< 2 Mafumu 7 >

1 Ndipo Elisa anati, “Mverani mawu a Yehova. Yehova akuti, ‘Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.’”
Kinuna ni Eliseo, “Denggenyo ti sao ni Yahweh. Kastoy ti imbaga ni Yahweh: 'Inton bigat iti kastoy nga oras, mailakonto ti sangkasukat a napino nga arina iti maysa a siklo, ken dua a sukat a trigo iti maysa a siklo, idiay ruangan ti Samaria.'”
2 Mtsogoleri amene mfumu inkamudalira anati kwa munthu wa Mulungu, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Elisa anamuyankha kuti, “Taona, iweyo udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”
Ket simmungbat ti kapitan a nangkuyog iti ari iti tao ti Dios, ket kinunana, “Kitaem, uray no mangaramid ni Yahweh kadagiti tawa idiay langit, mapasamak kadi met daytoy a banag?” Simmungbat ni Eliseo, “Kitaem, maimatangamto daytoy a mapasamak babaen kadagiti bukodmo a mata, ngem saanka makapangan iti uray ania iti daytoy.”
3 Tsono pa chipata cholowera mu mzinda wa Samariya pankakhala anthu anayi akhate. Iwo anayankhulana kuti, “Chifukwa chiyani tikungokhala pano kudikira kufa?
Ita, adda uppat a lallaki a kinetong iti laeng ruar ti ruangan ti siudad. Kinunada iti tunggal maysa, “Apay ketdin nga agtugawtayo ditoy agingga a mataytayo?
4 Ngati tinganene kuti, ‘Tidzalowa mu mzinda,’ njala ili mu mzindamo ndipo tidzafa. Ndipo ngati tikhalebe pano, tidzafa ndithu. Choncho tiyeni tipite ku msasa wa Aaramu ndi kukadzipereka. Ngati sakatipha, tidzakhala ndi moyo, ngati akatipha, basi tikafa.”
No ibagatayo a mapantayo idiay siudad ket adda panagbisin iti siudad, ket mataytayonto sadiay. Ngem no agtugawtayo latta ditoy, mataytayonto latta. Ita ngarud, umaykayo, mapantayo iti armada dagiti Arameo. No pagtalinaedendatayo a sibibiag, agbiagtayo, ket no papatayendatayo, mataytayonto laeng.”
5 Iwo ananyamuka ndi kachisisira kupita ku msasa wa Aaramu. Atafika mʼmalire a msasa, taonani, sanapeze munthu ndi mmodzi yemwe,
Timmakderda ngarud a mapan kadagiti kampo dagiti Arameo iti sumipngeten; idi nakadanonda iti kaadaywan a paset ti kampo, awan ti uray maysa sadiay.
6 pakuti Ambuye anali atamveketsa phokoso la magaleta ndi akavalo ndiponso mdidi wa gulu lalikulu la ankhondo, kotero anayamba kuwuzana kuti, “Taonani, mfumu ya ku Israeli yalemba ganyu mafumu a Ahiti ndi a Aigupto kuti adzatithire nkhondo!”
Ta impadengngeg ti Apo iti armada dagiti Arameo ti daranudor dagiti karwahe ken kabkabalio - ti tagari iti sabali pay a dakkel nga armada, ket kinunada iti tunggal maysa, “Tinangdanan ti ari ti Israel dagiti ari dagiti Heteo ken Egipsio nga umay a maibusor kadatayo.”
7 Choncho ananyamuka nathawa ndi kachisisira ndipo anasiya matenti, akavalo ndi abulu awo. Iwo anasiya msasa wawo momwe unalili nathawa kupulumutsa miyoyo yawo.
Isu a nagrubbuat dagiti soldado ket naglibasda idi sumipngeten; pinanawanda dagiti toldada, kabalioda, asnoda, ken ti kampoda ket timmarayda tapno insalakanda dagiti biagda.
8 Anthu akhate aja atafika mʼmalire mwa msasa analowa mʼtenti imodzi. Anadya ndi kumwa, natenga siliva, golide ndi zovala ndipo anachoka kupita kukazibisa. Atabwerera anakalowa mʼtenti ina ndipo anatenga zinthu mʼmenemo nakazibisanso.
Idi nakadanon dagiti kinetong a lallaki iti kaadaywan a paset ti kampo, immunegda iti maysa a tolda ket nangan ken imminumda, ken nangalada kadagiti pirak, balitok ken kawkawes, pimmanawda ket napanda indulin dagitoy. Nagsublida ket simrekda pay iti sabali a tolda ket nagtakawda pay sadiay, ket napanda indulin daytoy.
9 Kenaka akhate aja anawuzana kuti, “Ife sitikuchita bwino. Lero ndi tsiku la uthenga wabwino ndipo tikungokhala chete. Tikadikira mpaka kucha, tidzalangidwa. Tiyeni msanga tikafotokoze zimenezi ku nyumba yaufumu.”
Kalpasanna, kinunada iti tunggal maysa, “Saan nga umno ti ar-aramidentayo. Daytoy nga aldaw ket aldaw ti naimbag a damag, ngem ilimlimedtayo ti maipapan iti daytoy. No aguraytayo agingga iti agsapa, kamakamennatayo ti pannusa. Ita ngarud, umaykayo, intayo ibaga iti sangkabalayan ti ari.”
10 Choncho anapita nakayitana alonda a pa chipata cha mzinda ndi kufotokoza kuti, “Ife tinapita ku msasa wa Aaramu ndipo sitinapezeko munthu, kapena phokoso la wina aliyense koma tinangopeza akavalo okha pamodzi ndi abulu ali chimangire.”
Isu a napanda ket pinukkawanda dagiti mangay-aywan iti ruangan ti siudad. Imbagada kadakuada, a kunada, “Napankami iti kampo dagiti Arameo, ngem awan ti uray maysa sadiay, uray uni ti siasinoman, ngem adda sadiay a nakatali dagiti kabalio ken asno, ken adda pay laeng sadiay dagiti tolda a sitatakder.”
11 Alonda a pa chipata aja analengeza uthengawu kwa okhala mʼnyumba yaufumu.
Ket impukpukkaw dagiti mangay-aywan iti ruangan ti siudad ti damag, ket kalpasanna, naibaga daytoy iti uneg ti sangkabalayan ti ari.
12 Mfumu inadzuka usiku ndipo inawuza atsogoleri ake a ankhondo kuti, “Ndikukuwuzani zimene Aaramu atichitira ife. Akudziwa kuti tikufa ndi njala; kotero achoka mu msasa wawo kukabisala kuthengo ndi kuti, ‘Iwowa atuluka ndithu, ndipo ife tidzawagwira amoyo ndi kulowa mu mzindamo.’”
Bimmangon ngarud ti ari iti rabii ket kinunana kadagiti adipenna, “Ibagak ita kadakayo no ania ti inaramid dagiti Arameo kadatayo. Ammoda a mabisintayo, isu a pimmanawda kadagiti kampo tapno mapanda aglemmeng kadagiti talon. Kunada, “Inton rummuarda iti siudad, tiliwentayo ida a sibibiag, ket serrekentayo ti siudad.'”
13 Mmodzi mwa atsogoleri ake ankhondo anayankha kuti, “Chonde uzani anthu ena atenge akavalo asanu amene atsala mu mzinda muno. Taonani, zomwe zingawachitikire zidzakhala zofanana ndi zomwe zingachitikire ena onse amene atsala. Inde iwo adzangokhala ngati Aisraeli ena onse amene awonongeka kale. Choncho tiyeni tiwatume akafufuze zomwe zachitika.”
Maysa kadagiti adipen ti ari ti simmungbat ket kinuna, “Agpakpakaasiak kenka, pangalaem koma dagiti lallaki iti lima a kabalio kadagiti natda, a nabati iti siudad. Maiyarigda amin kadagiti nabati a tattao iti Israel - kaaduan ket natayen; ibaontayo koma ida ket kitaentayo ti mapasamak.”
14 Choncho anasankha magaleta awiri pamodzi ndi akavalo ake, ndipo mfumu inawatuma kuti alondole gulu lankhondo la Aaramu. Mfumuyo inalamula oyendetsa akavalowo kuti, “Pitani kaoneni.”
Isu a nangalada iti dua a karwahe agraman kadagiti kabalio, ket imbaon ti ari ida a mangsaruno iti armada dagiti Arameo, kunana, “Inkayo kitaen.”
15 Anthuwa anawalondola mpaka ku Yorodani, ndipo taonani, mʼnjira monse munali zovala zokhazokha ndi zinthu zimene Aaramu ankazitaya pamene ankathawa mofulumira. Ndipo amithengawo anabwerera ndi kudzafotokozera mfumu.
Sinurotda ida iti Karayan Jordan, ket nagkaiwara iti amin a dalan dagiti kawes ken alikamen nga imbelleng dagiti Arameo iti panagdardarasda. Isu a nagsubli dagiti mensahero ket imbagada iti ari.
16 Tsono anthu a mu Samariya anatuluka nakafunkha ku msasa wa Aaramu. Kotero kuti makilogalamu atatu a ufa ankawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele ankawagulitsanso pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, monga momwe ananenera Yehova.
Rimmuar dagiti tattao ket sinamsamda ti adda iti kampo dagiti Arameo. Isu a nailako ti sangkasukat a napino nga arina iti maysa a siklo, ken dua a sukat a trigo iti maysa a siklo, kas naibaga ti sao ni Yahweh.
17 Tsono mfumu inayika mtsogoleri amene ankamudalira uja kuti akhale woyangʼanira pa chipata ndipo anthu anamupondaponda ku chipata kuja, ndipo anafa, monga momwe Elisa munthu wa Mulungu ananenera mfumu itapita ku nyumba yake.
Binilin ti ari ti kapitan a nangkuyog kenkuana nga isu ti mangimaton iti ruangan, ket binaddebaddekan isuna dagiti tattao iti pagserkan. Natay isuna a kas iti imbaga ti tao ti Dios, a nagsao idi napan ti ari kenkuana.
18 Zinachitika molingana ndi zomwe ananena munthu wa Mulungu zija kuti “Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.”
Napasamak ngarud daytoy a kas imbaga ti tao ti Dios iti ari, a kunana, ''Iti kastoy nga oras idiay ruangan ti Samaria, mailakonto ti dua a rukod ti trigo a iti maysa a siklo, ken maysa a rukod ti kasasayaatan nga arina iti maysa a siklo.”
19 Mtsogoleriyu ananena kwa munthu wa Mulungu kuti, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Munthu wa Mulungu anamuyankha kuti, “Iwe udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”
Simmungbat dayta a kapitan iti tao ti Dios a kinunana, “Kitaem, uray no mangaramid ni Yahweh kadagiti tawa idiay langit, mabalin met aya a mapasamak daytoy a banag?” Naibaga ni Eliseo, “Kitaem, maimatangamto daytoy a mapasamak babaen kadagiti bukodmo a mata, ngem saankanto a makapangan iti uray ania iti daytoy.”
20 Ndipo izi ndi zomwe zinamuchitikiradi mtsogoleriyu, pakuti anthu anamupondaponda pa chipata ndipo anafa.
Ket kasta ngarud ti napasamak kenkuana, ta binaddebaddekan isuna dagiti tattao idiay ruangan, ket natay isuna.

< 2 Mafumu 7 >