< 2 Mafumu 8 >

1 Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.”
Or Élisée parla à cette femme dont il avait ressuscité le fils, disant: Lève-toi, va, toi et ta maison, et fais ton séjour partout où tu trouveras; car le Seigneur a appelé la famine, et elle viendra sur la terre pendant sept ans.
2 Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.
Cette femme se leva, et fit selon la parole de l’homme de Dieu, et, s’en allant avec sa maison, elle séjourna dans la terre des Philistins durant un grand nombre de jours.
3 Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake.
Et lorsque les sept années de famine furent passées, cette femme revint de la terre des Philistins; et elle sortit pour réclamer auprès du roi sa maison et ses champs.
4 Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.”
Le roi alors parlait avec Giézi, serviteur de l’homme de Dieu, disant: Raconte-moi toutes les grandes œuvres qu’a faites Élisée.
5 Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake. Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.”
Et comme Giézi racontait au roi de quelle manière il avait ressuscité le mort, parut la femme dont il avait ressuscité le fils, réclamant auprès du roi sa maison et ses champs. Et Giézi dit: Mon seigneurie roi, c’est cette femme, et c’est son fils qu’a ressuscité Élisée.
6 Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo. Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”
Et le roi interrogea la femme, qui lui raconta tout; et le roi lui donna un eunuque, disant: Fais-lui rendre tout ce qui est à elle, et tous les revenus des champs, depuis le jour qu’elle a quitté le pays jusqu’à présent.
7 Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,”
Élisée vint aussi à Damas; et Bénadad, roi de Syrie, était malade, et ses serviteurs lui annoncèrent l’arrivée du prophète, disant: L’homme de Dieu est venu ici.
8 inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
Et le roi dit à Hazaël: Prends avec toi des présents, et va à la rencontre de l’homme de Dieu, et consulte par lui le Seigneur, disant: Si je pourrai échapper de cette maladie.
9 Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
Hazaël alla donc à la rencontre de l’homme de Dieu, ayant avec lui des présents et de toutes les bonnes choses de Damas, la charge de quarante chameaux. Et, lorsqu’il se fut présenté devant Élisée, il dit: Ton fils Bénadad, roi de Syrie, m’a envoyé vers toi, disant: Si je pourrai être guéri de cette maladie.
10 Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.”
Et Élisée lui répondit: Va, dis-lui: Vous guérirez; mais le Seigneur m’a montré qu’il mourra de mort,
11 Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.
Et il s’arrêta avec lui, et il se troubla tellement que son visage rougit; et l’homme de Dieu pleura.
12 Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?” Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”
Hazaël lui demanda: Pourquoi mon seigneur pleure-t-il? Et Élisée lui répondit: Parce que je sais quels maux tu dois faire aux enfants d’Israël. Tu mettras à feu leurs villes fortifiées, tu tueras par le glaive leurs jeunes hommes, tu écraseras leurs enfants, et tu couperas en deux leurs femmes enceintes.
13 Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?” Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”
Hazaël dit: Qui suis-je donc, moi ton serviteur, un chien, pour faire cette grande chose? Et Élisée répondit: Le Seigneur m’a fait voir que tu seras roi de Syrie.
14 Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.”
Lorsque Hazaël se fut retiré d’auprès d’Élisée, il vint vers son maître, qui lui demanda: Que t’a dit Élisée? Et celui-ci répondit: Il m’a dit que vous recouvrerez la santé.
15 Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et lorsque vint le jour suivant, il prit la couverture du lit, il la trempa dans l’eau, et il retendit sur la face du roi; et, le roi mort, Hazaël régna en sa place.
16 Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda.
La cinquième année de Joram, fils d’Achab, roi d’Israël, et de Josaphat, roi de Juda, Joram, fils de Josaphat, régna sur Juda.
17 Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
Il avait trente-deux ans lorsqu’il commença à régner, et il régna huit ans dans Jérusalem.
18 Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
Et il marcha dans les voies des rois d’Israël, comme y avait marché la maison d’Achab; car sa femme était fille d’Achab; et il fit ce qui est mal en la présence du Seigneur.
19 Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
Or le Seigneur ne voulut pas perdre Juda, à cause de David, son serviteur, puisqu’il lui avait promis qu’il lui donnerait une lampe, à lui et à ses fils, tous les jours.
20 Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
Durant les jours de Joram, Edom se retira, pour ne pas être sous Juda, et s’établit un roi.
21 Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo.
Et Joram vint à Séira et tous ses chariots avec lui, et il se leva pendant la nuit, et battit les Iduméens qui l’avaient environné, et ceux qui commandaient leurs chariots; et le peuple s’enfuit dans ses tabernacles.
22 Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.
Edom se retira donc, pour ne pas être sous Juda, jusqu’à ce jour. D’après cela Lobna se retira en ce temps-là.
23 Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Quand au reste des actions de Joram, et tout ce qu’il a fait, n’est-ce pas écrit dans le Livre des actions des jours des rois de Juda?
24 Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et Joram dormit avec ses pères, et il fut enseveli avec eux dans la cité de David, et Ochozias, son fils, régna en sa place.
25 Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
La douzième année de Joram, fils d’Achab, roi d’Israël, régna Ochozias, fils de Joram, roi de Juda.
26 Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli.
Ochozias avait vingt-deux ans quand il commença à régner, et il régna un an dans Jérusalem: le nom de sa mère était Athalie, fille d’Amri, roi d’Israël.
27 Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.
Et il marcha dans les voies de la maison d’Achab, et il fit ce qui est mal devant le Seigneur, comme la maison d’Achab; car il fut gendre de la maison d’Achab.
28 Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu.
Il alla aussi avec Joram, fils d’Achab, pour combattre contre Hazaël, roi de Syrie, à Ramoth-Galaad; et les Syriens blessèrent Joram,
29 Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu. Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.
Qui revint à Jezrahel pour être guéri, parce que les Syriens l’avaient blessé à Ramoth, lorsqu’il combattait contre Hazaël, roi de Syrie. Or Ochozias, fils de Joram, roi de Juda, descendit pour voir Joram, fils d’Achab, à Jezrahel, parce qu’il y était malade.

< 2 Mafumu 8 >