< 2 Mafumu 8 >
1 Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.”
Élisée avait parlé à la femme dont il avait rendu la vie au fils, en disant: « Lève-toi, va, toi et ta famille, et reste quelque temps où tu pourras, car Yahvé a annoncé une famine. Elle s'abattra sur le pays pendant sept ans. »
2 Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.
La femme se leva, et fit ce que l'homme de Dieu lui avait dit. Elle partit avec sa famille, et elle vécut sept ans dans le pays des Philistins.
3 Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake.
Au bout de sept ans, la femme revint du pays des Philistins. Elle sortit pour demander au roi sa maison et son pays.
4 Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.”
Or, le roi parlait avec Guéhazi, le serviteur de l'homme de Dieu, en disant: « Je te prie de me raconter toutes les grandes choses qu'Élisée a faites. »
5 Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake. Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.”
Comme il racontait au roi comment il avait rendu la vie à celui qui était mort, voici que la femme dont il avait rendu la vie au fils supplia le roi pour sa maison et pour son pays. Guéhazi dit: « Mon seigneur, ô roi, voici la femme et voici son fils qu'Élisée a rendu à la vie. »
6 Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo. Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”
Le roi interrogea la femme, et elle lui répondit. Alors le roi lui nomma un officier, en disant: « Restaure tout ce qui lui appartenait, et tous les fruits des champs depuis le jour où elle a quitté le pays, jusqu'à maintenant. »
7 Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,”
Elisée arriva à Damas, et Benhadad, le roi de Syrie, était malade. On lui dit: « L'homme de Dieu est venu ici. »
8 inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
Le roi dit à Hazaël: « Prends un présent dans ta main, va à la rencontre de l'homme de Dieu, et interroge par lui Yahvé en disant: « Vais-je guérir de cette maladie? »"
9 Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
Hazaël alla au-devant de lui et prit avec lui un présent, de tout ce qu'il y avait de bon à Damas, quarante charges de chameaux, puis il vint se placer devant lui et dit: « Ton fils Benhadad, roi de Syrie, m'a envoyé vers toi, en disant: « Vais-je guérir de cette maladie? »
10 Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.”
Élisée lui dit: « Va, dis-lui: « Tu vas guérir », mais l'Éternel m'a montré qu'il allait mourir. »
11 Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.
Il fixa son regard sur lui, jusqu'à ce qu'il ait honte. Alors l'homme de Dieu pleura.
12 Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?” Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”
Hazaël dit: « Pourquoi pleures-tu, mon seigneur? » Il répondit: « Parce que je sais le mal que tu feras aux enfants d'Israël. Vous mettrez le feu à leurs forteresses, vous tuerez leurs jeunes gens par l'épée, vous mettrez en pièces leurs petits enfants et vous déchirerez leurs femmes enceintes. »
13 Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?” Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”
Hazaël dit: « Mais qu'est-ce que ton serviteur, qui n'est qu'un chien, pour qu'il puisse faire cette grande chose? » Elisée répondit: « Yahvé m'a montré que tu seras roi de Syrie. »
14 Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.”
Puis il se sépara d'Élisée et vint vers son maître, qui lui dit: « Que t'a dit Élisée? » Il a répondu: « Il m'a dit que vous alliez sûrement guérir. »
15 Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.
Le lendemain, il prit un linge épais, le trempa dans l'eau et l'étendit sur le visage du roi, de sorte qu'il mourut. Hazaël régna à sa place.
16 Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda.
La cinquième année de Joram, fils d'Achab, roi d'Israël, Josaphat étant alors roi de Juda, Joram, fils de Josaphat, roi de Juda, commença à régner.
17 Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
Il avait trente-deux ans lorsqu'il devint roi. Il régna huit ans à Jérusalem.
18 Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
Il marcha dans la voie des rois d'Israël, comme la maison d'Achab, car il avait épousé la fille d'Achab. Il fit ce qui est mal aux yeux de l'Éternel.
19 Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
Cependant, l'Éternel ne voulut pas détruire Juda, à cause de David, son serviteur, car il lui avait promis de lui donner une lampe pour ses enfants, pour toujours.
20 Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
De son temps, Édom se révolta de dessous la main de Juda, et se fit un roi.
21 Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo.
Et Joram passa à Zaïr, et tous ses chars avec lui; et il se leva de nuit et frappa les Édomites qui l'entouraient avec les chefs des chars; et le peuple s'enfuit dans ses tentes.
22 Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.
Ainsi Édom se révolta de dessous la main de Juda jusqu'à ce jour. En même temps, Libna se révolta.
23 Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Le reste des actes de Joram, et tout ce qu'il a fait, n'est-ce pas écrit dans le livre des Chroniques des rois de Juda?
24 Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Joram se coucha avec ses pères et fut enterré avec ses pères dans la ville de David; et Achazia, son fils, régna à sa place.
25 Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
La douzième année de Joram, fils d'Achab, roi d'Israël, Achazia, fils de Joram, roi de Juda, commença à régner.
26 Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli.
Achazia avait vingt-deux ans lorsqu'il devint roi, et il régna un an à Jérusalem. Le nom de sa mère était Athalie, fille d'Omri, roi d'Israël.
27 Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.
Il marcha dans la voie de la maison d'Achab et fit ce qui est mal aux yeux de Yahvé, comme la maison d'Achab, car il était le gendre de la maison d'Achab.
28 Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu.
Il alla avec Joram, fils d'Achab, à la guerre contre Hazaël, roi de Syrie, à Ramoth Galaad, et les Syriens blessèrent Joram.
29 Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu. Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.
Le roi Joram revint se faire guérir à Jizreel des blessures que les Syriens lui avaient faites à Rama, lorsqu'il combattait contre Hazaël, roi de Syrie. Achazia, fils de Joram, roi de Juda, descendit voir Joram, fils d'Achab, à Jizreel, car il était malade.