< 2 Mafumu 7 >
1 Ndipo Elisa anati, “Mverani mawu a Yehova. Yehova akuti, ‘Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.’”
I MAI la o Elisai, E hoolohe oukou i ka olelo a Iehova, Ke olelo mai nei o Iehova peneia, Ma keia manawa i ka la apopo, e lilo kekahi bakeke palaoa no ka sekela hookahi, a elua bakeke bale no ka sekela hookahi ma ka ipuka o Samaria.
2 Mtsogoleri amene mfumu inkamudalira anati kwa munthu wa Mulungu, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Elisa anamuyankha kuti, “Taona, iweyo udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”
Alaila kekahi luna kiai no ke alii ka mea ana i hilinai ai ma kona lima, olelo mai la ia i ke kanaka o ke Akua, i mai la, Aia hoi, ina e hana mai o Iehova i na puka ma ka Iani, e hiki mai anei keia mea? I aku la ia, E ike auanei kou mau maka, aka, aole oe e ai ia mea.
3 Tsono pa chipata cholowera mu mzinda wa Samariya pankakhala anthu anayi akhate. Iwo anayankhulana kuti, “Chifukwa chiyani tikungokhala pano kudikira kufa?
A eha kanaka lepera ma ke komo ana o ka ipuka; a i ae la lakou i kekahi i kekahi, No ke aha la kakou e noho maanei, a make kakou?
4 Ngati tinganene kuti, ‘Tidzalowa mu mzinda,’ njala ili mu mzindamo ndipo tidzafa. Ndipo ngati tikhalebe pano, tidzafa ndithu. Choncho tiyeni tipite ku msasa wa Aaramu ndi kukadzipereka. Ngati sakatipha, tidzakhala ndi moyo, ngati akatipha, basi tikafa.”
A i olelo kakou, e komo iloko o ke kulanakauhale, aia hoi, maloko o ke kulanakauhale ka wi, a e make auanei kakou malaila: a i noho kakou maanei, e make kakou. Ano hoi, ea, e haule kakou i ka poe kaua o ko Suria, ina e hoola lakou ia kakou, ua ola; aka, ina e pepehi mai lakou ia kakou, ua make no hoi.
5 Iwo ananyamuka ndi kachisisira kupita ku msasa wa Aaramu. Atafika mʼmalire a msasa, taonani, sanapeze munthu ndi mmodzi yemwe,
Ku ae la lakou i ka wanaao e hele aku i kahi hoomoana o ko Suria: a hiki lakou ma ka palena o kahi hoomoana o ko Suria, aia hoi, aohe kanaka malaila.
6 pakuti Ambuye anali atamveketsa phokoso la magaleta ndi akavalo ndiponso mdidi wa gulu lalikulu la ankhondo, kotero anayamba kuwuzana kuti, “Taonani, mfumu ya ku Israeli yalemba ganyu mafumu a Ahiti ndi a Aigupto kuti adzatithire nkhondo!”
No ka mea, ua haawi mai o Iehova i ka poe kaua o ko Suria i ka lohe i ka halulu o na halekaa, a me ka halulu o na lio, ka halulu o ke kaua nui; i ae la lakou i kekahi i kekahi, Aia hoi, ua hoolimalima ke alii o ka Iseraela i na'lii o ka Heta e ku e mai ia kakou, a me na'lii o Aigupita e hele mai maluna o kakou.
7 Choncho ananyamuka nathawa ndi kachisisira ndipo anasiya matenti, akavalo ndi abulu awo. Iwo anasiya msasa wawo momwe unalili nathawa kupulumutsa miyoyo yawo.
No ia mea, ku ae la lakou, a holo i ka wanaao, a haalele aku la lakou i ko lakou mau halelewa, a me ko lakou lio, a me na hoki o lakou, a i kahi hoomoana pela, a holo aku la lakou, i ola.
8 Anthu akhate aja atafika mʼmalire mwa msasa analowa mʼtenti imodzi. Anadya ndi kumwa, natenga siliva, golide ndi zovala ndipo anachoka kupita kukazibisa. Atabwerera anakalowa mʼtenti ina ndipo anatenga zinthu mʼmenemo nakazibisanso.
A hiki aku la na lepero ma ka palena o kahi hoomoana, komo aku la lakou iloko o kekahi halelewa, a ai iho la lakou, a inu hoi, a lawe aku lakou i ke kala a me ke gula, a me na aahu mai laila aku, hele aku, a huna; a hoi mai a komo aku iloko o kekahi halelewa e ae, a lawe aku no hoi mai laila aku, a hele aku, a huna.
9 Kenaka akhate aja anawuzana kuti, “Ife sitikuchita bwino. Lero ndi tsiku la uthenga wabwino ndipo tikungokhala chete. Tikadikira mpaka kucha, tidzalangidwa. Tiyeni msanga tikafotokoze zimenezi ku nyumba yaufumu.”
I ae la lakou i kekahi i kekahi. Aole pono ka kakou hana ana; o keia la, he la pomaikai, a ke noho malie nei kakou; a i noho a hiki i ka malamalama o ke ao, e loaa uanei ia kakou ka hewa: ano hoi e hele aku kakou, a o hai aku i ko ka hale o ke alii.
10 Choncho anapita nakayitana alonda a pa chipata cha mzinda ndi kufotokoza kuti, “Ife tinapita ku msasa wa Aaramu ndipo sitinapezeko munthu, kapena phokoso la wina aliyense koma tinangopeza akavalo okha pamodzi ndi abulu ali chimangire.”
A hele lakou, a kahea aku i ke kiai-puka o ke kulanakauhale; a hai aku ia lakou, i aku la, Hele aku makou i kahi hoomoana o ko Suria, aia hoi, aohe kanaka malaila, aohe leo o ke kanaka, o na lio wale no i nakiiia, a me na hoki i nakiiia, a me na halelewa e waiho ana pela.
11 Alonda a pa chipata aja analengeza uthengawu kwa okhala mʼnyumba yaufumu.
Kahea aku la ia i na kiai-puka, a hai aku la lakou i ko ka hale o ke alii maloko.
12 Mfumu inadzuka usiku ndipo inawuza atsogoleri ake a ankhondo kuti, “Ndikukuwuzani zimene Aaramu atichitira ife. Akudziwa kuti tikufa ndi njala; kotero achoka mu msasa wawo kukabisala kuthengo ndi kuti, ‘Iwowa atuluka ndithu, ndipo ife tidzawagwira amoyo ndi kulowa mu mzindamo.’”
Ala mai ke alii i ka po, i aku la i kana poe kauwa, Ano e hoike aku au ia oukou i ka mea a ko Suria i hana mai ai ia kakou. Ua ike lakou i ko kakou pololi ana; nolaila, ua hele aku lakou mai ko lakou wahi hoomoana aku e pee ma ke kula, i ka i ana'e, Aia puka lakou mailoko mai o ke kulanakauhale, alaila lawe pio kakou ia lakou e ola ana, a komo iloko o ke kulanakauhale.
13 Mmodzi mwa atsogoleri ake ankhondo anayankha kuti, “Chonde uzani anthu ena atenge akavalo asanu amene atsala mu mzinda muno. Taonani, zomwe zingawachitikire zidzakhala zofanana ndi zomwe zingachitikire ena onse amene atsala. Inde iwo adzangokhala ngati Aisraeli ena onse amene awonongeka kale. Choncho tiyeni tiwatume akafufuze zomwe zachitika.”
Olelo mai kekahi o na kauwa ana, i mai la, Ke noi aku nei au ia oe, e lawe lakou i elima o na lio e koe ana, na mea i koe iloko olaila, (aia, ua like lakou me ka Iseraela a pau e koe ana; aia hoi, ua like lakou mo ka poe nui o ka Iseraela i make, ) a hoouna aku kakou, a ike.
14 Choncho anasankha magaleta awiri pamodzi ndi akavalo ake, ndipo mfumu inawatuma kuti alondole gulu lankhondo la Aaramu. Mfumuyo inalamula oyendetsa akavalowo kuti, “Pitani kaoneni.”
A lawe lakou i elua kaulualio, a hoouna aku la ke alii mahope o ka poe kaua o ko Suria, i aku la, E hele aku a ike.
15 Anthuwa anawalondola mpaka ku Yorodani, ndipo taonani, mʼnjira monse munali zovala zokhazokha ndi zinthu zimene Aaramu ankazitaya pamene ankathawa mofulumira. Ndipo amithengawo anabwerera ndi kudzafotokozera mfumu.
A hele aku lakou mahope o lakou la, a Ioredane; aia hoi, ua paapu ke alanui a pau i na aahu, a me na mea kaua a ko Suria i hoolei ai i ko lakou holo kiki ana. A hoi mai na elele, a hai mai i ke alii.
16 Tsono anthu a mu Samariya anatuluka nakafunkha ku msasa wa Aaramu. Kotero kuti makilogalamu atatu a ufa ankawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele ankawagulitsanso pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva, monga momwe ananenera Yehova.
A hele aku na kanaka, a hao lakou i ko kahi hoomoana o ko Suria. No ia mea, ua lilo ka bakeke palaoa no ka sekela hookahi, a elua bakeke bale no ka sekela hookahi, e like me ka olelo a Iehova.
17 Tsono mfumu inayika mtsogoleri amene ankamudalira uja kuti akhale woyangʼanira pa chipata ndipo anthu anamupondaponda ku chipata kuja, ndipo anafa, monga momwe Elisa munthu wa Mulungu ananenera mfumu itapita ku nyumba yake.
A hoonoho aku la ke alii i ka lunakiai, i ka mea ana i hilinai ai ma kona lima, e malama i ka ipuka; a hehi iho la na kanaka maluna ona, a make iho la ia, e like me ka olelo a ke kanaka o ke Akua, ana i olelo ai i ka hele ana o ke alii io na la.
18 Zinachitika molingana ndi zomwe ananena munthu wa Mulungu zija kuti “Mawa nthawi ngati yomwe ino, makilogalamu atatu a ufa adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ndipo makilogalamu asanu ndi limodzi a barele adzawagulitsa pa mtengo wa ndalama imodzi yasiliva ku chipata cha Samariya.”
E like no me ka olelo a ke kanaka o ke Akua i ke alii, i ka i ana'e, Elua bakeke bale no ka sekela hookahi, a hookahi bakeke palaoa no ka sekela hookahi, i keia manawa i ka la apopo ma ka ipuka o Samaria.
19 Mtsogoleriyu ananena kwa munthu wa Mulungu kuti, “Taona, ngakhale Yehova atatsekula zipata zakumwamba, kodi zimenezi zingachitikedi?” Munthu wa Mulungu anamuyankha kuti, “Iwe udzaziona zimenezi ndi maso ako, koma sudzadyako kanthu.”
A olelo mai ua lunakiai la i ke kanaka o ke Akua, i mai la, Aia hoi, ina e hana mai o Iehova i na puka ma ka lani, e hiki mai anei keia mea? I aku la ia, Aia hoi, e ike auanei kou mau maka, aka, aole oe e ai ia mea.
20 Ndipo izi ndi zomwe zinamuchitikiradi mtsogoleriyu, pakuti anthu anamupondaponda pa chipata ndipo anafa.
A pela i hanaia mai ai ia ia: no ka mea, hehi iho la na kanaka maluna ona ma ka ipuka, a make iho la ia.