 Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake.
И бысть но скончании седми лет, и возвратися жена от земли иноплеменничи во град, и прииде возопити к царю о доме своем и о селех своих.
4 Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.”
И глагола царь ко Гиезию отроку Елиссеа человека Божия глаголя: повеждь ми ныне вся великая, яже сотвори Елиссей.
5 Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake. Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.”
И бысть ему поведающу цареви, яко жива сотвори сына умершаго: и се, жена, еяже воскреси Елиссей сына ея, вопиющи ко цареви о доме своем и о селех своих, и рече Гиезий: господине царю, сия жена и сей сын ея, егоже жива сотвори Елиссей.
6 Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo. Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”
И вопроси царь жену: и поведа ему. И даде ей царь скопца единаго, глаголя возврати вся, яже ея суть, и вся плоды села ея, от да, в оньже остави землю, даже до ныне.
7 Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,”
И прииде Елиссей в Дамаск. И сын Адеров царь Сирский разболеся, и возвестиша ему, глаголюще: прииде человек Божий до зде.
8 inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
И рече царь ко Азаилу: приими в руку свою дар, и иди во сретение человеку Божию, и вопроси Господа им, глаголя: аще ли жив буду от болезни сея?
9 Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
И иде Азаил на сретение ему, и взя дар в руку свою, и вся благая Дамаскова, бремя четыредесять велблюдов, и прииде, и ста пред ним, и рече ко Елиссею: сын твой, сын Адеров, царь Сирский, посла мя к тебе вопросити, глаголя: буду ли жив от болезни моея сея?
10 Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.”
И рече к нему Елиссей: иди и рцы ему: живя поживеши: но показа ми Господь, яко смертию умрет.
11 Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.
И предста лицу его, и возложи (руки) даже до постыдения, и плакася человек Божий.
12 Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?” Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”
И рече Азаил: что яко господин мой плачет? И рече: вем елика сотвориши сыном Израилевым зла: крепости их сожжеши огнем, и избранныя их избиеши мечем, и младенцы их разбиеши, и во чреве имеющыя их расторгнеши.
13 Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?” Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”
И рече Азаил: кто есть раб твой, пес мертвый, яко сотворит глагол сей? И рече Елиссей: показа ми тя Господь царствующа над Сириею.
14 Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.”
И отиде от Елиссеа и вниде ко господину своему. И рече ему (царь): что ти рече Елиссей? Отвеща: рече ми Елиссей, живя поживеши.
15 Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.
И бысть во утрии, и взя одеяло, и намочи в воде, и обложи на лице его, и умре: и воцарися Азаил вместо его.
16 Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda.
В лето пятое Иорама сына Ахаава царя Израилева и Иосафата царя Иудина, воцарися Иорам сын Иосафатов царь Иудин:
17 Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
сын тридесяти и двою лету бе, внегда воцаритися ему, и осмь лет царствова во Иерусалиме,
18 Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
и ходи в пути царей Израилевых, якоже сотвори дом Ахаавль, бе бо дщи Ахаавля жена ему, и сотвори лукавое пред Господем.
19 Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
И не хотяше Господь потребити Иуды, Давида ради раба Своего, якоже рече дати ему светилник и сыном его во вся дни.
20 Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
Во дни его отвержеся Едом из под руки Иудины и постави над собою царя.
21 Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo.
И взыде Иорам в Сиор, и вся колесницы яже с ним. И бысть ему воставшу, и изби Едома обступившаго окрест его, и князи колесниц, и бежаша людие в селения своя.
22 Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.
И отступи Едом из под руки Иудины да дне сего: тогда отвержеся Ловна во время оно.
23 Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
И прочая словес Иорамлих, и вся елика сотвори, не се ли, сия писана в книзе словес дний царей Иудиных?
24 Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
И успе Иорам со отцы своими, и погребен бысть со отцы своими во граде Давида отца своего: и царствова Охозиа сын его вместо его.
25 Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
В лето второенадесять Иорама сына Ахаавля царя Израилева, царствовати нача Охозиа сын Иорама царя Иудина:
26 Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli.
сын двадесяти двух лет бысть Охозиа, егда нача царствовати, и лето едино царствова во Иерусалиме. Имя же матери его Гофолиа, дщерь Амвриа царя Израилева.
27 Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.
И хождаше по путем дому Ахаавля, и сотвори лукавое пред Господем, якоже дом Ахаавль: зять бо бе дому Ахаавля.
28 Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu.
И иде со Иорамом сыном Ахаавлим на брань, на Азаила царя иноплеменнича в Рамоф Галаадский, и уязвиша Сиряне Иорама.
29 Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu. Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.
И возвратися царь Иорам целитися во Иезраель от язв, имиже уязвиша его в Рамофе, егда ратоваше той на Азаила царя Сирска, и Охозиа сын Иорамль царь Иудин сниде видети Иорама, сына Ахаавля, во Иезраель, яко боляше той.